Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 2 - Buku Lopatulika


Ufumu wa wodzozedwa wa Yehova

1 Aphokoseranji amitundu, nalingiriranji anthu zopanda pake?

2 Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,

3 Tidule zomangira zao, titaye nsinga zao.

4 Wokhala m'mwambayo adzaseka; Ambuye adzawanyoza.

5 Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wake, nadzawaopsa mu ukali wake.

6 Koma Ine ndadzoza mfumu yanga Pa Ziyoni, phiri langa loyera.

7 Ndidzauza za chitsimikizo: Yehova ananena ndi Ine, Iwe ndiwe Mwana wanga; Ine lero ndakubala.

8 Undifunse, ndipo ndidzakupatsa amitundu akhale cholowa chako, ndi malekezero a dziko lapansi akhale akoako.

9 Udzawathyola ndi ndodo yachitsulo; udzawaphwanya monga mbiya ya woumba.

10 Tsono, mafumu inu, chitani mwanzeru; langikani, oweruza inu a dziko lapansi.

11 Tumikirani Yehova ndi mantha, ndipo kondwerani ndi chinthenthe.

12 Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye, ndipo mungatayike m'njira ukayaka pang'ono pokha mkwiyo wake. Odala onse akumkhulupirira Iye.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa