Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

105 Mau a m'Baibulo Okhudza Chimwemwe

Monga mwana wa Mulungu, usakayikire ubwino wake wopanda malire. Uyenera kukhulupirira chikondi chake ndi chisamaliro chake, ngakhale pamene akulola kuti tidutse mu zinthu zovuta. Pa nthawi ngati zimenezi, tingapeze chitetezo mwa Iye.

Ena amaganiza kuti Mulungu ndi wachisoni kapena wokwiya, koma zoona zake n’zakuti Iye ndi wamphamvu ndi wodzala ndi chimwemwe. Chimwemwe chake sichimadalira kanthu kalikonse kapena munthu wina aliyense, ndipo Iye yekha ndiye amene angachipatse kwa ife.

Chimwemwe chathu chimachokera kwa Mulungu, chifukwa nthawi zonse padzakhala zifukwa zolilira, kuvutika, ndi kutaya mtima. Komabe, Iye walonjeza kuti adzakhala nafe masiku onse, kufikira chimaliziro cha dziko lapansi. Monga mmene lemba la Mateyu 28:20 limati, “ndipo onani, Ine ndili pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira chimaliziro cha nthawi ino.”

Chimwemwe mwa Mulungu sichimamveka chabe, koma chimachokera pakulandiridwa ndi Iye, pokhala ndi mtima woyera ndi womasuka pamaso pake. Tiyeni tikondwere ndi choonadi chodabwitsa ichi!


Yesaya 55:12

Pakuti inu mudzatuluka ndi kukondwa, ndi kutsogozedwa ndi mtendere; mapiri ndi zitunda, zidzaimba zolimba pamaso panu, ndi mitengo yonse ya m'thengo idzaomba m'manja mwao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 118:24

Tsiku ili ndilo adaliika Yehova; tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 30:5

Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha; koma kuyanja kwake moyo wonse. Kulira kuchezera, koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 1:1-3

Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa, kapena wosaimirira m'njira ya ochimwa, kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.

Komatu m'chilamulo cha Yehova muli chikondwerero chake; ndipo m'chilamulo chake amalingirira usana ndi usiku.

Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi; wakupatsa chipatso chake pa nyengo yake, tsamba lake lomwe losafota; ndipo zonse azichita apindula nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 1:4

ndipo izi tilemba ife, kuti chimwemwe chathu chikwaniridwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 4:7

Mwapatsa chimwemwe mumtima mwanga, chakuposa chao m'nyengo yakuchuluka dzinthu zao ndi vinyo wao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:21

Pakuti mtima wathu udzakondwera mwa Iye, chifukwa takhulupirira dzina lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 16:11

Mudzandidziwitsa njira ya moyo, pankhope panu pali chimwemwe chokwanira; m'dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:11

Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu, afuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira; nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:5

Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kufuula mokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:11

Izi ndalankhula ndi inu, kuti chimwemwe changa chikhale mwa inu, ndi kuti chimwemwe chanu chidzale.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:47

ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:8

Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima; malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 15:16

Mau anu anapezeka, ndipo ndinawadya; mau anu anakhala kwa ine chikondwero ndi chisangalalo cha mtima wanga; pakuti ndatchedwa dzina lanu, Yehova Mulungu wa makamu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 28:7

Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi chikopa changa; mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza, chifukwa chake mtima wanga ukondwera kwakukulu; ndipo ndidzamyamika nayo nyimbo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Zefaniya 3:14-15

Imba, mwana wamkazi wa Ziyoni; fuula, Israele; kondwera nusekerere ndi mtima wonse, mwana wamkazi wa Yerusalemu.

Yehova wachotsa maweruzo ako, anataya kunja mdani wako; mfumu ya Israele, Yehova, ali pakati pako, sudzaopanso choipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 30:11

Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera; munandivula chiguduli changa, ndipo munandiveka chikondwero,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 33:1

Fuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima, oongoka mtima ayenera kulemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:5

Iwo anayang'ana Iye nasanguluka; ndipo pankhope pao sipadzachita manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:8

Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino; wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:8

kuchita chikondwero chanu kundikonda, Mulungu wanga; ndipo malamulo anu ali m'kati mwamtima mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 51:12

Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu; ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:3

Koma olungama akondwere; atumphe ndi chimwemwe pamaso pa Mulungu; ndipo asekere nacho chikondwerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11

Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:14

Mutikhutitse nacho chifundo chanu m'mawa; ndipo tidzafuula mokondwera ndi kukondwera masiku athu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 92:4

Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kuchita kwanu, ndidzafuula mokondwera pa ntchito ya manja anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:19

Pondichulukira zolingalira zanga m'kati mwanga, zotonthoza zanu zikondweretsa moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 97:11-12

Kuunika kufesekera wolungama, ndi chikondwerero oongoka mtima.

Kondwerani mwa Yehova, olungama inu; ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 100:1-2

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

Tumikirani Yehova ndi chikondwerero: Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:2-5

Lemekeza Yehova, moyo wanga, ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:

Lemekezani Yehova, inu angelo ake; a mphamvu zolimba, akuchita mau ake, akumvera liu la mau ake.

Lemekezani Yehova, inu makamu ake onse; inu atumiki ake akuchita chomkondweretsa Iye.

Lemekezani Yehova, inu, ntchito zake zonse, ponseponse pali ufumu wake: Lemekeza Yehova, moyo wanga iwe.

Amene akhululukira mphulupulu zako zonse; nachiritsa nthenda zako zonse;

amene aombola moyo wako ungaonongeke; nakuveka korona wa chifundo ndi nsoni zokoma:

Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino; nabweza ubwana wako unge mphungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 112:1

Aleluya. Wodala munthu wakuopa Yehova, wakukondwera kwambiri ndi malamulo ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 126:2-3

Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka, ndi lilime lathu linafuula mokondwera; pamenepo anati kwa amitundu, Yehova anawachitira iwo zazikulu.

Yehova anatichitira ife zazikulu; potero tikhala okondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 128:1-2

Wodala yense wakuopa Yehova, wakuyenda m'njira zake.

Pakuti udzadya za ntchito ya manja ako; wodala iwe, ndipo kudzakukomera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 144:15

Odala anthu akuona zotere; odala anthu amene Mulungu wao ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:13

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:28

Chiyembekezo cha olungama ndicho chimwemwe; koma chidikiro cha oipa chidzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:20

Chinyengo chili m'mitima ya oganizira zoipa; koma aphungu a mtendere amakondwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:9

Kuunika kwa olungama kukondwa; koma nyali ya oipa idzazima.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:13

Ngakhale m'kuseka mtima uwawa; ndipo matsiriziro a chiphwete ndi chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:13

Mtima wokondwa usekeretsa nkhope; koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:15

Masiku onse a wosauka ali oipa; koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:30

Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima; ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:20

Wolabadira mau adzapeza bwino; ndipo wokhulupirira Yehova adala.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:22

Mtima wosekerera uchiritsa bwino; koma mzimu wosweka uphwetsa mafupa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:15

Kuchita chiweruzo kukondweretsa wolungama; koma kuwaononga akuchita mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:14

Wodala munthu wakuopa kosalekeza; koma woumitsa mtima wake adzagwa m'zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:18

Popanda chivumbulutso anthu amasauka; koma wosunga chilamulo adalitsika.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 2:26

Pakuti yemwe Mulungu amuyesa wabwino ampatsa nzeru ndi chidziwitso ndi chimwemwe; koma wochimwa amlawitsa vuto la kusonkhanitsa ndi kukundika, kuti aperekere yemwe Mulungu amuyesa wabwino. Ichinso ndi chabe ndi kungosautsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 3:12-13

Ndidziwa kuti iwo alibe ubwino, koma kukondwa ndi kuchita zabwino pokhala ndi moyo.

Ndiponso kuti munthu yense adye namwe naone zabwino m'ntchito zake zonse; ndiwo mtulo wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 5:19-20

Inde yemwe Mulungu wamlemeretsa nampatsa chuma, namninkhanso mphamvu ya kudyapo, ndi kulandira gawo lake ndi kukondwera ndi ntchito zake; umenewu ndiwo mtulo wa Mulungu.

Usalankhule mwanthuku mtima wako, usafulumire kunena kanthu pamaso pa Mulungu; pakuti Mulungu ali kumwamba, iwe uli pansi; chifukwa chake mau ako akhale owerengeka.

Pakuti sadzakumbukira masiku a moyo wake kwambiri; chifukwa Mulungu amvomereza m'chimwemwe cha mtima wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 9:7

Tiye, idya zakudya zako mokondwa, numwe vinyo wako mosekera mtima; pakuti Mulungu wavomerezeratu zochita zako.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 12:2-3

Taonani, Mulungu ndiye chipulumutso changa; ndidzakhulupirira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye chipulumutso changa.

Chifukwa chake mudzakondwera pakutunga madzi m'zitsime za chipulumutso.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 35:10

ndipo oomboledwa a Yehova adzabwera, nadzafika ku Ziyoni alikuimba; kukondwa kosatha kudzakhala pa mitu yao; iwo adzakhala ndi kusekerera ndi kukondwa, ndipo chisoni ndi kuusa moyo kudzachoka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 51:11

Ndipo oomboledwa a Yehova adzabwera, nadzafika ku Ziyoni; ndi nyimbo ndi kukondwa kosatha kudzakhala pa mitu yao; adzakhala m'kusangalala ndi kukondwa, ndipo chisoni ndi kuusa moyo kudzachoka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:3

ndikakonzere iwo amene alira maliro mu Ziyoni, ndi kuwapatsa chovala kokometsa m'malo mwa phulusa, mafuta akukondwa m'malo mwa maliro, chovala cha matamando m'malo mwa mzimu wopsinjika; kuti iwo atchedwe mitengo ya chilungamo yakuioka Yehova, kuti Iye alemekezedwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 65:18-19

Koma khalani inu okondwa ndi kusangalala kunthawi zonse ndi ichi ndichilenga; pakuti taonani, ndilenga Yerusalemu wosangalala, ndi anthu ake okondwa.

Ndipo ndidzasangalala mu Yerusalemu, ndi kukondwera mwa anthu anga; ndipo mau akulira sadzamvekanso mwa iye, pena mau akufuula.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 31:13

Ndipo namwali adzasangalala m'masewero, ndi anyamata ndi nkhalamba pamodzi; pakuti ndidzasandutsa kulira kwao kukhale kukondwera, ndipo ndidzatonthoza mitima yao, ndi kuwasangalatsa iwo asiye chisoni chao.

Mutu    |  Mabaibulo
Zefaniya 3:17

Yehova Mulungu wako ali pakati pako, wamphamvu wakupulumutsa; adzakondwera nawe ndi chimwemwe, adzakhala wopanda thamo m'chikondi chake; adzasekerera nawe ndi kuimbirapo.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:12

Sekerani, sangalalani: chifukwa mphotho yanu ndi yaikulu mu Mwamba: pakuti potero anazunza aneneri anakhalawo musanabadwe inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:33

Koma muyambe mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 9:2

Ndipo onani, anabwera naye kwa Iye munthu wamanjenje, wakugona pamphasa: ndipo Yesu pakuona chikhulupiriro chao, anati kwa wodwalayo, Limba mtima, mwana, machimo ako akhululukidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 25:21

Mbuye wake anati kwa iye, Chabwino, kapolo iwe wabwino ndi wokhulupirika; unali wokhulupirika pa zinthu zazing'ono, ndidzakhazika iwe pa zinthu zambiri; lowa iwe m'chikondwerero cha mbuye wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 28:8

Ndipo iwo anachoka msanga kumanda, ndi mantha ndi kukondwera kwakukulu, nathamanga kukauza ophunzira ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:21

Odala inu akumva njala tsopano; chifukwa mudzakhuta. Odala inu akulira tsopano; chifukwa mudzaseka.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 10:20

Koma musakondwera nako kuti mizimu idakugonjerani, koma kondwerani kuti maina anu alembedwa mu Mwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 15:7

Ndinena kwa inu, kotero kudzakhala chimwemwe Kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi wotembenuka mtima, koposa anthu olungama makumi asanu ndi anai mphambu asanu ndi anai, amene alibe kusowa kutembenuka mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 15:10

Chomwecho, ndinena kwa inu, kuli chimwemwe pamaso pa angelo a Mulungu chifukwa cha munthu wochimwa mmodzi amene atembenuka mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 10:10

Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga. Ndadza Ine kuti akhale ndi moyo, ndi kukhala nao wochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 16:20

Indetu, indetu, ndinena ndi inu, kuti mudzalira ndi kubuma maliro inu, koma dziko lapansi lidzakondwera; mudzachita chisoni inu, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 16:22

Ndipo inu tsono muli nacho chisoni tsopano lino, koma ndidzakuonaninso, ndipo mtima wanu udzakondwera, ndipo palibe wina adzachotsa kwa inu chimwemwe chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 17:13

Koma tsopano ndidza kwa Inu; ndipo izi ndilankhula m'dziko lapansi, kuti akhale nacho chimwemwe changa chokwaniridwa mwa iwo okha.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 2:28

munandidziwitsa ine njira za moyo; mudzandidzaza ndi kukondwera pamaso panu.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 13:52

Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chimwemwe ndi Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 5:2-3

amene ife tikhoza kulowa naye ndi chikhulupiriro m'chisomo ichi m'mene tilikuimamo; ndipo tikondwera m'chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.

Ndipo lamulo linalowa moonjezera, kuti kulakwa kukachuluke; koma pamene uchimo unachuluka, pomwepo chisomo chinachuluka koposa;

kuti, monga uchimo unachita ufumu muimfa, chomwechonso chisomo chikachite ufumu mwa chilungamo, kufikira moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye wathu.

Ndipo si chotero chokha, komanso tikondwera m'zisautso; podziwa ife kuti chisautso chichita chipiriro; ndi chipiriro chichita chizolowezi;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:12

kondwerani m'chiyembekezo, pirirani m'masautso; limbikani chilimbikire m'kupemphera.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 14:17

Pakuti ufumu wa Mulungu sukhala chakudya ndi chakumwa, koma chilungamo, ndi mtendere, ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:13

Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 7:4

Ndilimbika mtima kwambiri pakunena nanu, kudzitamandira kwanga chifukwa cha inu nkwakukulu; ndidzazidwa nacho chitonthozo, ndisefukira nacho chimwemwe m'chisautso chathu chonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:22

Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:4

nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:2

kwaniritsani chimwemwe changa, kuti mukalingalire mtima zomwezo, akukhala nacho chikondi chomwe, a moyo umodzi, olingalira mtima umodzi;

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:17-18

Komatu ngatinso ndithiridwa pa nsembe ndi kutumikira kwa chikhulupiriro chanu, ndikondwera, ndipo ndikondwera pamodzi ndi inu nonse;

momwemonso kondwerani inu, nimukondwere pamodzi ndi ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 3:1

Chotsalira, abale anga, kondwerani mwa Ambuye. Kulembera zomwezo kwa inu, sikundivuta ine, koma kwa inu kuli kukhazikitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:4

Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:7

Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:11

olimbikitsidwa m'chilimbiko chonse, monga mwa mphamvu ya ulemerero wake, kuchitira chipiriro chonse ndi kuleza mtima konse pamodzi ndi chimwemwe,

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalimo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 1:6

Ndipo munayamba kukhala akutsanza athu, ndi a Ambuye, m'mene mudalandira mauwo m'chisautso chambiri, ndi chimwemwe cha Mzimu Woyera;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:16

Kondwerani nthawi zonse;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 1:4

pokhumba usiku ndi usana kukuona iwe, ndi kukumbukira misozi yako, kuti ndidzazidwe nacho chimwemwe;

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:2

Yesu, ameneyo, chifukwa cha chimwemwe choikidwacho pamaso pake, anapirira mtanda, nanyoza manyazi, nakhala padzanja lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:2-3

Muchiyese chimwemwe chokha, abale anga, m'mene mukugwa m'mayesero a mitundumitundu;

Pakuti mkwiyo wa munthu suchita chilungamo cha Mulungu.

Mwa ichi, mutavula chinyanso chonse ndi chisefukiro cha choipa, landirani ndi chifatso mau ookedwa mwa inu, okhoza kupulumutsa moyo wanu.

Khalani akuchita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.

Pakuti ngati munthu ali wakumva mau, wosati wakuchita, iyeyu afanana ndi munthu wakuyang'anira nkhope yake ya chibadwidwe chake m'kalirole;

pakuti wadziyang'anira yekha, nachoka, naiwala pompaja nali wotani.

Koma iye wakupenyerera m'lamulo langwiro, ndilo laufulu, natero chipenyerere, ameneyo, posakhala wakumva wakuiwala, komatu wakuchita ntchito, adzakhala wodala m'kuchita kwake.

Ngati wina adziyesera ali wopembedza Mulungu, ndiye wosamanga lilime lake, koma adzinyenga mtima wake, kupembedza kwake kwa munthuyu nkopanda pake.

Mapembedzedwe oyera ndi osadetsa pamaso pa Mulungu ndi Atate ndiwo: kucheza ndi ana amasiye ndi akazi amasiye m'chisautso chao, ndi kudzisungira mwini wosachitidwa mawanga ndi dziko lapansi.

pozindikira kuti chiyesedwe cha chikhulupiriro chanu chichita chipiriro.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 5:13

Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere. Kodi wina asekera? Aimbire.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:8

amene mungakhale simunamuone mumkonda; amene mungakhale simumpenya tsopano, pokhulupirira, mukondwera naye ndi chimwemwe chosaneneka, ndi cha ulemerero:

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:13

koma popeza mulawana ndi Khristu zowawa zake, kondwerani: kutinso pa vumbulutso la ulemerero wake mukakondwere kwakukulukulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 32:11

Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima; ndipo fuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 146:5

Wodala munthu amene akhala naye Mulungu wa Yakobo kuti amthandize, chiyembekezo chake chili pa Yehova, Mulungu wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:6

M'kulakwa kwa woipa muli msampha; koma wolungama aimba, nakondwera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:1

Mwana wanzeru akondweretsa atate; koma mwana wopusa amvetsa amake chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 9:3

Inu mwachulukitsa mtundu, inu mwaenjezera kukondwa kwao; iwo akondwa pamaso panu monga akondwera m'masika, monga anthu akondwa pogawana zofunkha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 16:24

Kufikira tsopano simunapemphe kanthu m'dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikwaniridwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:14

Ndipo udzakhala nako kukondwera ndi msangalalo; ndipo anthu ambiri adzakondwera pa kubadwa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:18-20

Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli chitayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

ndi kudzilankhulira nokha ndi masalimo, ndi mayamiko, ndi nyimbo zauzimu, kuimbira ndi kuimba m'malimba Ambuye mumtima mwanu;

ndipo yendani m'chikondi monganso Khristu anakukondani inu, nadzipereka yekha m'malo mwathu, chopereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale fungo lonunkhira bwino.

ndi kuyamika Mulungu Atate masiku onse, chifukwa cha zonse, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 14:27

Mtendere ndikusiyirani inu, mtendere wanga ndikupatsani; Ine sindikupatsani inu monga dziko lapansi lipatsa. Mtima wanu usavutike, kapena usachite mantha.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga, muli wabwino ndipo chifundo chanu ndi kukoma mtima kwanu kuli kwamuyaya. Mphamvu yanu ndi yaikulu bwanji! Ndimawerama pamaso pa ntchito zanu zazikulu, Ambuye wanga, chifukwa ndinu wosayerekezeka. Atate, zikomo chifukwa mwa inu muli chimwemwe chokwanira ndipo ndikusangalala chifukwa ndili ndi ufulu wosangalala ndi kukhalapo kwanu, chifukwa kudzera mwa Mzimu wanu Woyera wokondedwa ndingapeze chimwemwe chenicheni. Zikomo chifukwa cha zabwino ndi zoyipa zonse, ndithudi ndi mwayi womwe mumandipatsa kuti ndionetse chikondi chanu chachikulu pa ine, chifukwa kwa ife okukondani zonse zimatithandiza pa zabwino. Ndidziwitseni tsiku lililonse kuyenda ndi chipatso cha Mzimu wanu Woyera, kuti nditha kuwonetsa chimwemwe m'zonse zomwe ndimanena komanso m'zonse zomwe ndimachita motero ndikufalitsa kwa omwe ali pafupi nane. Ambuye Yesu, ndithandizeni nthawi zonse kukhala ndi mtima woyamikira pazinthu zonse, kuti chimwemwe chanu chikhale mwa ine, ngakhale pazovuta kwambiri, chifukwa ndikudziwa kuti chochitika chilichonse chili ndi cholinga chamtengo wapatali, phunziro losayerekezeka ndi kuphunzira. Ambuye, lolani kuti chimwemwe ichi chisathe kuti ndipitirizebe kukhala ndi masiku anga, mpaka nthawi yoti ndikhale ndi chimwemwe chachikulu kwambiri chodzikonzekera kukumana nanu kopambana. Mawu anu amati: «Mundionetse njira ya moyo; pamaso panu pali chimwemwe chokwanira; zokondweretsa kudzanja lanu lamanja kwamuyaya». M'dzina la Yesu. Ameni.