Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 61 - Buku Lopatulika


Poopsedwa Davide athamangira Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Davide.

1 Imvani mfuu wanga, Mulungu; mverani pemphero langa.

2 Ku malekezero a dziko lapansi ndidzafuulira kwa Inu, pomizika mtima wanga. Nditsogolereni kuthanthwe londiposa ine m'kutalika kwake.

3 Pakuti munakhala pothawirapo panga; nsanja yolimba pothawa mdani ine.

4 Ndidzagoneragonerabe m'chihema mwanu; ndidzathawira mobisalamo m'mapiko anu.

5 Pakuti Inu, Mulungu, mudamva zowinda zanga; munandipatsa cholowa cha iwo akuopa dzina lanu.

6 Mudzatalikitsa moyo wa mfumu. Zaka zake zidzafikira mibadwomibadwo.

7 Adzakhala nthawi zonse pamaso pa Mulungu; mumpatse chifundo ndi choonadi zimsunge.

8 Potero ndidzaimba zolemekeza dzina lanu kunthawi zonse, kuti ndichite zowinda zanga tsiku ndi tsiku.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa