Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Yona 2 - Buku Lopatulika


Pemphero la Yona ali m'mimba mwa chinsomba

1 Pamenepo Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wake ali m'mimba mwa nsombayo.

2 Ndipo anati, Ndinaitana Yehova m'nsautso wanga, ndipo anandiyankha ine; ndinafuula ndili m'mimba ya manda, ndipo munamva mau anga.

3 Pakuti munandiponya mwakuya m'kati mwa nyanja, ndipo madzi anandizinga; mafunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.

4 Ndipo ndinati, Ndatayika ndichoke pamaso panu; koma ndidzapenyanso Kachisi wanu wopatulika.

5 Madzi anandizinga mpaka moyo wanga, madzi akuya anandizungulira, kayandeyande wa m'nyanja anandikulunga mutu.

6 Ndinatsikira kumatsinde a mapiri, mipingiridzo ya dziko inanditsekereza kosatha; koma munandikwezera moyo wanga kuuchotsa kuchionongeko, Yehova Mulungu wanga.

7 Pokomoka moyo wanga m'kati mwanga ndinakumbukira Yehova; ndi pemphero langa linafikira Inu mu Kachisi wanu wopatulika.

8 Iwo osamalira mabodza opanda pake ataya chifundo chaochao.

9 Koma ine ndidzakupherani Inu nsembe ndi mau akuyamika, ndidzakwaniritsa chowinda changa. Chipulumutso ncha Yehova.

10 Pamenepo Yehova analankhula ndi nsombayo, ndipo inamsanzira Yona kumtunda.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa