Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

128 Mau a m'Baibulo Oletsa Kuipitsa

Ndikufuna ndikuuzeni kuti Mulungu amafuna kuti tonse timupatse miyoyo yathu. Yesu anaphunzitsa ophunzira ake kuti si chimene chimalowa mkamwa chimene chimadetsa munthu, koma chimene chimatuluka mumtima mwake.

Masiku ano, tikudziwa bwino kuti dziko lapansi laipa kwambiri, kuipa ndi chiwerewere zikuchulukirachulukira. Pachifukwa ichi, tiyenera kusamala kuti tisachite zinthu zomwe sizikondweretsa Ambuye wathu.

Muyenera kudziwa kuti mtima wa munthu ungadetsedwe ndi zinthu zosiyanasiyana zomwe zimakhudza makhalidwe athu, malingaliro athu ndi momwe timamvera. Zinthu monga nsanje, mkwiyo, maganizo oipa, kudzikuza, dyera, umbombo, bodza, ndi zina zambiri, zingawononge mitima yathu mosavuta ndikutipatutsa kutali ndi Mulungu wathu.

Kumbukirani kuti kudetsedwa kwa mtima kungawonekere m'njira zosiyanasiyana, monga kusakhululukira anthu otilakwira, kufuna chuma ndi mphamvu, kusasamala anthu ovutika, kufuna kubwezera, kusamvera mawu a Mulungu, komanso ulesi wotsatira chifuniro chake.

Lero, ndikukupemphani mwachikondi kuti musankhe kukhala moyo woyera wokondweretsa Mulungu. Pitani kwa Mulungu ndipo tulutsani chilichonse chomwe chikukudetsani ndikukupangitsani kukhala kutali ndi iye. Ngakhale machimo anu atakhala ofiira ngati nsalu yofiira, magazi a Yesu adzawachapa oyera ngati ubweya. Dzukani, yendani m'chiyero kuti moyo wanu upulumuke.


Machitidwe a Atumwi 15:20

koma kuti tilembere kwa iwo, kuti asale zonyansa za mafano, ndi dama, ndi zopotola, ndi mwazi.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 7:1

Pokhala nao tsono malonjezano amenewa, okondedwa, tidzikonzere tokha kuleka chodetsa chonse cha thupi ndi cha mzimu, ndi kutsiriza chiyero m'kuopa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:16

popeza kwalembedwa, Muzikhala oyera mtima, pakuti Ine ndine woyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 20:3

Ndipo nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndi kumsadza kumchotsa pakati pa anthu a mtundu wake; popeza anapereka a mbeu zake kwa Moleki, kudetsa nako malo anga opatulika, ndi kuipsa dzina langa lopatulika.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 20:7

ndipo ndinanena nao, Aliyense ataye zonyansa za pamaso pake, nimusadzidetsa ndi mafano a Ejipito; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 20:18

Ndipo ndinati kwa ana ao m'chipululu, Musamayenda m'malemba a atate anu, musawasunga maweruzo ao, kapena kudzidetsa ndi mafano ao;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 6:17

Chifukwa chake, Tulukani pakati pao, ndipo patukani, ati Ambuye, Ndipo musakhudza kanthu kosakonzeka; ndipo Ine ndidzalandira inu,

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:4

Akazi achigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uli udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:21

Mwa ichi, mutavula chinyanso chonse ndi chisefukiro cha choipa, landirani ndi chifatso mau ookedwa mwa inu, okhoza kupulumutsa moyo wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,

Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu.

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 7:20-23

Ndipo anati, Chotuluka mwa munthu ndicho chidetsa munthu.

Pakuti m'kati mwake mwa mitima ya anthu, mutuluka maganizo oipa, zachiwerewere,

zakuba, zakupha, zachigololo, masiriro, zoipa, chinyengo, chinyanso, diso loipa, mwano, kudzikuza, kupusa:

zoipa izi zonse zituluka m'kati, nkudetsa munthu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 6:19-20

Kapena simudziwa kuti thupi lanu lili Kachisi wa Mzimu Woyera, amene ali mwa inu, amene muli naye kwa Mulungu? Ndipo simukhala a inu nokha.

Kapena kodi simudziwa kuti oyera mtima adzaweruza dziko lapansi? Ndipo ngati dziko lapansi liweruzidwa ndi inu, muli osayenera kodi kuweruza timilandu tochepachepa?

Pakuti munagulidwa ndi mtengo wake wapatali; chifukwa chake lemekezani Mulungu m'thupi lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:22

Mupewe maonekedwe onse a choipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:8

Chotsalira, abale, zinthu zilizonse zoona, zilizonse zolemekezeka, zilizonse zolungama, zilizonse zoyera, zilizonse zokongola, zilizonse zimveka zokoma; ngati kuli chokoma mtima china, kapena chitamando china, zilingirireni izi.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 1:9

Ngati tivomereza machimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama Iye, kuti atikhululukire machimo athu, ndi kutisambitsa kutichotsera chosalungama chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:15-17

Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko lapansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, chikondi cha Atate sichili mwa iye.

Pakuti chilichonse cha m'dziko lapansi, chilakolako cha thupi ndi chilakolako cha maso, matamandidwe a moyo, sizichokera kwa Atate, koma kudziko lapansi.

Ndipo dziko lapansi lipita, ndi chilakolako chake; koma iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala kunthawi yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:8

Yandikirani kwa Mulungu, ndipo adzayandikira kwa inu. Sambani m'manja, ochimwa inu; yeretsani mitima, a mitima iwiri inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:11

ndipo musayanjane nazo ntchito za mdima zosabala kanthu, koma makamakanso muzitsutse;

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:16

Sambani, dziyeretseni; chotsani machitidwe anu oipa pamaso panga; lekani kuchita zoipa;

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 2:14

amene anadzipereka yekha m'malo mwa ife, kuti akatiombole ife kuzoipa zonse, nakadziyeretsere yekha anthu akhale ake enieni, achangu pa ntchito zokoma.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:23

Chinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga; pakuti magwero a moyo atulukamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 12:10

Ambiri adzadzitsuka ndi kudziyeretsa, nadzayesedwa ndi moto; koma oipa adzachita moipa; ndipo palibe mmodzi wa oipa adzazindikira; koma aphunzitsi ndiwo adzazindikira.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 2:22

Koma thawa zilakolako za unyamata, nutsate chilungamo, chikhulupiriro, chikondi, mtendere, pamodzi ndi iwo akuitana pa Ambuye ndi mitima yoyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:8

Odala ali oyera mtima; chifukwa adzaona Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 22:16

Ndipo tsopano uchedweranji? Tauka, nubatizidwe ndi kusamba kuchotsa machimo ako, nuitane pa dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:18

Tiyeni, tsono, tiweruzane, ati Yehova; ngakhale zoipa zanu zili zofiira, zidzayera ngati matalala; ngakhale zili zofiira ngati kapezi, zidzakhala ngati ubweya wa nkhosa, woti mbuu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:14

Koma valani inu Ambuye Yesu Khristu, ndipo musaganizire za thupi kuchita zofuna zake.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 2:20

Pakuti ngati, adatha kuthawa zodetsa za dziko lapansi mwa chizindikiritso cha Ambuye ndi Mpulumutsi Yesu Khristu, akondwanso nazo, nagonjetsedwa, zotsiriza zao zidzaipa koposa zoyambazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 24:3-4

Adzakwera ndani m'phiri la Yehova? Nadzaima m'malo ake oyera ndani?

Woyera m'manja, ndi woona m'mtima, ndiye; iye amene sanakweze moyo wake kutsata zachabe, ndipo salumbira monyenga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 5:11

koma tsopano ndalembera inu kuti musayanjane naye, ngati wina wotchedwa mbale ali wachigololo, kapena wosirira, kapena wopembedza mafano, kapena wolalatira, kapena woledzera, kapena wolanda, kungakhale kukadya naye wotere, iai.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 18:20

Usagona naye mkazi wa mnansi wako, kudetsedwa naye limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 18:25

dziko lomwe lidetsedwa; chifukwa chake ndililanga, ndi dzikoli lisanza okhala m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 18:27

(Pakuti eni dziko okhalako, musanafike inu, anazichita zonyansa izi zonse, ndi dziko linadetsedwa)

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:9

Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ake bwanji? Akawasamalira monga mwa mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 19:29

Usamaipsa mwana wako wamkazi ndi kumchititsa chigololo; lingadzale ndi chigololo dzikoli, ndi kudzazidwa nazo zochititsa manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 19:31

Musamatembenukira kwa obwebweta, kapena anyanga; musawafuna, ndi kudetsedwa nao; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 10:13

Sichinakugwerani inu chiyeso koma cha umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi chiyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 106:38

nakhetsa mwazi wosachimwa, ndiwo mwazi wa ana ao aamuna ndi aakazi, amene anawaperekera nsembe mafano a Kanani; m'mwemo analidetsa dziko ndi mwaziwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:5

Chifukwa chake fetsani ziwalozo zili padziko; dama, chidetso, chifunitso chamanyazi, chilakolako choipa, ndi chisiriro, chimene chili kupembedza mafano;

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 59:3

Pakuti manja anu adetsedwa ndi mwazi, ndi zala zanu ndi mphulupulu, milomo yanu yanena zonama, lilime lanu lilankhula moipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 2:7

Ndipo ndinakulowetsani m'dziko la minda, kuti mudye zipatso zake, ndi zabwino zake; koma pamene munalowa, munaipitsa dziko langa, ndi kuyesa cholowa changa chonyansa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:11

Okondedwa, ndikudandaulirani ngati alendo ndi ogonera mudzikanize zilakolako za thupi zimene zichita nkhondo pa moyo;

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:22-24

kuti muvule, kunena za makhalidwe anu oyamba, munthu wakale, wovunda potsata zilakolako za chinyengo;

koma kuti mukonzeke, mukhale atsopano mu mzimu wa mtima wanu,

nimuvale munthu watsopano, amene analengedwa monga mwa Mulungu, m'chilungamo, ndi m'chiyero cha choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 3:9

Ndipo kunali kuti mbiri ya dama lake inaipitsa dziko, ndipo anachita chigololo ndi miyala ndi mitengo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 32:34

Koma anaika zonyansa zao m'nyumba yotchedwa dzina langa, kuti aidetse.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:14

Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi chiyeretso chimene, akapanda ichi, palibe mmodzi adzaona Ambuye:

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:27-28

Kodi mwamuna angatenge moto pa chifuwa chake, osatentha zovala zake?

Pena kodi mwamuna angayende pa makala oyaka, osapsa mapazi ake?

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 4:14

Asochera m'makwalala ngati akhungu, aipsidwa ndi mwazi; anthu sangakhudze zovala zao.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:12

Munthu asapeputse ubwana wako; komatu khala chitsanzo kwa iwo okhulupirira, m'mau, m'mayendedwe, m'chikondi, m'chikhulupiriro, m'kuyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 23:38

Anandichitiranso ichi, anadetsa malo anga opatulika tsiku lomwelo, naipsa masabata anga;

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 5:3

Ndimdziwa Efuremu, ndi Israele sandibisikira; pakuti Efuremu iwe, wachita uhule tsopano, Israele wadetsedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:27

Mapembedzedwe oyera ndi osadetsa pamaso pa Mulungu ndi Atate ndiwo: kucheza ndi ana amasiye ndi akazi amasiye m'chisautso chao, ndi kudzisungira mwini wosachitidwa mawanga ndi dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Mika 2:10

Nyamukani, chokani, pakuti popumula panu si pano ai; chifukwa cha udyo wakuononga ndi chionongeko chachikulu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 15:33

Musanyengedwe; mayanjano oipa aipsa makhalidwe okoma.

Mutu    |  Mabaibulo
Zefaniya 3:1

Tsoka uyo wopanduka, ndi wodetsedwa, ndiye mzinda wozunza!

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 52:11

Chokani inu, chokani inu, tulukani ku Babiloni; musakhudze kanthu kodetsa; tulukani pakati pake, khalani okonzeka, inu amene munyamula zotengera za Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Zefaniya 3:4

Aneneri ake ndiwo anthu a matukutuku ndi onyenga; ansembe ao anaipsa malo opatulika, napotoza chilamulo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 15:11

si chimene chilowa m'kamwa mwake chiipitsa munthu; koma chimene chituluka m'kamwa mwake, ndicho chiipitsa munthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 17:15-16

Sindipempha kuti muwachotse iwo m'dziko lapansi, koma kuti muwasunge iwo kuletsa woipayo.

Siali a dziko lapansi monga Ine sindili wa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:11

Odala muli inu m'mene adzanyazitsa inu, nadzazunza inu, nadzakunenerani monama zoipa zilizonse chifukwa cha Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 15:18

Koma zakutuluka m'kamwa zichokera mumtima; ndizo ziipitsa munthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 15:20

izi ndizo ziipitsa munthu, koma kudya osasamba manja sikuipitsa munthu ai.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 6:12-13

Chifukwa chake musamalola uchimo uchite ufumu m'thupi lanu la imfa kumvera zofuna zake:

ndipo musapereke ziwalo zanu kuuchimo, zikhale zida za chosalungama; koma mudzipereke inu nokha kwa Mulungu, monga amoyo atatuluka mwa akufa, ndi ziwalo zanu kwa Mulungu zikhale zida za chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:16

Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse chilakolako cha thupi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:3

Koma dama ndi chidetso chonse, kapena chisiriro, zisatchulidwe ndi kutchulidwa komwe mwa inu, monga kuyenera oyera mtima;

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:4

Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:3

Ndipo yense wakukhala nacho chiyembekezo ichi pa Iye, adziyeretsa yekha, monga Iyeyu ali Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 4:3-4

Pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu, chiyeretso chanu, kuti mudzipatule kudama;

yense wa inu adziwe kukhala nacho chotengera chake m'chiyeretso ndi ulemu,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 5:8

Siyanitsa njira yako kutali kwa iyeyo, osayandikira ku khomo la nyumba yake;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:13

Ndipo musatitengere kokatiyesa, koma mutipulumutse kwa woipayo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 3:16-17

Kodi simudziwa kuti muli Kachisi wa Mulungu, ndi kuti Mzimu wa Mulungu agonera mwa inu?

Ngati wina aononga Kachisi wa Mulungu, ameneyo Mulungu adzamuononga; pakuti Kachisi wa Mulungu ali wopatulika, ameneyo ndi inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:10

Mundilengere mtima woyera, Mulungu; mukonze mzimu wokhazikika m'kati mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:17

Chifukwa chake ngati munthu aliyense ali mwa Khristu ali wolengedwa watsopano; zinthu zakale zapita, taonani, zakhala zatsopano.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:6-8

pakuti chisamaliro cha thupi chili imfa; koma chisamaliro cha mzimu chili moyo ndi mtendere.

Chifukwa chisamaliro cha thupi chidana ndi Mulungu; pakuti sichigonja ku chilamulo cha Mulungu, pakuti sichikhoza kutero.

Ndipo iwo amene ali m'thupi sangathe kukondweretsa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:29

Nkhani yonse yovunda isatuluke m'kamwa mwanu, koma ngati pali ina yabwino kukumangirira monga mofunika ndiyo, kuti ipatse chisomo kwa iwo akumva.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:15

kuti mukakhale osalakwa ndi oona, ana a Mulungu opanda chilema pakati pa mbadwo wokhotakhota ndi wopotoka, mwa iwo amene muonekera monga mauniko m'dziko lapansi,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:15-16

koma mumpatulikitse Ambuye Khristu m'mitima yanu; okonzeka nthawi zonse kuchita chodzikanira pa yense wakukufunsani chifukwa cha chiyembekezo chili mwa inu, komatu ndi chifatso ndi mantha;

ndi kukhala nacho chikumbumtima chabwino, kuti umo akunenerani, iwo akunenera konama mayendedwe anu abwino mu Khristu akachitidwe manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:31-32

Usayang'ane pavinyo alikufiira, alikung'azimira m'chikho, namweka mosalala.

Pa chitsiriziro chake aluma ngati njoka, najompha ngati mamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 14:13

Chifukwa chake tisaweruzanenso wina mnzake; koma weruzani ichi makamaka, kuti munthu asaike chokhumudwitsa panjira ya mbale wake, kapena chomphunthwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 8:9

Koma yang'anirani kuti ulamuliro wanu umene ungakhale chokhumudwitsa ofookawo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 101:3

Sindidzaika chinthu choipa pamaso panga; chochita iwo akupatuka padera chindiipira; sichidzandimamatira.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:18

Tidziwa kuti yense wobadwa kuchokera mwa Mulungu sachimwa, koma iye wobadwa kuchokera mwa Mulungu adzisunga yekha, ndipo woipayo samkhudza.

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 2:12

ndi kutiphunzitsa ife kuti, pokana chisapembedzo ndi zilakolako za dziko lapansi, tikhale ndi moyo m'dziko lino odziletsa, ndi olungama, ndi opembedza;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:20

Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:5

akukhala nao maonekedwe a chipembedzo, koma mphamvu yake adaikana; kwa iwonso udzipatule.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:37

Muchititse mlubza maso anga ndisapenye zachabe, mundipatse moyo mu njira yanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 4:7

Pakuti Mulungu sanaitane ife titsate chidetso, koma chiyeretso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:16

Wanzeru amaopa nasiya zoipa; koma wopusa amanyada osatekeseka.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:41

Chezerani ndi kupemphera, kuti mungalowe m'kuyesedwa: mzimutu uli wakufuna, koma thupi lili lolefuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:8

Pakuti wakufesera kwa thupi la iye yekha, chochokera m'thupi adzatuta chivundi; koma wakufesera kwa Mzimu, chochokera mu Mzimu adzatuta moyo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:2

Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:9

Yense wobadwa kuchokera mwa Mulungu sachita tchimo, chifukwa mbeu yake ikhala mwa iye; ndipo sangathe kuchimwa, popeza wabadwa kuchokera mwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 7:18

Pakuti ndidziwa kuti m'kati mwanga, ndiko m'thupi langa, simukhala chinthu chabwino; pakuti kufuna ndili nako, koma kuchita chabwino sindikupeza.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 9:27

koma ndipumpuntha thupi langa, ndipo ndiliyesa kapolo; kuti, kapena ngakhale ndalalikira kwa ena, ndingakhale wotayika ndekha.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 3:14

Momwemo, okondedwa, popeza muyembekeza izi, chitani changu kuti mupezedwe ndi Iye mumtendere, opanda banga ndi opanda chilema.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:15

Pakuti sitili naye mkulu wa ansembe wosatha kumva chifundo ndi zofooka zathu; koma wayesedwa m'zonse monga momwe ife, koma wopanda uchimo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:11

Tavalani zida zonse za Mulungu, kuti mudzakhoze kuchilimika pokana machenjerero a mdierekezi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:17

Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa; wosunga njira yake atchinjiriza moyo wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:13

Tiyendeyende koyenera, monga usana; si m'madyerero ndi kuledzera ai, si m'chigololo ndi chonyansa ai, si mu ndeu ndi nkhwidzi ai.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:4

Inu ndinu ochokera mwa Mulungu, tiana, ndipo munaipambana; pakuti Iye wakukhala mwa inu aposa iye wakukhala m'dziko lapansi. Iwo ndiwo ochokera m'dziko lapansi;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 1:4

mwa izi adatipatsa malonjezano a mtengo wake ndi aakulu ndithu; kuti mwa izi mukakhale oyanjana nao umulungu wake, mutapulumuka kuchivundi chili padziko lapansi m'chilakolako.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:22

tiyandikire ndi mtima woona, m'chikhulupiriro chokwanira, ndi mitima yathu yowazidwa kuichotsera chikumbumtima choipa, ndi matupi athu osambitsidwa ndi madzi oyera;

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:27

Chokhachi, mayendedwe anu ayenere Uthenga Wabwino wa Khristu: kuti, ndingakhale nditi ndilinkudza ndi kuona inu, ndingakhale nditi ndili kwina, ndikamva za kwa inu, kuti muchilimika mu mzimu umodzi, ndi kugwirira pamodzi ndi moyo umodzi chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 6:19

Ndilankhula manenedwe a anthu, chifukwa cha kufooka kwa thupi lanu; pakuti monga inu munapereka ziwalo zanu zikhale akapolo a chonyansa ndi a kusaweruzika kuti zichite kusaweruzika, inde kotero tsopano perekani ziwalo zanu zikhale akapolo a chilungamo kuti zichite chiyeretso.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 6:18

Thawani dama. Tchimo lililonse munthu akalichita lili kunja kwa thupi; koma wachiwerewere achimwira thupi lake la iye yekha.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 11:2

Pakuti ndichita nsanje pa inu ndi nsanje ya Mulungu; pakuti ndinakupalitsani ubwenzi mwamuna mmodzi, kuti ndikalangize inu ngati namwali woyera mtima kwa Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:6

chifukwa chake tsono tisagone monga otsalawo, komatu tidikire, ndipo tisaledzere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:11

Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga, kuti ndisalakwire Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:29-30

Koma ngati diso lako lamanja likulakwitsa iwe, ulikolowole, nulitaye; pakuti nkwabwino kwa iwe, kuti chimodzi cha ziwalo zako chionongeke, losaponyedwa thupi lako lonse mu Gehena.

Odala ali osauka mumzimu; chifukwa uli wao Ufumu wa Kumwamba.

Ndipo ngati dzanja lako lamanja likulakwitsa iwe, ulidule, nulitaye; pakuti nkwabwino kwa iwe kuti chimodzi cha ziwalo zako chionongeke, losamuka thupi lako lonse ku Gehena.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:5

Pakuti ichi muchidziwe kuti wadama yense, kapena wachidetso, kapena wosirira, amene apembedza mafano, alibe cholowa mu ufumu wa Khristu ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:3-4

Pakuti nthawi yapitayi idakufikirani kuchita chifuniro cha amitundu, poyendayenda inu m'kukhumba zonyansa, zilakolako, maledzero, madyerero, maimwaimwa, ndi kupembedza mafano kosaloleka;

m'menemo ayesa nchachilendo kuti simuthamanga nao kufikira kusefukira komwe kwa chitayiko, nakuchitirani mwano;

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:10-12

Mochokera m'kamwa momwemo mutuluka chiyamiko ndi temberero. Abale anga, izi siziyenera kutero.

Kodi kasupe atulutsira pa uno womwewo madzi okoma ndi owawa?

Kodi mkuyu ukhoza kubala azitona, abale anga, kapena mpesa kubala nkhuyu? Kotero madzi amchere sangathe kutulutsa okoma.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:10

Mwananga, akakukopa ochimwa usalole.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:6

iye wakunena kuti akhala mwa Iye, ayeneranso mwini wake kuyenda monga anayenda Iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 141:4

Mtima wanga usalinge kuchinthu choipa, kuchita ntchito zoipa ndi anthu akuchita zopanda pake; ndipo ndisadye zankhuli zao.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 6:14

Musakhale omangidwa m'goli ndi osakhulupirira osiyana; pakuti chilungamo chigawana bwanji ndi chosalungama? Kapena kuunika kuyanjana bwanji ndi mdima?

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:13

pakuti ngati mukhala ndi moyo monga mwa thupi, mudzafa; koma ngati ndi mzimu mufetsa zochita zake za thupi, mudzakhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:6

Mphulupulu iomboledwa ndi chifundo ndi ntheradi; apatuka pa zoipa poopa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:1

Chifukwa chake ifenso, popeza tizingidwa nao mtambo waukulu wotere wa mboni, titaye cholemetsa chilichonse, ndi tchimoli limangotizinga, ndipo tithamange mwachipiriro makaniwo adatiikira, ndi kupenyerera woyambira ndi womaliza wa chikhulupiriro chathu,

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:3

Mwakhala okonzeka tsopano inu chifukwa cha mau amene ndalankhula ndi inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:25

Mwa ichi, mutataya zonama, lankhulani zoona yense ndi mnzake; pakuti tili ziwalo wina ndi mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:13-14

Lowani pa chipata chopapatiza; chifukwa chipata chili chachikulu, ndi njira yakumuka nayo kukuonongeka ili yotakata; ndipo ali ambiri amene alowa pa icho.

Pakuti chipata chili chopapatiza, ndi ichepetsa njirayo yakumuka nayo kumoyo, ndimo akuchipeza chimenecho ali owerengeka.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 2:10

Inu ndinu mboni, Mulungunso, kuti tinakhala oyera mtima ndi olungama ndi osalakwa kwa inu akukhulupirira;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:15

komatu monga Iye wakuitana inu ali woyera mtima, khalani inunso oyera mtima m'makhalidwe anu onse;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:9

Woyenda moongoka amayenda osatekeseka; koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:9

Chikondano chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choipa; gwirizana nacho chabwino.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Atate wanga wakumwamba, moyo wanga wonse ukukwezetsa ndi kudalitsa dzina lanu, ndinu mlengi wa moyo wanga, zonse zomwe ndili nazo ndi chifukwa cha chisomo chanu chomwe chikuwonekera pa ine tsiku lililonse. Chikondi chanu ndi chachikulu kwambiri kotero kuti ngakhale kuipa kwanga simuleka kundionetsa chifundo chanu. Munandikonda ndipo munatumiza Mwana wanu Yesu kuti ndikhale woyera mwa magazi ake amtengo wapatali. Chifukwa chake pakali pano ndikubwera kwa Yesu, ndikuvomereza machimo anga pamaso panu. Pali zinthu zambiri mwa ine zomwe zayipitsa moyo wanga ndi maganizo anga. Ndikupemphani munditsuke ndi magazi anu ndi kundiyera chifukwa ndikufuna kukhala moyera. Sindikufuna kukukhumudwitsani Ambuye. Mundifufuze, konzani zolinga zanga, kuti chinthu chofunika kwambiri pa moyo wanga mukhale inu, kuti pasakhale chilichonse chomwe ndingadzitamandire nacho kupatula kukhala nanu. Moyo wanga uli m'manja mwanu, mundipange monga momwe mukufunira, mundikwaniritse mu chiyero chanu ndi kuopa kwanu kuti ndikhale molungama pamaso panu, ndi mtima woyera. M'dzina la Yesu, Ameni.