Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 14:23 - Buku Lopatulika

23 Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m'phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

23 Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m'phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

23 Tsono atatsazikana nawo anthu aja, Iye adakwera ku phiri yekha kukapemphera. M'mene kunkayamba kuda, nkuti ali komweko yekhayekha.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

23 Atatha kuwawuza kuti azipita kwawo, Iye anakwera ku phiri yekha kukapemphera. Pamene kumada anali kumeneko yekha.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 14:23
11 Mawu Ofanana  

Pomwepo Yesu anadza ndi iwo kumalo otchedwa Getsemani, nanena kwa ophunzira ake, Bakhalani inu pompano, ndipite uko ndikapemphere.


Koma iwe popemphera, lowa m'chipinda chako, nutseke chitseko chako, nupemphere Atate wako ali m'tseri, ndipo Atate wako wakuona m'tseri adzakubwezera iwe.


Ndipo m'mawa mwake anauka usikusiku, natuluka namuka kuchipululu, napemphera kumeneko.


Ndipo atalawirana nao, anachoka Iye, nalowa m'phiri kukapemphera.


Pamene anthu onse anabatizidwa, Yesu nayenso anabatizidwa. Iye anali kupemphera, ndipo kuthambo kunatseguka,


Koma Iye anazemba, nanka m'mapululu, nakapemphera.


Ndipo kunali masiku awa, Iye anatuluka nanka kuphiri kukapemphera; nachezera usiku wonse m'kupemphera kwa Mulungu.


Ndipo kunali, pamene Iye anali kupemphera padera, ophunzira anali naye; ndipo anawafunsa iwo, kuti, Makamuwo a anthu anena kuti Ine ndine yani?


Ndipo pamene padatha ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau amenewa, Iye anatenga Petro ndi Yohane ndi Yakobo apite naye, nakwera m'phiri kukapemphera.


Koma ife tidzalimbika m'kupemphera, ndi kutumikira mau.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa