Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -

Miyambo 1 - Buku Lopatulika


Zochitira miyambo

1 Miyambo ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israele.

2 Kudziwa nzeru ndi mwambo; kuzindikira mau ozindikiritsa;

3 kulandira mwambo wakusamalira machitidwe, chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika;

4 kuchenjeza achibwana, kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;

5 kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira; ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

6 kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lake, mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.


Munthu asalole oipa amchete

7 Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa; opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

8 Mwananga, tamva mwambo wa atate wako, ndi kusasiya chilangizo cha amai ako;

9 pakuti izi ndi korona wa chisomo pamutu pako, ndi mkanda pakhosi pako.

10 Mwananga, akakukopa ochimwa usalole.

11 Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi, tilalire osachimwa opanda chifukwa;

12 tiwameze ali ndi moyo ngati manda, ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13 tidzapeza chuma chonse cha mtengo wake, tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

14 udzachita nafe maere, tonse tidzakhala ndi chotengeramo chimodzi.

15 Mwananga, usayende nao m'njira; letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16 pakuti mapazi ao athamangira zoipa, afulumira kukhetsa mwazi.

17 Pakuti kutchera msampha pamaso pa mbalame ndi chabe;

18 ndipo awa abisalira mwazi waowao, alalira miyoyo yaoyao.

19 Mayendedwe a yense wopindula chuma monyenga ngotere; chilanda moyo wa eni ake.


Chenjezo la Nzeru

20 Nzeru ifuula panja; imveketsa mau ake pabwalo;

21 iitana posonkhana anthu polowera pachipata; m'mzinda inena mau ake,

22 Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu? Onyoza ndi kukonda kunyoza, opusa ndi kuda nzeru?

23 Tembenukani pamene ndikudzudzulani; taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga, ndikudziwitsani mau anga.

24 Chifukwa ndaitana, ndipo munakana; ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;

25 koma munapeputsa uphungu wanga wonse, ndi kukana kudzudzula kwanga.

26 Inetu ndidzachitira chiphwete tsoka lanu, ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27 pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula, ndi pofika tsoka lanu ngati kamvulumvulu; pakudza kwa inu vuto ndi nsautso.

28 Pamenepo adzandiitana, koma sindidzavomera; adzandifunatu, osandipeza ai;

29 chifukwa anada nzeru, sanafune kuopa Yehova;

30 anakana uphungu wanga, nanyoza kudzudzula kwanga konse;

31 momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao, nadzakhuta zolingalira zao.

32 Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa achibwana kudzawapha; ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

33 Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka, nadzakhala phee osaopa zoipa.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa