Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Masalimo 34:5 - Buku Lopatulika

5 Iwo anayang'ana Iye nasanguluka; ndipo pankhope pao sipadzachita manyazi.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

5 Iwo anayang'ana Iye nasanguluka; ndipo pankhope pao sipadzachita manyazi.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

5 Ozunzikawo atayang'ana kwa Chauta, nkhope zao zidasangalala, sadachite manyazi.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 34:5
17 Mawu Ofanana  

Ndipo Yowabu anafika kunyumba ya mfumu, nati, Lero mwachititsa manyazi nkhope zao za anyamata anu onse, amene anapulumutsa moyo wanu lero, ndi miyoyo ya ana anu aamuna ndi aakazi, ndi miyoyo ya akazi anu, ndi miyoyo ya akazi anu aang'ono;


Ayuda anali nako kuunika, ndi kukondwera, ndi chimwemwe, ndi ulemu.


Penyani, ndiyankheni, Yehova Mulungu wanga. Penyetsani maso anga, kuti ndingagone tulo ta imfa;


Tsiku loitana ine, munandiyankha, munandilimbitsa ndi mphamvu m'moyo mwanga.


Pakuti Inu muyatsa nyali yanga; Yehova, Mulungu wanga, aunikira mdima wanga.


Inde, onse akuyembekezera Inu sadzachita manyazi; adzachita manyazi iwo amene achita monyenga kopanda chifukwa.


Ndinagona ine pansi, ndinagona tulo; ndinauka; pakuti Yehova anandichirikiza.


Pakuti chitsime cha moyo chili ndi Inu, M'kuunika kwanu tidzaona kuunika.


Ndipo undiitane tsiku la chisautso, ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.


Wopereka nsembe yachiyamiko andilemekeza Ine; ndipo kwa iye wosunga mayendedwe ake ndidzamuonetsa chipulumutso cha Mulungu.


Achititseni manyazi pankhope pao; kuti afune dzina lanu, Yehova.


Kuunika kufesekera wolungama, ndi chikondwerero oongoka mtima.


Yang'anani kwa Ine, mupulumutsidwe, inu malekezero onse a dziko; pakuti Ine ndine Mulungu, palibe wina.


Pamenepo udzaona ndi kuunikidwa, ndipo mtima wako udzanthunthumira ndi kukuzidwa; pakuti unyinji wa nyanja udzakutembenukira, chuma cha amitundu chidzafika kwa iwe.


Yesu, ameneyo, chifukwa cha chimwemwe choikidwacho pamaso pake, anapirira mtanda, nanyoza manyazi, nakhala padzanja lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu.


Potero Davide ndi anyamata ake, ndiwo monga ngati mazana asanu ndi limodzi, ananyamuka, natuluka ku Keila, nayendayenda kulikonse adakhoza kuyendako. Ndipo anauza Saulo kuti Davide wapulumuka ku Keila; iye naleka kumtsata.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa