Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yeremiya 5:23 - Buku Lopatulika

23 Koma anthu awa ali ndi mtima woukirana ndi wopikisana; anapanduka nachoka.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

23 Koma anthu awa ali ndi mtima woukirana ndi wopikisana; anapanduka nachoka.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

23 Koma anthu ameneŵa ndi okanika ndiponso a mtima waupandu. Adapatuka ndipo adapitiratu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

23 Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 5:23
14 Mawu Ofanana  

Ndi kuti asange makolo ao, ndiwo mbadwo woukirana ndi wopikisana ndi Mulungu; mbadwo wosakonza mtima wao, ndi mzimu wao sunakhazikike ndi Mulungu.


Zaka makumi anai mbadwo uwu unandimvetsa chisoni, ndipo ndinati, Iwo ndiwo anthu osokerera mtima, ndipo sadziwa njira zanga.


Nanga bwanji mukali chimenyedwere kuti inu mulikupandukirabe? Mutu wonse ulikudwala, ndi mtima wonse walefuka.


Bwerani kwa Iye amene mwampandukira kolimba, ana a Israele inu.


Mtima ndiwo wonyenga koposa, ndi wosachiritsika, ndani angathe kuudziwa?


Monga adindo a m'munda amzinga iye; chifukwa andipandukira Ine, ati Yehova.


Ine ndidzanka kwa akulu, ndidzanena ndi iwo; pakuti adziwa njira ya Yehova, ndi chiweruzo cha Mulungu wao. Koma awa anavomerezana nathyola goli, nadula zomangira zao.


Onse ali opikisana ndithu, ayendayenda ndi maugogodi; ndiwo mkuwa ndi chitsulo; onsewa achita movunda;


Ndipo anthu anga alimbika kubwerera m'mbuyo kundileka Ine; chinkana akawaitana atsate Iye ali m'mwamba, sadzakweza ndi mmodzi yense.


Adyerera tchimo la anthu anga, nakhumbira chosalungama chao, yense ndi mtima wake.


Tsoka uyo wopanduka, ndi wodetsedwa, ndiye mzinda wozunza!


Munthu akakhala naye mwana wamwamuna wopulukira, ndi wopikisana naye, wosamvera mau a atate wake, kapena mau a mai wake, wosawamvera angakhale anamlanga;


Pakuti ndidziwa kupikisana kwanu, ndi kupulukira kwanu; taonani, pokhala ndikali ndi moyo pamodzi ndi inu lero, mwapikisana ndi Yehova; koposa kotani nanga nditamwalira ine!


Tapenyani, abale, kuti kapena ukakhale mwa wina wa inu mtima woipa wosakhulupirira, wakulekana ndi Mulungu wamoyo;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa