Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 92 - Buku Lopatulika


Anthu onse ayamike Mulungu chifukwa cha ntchito zake, chilungamo chake, ndi chifundo chake
Salimo, Nyimbo ya pa Sabata.

1 Nkokoma kuyamika Yehova, ndi kuimbira nyimbo dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.

2 Kuonetsera chifundo chanu mamawa, ndi chikhulupiriko chanu usiku uliwonse.

3 Pa choimbira cha zingwe khumi ndi pachisakasa; pazeze ndi kulira kwake.

4 Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kuchita kwanu, ndidzafuula mokondwera pa ntchito ya manja anu.

5 Ha! Ntchito zanu nzazikulu, Yehova, zolingalira zanu nzozama ndithu.

6 Munthu wopulukira sachidziwa; ndi munthu wopusa sachizindikira ichi;

7 chakuti pophuka oipa ngati msipu, ndi popindula ochita zopanda pake; chitero kuti adzaonongeke kosatha.

8 Koma Inu, Yehova, muli m'mwamba kunthawi yonse.

9 Pakuti, taonani, adani anu, Yehova, pakuti, taonani, adani anu adzatayika; ochita zopanda pake onse adzamwazika.

10 Koma munakweza nyanga yanga ngati ya njati; anandidzoza mafuta atsopano.

11 Diso langa lapenya chokhumba ine pa iwo ondilalira, m'makutu mwanga ndamva chokhumba ine pa iwo akuchita zoipa akundiukira.

12 Wolungama adzaphuka ngati mgwalangwa; adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni.

13 Iwo ookedwa m'nyumba ya Yehova, adzaphuka m'mabwalo a Mulungu wathu.

14 Atakalamba adzapatsanso zipatso; adzadzazidwa ndi madzi nadzakhala abiriwiri,

15 kulalikira kuti Yehova ngwolunjika; Iye ndiye thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe chosalungama.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa