Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

100 Mau a m'Baibulo Okhudza Kupemphera


Yobu 22:27

Udzampemphera ndipo adzakumvera; nudzatsiriza zowinda zako.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 21:36

Koma inu dikirani nyengo zonse, ndi kupemphera, kuti mukalimbike kupulumuka zonse zimene zidzachitika, ndi kuimirira pamaso pa Mwana wa Munthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 143:1

Imvani pemphero langa, Yehova; nditcherere khutu kupemba kwanga; ndiyankheni mwa chikhulupiriko chanu, mwa chilungamo chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 1:27

Ndinampempha mwanayu; ndipo Yehova anandipatsa chopempha changa ndinachipempha kwa Iye;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 9:38

Chifukwa chake pempherani Mwini zotuta kuti akokose antchito kukututa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yona 2:1

Pamenepo Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wake ali m'mimba mwa nsombayo.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 18:7

Ndipo kodi Mulungu sadzachitira chilungamo osankhidwa ake akumuitana usana ndi usiku, popeza aleza nao mtima?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4

Mundidziwitse njira zanu, Yehova; Mundiphunzitse mayendedwe anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 9:11

Ndipo Ambuye anati kwa iye, Tauka, pita ku khwalala lotchedwa Lolunjika, ndipo m'nyumba ya Yudasi ufunse za munthu dzina lake Saulo, wa ku Tariso: pakuti taona, alikupemphera

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:16

sindileka kuyamika chifukwa cha inu, ndi kukumbukira inu m'mapemphero anga;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 4:12

Akupatsani moni Epafra ndiye wa kwa inu, ndiye kapolo wa Khristu Yesu, wakulimbika m'mapemphero ake masiku onse chifukwa cha inu, kuti mukaime amphumphu ndi odzazidwa m'chifuniro chonse cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:2

Mulakalaka, ndipo zikusowani; mukupha, nimuchita kaduka, ndipo simungathe kupeza; mulimbana, nimuchita nkhondo; mulibe kanthu, chifukwa simupempha.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 10:4

Ndipo pompenyetsetsa iye ndi kuopa, anati, Nchiyani, Mbuye? Ndipo anati kwa iye, Mapemphero ako ndi zachifundo zako zinakwera zikhala chikumbutso pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:8

Koma usana Yehova adzalamulira chifundo chake, ndipo usiku nyimbo yake idzakhala ndi ine. Inde pemphero la kwa Mulungu wa moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:41

Chezerani ndi kupemphera, kuti mungalowe m'kuyesedwa: mzimutu uli wakufuna, koma thupi lili lolefuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:12

Ndipo kunali masiku awa, Iye anatuluka nanka kuphiri kukapemphera; nachezera usiku wonse m'kupemphera kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 6:4

Koma ife tidzalimbika m'kupemphera, ndi kutumikira mau.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:7

Ngati mukhala mwa Ine, ndi mau anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene muchifuna ndipo chidzachitika kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 2:8

Chifukwa chake ndifuna kuti amunawo apemphere pamalo ponse, ndi kukweza manja oyera, opanda mkwiyo ndi makani.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 2:42

Ndipo anali chikhalire m'chiphunzitso cha atumwi ndi m'chiyanjano, m'kunyema mkate ndi mapemphero.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 4:1

Pakufuula ine mundiyankhe, Mulungu wa chilungamo changa; pondichepera mwandikulitsira malo. Ndichitireni chifundo, imvani pemphero langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 14:23

Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m'phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 5:7

Ameneyo, m'masiku a thupi lake anapereka mapemphero ndi mapembedzero pamodzi ndi kulira kwakukulu ndi misozi kwa Iye amene anakhoza kumpulumutsa Iye muimfa, ndipo anamveka popeza anaopa Mulungu,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 17:6

Ine ndinakuitanani, pakuti mudzandiyankha, Mulungu; tcherani khutu lanu kwa ine, imvani mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:6

Funani Yehova popezeka Iye, itanani Iye pamene ali pafupi;

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 42:10

Ndipo Yehova anachotsa ukapolo wa Yobu, pamene anapempherera mabwenzi ake; Yehova nachulukitsa zake zonse za Yobu mpaka kuziwirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 5:16

Koma Iye anazemba, nanka m'mapululu, nakapemphera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 141:2

Pemphero langa liikike ngati chofukiza pamaso panu; kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 6:21

Ndipo mverani mapembedzero a kapolo wanu ndi a anthu anu Israele, popemphera iwo kuloza konkuno; ndipo mumvere Inu mu Mwamba mokhala Inumo, ndipo pakumva Inu, mukhululukire.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:4

nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,

Mutu    |  Mabaibulo
Yuda 1:20

Koma inu, okondedwa, podzimangirira nokha pa chikhulupiriro chanu choyeretsetsa, ndi kupemphera mu Mzimu Woyera,

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:9

Pakuti Mulungu ali mboni yanga, amene ndimtumikira mu mzimu wanga, mu Uthenga Wabwino wa Mwana wake, kuti kosalekeza ndikumbukira inu,

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 16:25

Koma ngati pakati pa usiku, Paulo ndi Silasi analinkupemphera, naimbira Mulungu nyimbo, ndipo a m'ndendemo analinkuwamva;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 6:9

Wamva Yehova kupemba kwanga; Yehova adzalandira pemphero langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 22:41

Ndipo anapatukana nao kutalika kwake ngati kuponya mwala, nagwada pansi napemphera,

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 65:24

Ndipo padzakhala kuti iwo asanaitane Ine, ndidzayankha; ndipo ali chilankhulire, Ine ndidzamva.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 10:2

Ndipo ananena kwa iwo, Dzinthu dzichuluka, koma antchito achepa; potero pemphani Mwini dzinthu, kuti akankhe antchito kukututa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 69:13

Koma ine, pemphero langa lili kwa Inu, Yehova, m'nyengo yolandirika; Mulungu, mwa chifundo chanu chachikulu, mundivomereze ndi choonadi cha chipulumutso chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 8:28

Koma mucheukire pemphero la kapolo wanu, ndi pembedzero lake, Yehova Mulungu wanga, kumvera kulira ndi kupempha kwake kumene kapolo wanu apempha pamaso panu lero;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 3:10

ndi kuchulukitsa mapemphero athu usiku ndi usana kuti tikaone nkhope yanu, ndi kukwaniritsa zoperewera pa chikhulupiriro chanu?

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 1:11

Kukatero tikupemphereraninso nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akakuyeseni inu oyenera kuitanidwa kwanu, nakakwaniritse chomkomera chonse, ndi ntchito ya chikhulupiriro mumphamvu;

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 6:10

Ndipo podziwa Daniele kuti adatsimikiza cholembedwacho, analowa m'nyumba mwake, m'chipinda mwake, chimene mazenera ake anatseguka oloza ku Yerusalemu; ndipo anagwada maondo ake tsiku limodzi katatu, napemphera, navomereza pamaso pa Mulungu wake monga umo amachitira kale lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 22:32

koma ndinakupempherera kuti chikhulupiriro chako chingazime; ndipo iwe, pamene watembenuka ukhazikitse abale ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 12:5

Pamenepo ndipo Petro anasungika m'ndende; koma Mpingo anampempherera iye kwa Mulungu kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 61:1

Imvani mfuu wanga, Mulungu; mverani pemphero langa.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 33:11

Ndipo Yehova ananena ndi Mose kopenyana maso, monga munthu alankhula ndi bwenzi lake. Ndipo anabwerera kunka kuchigono; koma mtumiki wake Yoswa mwana wa Nuni, ndiye mnyamata msinkhu wake, sanachoke m'chihemamo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 13:9

Pakuti tikondwera, pamene ife tifooka ndi inu muli amphamvu; ichinso tipempherera, ndicho ungwiro wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 13:3

Pamenepo, m'mene adasala chakudya ndi kupemphera ndi kuika manja pa iwo, anawatumiza amuke.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 11:6

koma wopanda chikhulupiriro sikutheka kumkondweretsa; pakuti iye wakudza kwa Mulungu ayenera kukhulupirira kuti alipo, ndi kuti ali wobwezera mphotho iwo akumfuna Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:17

Pempherani kosaleka;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:7

Koma chitsiriziro cha zinthu zonse chili pafupi; chifukwa chake khalani anzeru, ndipo dikirani m'mapemphero;

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:16

Potero tilimbike mtima poyandikira mpando wachifumu wachisomo, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo cha kutithandiza nthawi yakusowa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 21:22

Ndipo zinthu zilizonse mukazifunsa m'kupemphera ndi kukhulupirira, mudzazilandira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 18:6

M'kusauka kwanga ndinaitana Yehova, ndipo ndinakuwira Mulungu wanga; mau anga anawamva mu Kachisi mwake, ndipo mkuwo wanga wa pankhope pake unalowa m'makutu mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 16:24

Kufikira tsopano simunapemphe kanthu m'dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikwaniridwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:29

Yehova atalikira oipa; koma pemphero la olungama alimvera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:8

Yandikirani kwa Mulungu, ndipo adzayandikira kwa inu. Sambani m'manja, ochimwa inu; yeretsani mitima, a mitima iwiri inu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 2:1

Ndidandaulira tsono, poyambayamba, kuti achitike mapembedzo, mapemphero, mapembedzero, mayamiko, chifukwa cha anthu onse;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 102:17

anasamalira pemphero la iwo akusowa konse, osapepula pemphero lao.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 4:2

Chitani khama m'kupemphera, nimudikire momwemo ndi chiyamiko;

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 18:1

Ndipo anawanenera fanizo lakuti ayenera iwo kupemphera nthawi zonse, osafooka mtima;

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:18

mwa pemphero lonse ndi pembedzero mupemphere nthawi yonse mwa Mzimu, ndipo pochezera pamenepo chichezerere ndi kupembedzera oyera mtima onse,

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:6

Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:6

Koma iwe popemphera, lowa m'chipinda chako, nutseke chitseko chako, nupemphere Atate wako ali m'tseri, ndipo Atate wako wakuona m'tseri adzakubwezera iwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 29:12

Pamenepo mudzandiitana Ine, ndipo mudzanka ndi kupemphera kwa Ine, ndipo ndidzakumverani inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:7

Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo chidzatsegulidwa kwa inu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 145:18

Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa Iye, onse akuitanira kwa Iye m'choonadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:13-14

Ndipo chimene chilichonse mukafunse m'dzina langa, ndidzachichita, kuti Atate akalemekezedwe mwa Mwana.

Ngati mudzapempha kanthu m'dzina langa, ndidzachita.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:14

Ndipo uku ndi kulimbika mtima kumene tili nako kwa Iye, kuti ngati tipempha kanthu monga mwa chifuniro chake, atimvera;

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 5:16

Chifukwa chake muvomerezane wina ndi mnzake machimo anu, ndipo mupempherere wina kwa mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama likhoza kwakukulu m'machitidwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:12

kondwerani m'chiyembekezo, pirirani m'masautso; limbikani chilimbikire m'kupemphera.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 11:24

Chifukwa chake ndinena ndi inu, Zinthu zilizonse mukazipemphera ndi kuzipempha, khulupirirani kuti mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:3

M'mawa, Yehova, mudzamva mau anga; m'mawa, ndidzakukonzerani pemphero langa, ndipo ndidzadikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 9:3

Ndipo ndinaika nkhope yanga kwa Ambuye Mulungu, kumfunsa Iye m'pemphero, ndi mapembedzero, ndi kusala, ndi ziguduli, ndi mapulusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 33:3

Undiitane Ine, ndipo Ine ndidzakuyankha iwe, ndipo ndidzakusonyeza iwe zazikulu, ndi zopambana, zimene suzidziwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 22:40

Ndipo pofika pomwepo, anati kwa iwo, Pempherani kuti mungalowe m'kuyesedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 5:20

Ndipo anathandizidwa polimbana nao; ndi Ahagiri anaperekedwa m'dzanja lao, ndi onse anali nao; pakuti anafuulira kwa Mulungu pomenyana nao, ndipo anapembedzeka nao, popeza anamkhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Nehemiya 1:11

Ambuye, mutcherere khutu pemphero la kapolo wanu, ndi pemphero la akapolo anu okondwera nako kuopa dzina lanu; ndipo mupambanitse kapolo wanu lero lino, ndi kumuonetsera chifundo pamaso pa munthu uyu. Koma ndinali ine wothirira mfumu chakumwa chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:1-2

Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.

Ndinakhulupirira, chifukwa chake ndinalankhula; ndinazunzika kwambiri.

Pofulumizidwa mtima ndinati ine, anthu onse nga mabodza.

Ndidzabwezera Yehova chiyani chifukwa cha zokoma zake zonse anandichitira?

Ndidzanyamula chikho cha chipulumutso, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Ndidzachita zowinda zanga za kwa Yehova, tsopano, pamaso pa anthu ake onse.

Imfa ya okondedwa ake nja mtengo wake pamaso pa Yehova.

Ndiloleni, Yehova, indetu ndine mtumiki wanu; ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; mwandimasulira zondimanga.

Ndidzapereka kwa Inu nsembe yachiyamiko, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Ndidzachita zowinda zanga za kwa Yehova, tsopano, pamaso pa anthu ake onse.

M'mabwalo a nyumba ya Yehova, pakati pa inu, Yerusalemu. Aleluya.

Popeza amanditcherera khutu lake, chifukwa chake ndidzaitanira Iye masiku anga onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 4:31

Ndipo m'mene adapemphera iwo, panagwedezeka pamalo pamene adasonkhanirapo; ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nalankhula mau a Mulungu molimbika mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:17

Madzulo, m'mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula, ndipo adzamva mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:9

Mwa ichi ifenso, kuyambira tsiku limene tidamva, sitileka kupembedzera ndi kupempherera inu, kuti mukadzazidwe ndi chizindikiritso cha chifuniro chake mu nzeru zonse ndi chidziwitso cha mzimu,

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 1:35

Ndipo m'mawa mwake anauka usikusiku, natuluka namuka kuchipululu, napemphera kumeneko.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 3:12

amene tili naye chokhazikika mtima ndi chiyandiko cholimbika, mwa chikhulupiriro cha pa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:15

Maso a Yehova ali pa olungama mtima, ndipo makutu ake atchereza kulira kwao.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:22

ndipo chimene chilichonse tipempha, tilandira kwa Iye, chifukwa tisunga malamulo ake, ndipo tichita zomkondweretsa pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mbiri 16:11

Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yake; funani nkhope yake nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 12:23

Ndipo inenso, kukhale kutali ndi ine, kuchimwira Yehova ndi kuleka kukupemphererani; koma ndidzakulangizani njira yabwino ndi yolungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:20

Pakuti kumene kuli awiri kapena atatu asonkhanira m'dzina langa, ndili komweko pakati pao.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 1:14

Iwo onse analikukangalika m'kupemphera, pamodzi ndi akazi, ndi Maria, amake wa Yesu, ndi abale ake omwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:26

Ndipo momwemonso Mzimu athandiza kufooka kwathu; pakuti chimene tizipempha monga chiyenera, sitidziwa; koma Mzimu mwini atipempherera ndi zobuula zosatheka kuneneka;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 66:19-20

Koma Mulungu anamvadi; anamvera mau a pemphero langa.

Imbirani ulemerero wa dzina lake; pomlemekeza mumchitire ulemerero.

Wolemekezeka Mulungu, amene sanandipatutsire ine pemphero langa, kapena chifundo chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 5:13

Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere. Kodi wina asekera? Aimbire.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:7

Ndipo popemphera musabwerezebwereze chabe iai, monga amachita anthu akunja, chifukwa ayesa kuti adzamvedwa ndi kulankhulalankhula kwao.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 7:14

ndipo anthu anga otchedwa dzina langa akadzichepetsa, nakapemphera, nakafuna nkhope yanga, nakatembenuka kuleka njira zao zoipa; pamenepo ndidzamvera mu Mwamba, ndi kukhululukira choipa chao, ndi kuchiritsa dziko lao.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:15

Pakuti inu simunalandire mzimu wa ukapolo kuchitanso mantha; koma munalandira mzimu wa umwana, umene tifuula nao, kuti, Abba! Atate!

Mutu    |  Mabaibulo