Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 102 - Buku Lopatulika


Wopsinjika apempha Mulungu achitire anthu ake chifundo, amitundu nammverenso
Pemphero la Wozunzika, m'mene anakomoka natsanulira cholingalira chake pamaso pa Yehova.

1 Yehova, imvani pemphero langa, ndipo mfuu wanga ufikire Inu.

2 Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga; munditchereze khutu lanu; tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga.

3 Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi, ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.

4 Mtima wanga ukunga udzu womweta, nufota; popeza ndiiwala kudya mkate wanga.

5 Chifukwa cha liu la kubuula kwanga mnofu wanga umamatika kumafupa anga.

6 Ndikunga vuwo m'chipululu; ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.

7 Ndidikira, ndikhala ngati mbalame ili yokha pamwamba pa tsindwi.

8 Adani anga anditonza tsiku lonse; akundiyalukirawo alumbirira ine.

9 Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate, ndi kusakaniza chomwera changa ndi misozi,

10 chifukwa cha ukali wanu ndi kuzaza kwanu; popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.

11 Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali; ndipo ine ndauma ngati udzu.

12 Koma Inu, Yehova, mukhalabe kunthawi yonse; ndi chikumbukiro chanu ku mibadwomibadwo.

13 Inu mudzauka, ndi kuchitira nsoni Ziyoni; popeza yafika nyengo yakumchitira chifundo, nyengo yoikika.

14 Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yake, nachitira chifundo fumbi lake.

15 Pamenepo amitundu adzaopa dzina la Yehova, ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu.

16 Pakuti Yehova anamanga Ziyoni, anaoneka mu ulemerero wake;

17 anasamalira pemphero la iwo akusowa konse, osapepula pemphero lao.

18 Ichi adzachilembera mbadwo ukudza; ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19 Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ake opatulika; Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20 kuti amve kubuula kwa wandende; namasule ana a imfa.

21 Kuti anthu alalikire dzina la Yehova mu Ziyoni, ndi chilemekezo chake mu Yerusalemu;

22 Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu, ndi maufumu kuti atumikire Yehova.

23 Iye analanda mphamvu yanga panjira; anachepsa masiku anga.

24 Ndinati, Mulungu wanga, musandichotse pakati pa masiku anga: Zaka zanu zikhalira m'mibadwomibadwo.

25 Munakhazika dziko lapansi kalelo; ndipo zakumwamba ndizo ntchito ya manja anu.

26 Zidzatha izi, koma Inu mukhala: Inde, zidzatha zonse ngati chovala; mudzazisintha ngati malaya, ndipo zidzasinthika:

27 Koma Inu ndinu yemweyo, ndi zaka zanu sizifikira kutha.

28 Ana a atumiki anu adzakhalitsa, ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa