Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -

Miyambo 4 - Buku Lopatulika


Chenjezo lakuti afune Nzeru nalewe njira za oipa

1 Ananu, mverani mwambo wa atate, nimutchere makutu mukadziwe luntha;

2 pakuti ndikuphunzitsani zabwino; musasiye chilangizo changa.

3 Pakuti ndinali mwana kwa atate wanga, wokondedwa ndi mai, ndine ndekha, sanabale wina.

4 Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine, mtima wako uumirire mau anga; sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.

5 Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

6 usasiye nzeru, ndipo idzakusunga; uikonde, idzakutchinjiriza.

7 Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

8 Uilemekeze, ndipo idzakukweza; idzakutengera ulemu pamene uifungatira.

9 Idzaika chisada cha chisomo pamutu pako; idzakupatsa korona wokongola.

10 Tamvera mwananga, nulandire mau anga; ndipo zaka za moyo wako zidzachuluka.

11 Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru, ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.

12 Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda; ukathamanga, sudzaphunthwa.

13 Gwira mwambo, osauleka; uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

14 Usalowe m'mayendedwe ochimwa, usayende m'njira ya oipa.

15 Pewapo, osapitamo; patukapo, nupitirire.

16 Pakuti akapanda kuchita zoipa, samagona; ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwachokera.

17 Pakuti amadya chakudya cha uchimo, namwa vinyo wa chifwamba.

18 Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha, kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee.

19 Njira ya oipa ikunga mdima; sadziwa chimene chiwaphunthwitsa.

20 Mwananga, tamvera mau anga; tcherera makutu ku zonena zanga.

21 Asachoke kumaso ako; uwasunge m'kati mwa mtima wako.

22 Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza, nalamitsa thupi lao lonse.

23 Chinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga; pakuti magwero a moyo atulukamo.

24 Tasiya m'kamwa mokhota, uike patali milomo yopotoka.

25 Maso ako ayang'ane m'tsogolo, zikope zako zipenye moongoka.

26 Sinkhasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako; njira zako zonse zikonzeke.

27 Usapatuke kudzanja lamanja kapena kulamanzere; suntha phazi lako kusiya zoipa.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa