Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

114 Mauvesi a M’Baibulo Ponena za Kupanduka

Ndikufuna ndikuuzeni nkhani yofunika kwambiri. Munthu akamakana kumvera ndi kutsata malamulo, zimenezo zimatchedwa kupanduka. Zimaonetsa mtima wosasamala, wonyoza, komanso wopanda chifundo. Ambiri amene amachita zinthu monyadira, mwadyera, komanso osamvera akuluakulu awo, ali ndi mzimu wopanduka, womwe Mulungu sawukonda.

Ngati umati ndiwe mwana wa Atate Wathu wakumwamba, koma ukuchita zinthu zopanduka, suli paubwenzi wabwino ndi Mzimu Woyera. M'malo mwake, mizimu yoipa ndiyo ikukutsogolera. Kupanduka ndi chifukwa chachikulu chomwe anthu ambiri amathawa Mulungu. Amakana kulandira uphungu ndi kutsata malamulo ake, m'malo mwake amasankha kutsata zilakolako zawo ndi maganizo awo, akuchimwira Mulungu Wamphamvuyonse.

Wopanduka amadziona ngati wanzeru, koma sakudziwa kuti akulowera m'mavuto, kutanthauza chilango chosatha ku gehena. Buku la Deuteronomo 1:43-45 limati: "Ndinakuuzani, koma simunamvere; munapandukira lamulo la Yehova, ndipo monyadira munakwera phiri. Koma Aamori amene anakhala m’phirilo anatuluka kukakumana nanu, anakulondolani monga momwe njuchi zimachitira, ndipo anakugonjetsani ku Seiri, kufikira ku Horima. Pamenepo munabwerera ndi kulira pamaso pa Yehova, koma iye sanamvere mawu anu, kapena kukuyang’anirani.”

Kumbukirani kuti Yesu sakonda anthu opanduka. Amakukondani ndipo akufuna kukupulumutsani, koma sakonda kuti simukulapa machimo anu. Mukadali ndi nthawi yopeza chifundo cha Mulungu. Ingotsegula mtima wanu, dzichepetse pamaso pa Ambuye, pemphani chikhululukiro, ndi kuvomereza zolakwa zanu modzichepetsa. Musamadzilungamitse, ndipo landirani chilango chimene mukuyenera kuti musinthe mkati mwanu.

Yandikirani Mzimu Woyera, muuzeni kuti mukumufuna, ndipo musamakhale popanda chikondi chake changwiro. Mukatero, mudzapeza chisomo pamaso pa Mulungu ndi anthu. Pemphani chikhululukiro kwa akuluakulu anu ndi kuyambiranso moyo watsopano.


Masalimo 68:23

kuti uviike phazi lako m'mwazi, kuti malilime a agalu ako alaweko adani ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:1-2

Anthu onse amvere maulamuliro a akulu; pakuti palibe ulamuliro wina koma wochokera kwa Mulungu; ndipo iwo amene alipo aikidwa ndi Mulungu.

Chikondano sichichitira mnzake choipa; chotero chikondanocho chili chokwanitsa lamulo.

Ndipo chitani ichi, podziwa inu nyengo, kuti tsopano ndiyo nthawi yabwino yakuuka kutulo; pakuti tsopano chipulumutso chathu chili pafupi koposa pamene tinayamba kukhulupirira.

Usiku wapita, ndi mbandakucha wayandikira; chifukwa chake tivule ntchito za mdima, ndipo tivale zida za kuunika.

Tiyendeyende koyenera, monga usana; si m'madyerero ndi kuledzera ai, si m'chigololo ndi chonyansa ai, si mu ndeu ndi nkhwidzi ai.

Koma valani inu Ambuye Yesu Khristu, ndipo musaganizire za thupi kuchita zofuna zake.

Kotero kuti iye amene atsutsana nao ulamuliro, akaniza choikika ndi Mulungu; ndipo iwo akukaniza, adzadzitengera kulanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 3:12-13

Tapenyani, abale, kuti kapena ukakhale mwa wina wa inu mtima woipa wosakhulupirira, wakulekana ndi Mulungu wamoyo;

komatu dandaulirananani nokha tsiku ndi tsiku, pamene patchedwa, Lero; kuti angaumitsidwe wina wa inu ndi chenjerero la uchimo;

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:1

Tsoka kwa ana opanduka, ati Yehova, amene atenga uphungu koma si pa Ine; napangana pangano opanda mzimu wanga, kuti aonjezere tchimo ndi tchimo;

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,

Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu.

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:8

Ndi kuti asange makolo ao, ndiwo mbadwo woukirana ndi wopikisana ndi Mulungu; mbadwo wosakonza mtima wao, ndi mzimu wao sunakhazikike ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 2:3-4

Nati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, ndikutumizira kwa ana a Israele, kwa mitundu ya anthu opanduka, amene anapandukana nane; iwo ndi makolo ao anandilakwira mpaka lero lomwe.

Ndipo anawa, ndiwo achipongwe ndi ouma mtima, ndikutumiza kwa iwo; ndipo ukanene nao, Atero Yehova Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:118

Mupepula onse akusokera m'malemba anu; popeza chinyengo chao ndi bodza.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:30

Iye wosakhala pamodzi ndi Ine akana Ine, ndi iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwazamwaza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 34:37

Pakuti pa kuchimwa kwake aonjeza kupikisana ndi Mulungu, asansa manja pakati pa ife, nachulukitsa maneno ake pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:5-6

Koma ochuluka a iwo Mulungu sanakondwere nao; pakuti anamwazika m'chipululu.

Koma zinthu izi zinachitika, zikhale zotichenjeza ife, kuti tisalakalake zoipa ife, monganso iwowo analakalaka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 2:19

Choipa chako chidzakulanga iwe, mabwerero ako adzakudzudzula iwe; dziwa, nuone, kuti ichi ndi choipa ndi chowawa, kuti wasiya Yehova Mulungu wako, ndi kuti kundiopa Ine sikuli mwa iwe, ati Ambuye, Yehova wa makamu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 8:5

Bwanji abwerera anthu awa a Yerusalemu chibwererere? Agwiritsa chinyengo, akana kubwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 106:23

Potero Iye adati awaononge, pakadapanda Mose wosankhika wake, kuima pamaso pake pogamukapo, kubweza ukali wake ungawaononge.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:1

Yemwe aumitsa khosi atadzudzulidwa kwambiri, adzasweka modzidzimuka, palibe chomchiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 3:15

umo anenamo, Lero ngati mudzamva mau ake, musaumitse mitima yanu, monga pa kupsetsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 31:6

Bwerani kwa Iye amene mwampandukira kolimba, ana a Israele inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 24:13

Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika, sadziwa njira zake, Sasunga mayendedwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 9:23

Ndipo pamene Yehova anakutumizani kuchokera ku Kadesi-Baranea, ndi kuti Kwerani, landirani dziko limene ndakupatsani; munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu, osamkhulupirira, kapena kumvera mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:2-3

Imvani, miyamba inu, tchera makutu, iwe dziko lapansi, chifukwa Yehova wanena, Ndakulitsa ndipo ndalera ana, ndipo iwo anandipandukira Ine.

koma ngati mukana ndi kupanduka, mudzathedwa ndi lupanga; chifukwa m'kamwa mwa Yehova mwatero.

Mzinda wokhulupirika wasanduka wadama! Wodzala chiweruzowo! Chilungamo chinakhalamo koma tsopano ambanda.

Siliva wako wasanduka mphala, vinyo wako wasakanizidwa ndi madzi.

Akulu ako apanduka, ali anzao a mbala; onse akonda mitulo, natsata zokometsera milandu; iwo saweruzira amasiye; ngakhale mlandu wa mkazi wamasiye suwafika.

Chifukwa chake Ambuye ati, Yehova wa makamu wamphamvu wa Israele, Ha! Ndidzatonthoza mtima wanga pochotsa ondivuta, ndi kubwezera chilango adani anga;

ndipo ndidzaikanso dzanja langa pa iwe, ndi kukusungunula kukusiyanitsa iwe ndi mphala yako, ndipo ndidzachotsa seta wako wonse:

ndidzabweza oweruza ako monga poyamba, ndi aphungu ako monga pachiyambi; pambuyo pake udzatchedwa Mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.

Ziyoni adzaomboledwa ndi chiweruzo, ndi otembenuka mtima ake ndi chilungamo.

Koma kupasula kwa olakwa ndi kwa ochimwa kudzakhala kumodzi, ndi iwo amene asiya Yehova adzathedwa.

Chifukwa adzakhala ndi manyazi, chifukwa cha mitengo yathundu munaikhumba, ndipo inu mudzagwa nkhope, chifukwa cha minda imene mwaisankha.

Ng'ombe idziwa mwini wake, ndi bulu adziwa pomtsekereza: koma Israele sadziwa, anthu anga sazindikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 9:5

tachimwa, tachita mphulupulu, tachita zoipa, tapanduka, kupatuka ndi kusiya maneno anu ndi maweruzo anu;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 21:28-31

Nanga mutani? Munthu anali nao ana awiri; nadza iye kwa woyamba nati, Mwanawe, kagwire lero ntchito kumunda wampesa.

Koma iye anakana, nati, Sindifuna ine; koma pambuyo pake analapa mtima napita.

Ndipo munthu akanena kanthu ndi inu, mudzati, Ambuye asowa iwo, ndipo pomwepo adzawatumiza.

Ndipo anadza kwa winayo, natero momwemo. Ndipo iye anavomera, nati, Ndipita mbuye; koma sanapite.

Ndani wa awiriwo anachita chifuniro cha atate wake? Iwo ananena, Woyambayo. Yesu ananena kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, kuti amisonkho ndi akazi achiwerewere amatsogolera inu, kulowa mu Ufumu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 7:11

Koma anakana kumvera, nakaniza phewa lao, natseka makutu ao, kuti asamve.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:25

Penyani musakane wolankhulayo. Pakuti ngati iwowa sanapulumuke, pomkana Iye amene anawachenjeza padziko, koposatu sitidzapulumuka ife, odzipatulira kwa Iye wa Kumwamba;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:21-22

chifukwa kuti, ngakhale anadziwa Mulungu, sanamchitire ulemu wakuyenera Mulungu, ndipo sanamyamike; koma anakhala opanda pake m'maganizo ao, ndipo unada mtima wao wopulukira.

Pakunena kuti ali anzeru, anapusa;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:13-14

Tadzigonjani kwa zoikika zonse za anthu, chifukwa cha Ambuye; ngakhale kwa mfumu, monga mutu wa onse;

kapena kwa akazembe, monga otumidwa ndi iye kukalanga ochita zoipa, koma kusimba ochita zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:16

Nkhope ya Yehova itsutsana nao akuchita zoipa, kudula chikumbukiro chao padziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:1

Woipa athawa palibe momthamangitsa; koma olungama alimba mtima ngati mkango.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 11:4-6

Ndipo anati, Tiyeni, timange mzinda ndi nsanja, pamutu pake pafikire kumwamba; ndipo tidzipangire ife tokha dzina kuti tisabalalike padziko lonse lapansi.

Ndipo Yehova anatsikira kudzaona mzinda ndi nsanja imene analinkumanga ana a anthu.

Ndipo Yehova anati, Taonani, anthu ali amodzi, ndipo onse ali nacho chinenedwe chao chimodzi; ndipo ichi ayamba kuchita: ndipo tsopano palibe kanthu kakuletsedwa nao kamene akafuna kuchita.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:7

Potero mverani Mulungu; koma kanizani mdierekezi, ndipo adzakuthawani inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:3

Utsiru wa munthu ukhotetsa njira yake; mtima wake udandaula pa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:37

Popeza mtima wao sunakonzekere Iye, ndipo sanakhazikike m'chipangano chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:24

Ndipo iwo adzatuluka ndi kuyang'ana mitembo ya anthu amene andilakwira Ine, pakuti mphutsi yao sidzafa, pena moto wao sudzazimidwa; ndipo iwo adzanyansa anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:113

Ndidana nao a mitima iwiri; koma ndikonda chilamulo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:10-12

Odala ali akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo: chifukwa uli wao Ufumu wa Kumwamba.

Odala muli inu m'mene adzanyazitsa inu, nadzazunza inu, nadzakunenerani monama zoipa zilizonse chifukwa cha Ine.

Sekerani, sangalalani: chifukwa mphotho yanu ndi yaikulu mu Mwamba: pakuti potero anazunza aneneri anakhalawo musanabadwe inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 53:6

Tonse tasochera ngati nkhosa; tonse tayenda yense m'njira ya mwini yekha; ndipo Yehova anaika pa Iye mphulupulu ya ife tonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:11

popeza anapikisana nao mau a Mulungu, napeputsa uphungu wa Wam'mwambamwamba;

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 10:4

Ngati mkulu akukwiyira, usasiye malo ako; chifukwa chifatso chipembedza utachimwa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:17

Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka; Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 59:12

Pakamwa pao achimwa ndi mau onse a pa milomo yao, potero akodwe m'kudzitamandira kwao, ndiponso chifukwa cha kutemberera ndi bodza azilankhula.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 7:14

ndipo anthu anga otchedwa dzina langa akadzichepetsa, nakapemphera, nakafuna nkhope yanga, nakatembenuka kuleka njira zao zoipa; pamenepo ndidzamvera mu Mwamba, ndi kukhululukira choipa chao, ndi kuchiritsa dziko lao.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:10

M'menemo aoneka ana a Mulungu, ndi ana a mdierekezi: yense wosachita chilungamo siali wochokera mwa Mulungu; ndi iye wosakonda mbale wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:8-9

Musaumitse mitima yanu, ngati ku Meriba, ngati tsiku la ku Masa m'chipululu.

Pamene makolo anu anandisuntha, anandiyesa, anapenyanso chochita Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 6:16

Kodi simudziwa kuti kwa iye amene mudzipereka eni nokha kukhala akapolo ake akumvera iye, mukhalatu akapolo ake a yemweyo mulikumvera iye; kapena a uchimo kulinga kuimfa, kapena a umvero kulinga kuchilungamo?

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 11:28

koma temberero, ngati simudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi kupatuka m'njira ndikuuzani lero lino, kutsata milungu ina imene simunaidziwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 65:2

Ndatambasulira manja anga tsiku lonse kwa anthu opanduka, amene ayenda m'njira mosati mwabwino, kutsata maganizo aoao;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:104

Malangizo anu andizindikiritsa; chifukwa chake ndidana nao mayendedwe onse achinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:7

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:21-22

Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe, osadudukira anthu osinthasintha.

Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka; ndipo ndani adziwa chionongeko cha zaka zao?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 58:3

Oipa achita chilendo chibadwire, asokera kuyambira kubadwa kwao, nanena bodza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:155

Chipulumutso chitalikira oipa; popeza safuna malemba anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 5:23

Koma anthu awa ali ndi mtima woukirana ndi wopikisana; anapanduka nachoka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:14-15

koma munthu aliyense ayesedwa pamene chilakolako chake cha iye mwini chimkokera, ndikumnyenga.

Pamenepo chilakolakocho chitaima, chibala uchimo; ndipo uchimo, utakula msinkhu, ubala imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:15

Kuchita chiweruzo kukondweretsa wolungama; koma kuwaononga akuchita mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:13

Ndiponso muletse kapolo wanu pa zodzitama; zisachite ufumu pa ine. Pamenepo ndidzakhala wangwiro, ndi wosachimwa cholakwa chachikulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 3:6-7

Ndipo pamene anaona mkaziyo kuti mtengo unali wabwino kudya, ndi kuti unali wokoma m'maso, mtengo wolakalakika wopatsa nzeru, anatenga zipatso zake, nadya, napatsanso mwamuna wake amene anali naye, nadya iyenso.

Ndipo anatseguka maso ao a onse awiri, nadziwa kuti anali amaliseche: ndipo adasoka masamba amkuyu, nadzipangira matewera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 82:5

Sadziwa, ndipo sazindikira; amayendayenda mumdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 18:30

Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:26-27

Pakuti tikachimwa ife eni ake, titatha kulandira chidziwitso cha choonadi, siitsalanso nsembe ya kwa machimo,

koma kulindira kwina koopsa kwa chiweruziro, ndi kutentha kwake kwa moto wakuononga otsutsana nao.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 48:8

Inde, iwe sunamve; inde, sunadziwe; inde kuyambira kale khutu lako silinatsegudwe; pakuti ndinadziwa kuti iwe wachita mwachiwembu ndithu, ndipo unayesedwa wolakwa chibadwire.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:21

Simungathe kumwera chikho cha Ambuye, ndi chikho cha ziwanda; simungathe kulandirako kugome la Ambuye, ndi kugome la ziwanda.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:21

Si yense wakunena kwa Ine, Ambuye, Ambuye, adzalowa mu Ufumu wa Kumwamba; koma wakuchitayo chifuniro cha Atate wanga wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 106:14

Popeza analakalakatu kuchidikhako, nayesa Mulungu m'chipululu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 2:8

koma kwa iwo andeu, ndi osamvera choonadi, koma amvera chosalungama, adzabwezera mkwiyo ndi kuzaza,

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 57:17

Chifukwa cha kuipa kwa kusirira kwake ndinakwiya ndi kummenya iye; ndinabisa nkhope yanga, ndipo ndinakwiya; ndipo iye anankabe mokhota m'njira ya mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 1:19

ndi kukhala nacho chikhulupiriro ndi chikumbumtima chokoma, chimene ena adachikankha, chikhulupiriro chao chidatayika;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 86:14

Mulungu, odzikuza andiukira, ndi msonkhano wa anthu oopsa afuna moyo wanga, ndipo sanaike Inu pamaso pao.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 22:15

Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana; koma nthyole yomlangira idzauingitsira kutali.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 50:16-17

Koma kwa woipa Mulungu anena, Uli nao chiyani malemba anga kulalikira, ndi kutchula pangano langa pakamwa pako?

Popeza udana nacho chilangizo, nufulatira mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:16

Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse chilakolako cha thupi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:115

Mundichokere ochita zoipa inu; kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:4

pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu, kuchitira iwe zabwino. Koma ngati uchita choipa, opatu, pakuti iye sagwira lupanga kwachabe; pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu wakukwiyira ndi kubwezera chilango wochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:16

Pakuti pomwe pali kaduka ndi zotetana, pamenepo pali chisokonekero ndi chochita choipa chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 59:2

Mundilanditse kwa ochita zopanda pake, ndipo ndipulumutseni kwa anthu olira mwazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:15

Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake; koma wanzeru amamvera uphungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 15:9

Mdani anati, Ndiwalondola, ndiwapeza, ndidzagawa zofunkha; ndidzakhuta nao mtima; ndidzasolola lupanga langa, dzanja langa lidzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 24:10-12

Ndipo pomwepo ambiri adzakhumudwa, nadzaperekana wina ndi mnzake, nadzadana wina ndi mnzake.

Ndipo aneneri onama ambiri adzauka, nadzasokeretsa anthu ambiri.

Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa kusaweruzika, chikondano cha anthu aunyinji chidzazilala.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 14:1

Wauchitsiru amati mumtima mwake, Kulibe Mulungu. Achita zovunda, achita ntchito zonyansa; kulibe wakuchita bwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 14:12-14

Wagwadi kuchokera kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mbandakucha! Wagwetsedwa pansi, iwe wolefula amitundu!

Ndipo iwe unati mumtima mwako, Ndidzakwera kumwamba, ndidzakweza mpando wanga wachifumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pamwamba paphiri la khamu, m'malekezero a kumpoto;

ndidzakwera pamwamba pa mitambo, ndidzafanana ndi Wam'mwambamwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 2:3-4

munthu asakunyengeni konseko; kuti silifika, koma chiyambe chafika chipatukocho, navumbulutsike munthu wosaweruzika, mwana wa chionongeko,

amene atsutsana nazo, nadzikuza pa zonse zotchedwa Mulungu, kapena zopembedzeka; kotero kuti iye wakhala pansi ku Kachisi wa Mulungu, nadzionetsera yekha kuti ali Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:29

ndipo mutani, kulanga koposa kotani nanga adzayesedwa woyenera iye amene anapondereza Mwana wa Mulungu, nayesa mwazi wa chipangano umene anayeretsedwa nao chinthu wamba, nachitira chipongwe Mzimu wa chisomo;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:7

Chifukwa chisamaliro cha thupi chidana ndi Mulungu; pakuti sichigonja ku chilamulo cha Mulungu, pakuti sichikhoza kutero.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:17

Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa; uferenji nthawi yako isanafike?

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:20

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:26

Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa; koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 89:30-32

Ana ake akataya chilamulo changa, osayenda m'maweruzo anga,

nakaipsa malembo anga; osasunga malamulo anga.

Pamenepo ndidzazonda zolakwa zao ndi ndodo, ndi mphulupulu zao ndi mikwingwirima.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:20

Pakuti ndinena ndi inu, ngati chilungamo chanu sichichuluka choposa cha alembi ndi Afarisi, simudzalowa konse mu Ufumu wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 95:9

Pamene makolo anu anandisuntha, anandiyesa, anapenyanso chochita Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:28-32

Ndipo monga iwo anakana kukhala naye Mulungu m'chidziwitso chao, anawapereka Mulungu kumtima wokanika, kukachita zinthu zosayenera;

anadzala ndi zosalungama zonse, kuipa, kusirira, dumbo; odzala ndi kaduka, mbanda, ndeu, chinyengo, udani;

wakunena za Mwana wake, amene anabadwa, wa mbeu ya Davide, monga mwa thupi,

akazitape, osinjirira, akumuda Mulungu, achipongwe, odzitama, amatukutuku, oyamba zoipa, osamvera akulu ao,

opanda nzeru, osasunga mapangano, opanda chikondi cha chibadwidwe, opanda chifundo;

amene ngakhale adziwa kuweruza kwake kwa Mulungu, kuti iwo amene achita zotere ayenera imfa, azichita iwo okha, ndiponso avomerezana ndi iwo akuzichita.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:21-22

Kodi sindidana nao iwo akudana ndi Inu, Yehova? Ndipo kodi sindimva nao chisoni iwo akuukira Inu?

Ndidana nao ndi udani weniweni, ndiwayesa adani.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 15:8-9

Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao; koma mtima wao uli kutali ndi Ine.

Koma andilambira Ine kwachabe, ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 3:19

Si awo kodi osamverawo? Ndipo tiona kuti sanathe kulowa chifukwa cha kusakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 5:20

Ndipo lamulo linalowa moonjezera, kuti kulakwa kukachuluke; koma pamene uchimo unachuluka, pomwepo chisomo chinachuluka koposa;

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:1-2

Tsoka kwa ana opanduka, ati Yehova, amene atenga uphungu koma si pa Ine; napangana pangano opanda mzimu wanga, kuti aonjezere tchimo ndi tchimo;

amene amati kwa alauli, Mtima wanu usapenye; ndi kwa aneneri, Musanenere kwa ife zinthu zoona, munene kwa ife zinthu zamyadi, munenere zonyenga;

chokani inu munjira, patukani m'bande, tiletsereni Woyera wa Israele pamaso pathu.

Chifukwa chake atero Woyera wa Israele, Popeza inu mwanyoza mau awa, nimukhulupirira nsautso ndi mphulupulu, ndi kukhala m'menemo;

chifukwa chake kuipa kumeneku kudzakhala kwa inu monga pogumuka pofuna kugwa, monga potukuka m'khoma lalitali, kugumuka kwake kufika modzidzimutsa dzidzidzi.

Ndipo Iye adzagumulapo, monga mbiya ya woumba isweka, ndi kuiswaiswa osaileka; ndipo sipadzapezedwa m'zigamphu zake phale lopalira moto pachoso, ngakhale lotungira madzi padziwe.

Pakuti atero Ambuye, Yehova Woyera wa Israele, M'kubwera ndi m'kupuma inu mudzapulumutsidwa; m'kukhala chete ndi m'kukhulupirira mudzakhala mphamvu yanu; ndipo simunafune.

Koma munati, Iai, pakuti tidzathawa pa akavalo; chifukwa chake inu mudzathawadi; ndipo ife tidzakwera pa akavalo aliwiro; chifukwa chake iwo amene akuthamangitsani, adzakhala aliwiro.

Chikwi chimodzi chidzathawa pakuwadzudzula mmodzi; pakukudzudzulani anthu asanu mudzathawa; kufikira inu mudzasiyidwa ngati mlongoti pamwamba paphiri, ndi ngati mbendera pamwamba pa chitunda.

Chifukwa chake Yehova adzadikira, kuti akukomereni mtima, ndipo chifukwa chake Iye adzakuzidwa, kuti akuchitireni inu chifundo; pakuti Yehova ndiye Mulungu wa chiweruziro; odala ali onse amene amdikira Iye.

Pakuti anthu adzakhala mu Ziyoni pa Yerusalemu; iwe sudzaliranso, Iye ndithu adzakukomera mtima pakumveka kufuula kwako; pakumva Iye adzayankha.

amene ayenda kutsikira ku Ejipito, osafunsa kukamwa kwanga, kudzilimbitsa iwo okha ndi mphamvu za Farao, ndi kukhulupirira mthunzi wa Ejipito!

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:4

Akazi achigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uli udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 11:5

Yehova ayesa wolungama mtima, koma moyo wake umuda woipa ndi iye wakukonda chiwawa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:5

Yense wonyada mtima anyansa Yehova; zoonadi sadzapulumuka chilango.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 3:23

pakuti onse anachimwa, naperewera pa ulemerero wa Mulungu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:20

Yehova asunga onse akukondana naye; koma oipa onse adzawaononga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 15:23

Pakuti kupanduka kuli ngati choipa cha kuchita nyanga, ndi mtima waliuma uli ngati kupembedza milungu yachabe ndi maula. Popeza inu munakaniza mau a Yehova, Iyenso anakaniza inu, kuti simudzakhalanso mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:11

Woipa amafuna kupanduka kokha; koma adzamtumizira mthenga wankhanza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:6

Mulungu amangitsira banja anthu a pa okha; atulutsa am'ndende alemerere; koma opikisana naye akhala m'dziko lopanda madzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 2:2

Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 20:24

Aroni adzaitanidwa kunka kwa anthu a mtundu wake; pakuti sadzalowa m'dziko limene ndapatsa ana a Israele, popeza munapikisana ndi mau anga ku madzi a Meriba.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:7

Achita ufumu mwa mphamvu yake kosatha; maso ake ayang'anira amitundu; opikisana ndi Iye asadzikuze.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 12:14

Mukaopa Yehova ndi kumtumikira ndi kumvera mau ake, ndi kusakana lamulo lake la Yehova, ndipo inu ndi mfumu imene iweruza inu mukadzatsata Yehova Mulungu wanu, chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 14:9

Chokhachi musamapikisana naye Yehova, musamaopa anthu a m'dzikomo; pakuti ndiwo mkate wathu; mthunzi wao wawachokera, ndipo Yehova ali nafe; musamawaopa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:10

Muwayese otsutsika Mulungu; agwe nao uphungu wao. M'kuchuluka kwa zolakwa zao muwapirikitse; pakuti anapikisana ndi Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 13:5

Ndipo mneneriyo, kapena wolota malotoyo, mumuphe; popeza ananena chosiyanitsa ndi Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani m'dziko la Ejipito, nakuombolani m'nyumba ya ukapolo; kuti akucheteni mutaye njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani muziyendamo. Potero muzichotsa choipacho pakati pa inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 28:16

Chifukwa chake Yehova atero, Taona, Ine ndidzakuchotsa iwe kudziko; chaka chino udzafa, pakuti wanena zopikisana ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 3:42

Ife tilakwa ndi kupikisana nanu, ndipo Inu simunatikhululukire.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu, ndinu nokha woyenera ulemerero, ulemu, chitamando ndi kulambira. Ndikubwera kwa inu kudzera mwa Ambuye wathu Yesu Khristu kukuthokozani chifukwa cha kukhulupirika kwanu, chikondi chanu ndi kundikhululukira nthawi zonse ndikalakwitsa. Ndimakukhulupirirani Ambuye wanga ndipo ndikudziwa kuti munditeteza ku choipa, maso anu anaona mwana wanga ali m'mimba, ndinu amene mukudziwa zobisika mumtima mwanga ndipo ndisanayambe kulankhula mukudziwa zomwe ndinganene. Lero ndikupempherera mtima wanga kuti ukukondweretseni ndipo muuyeretse, ndikupempha chisomo chanu chifukwa ndikudziwa kuti ndinali wopanduka kwa inu, kwa banja langa, abale ndi anzanga, ndinayesa kuiwala mawu anu ndipo ndinachita zomwe mdani anandiuza, koma ndimakhulupirira ndi mtima wonse kuti ndinu chishango changa ndi woteteza wanga, pakuti kwalembedwa: "Ife tinapanduka, ndipo sitinakhale okhulupirika; inu simunatikhululukire". Atate wokondedwa, ndikupemphani kuti mubisire moyo wanga chifukwa ndayesedwa kuti ndichoke m'njira yanu, ndilanditseni Mulungu wokondedwa ku mitsinje ya dziko lino, ku lilime lonyenga ndi lonama, sungani makutu ndi maso anga ku zokopa za satana. Ndikusiya mkwiyo, chidani, kudzidalira, kunyada ndi dyera m'dzina la Yesu. Mundichitire chifundo Mulungu, sungani pakamwa panga kuti pasatuluke mawu otsutsana nanu, mundibisire pamaso pa mdani, ndikudziwa kuti sindidzagwedezeka chifukwa muli kudzanja langa lamanja. Onetsani mphamvu yanu Ambuye, pakuti mwakhala pothawirapo panga ndi chitetezo changa pa tsiku la masautso anga. Zikomo m'dzina la Yesu chifukwa chondilanditsa ku imfa. M'dzina la Yesu, Ameni.