Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 4 - Buku Lopatulika


Pemphero posautsidwa
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Davide.

1 Pakufuula ine mundiyankhe, Mulungu wa chilungamo changa; pondichepera mwandikulitsira malo. Ndichitireni chifundo, imvani pemphero langa.

2 Amuna inu, ulemu wanga udzakhala wamanyazi kufikira liti? Mudzakonda zachabe, ndi kufunafuna bodza kufikira liti?

3 Koma dziwani kuti Yehova anadzipatulira yekha womkondayo, adzamva Yehova m'mene ndimfuulira Iye.

4 Chitani chinthenthe, ndipo musachimwe. Nenani mumtima mwanu pakama panu, ndipo mukhale chete.

5 Iphani nsembe za chilungamo, ndipo mumkhulupirire Yehova.

6 Ambiri amati, Adzationetsa chabwino ndani? Weramutsirani ife kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

7 Mwapatsa chimwemwe mumtima mwanga, chakuposa chao m'nyengo yakuchuluka dzinthu zao ndi vinyo wao.

8 Ndi mtendere ndidzagona pansi, pomwepo ndidzagona tulo; chifukwa Inu, Yehova, mundikhalitsa ine, ndikhale bwino.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa