Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 24 - Buku Lopatulika


Ulemerero wa Yehova
Salimo la Davide.

1 Dziko lapansi nla Yehova ndi zodzala zake zomwe, dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhala m'mwemo.

2 Pakuti Iye analimanga pazinyanja, nalikhazika pamadzi.

3 Adzakwera ndani m'phiri la Yehova? Nadzaima m'malo ake oyera ndani?

4 Woyera m'manja, ndi woona m'mtima, ndiye; iye amene sanakweze moyo wake kutsata zachabe, ndipo salumbira monyenga.

5 Iye adzalandira dalitso kwa Yehova, ndi chilungamo kwa Mulungu wa chipulumutso chake.

6 Uwu ndi mbadwo wa iwo akufuna Iye, iwo akufuna nkhope yanu, Mulungu wa Yakobo.

7 Weramutsani mitu yanu, zipata inu; ndipo kwezekani inu, zitseko zosatha, kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.

8 Mfumu imene ya ulemerero ndani? Yehova wamphamvu ndi wolimba, Yehova wolimba kunkhondo.

9 Weramutsani mitu yanu, zipata inu; inde weramutsani, zitseko zosatha inu, kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.

10 Mfumu imene ya ulemerero ndani? Yehova wa makamumakamu, ndiye Mfumu ya ulemerero.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa