Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


102 Mau a m’Baibulo Okhudza Chigololo ndi Chisudzulo

102 Mau a m’Baibulo Okhudza Chigololo ndi Chisudzulo

Kuswa pangano kumabweretsa chisoni chachikulu mumtima. Masiku ano, kusakhulupirika kwafala kwambiri, ulemu ndi kukhulupirirana zikuoneka ngati zinthu zakale. Dziko likuoneka ngati likutinenera kuti kukhulupirika ndi nkhani yakale, koma izi zimam’bweretsa chisoni Mulungu.

M’masiku ovuta ano, njira yokha yopewera mayesero ndi ziwembu za mdani ndi kukhala paubwenzi wolimba ndi Mzimu Woyera. Kusakhulupirika ndi tchimo pamaso pa Mulungu, kwa mnzanu, komanso kwa Yesu. Ndikofunikira kusamala mtima wanu, maso anu, ndi makutu anu, kupewa njira zoyipa, ndikupempha thandizo ngati mukuyesedwa kusakhulupirika.

Mulungu anakhazikitsa ukwati mpaka imfa ikalekanitse, osati chinyengo kapena ziwembu za mdierekezi. Ngati mukuyesedwa kusakhulupirika, pitani kwa Mulungu, pemphani chikhululukiro, ndikupempha thandizo kwa anthu okhwima m’chikhulupiriro kuti akupempherereni. Mukatero, mudzaona mpamvu ya Mzimu Woyera ikukuthandizani kupulumutsa moyo wanu ndi ubale wanu.




Mateyu 5:27-28

Munamva kuti kunanenedwa, Usachite chigololo; koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wakuyang'ana mkazi kumkhumba, pamenepo watha kuchita naye chigololo mumtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:32

Wochita chigololo ndi mkazi alibe nzeru; wofuna kuononga moyo wakewake ndiye amatero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:9

Ndipo Ine ndinena kwa inu, Amene aliyense akachotsa mkazi wake, kosakhala chifukwa cha chigololo, nadzakwatira wina, achita chigololo: ndipo iye amene akwatira wochotsedwayo, achita chigololo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:4

Akazi achigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uli udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 5:3-5

Pakuti milomo ya mkazi wachiwerewere ikukha uchi; m'kamwa mwake muti see koposa mafuta. Chimaliziro chake nchowawa ngati chivumulo, ndi chakuthwa ngati lupanga lakuthawa konsekonse. Mayendedwe ake atsikira kuimfa; mapazi ake aumirira kumanda;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 15:19

Pakuti mumtima muchokera maganizo oipa, zakupha, zachigololo, zachiwerewere, zakuba, za umboni wonama, zamwano;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 10:11-12

Ndipo Iye ananena nao, Munthu aliyense akachotsa mkazi wake, nakakwatira wina, achita chigololo kulakwira mkaziyo; ndipo ngati mkazi akachotsa mwamuna wake, nakwatiwa ndi wina, achita chigololo iyeyu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 7:25-27

Mtima wako usapatukire kunjira ya mkaziyo, usasochere m'mayendedwe ake. Pakuti amagwetsa ambiri, atawalasa; ndipo ophedwa ndi iye achulukadi. Nyumba yake ndiyo njira ya kumanda, yotsikira kuzipinda za imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:10-11

Mundilengere mtima woyera, Mulungu; mukonze mzimu wokhazikika m'kati mwanga. Musanditaye kundichotsa pamaso panu; musandichotsere Mzimu wanu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:26

ndipo ndinapeza kanthu kowawa koposa imfa, ndiko mkazi amene ndiye msampha, mtima wake ukunga maukonde, manja ake ndiwo matangadza; yemwe Mulungu amuyesa wabwino adzapulumuka kwa iye; koma wochimwa adzagwidwa naye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 5:7-8

Bwanji ndidzakhululukira iwe? Pamenepo ana ako andisiya Ine, nalumbira pa iyo yosati milungu; pamene ndinakhutitsa iwo, anachita chigololo, nasonkhana pamodzi m'nyumba za adama. Anali onga akavalo okhuta mamawa; yense wakumemesera mkazi wa mnansi wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 2:2

Ndipo akhumbira minda, nailanda; ngakhale nyumba, nazichotsa; asautsa mwamuna ndi nyumba yake, inde munthu ndi cholowa chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:37

Muchititse mlubza maso anga ndisapenye zachabe, mundipatse moyo mu njira yanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:4-6

Ndipo Iye anayankha, nati, Kodi simunawerenga kuti Iye amene adalenga anthu pachiyambi, anawalenga iwo mwamuna ndi mkazi, nati, Chifukwa cha ichi mwamuna adzasiya atate wake ndi amake, nadzaphatikizana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi? Chotero kuti salinso awiri koma thupi limodzi. Chifukwa chake ichi chimene Mulungu anachimanga pamodzi, munthu asachilekanitse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 7:2-3

Pakuti mkazi wokwatidwa amangidwa ndi lamulo kwa mwamuna wake wamoyo; koma mwamunayo akafa, iye amasulidwa ku lamulo la mwamunayo. Koma ngati ndichita chimene sindichifuna, si ndinenso amene ndichichita, koma uchimo wakukhalabe m'kati mwanga ndiwo. Ndipo chotero ndipeza lamulo ili, kuti, pamene ndifuna chabwino, choipa chiliko. Pakuti monga mwa munthu wa m'kati mwanga, ine ndikondwera ndi chilamulo cha Mulungu: koma ndiona lamulo lina m'ziwalo zanga, lilikulimbana ndi lamulo la mtima wanga, ndi kundigonjetsa kapolo wa lamulo la uchimo m'ziwalo zanga. Munthu wosauka ine; adzandilanditsa ndani m'thupi la imfa iyi? Ndiyamika Mulungu, mwa Yesu Khristu Ambuye wathu. Ndipo chotero ine ndekha ndi mtimatu nditumikira chilamulo cha Mulungu; koma ndi thupi nditumikira lamulo la uchimo. Ndipo chifukwa chake, ngati iye akwatiwa ndi mwamuna wina, pokhala mwamuna wake wamoyo, adzanenedwa mkazi wachigololo; koma mwamunayo akafa, iye amasulidwa ku lamuloli; chotero sakhala wachigololo ngati akwatiwa ndi mwamuna wina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:27

Pakuti, taonani, iwo okhala patali ndi Inu adzaonongeka; muononga onse akupembedza kwina, kosiyana ndi Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 16:32-34

Ndiwe mkazi wokwatibwa wochita chigololo, wolandira alendo m'malo mwa mwamuna wake. Anthu amaninkha akazi onse achigololo mphatso, koma iwe umaninkha mabwenzi ako onse mphatso zako ndi kuwalipira, kuti akudzere kuchokera kumbali zonse, kuti achite nawe chigololo. M'mwemo usiyana konse ndi akazi ena m'chigololo chako; pakuti palibe wokutsata kuchita nawe chigololo; popezanso uwalipira, koma sakupatsa iwe mphotho; potero usiyana nao konse ena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 2:16-17

Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere, kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake; wosiya bwenzi la ubwana wake, naiwala chipangano cha Mulungu wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:15-16

Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko lapansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, chikondi cha Atate sichili mwa iye. Pakuti chilichonse cha m'dziko lapansi, chilakolako cha thupi ndi chilakolako cha maso, matamandidwe a moyo, sizichokera kwa Atate, koma kudziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:155

Chipulumutso chitalikira oipa; popeza safuna malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:20

Chomwecho njira ya mkazi wachigololo; adya, napukuta pakamwa, nati, Sindinachite zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:6

Pakuti Yehova wakuitana iwe monga mkazi wakusiyidwa ndi wosauka m'mzimu, ngakhale mkazi wa ubwana wochotsedwa, ati Mulungu wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:12

Chifukwa chake iye wakuyesa kuti ali chilili, ayang'anire kuti angagwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:5

Chifukwa chake fetsani ziwalozo zili padziko; dama, chidetso, chifunitso chamanyazi, chilakolako choipa, ndi chisiriro, chimene chili kupembedza mafano;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:7

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:13

Tiyendeyende koyenera, monga usana; si m'madyerero ndi kuledzera ai, si m'chigololo ndi chonyansa ai, si mu ndeu ndi nkhwidzi ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:26

Wolungama atsogolera mnzake; koma njira ya oipa iwasokeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 101:3

Sindidzaika chinthu choipa pamaso panga; chochita iwo akupatuka padera chindiipira; sichidzandimamatira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:113

Ndidana nao a mitima iwiri; koma ndikonda chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:14

Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao; alikhe ozunzika ndi aumphawi, aphe amene ali oongoka m'njira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:15

Pakuti asamve zowawa wina wa inu ngati wambanda, kapena mbala, kapena wochita zoipa, kapena ngati wodudukira;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:26

Pakuti tikachimwa ife eni ake, titatha kulandira chidziwitso cha choonadi, siitsalanso nsembe ya kwa machimo,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:17

Usasirire nyumba yake ya mnzako, usasirire mkazi wake wa mnzako, kapena wantchito wake wa mwamuna, kapena wantchito wake wamkazi, kapena ng'ombe yake, kapena bulu wake, kapena kanthu kalikonse ka mnzako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 57:3

Koma sendererani kuno chifupi, inu ana aamuna a watsenga, mbeu yachigololo ndi yadama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:20

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 5:11

koma tsopano ndalembera inu kuti musayanjane naye, ngati wina wotchedwa mbale ali wachigololo, kapena wosirira, kapena wopembedza mafano, kapena wolalatira, kapena woledzera, kapena wolanda, kungakhale kukadya naye wotere, iai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:16-17

Koma kwa woipa Mulungu anena, Uli nao chiyani malemba anga kulalikira, ndi kutchula pangano langa pakamwa pako? Popeza udana nacho chilangizo, nufulatira mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:20

Usatemberere mfumu ngakhale poganizira; usatemberere wolemera m'chipinda chogona iwemo; pakuti mbalame ya mlengalenga idzanyamula mauwo, ndipo chouluka ndi mapiko chidzamveketsa zonenazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:3-9

Ndipo Afarisi anadza kwa Iye, namuyesa, nanena, Kodi nkuloledwa kuti munthu achotse mkazi wake pa chifukwa chilichonse? Koma ambiri oyamba adzakhala akuthungo, ndi akuthungo adzakhala oyamba. Ndipo Iye anayankha, nati, Kodi simunawerenga kuti Iye amene adalenga anthu pachiyambi, anawalenga iwo mwamuna ndi mkazi, nati, Chifukwa cha ichi mwamuna adzasiya atate wake ndi amake, nadzaphatikizana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi? Chotero kuti salinso awiri koma thupi limodzi. Chifukwa chake ichi chimene Mulungu anachimanga pamodzi, munthu asachilekanitse. Iwo ananena kwa Iye, Nanga chifukwa ninji Mose analamula kupatsa kalata yachilekaniro, ndi kumchotsa? Iye ananena kwa iwo, Chifukwa cha kuuma mtima kwanu, Mose anakulolezani kuchotsa akazi anu; koma pachiyambi sikunakhala chomwecho. Ndipo Ine ndinena kwa inu, Amene aliyense akachotsa mkazi wake, kosakhala chifukwa cha chigololo, nadzakwatira wina, achita chigololo: ndipo iye amene akwatira wochotsedwayo, achita chigololo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:10-11

Koma okwatitsidwawo ndiwalamulira, si ine ai, koma Ambuye, kuti mkazi asasiye mwamuna, komanso ngati amsiya akhale osakwatiwa, kapena ayanjanitsidwenso ndi mwamunayo, ndipo mwamuna asalekane naye mkazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Malaki 2:16

Pakuti ndidana nako kuleka kumene, ati Yehova Mulungu wa Israele, ndi iye wakukuta chovala chake ndi chiwawa, ati Yehova wa makamu; chifukwa chake sungani mzimu wanu kuti musachite mosakhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 2:24

Chifukwa chotero mwamuna adzasiya atate wake ndi amake nadzadziphatika kwa mkazi wake: ndipo adzakhala thupi limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:6

Chotero kuti salinso awiri koma thupi limodzi. Chifukwa chake ichi chimene Mulungu anachimanga pamodzi, munthu asachilekanitse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:7

Momwemonso amuna inu, khalani nao monga mwa chidziwitso, ndi kuchitira mkazi ulemu, monga chotengera chochepa mphamvu, monganso wolowa nyumba pamodzi wa chisomo cha moyo, kuti mapemphero anu angaletsedwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 127:1

Akapanda kumanga nyumba Yehova, akuimanga agwiritsa ntchito chabe; akapanda kusunga mzinda Yehova, mlonda adikira chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:20

Yehova asunga onse akukondana naye; koma oipa onse adzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:5

Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha; koma kuyanja kwake moyo wonse. Kulira kuchezera, koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:2-4

kwaniritsani chimwemwe changa, kuti mukalingalire mtima zomwezo, akukhala nacho chikondi chomwe, a moyo umodzi, olingalira mtima umodzi; Pakuti ndilibe wina wa mtima womwewo, amene adzasamalira za kwa inu ndi mtima woona. Pakuti onsewa atsata za iwo okha, si za Yesu Khristu. Koma muzindikira matsimikizidwe ake, kuti, monga mwana achitira atate wake, anatumikira pamodzi ndi ine Uthenga Wabwino. Ameneyo ndithu tsono ndiyembekeza kumtuma posachedwa m'mene ndikapenyerera za kwa ine zidzatani; koma ndikhulupirira mwa Ambuye kuti ine ndekhanso ndidzadza msanga. Koma ndinayesa nkofunika kutuma kwa inu Epafrodito mbaleyo, ndiye wantchito mnzanga ndi msilikali mnzanga, ndiye mtumwi wanu, ndi wonditumikira pa chosowa changa; popeza anali wolakalaka inu nonse, navutika mtima chifukwa mudamva kuti anadwala. Pakutinso anadwaladi pafupi imfa; komatu Mulungu anamchitira chifundo; koma si iye yekha, komatu inenso, kuti ndisakhale nacho chisoni chionjezereonjezere. Chifukwa chake ndamtuma iye chifulumizire, kuti pakumuona mukakondwerenso, ndi inenso chindichepere chisoni. Chifukwa chake mumlandire mwa Ambuye, ndi chimwemwe chonse; nimuchitire ulemu oterewa; musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini; pakuti chifukwa cha ntchito ya Khristu anafikira pafupi imfa, wosasamalira moyo wake, kuti akakwaniritse chiperewero cha utumiki wanu wa kwa ine. munthu yense asapenyerere zake za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:14

Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova, ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:19

Amuna inu, kondani akazi anu, ndipo musawawire mtima iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:31-32

Kunanenedwanso, Yense wakuchotsa mkazi wake ampatse iye kalata yachilekaniro: koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wakuchotsa mkazi wake, kosati chifukwa cha chigololo, amchititsa chigololo: ndipo amene adzakwata wochotsedwayo achita chigololo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:12-15

Koma kwa otsalawo ndinena ine, si Ambuye, Ngati mbale wina ali naye mkazi wosakhulupirira, ndipo iye avomera mtima kukhala naye pamodzi, asalekane naye. Ndipo mkazi amene ali naye mwamuna wosakhulupirira, navomera mtima iye kukhala naye pamodzi, asalekane naye mwamunayo. Pakuti mwamuna wosakhulupirirayo ayeretsedwa mwa mkaziyo, ndi mkazi wosakhulupirira ayeretsedwa mwa mbaleyo; ngati sikukadatero, ana anu akadakhala osakonzeka, koma tsopano akhala oyera. Koma ngati wosakhulupirirayo achoka, achoke. M'milandu yotere samangidwa ukapolo mbaleyo, kapena mlongoyo. Koma Mulungu watiitana ife mumtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:31

Chifukwa cha ichi munthu azisiya atate ndi amai, nadzaphatikizana ndi mkazi wake; ndipo iwo awiri adzakhala thupi limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:10

M'chikondano cha anzanu wina ndi mnzake mukondane ndi chikondi chenicheni; mutsogolerane ndi kuchitira wina mnzake ulemu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 5:18

Adalitsike kasupe wako; ukondwere ndi mkazi wokula nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:4-5

Ndipo Iye anayankha, nati, Kodi simunawerenga kuti Iye amene adalenga anthu pachiyambi, anawalenga iwo mwamuna ndi mkazi, nati, Chifukwa cha ichi mwamuna adzasiya atate wake ndi amake, nadzaphatikizana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:14

Mau a m'kamwa mwanga ndi maganizo a m'mtima wanga avomerezeke pamaso panu, Yehova, thanthwe langa, ndi Mombolo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:12

Udani upikisanitsa; koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:17

Kudya masamba, pali chikondano, kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:22-23

Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro, chifatso, chiletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:8

Iye ananena kwa iwo, Chifukwa cha kuuma mtima kwanu, Mose anakulolezani kuchotsa akazi anu; koma pachiyambi sikunakhala chomwecho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:28

Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwachitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 1:9

Ngati tivomereza machimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama Iye, kuti atikhululukire machimo athu, ndi kutisambitsa kutichotsera chosalungama chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:13

Sichinakugwerani inu chiyeso koma cha umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi chiyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:14

koma koposa izi zonse khalani nacho chikondano, ndicho chomangira cha mtima wamphumphu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:10-12

Mkazi wangwiro ndani angampeze? Pakuti mtengo wake uposa ngale. Mtima wa mwamuna wake umkhulupirira, sadzasowa phindu. Mkaziyo amchitira zabwino, si zoipa, masiku onse a moyo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:19

Chifukwa chake tilondole zinthu za mtendere, ndi zinthu zakulimbikitsana wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:7

Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo chidzatsegulidwa kwa inu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:22

Wopeza mkazi apeza chinthu chabwino; Yehova amkomera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 7:39

Mkazi amangika pokhala mwamuna wake ali ndi moyo; koma atamwalira mwamuna ali womasuka, kuti akwatiwe naye amene afuna, koma mwa Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:13

Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:6-7

Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu. Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:176

Ndinasochera ngati nkhosa yotayika; funani mtumiki wanu; pakuti sindiiwala malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 24:67

Ndipo Isaki anamlowetsa mkaziyo m'hema wa amake Sara, namtenga Rebeka, nakhala iye mkazi wake; ndipo anamkonda iye; ndipo Isaki anatonthozedwa mtima atafa amake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:2

Pamene udulitsa pamadzi ndili pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsa; ngakhale lawi silidzakutentha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:10

Chikondano sichichitira mnzake choipa; chotero chikondanocho chili chokwanitsa lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:14

Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa nchoopsa ndi chodabwitsa; ntchito zanu nzodabwitsa; moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:7-8

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta. Pakuti wakufesera kwa thupi la iye yekha, chochokera m'thupi adzatuta chivundi; koma wakufesera kwa Mzimu, chochokera mu Mzimu adzatuta moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 22:30

Pakuti m'kuuka kwa akufa sakwatira, kapena kukwatiwa, koma akhala ngati angelo a Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 4:1

Koma Mzimu anena monenetsa, kuti m'masiku otsiriza ena adzataya chikhulupiriro, ndi kusamala mizimu yosocheretsa ndi maphunziro a ziwanda,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 3:13

ntchito ya yense idzaonetsedwa; pakuti tsikulo lidzaisonyeza, chifukwa kuti yavumbululuka m'moto; ndipo moto wokha udzayesera ntchito ya yense ikhala yotani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:4

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:28

Ndipo monga iwo anakana kukhala naye Mulungu m'chidziwitso chao, anawapereka Mulungu kumtima wokanika, kukachita zinthu zosayenera;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:3

Pereka zochita zako kwa Yehova, ndipo zolingalira zako zidzakhazikika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 54:5

Pakuti Mlengi wako ndiye mwamuna wako; Yehova wa makamu ndiye dzina lake; ndi Woyera wa Israele ndiye Mombolo wako; Iye adzatchedwa Mulungu wa dziko lonse lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:32

Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:8

koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha; pakuti chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:4

Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:32

koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wakuchotsa mkazi wake, kosati chifukwa cha chigololo, amchititsa chigololo: ndipo amene adzakwata wochotsedwayo achita chigololo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 16:18

Yense wakusudzula mkazi wake, nakwatira wina, achita chigololo; ndipo iye amene akwatira wosudzulidwayo, achita chigololo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:26

Pakuti ukayamba ndi mkazi wadama, udzamaliza ndi nyenyeswa; ndipo mkazi wa mwini amasaka moyo wa mtengowapatali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 6:18

Thawani dama. Tchimo lililonse munthu akalichita lili kunja kwa thupi; koma wachiwerewere achimwira thupi lake la iye yekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:28

koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wakuyang'ana mkazi kumkhumba, pamenepo watha kuchita naye chigololo mumtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:14

Usachite chigololo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 18:20

Usagona naye mkazi wa mnansi wako, kudetsedwa naye limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 22:22

Akampeza munthu alikugona ndi mkazi wokwatibwa ndi mwamuna; afe onse awiri, mwamuna wakugona ndi mkazi, ndi mkazi yemwe; chotero muzichotsa choipacho mwa Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 3:8

Ndipo ndinaona, kuti, ndingakhale ndikamchotsa Israele wobwerera m'mbuyo, ndi kumpatsa kalata yachilekaniro chifukwa cha kuchita chigololo iye, mphwake Yuda wonyenga sanaope, koma iye yemwe ananka nachita dama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 16:26

Wachitanso chigololo ndi Ejipito oyandikizana nawe, aakulu thupi, ndi kuchulukitsa chigololo chako kuutsa mkwiyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga Wamuyaya, Wamkulu, Wamphamvu, chifundo chanu n'chopanda malire pa moyo wanga! Ndikudalirani chilichonse, ndipo chifukwa cha ichi, ndikupereka mtima wanga pamaso panu kuti ndikulemekezeni ndi kukudalitsani. Ndikulumbira Ambuye, ndili ndi chisoni chachikulu chifukwa cha kusakhulupirika kwa mkazi/mwamuna wanga, mtima wanga uli ndi udani ndi mkwiyo, chonde ndithandizeni kumukhululukira kuti inunso mundikhululukire. Inu munatipanga ndipo mukudziwa zobisika za mitima yathu, chifukwa cha ichi ndikupemphani kuti muchitire chifundo banja lino ndi kutsanulira Mzimu Woyera pa mkazi/mwamuna wanga amene walakwira kwambiri ndi munthu wina. Ndithandizeni Ambuye kukhala chiwonetsero cha chikondi chanu nthawi iliyonse ndikamalankhula naye. Inu munatiyang'ana ndipo munkadziwa zomwe zidzachitike, chiritsani mabala anga ndi kubwezeretsa ubwenzi wanga ndi inu kuti ndikwanitse kubwezeretsa mgwirizano wanga ndi munthu amene wandilakwira. Mzimu Woyera ndithandizeni kumuona mwa maso anu, ndi chikondi, chifundo ndi mtima wowona. Ndipatseni nzeru zomulankhulira ndi kumvetsera. Ndikutsutsa chilakolako cha kubwezera, mkwiyo, nsanje ndi ndewu. Yesu, inu munavutika, munanyengedwa ndi kugwidwa popanda chifukwa, ndithandizeni kupambana mayesero akulu amenewa omwe abwera m'nyumba mwanga. Pakuti mawu anu amati: «Thaŵani dama. Uchimo wina uliwonse umene munthu angachite uli kunja kwa thupi; koma wochita dama, uchimwira thupi lake lomwe.» Mulungu wokondedwa, sungani mtima wanga pamalo anu otetezeka kuti usawonongeke ndi mayesero a satana kapena ntchito za anthu. Ndilanditseni kwa mkazi wopanda nzeru ndi wachipanduko ndi mwamuna wonyenga ndi woipa. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa