Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 6 - Buku Lopatulika


Davide apempha chifundo kwa Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto, pa Seminiti. Salimo la Davide.

1 Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, ndipo musandilange muukali wanu.

2 Mundichitire chifundo, Yehova; pakuti ndalefuka ine. Mundichize, Yehova; pakuti anthunthumira mafupa anga.

3 Moyo wanganso wanthunthumira kwakukulu; ndipo Inu, Yehova, kufikira liti?

4 Bwererani Yehova, landitsani moyo wanga; ndipulumutseni chifukwa cha kukoma mtima kwanu.

5 Pakuti muimfa m'mosakumbukira Inu; m'mandamo adzakuyamikani ndani?

6 Ndalema nako kuusa moyo kwanga; ndiyandamitsa kama wanga usiku wonse; mphasa yanga ndiolobza ndi misozi yanga.

7 Lapuwala diso langa chifukwa cha chisoni; lakalamba chifukwa cha onse akundisautsa.

8 Chokani kwa ine, nonsenu akuchita zopanda pake; pakuti wamva Yehova mau a kulira kwanga.

9 Wamva Yehova kupemba kwanga; Yehova adzalandira pemphero langa.

10 Adzachita manyazi, nadzanthunthumira kwakukulu adani anga onse; adzabwerera, nadzachita manyazi modzidzimuka.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa