Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 97 - Buku Lopatulika


Ulemerero wa ufumu wa Mulungu

1 Yehova achita ufumu; dziko lapansi likondwere; zisumbu zambiri zikondwerere.

2 Pomzinga pali mitambo ndi mdima; chilungamo ndi chiweruzo ndizo zolimbitsa mpando wake wachifumu.

3 Moto umtsogolera, nupsereza otsutsana naye pozungulirapo.

4 Mphezi zake zinaunikira dziko lokhalamo anthu; dziko lapansi linaona nilinagwedezeka.

5 Mapiri anasungunuka ngati sera pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.

6 Kumwamba kulalikira chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu ipenya ulemerero wake.

7 Onse akutumikira fano losema, akudzitamandira nao mafano, achite manyazi: Mgwadireni Iye, milungu yonse inu.

8 Ziyoni anamva nakondwera, nasekerera ana aakazi a Yuda; chifukwa cha maweruzo anu, Yehova.

9 Pakuti Inu, Yehova, ndinu Wam'mwambamwamba padziko lonse lapansi, ndinu wokwezeka kwakukulu pamwamba pa milungu ina yonse.

10 Inu okonda Yehova, danani nacho choipa: Iye asunga moyo wa okondedwa ake; awalanditsa m'manja mwa oipa.

11 Kuunika kufesekera wolungama, ndi chikondwerero oongoka mtima.

12 Kondwerani mwa Yehova, olungama inu; ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa