Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 28 - Buku Lopatulika


Apempha chipulumutso, ayamika populumutsidwa
Salimo la Davide.

1 Kwa Inu, Yehova, ndidzafuulira; thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva; pakuti ngati munditontholera ine, ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.

2 Mverani mau a kupemba kwanga, pamene ndilirira Inu, pamene ndikweza manja anga kuloza ponenera panu poyera.

3 Musandikoke kundichotsa pamodzi ndi oipa, ndi ochita zopanda pake; amene alankhula zamtendere ndi anansi ao, koma mumtima mwao muli choipa.

4 Muwapatse monga mwa ntchito zao, ndi monga mwa choipa chochita iwo; muwapatse monga mwa machitidwe a manja ao; muwabwezere zoyenera iwo.

5 Pakuti sasamala ntchito za Yehova, kapena machitidwe a manja ake, adzawapasula, osawamanganso.

6 Wodalitsika Yehova, Pakuti adamva mau a kupemba kwanga.

7 Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi chikopa changa; mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza, chifukwa chake mtima wanga ukondwera kwakukulu; ndipo ndidzamyamika nayo nyimbo yanga.

8 Yehova ndiye mphamvu yao, inde mphamvu ya chipulumutso cha wodzozedwa wake.

9 Pulumutsani anthu anu, ndi kudalitsa cholowa chanu; muwawetenso, ndi kuwanyamula nthawi zonse.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa