Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 14 - Buku Lopatulika


Anthu oipadi
( Mas. 53 )
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Wauchitsiru amati mumtima mwake, Kulibe Mulungu. Achita zovunda, achita ntchito zonyansa; kulibe wakuchita bwino.

2 Yehova mu Mwamba anaweramira pa ana a anthu, kuti aone ngati aliko wanzeru, wakufuna Mulungu.

3 Anapatuka onse; pamodzi anavunda mtima; palibe wakuchita bwino ndi mmodzi yense.

4 Kodi onse ochita zopanda pake sadziwa kanthu? Pakudya anthu anga monga akudya mkate, ndipo saitana pa Yehova.

5 Pamenepa anaopaopatu, pakuti Mulungu ali mu mbadwo wa wolungama.

6 Munyazitsa uphungu wa wozunzika, koma Yehova ndiye pothawira pake.

7 Mwenzi chipulumutso cha Israele chitachokera ku Ziyoni! Pakubweretsa Yehova anthu ake a m'nsinga, pamenepo adzakondwera Yakobo, nadzasekera Israele.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa