Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Yona 2:10 - Buku Lopatulika

10 Pamenepo Yehova analankhula ndi nsombayo, ndipo inamsanzira Yona kumtunda.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Pamenepo Yehova analankhula ndi nsombayo, ndipo inamsanzira Yona kumtunda.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Apo Chauta adalamula chinsomba chija kuti chisanzire Yona ku mtunda.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

Onani mutuwo Koperani




Yona 2:10
18 Mawu Ofanana  

Mulungu ndipo anati, Dziko lapansi limere udzu, therere lobala mbeu, ndi mtengo wazipatso wakubala zipatso monga mwa mtundu wake, momwemo muli mbeu yake, padziko lapansi: ndipo kunatero.


Ndipo Mulungu anati, Pakhale zounikira pathambo la kumwamba, zakulekanitsa usana ndi usiku; zikhale zizindikiro ndi nyengo, ndi masiku, ndi zaka;


Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.


Ndipo Mulungu anapanga thambo, nalekanitsa madzi anali pansi pathambolo ndi madzi anali pamwamba pathambolo; ndipo kunatero.


Ndipo anati Mulungu, Madzi a pansi pakumwamba asonkhane pamodzi pamalo amodzi, uoneke mtunda: ndipo kunatero.


Ananena, ndipo inadza mitambo ya ntchentche, ndi nsabwe kufikira m'malire ao onse.


Ananena, ndipo linadza dzombe ndi mphuchi, ndizo zosawerengeka,


Ozunzika adzadya nadzakhuta, adzayamika Yehova iwo amene amfuna, ukhale moyo mtima wako nthawi zonse.


Pakuti ananena, ndipo chinachitidwa; analamulira, ndipo chinakhazikika.


Yehova ndiye wondipulumutsa ine; Chifukwa chake tidzaimba nyimbo zanga, ndi zoimba zazingwe Masiku onse a moyo wathu m'nyumba ya Yehova.


Ine, Inetu ndine Yehova; ndipo palibe Mpulumutsi, koma Ine ndekha.


Chifukwa chanji ndinafika osapeza munthu? Ndi kuitana koma panalibe wina woyankha? Kodi dzanja langa lafupika konse, kuti silingathe kuombola? Pena Ine kodi ndilibe mphamvu zakupulumutsa? Taona pa kudzudzula kwanga ndiumitsa nyanja, ndi kusandutsa mitsinje chipululu; nsomba zake zinunkha chifukwa mulibe madzi, ndipo zifa ndi ludzu.


Koma Ine ndiye Yehova Mulungu wako chichokere m'dziko la Ejipito, ndipo suyenera kudziwa mulungu wina koma Ine; ndi popanda Ine palibe mpulumutsi.


Asiriya sadzatipulumutsa; sitidzayenda pa akavalo, ndipo sitidzanenanso kwa ntchito ya manja athu, Inu ndinu milungu yathu; pakuti mwa Inu ana amasiye apeza chifundo.


Koma Yehova anaikiratu chinsomba chachikulu chimeze Yona; ndipo Yona anali m'mimba mwa nsombayi masiku atatu usana ndi usiku.


Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yona nthawi yachiwiri, ndi kuti,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa