Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 143 - Buku Lopatulika


Davide apempha Mulungu amlanditse msanga kwa adani ake
Salimo la Davide.

1 Imvani pemphero langa, Yehova; nditcherere khutu kupemba kwanga; ndiyankheni mwa chikhulupiriko chanu, mwa chilungamo chanu.

2 Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu; pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.

3 Pakuti mdani alondola moyo wanga; apondereza pansi moyo wanga; andikhalitsa mumdima monga iwo adafa kale lomwe.

4 Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine; mtima wanga utenga nkhawa m'kati mwanga.

5 Ndikumbukira masiku a kale lomwe; zija mudazichita ndilingirirapo; ndikamba pandekha za ntchito ya manja anu.

6 Nditambalitsira manja anga kwa Inu: Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

7 Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha. Musandibisire nkhope yanu; ndingafanane nao akutsikira kudzenje.

8 Mundimvetse chifundo chanu mamawa; popeza ndikhulupirira Inu: Mundidziwitse njira ndiyendemo; popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

9 Mundilanditse kwa adani anga, Yehova; ndibisala mwa Inu.

10 Mundiphunzitse chokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kuchidikha.

11 Mundipatse moyo, Yehova, chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu mutulutse moyo wanga m'sautso.

12 Ndipo mwa chifundo chanu mundidulire adani anga, ndipo muononge onse akusautsa moyo wanga; pakuti ine ndine mtumiki wanu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa