Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

103 Mau a m'Baibulo Okhudza Chidani

Ndikufuna ndikuuzeni anzanga, nkhani ya kaduka ndi yowopsa kwambiri. Mawu a Mulungu amatichenjeza za kuipa kwake.

M’mawu a Ambuye Yesu pa phiri, Iye anati, “Koma Ine ndinena kwa inu, kuti aliyense wakwiyira m’bale wake popanda chifukwa adzayankha mlandu kwa oweruza; ndipo aliyense wonenera m’bale wake, ‘Wopusa iwe,’ adzayankha mlandu ku bwalo lalikulu; ndipo aliyense wonenera, ‘Chitsiru,’ adzakhala woyenera moto wa gehena” (Mateyu 5:22).

Pamene tikumuyandikila Ambuye ndikukhala naye paubwenzi, timazindikira machimo athu, mkati ndi kunja. Tiyenera kusiya chinyengo ndi mkwiyo, chifukwa nthawi zina tingakhale ndi kaduka koma tioneka ngati tilibe.

Tiyenera kuchotsa mzimu wa kaduka mwa ife ndikupempha chikhululukiro kwa Mulungu, kudzipereka kwa Yesu. Kaduka kangawononge mitima yathu, maganizo athu, komanso matupi athu.


Levitiko 19:17

“Musadane ndi mbale wanu mumtima mwanu, koma mumdzudzule mosabisa kuti mungavomerezane naye pa tchimo lake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:9

Munthu akamati ali m'kuŵala, komabe nkumadana ndi mnzake, akali mu mdima ameneyo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:11

Munthu wodana ndi mnzake, ali mu mdima, ndipo akuyenda mu mdima. Sadziŵa kumene akupita, chifukwa mdima wamudetsa m'maso.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:20

Wina akamanena kuti, “Ndimakonda Mulungu”, komabe nkumadana ndi mbale wake, ndi wonama ameneyo. Pakuti munthu wosakonda mbale wake amene wamuwona, sangathe kukonda Mulungu amene sadamuwone.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:15

Aliyense wodana ndi mnzake, ndi wopha anthu. Ndipo mukudziŵa kuti aliyense wopha anthu, alibe moyo wosatha mumtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:27-28

“Koma inu amene mukumva mau anga, ndikukuuzani kuti, Muzikonda adani anu, muziŵachitira zabwino amene amadana nanu.

Muziŵafunira madalitso amene amakutembererani, muziŵapempherera amene amakuvutitsani.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 7:15

Chauta adzakutchinjirizani pa matenda onse. Iye sadzalolanso kuti matenda oopsa a ku Ejipito amene mumaŵadziŵa aja, afikenso pa inu, koma Mulungu adzadzetsa matenda ameneŵa pa adani anu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:12

Chidani chimautsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:41

kuti ndidzanola lupanga langa lochezimira, ndipo ndidzaona kuti chilungamo chichitike. Adani anga ndidzaŵabwezera chilango, amene amadana nane ndidzaŵalanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:104

Ndimakhala ndi nzeru za kumvetsa chifukwa cha malamulo anu. Nchifukwa chake ndimadana ndi njira iliyonse yonyenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:22

Anthu onse adzadana nanu chifukwa cha Ine. Koma yemwe adzalimbikire mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 3:8

Pali nthaŵi yokondana ndi nthaŵi yodana, nthaŵi ya nkhondo ndi nthaŵi ya mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:5

Anthu onyada sangathe kuwonekera pamaso panu. Inu mumadana ndi anthu onse ochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 11:5

Chauta amayesa anthu olungama namakondwera nawo, mtima wake umadana ndi anthu oipa okonda zachiwawa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 26:5

Ndimadana ndi anthu ochita zoipa, sindikhala pamodzi ndi anthu oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 31:6

Inu mumadana ndi opembedza mafano achabechabe. Koma ine ndimakhulupirira Inu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:21

Choipa chitsata mwini, anthu odana ndi munthu wa Mulungu adzalangidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 36:2

Amadzinyenga m'maganizo mwake, kotero kuti tchimo lake sangathe kulizindikira ndi kudana nalo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 3:20

Aliyense wochita zoipa, amadana ndi kuŵala. Saonekera poyera, kuwopa kuti zochita zakezo zingaonekere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 45:7

Mumakonda chilungamo ndipo mumadana ndi zoipa. Nchifukwa chake Mulungu, Mulungu wanu, wakusankhani. Wakudzozani ndi kukusangalatsani kupambana anzanu ena onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:18

“Ngati anthu odalira zapansipano adana nanu, kumbukirani kuti adadana ndi Ine asanadane nanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 50:17

Iwe sufuna kulangizidwa, umaponya mau anga ku nkhongo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:12-14

Akadakhala mdani wanga wondinyozayo, ndikadatha kupirira. Akadakhala mdani wanga wondichita chipongweyo, ndikadangobisala basi.

Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa wozoloŵerana naye, ndi amene ukuchita zimenezi.

Tinkakambirana nkhani zokoma tili aŵiri, tinkapembedza limodzi m'Nyumba ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:31-32

Muchotseretu pakati panu kuzondana, kukalipa, ndiponso kupsa mtima. Musachitenso chiwawa, kapena kulankhula mau achipongwe, tayani kuipa konse.

Muzikomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, ndipo muzikhululukirana monga momwe Mulungu mwa Khristu adakukhululukirani inunso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:1

Mulungu adzambatuke, adani ake amwazikane. Onse amene amamuda, athaŵe pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 69:4

Anthu odana nane popanda chifukwa ndi ochuluka kupambana tsitsi la kumutu kwanga. Ndi amphamvu anthu ongofuna kundiwononga, ndi kundineneza ndi mabodza ao. Kodi ndiyenera kubweza zimene sindinabe?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 97:10

Chauta amakonda anthu odana ndi zoipa. Iye amasunga moyo wa anthu ake oyera mtima. Amaŵapulumutsa kwa anthu oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 101:3

Sindidzaika maso anga pa chinthu chilichonse chachabechabe. Ndimadana ndi zochita za anthu okusiyani, sizindikomera konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 109:3-5

Ponseponse amandilankhula mau achidani, amandinena popanda chifukwa.

Ndidzathokoza Chauta kwambiri polankhula. Ndidzamtamanda pakati pa gulu la anthu.

Paja Chauta amaimirira pafupi ndi munthu wosoŵa, amafuna kumpulumutsa kwa anthu ogamula kuti iyeyo aphedwe.

M'malo mwa chikondi changa, iwo amandibwezera zondineneza, ngakhale pamene ndikuŵapempherera.

Motero amandibwezera zoipa m'malo mwa zabwino, amandiwonetsa chidani m'malo mwa chikondi changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:113

Ndimadana nawo anthu apaŵiripaŵiri, koma ndimakonda mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:163

Ndimadana ndi anthu abodza, zoonadi, ndimanyansidwa nawo, koma ndimakonda malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:16-19

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Chauta amadana nazo, makamaka zisanu ndi ziŵiri ndithu zimene zimamunyansa:

maso onyada, pakamwa pabodza, manja opha munthu wosalakwa,

mtima wokonzekera kuchita zoipa, mapazi othamangira msangamsanga ku zoipa,

mboni yonama yolankhula mabodza, ndi munthu woutsa chidani pakati pa abale.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:13

Kuwopa Chauta nkudana ndi zoipa. Kunyada, kudzitama, kuchita zoipa ndi kulankhula zonyenga, zonsezo ndimadana nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:17

Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino, koma munthu wankhwidzi amadzipweteka yekha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:20

Anthu a mtima woipa amamnyansa Chauta, koma anthu a makhalidwe abwino amamkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:17

Kuli bwino kudyera masamba pali chikondi, kupambana kudyera nyama ya ng'ombe yonenepa pali chidani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:26

Maganizo a anthu oipa amamnyansa Chauta, koma mau a anthu olungama amamkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:24-26

Munthu wachidani pakamwa pake pamalankhula zabwino, pamene mumtima mwake muli zonyenga.

Woteroyo akamalankhula mokometsa mau, usamkhulupirire, pakuti mumtima mwake mwadzaza zoipa.

Ngakhale amabisa chidani mochenjera, kuipa kwakeko kudzaoneka poyera pakati pa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:28

Munthu wonama amadana ndi amene iye adaŵapweteka, pakamwa poshashalika mpoononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:14

Zikondwerero zanu za pokhala mwezi ndi masiku anu oyera ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera, ndatopa nako kuŵapirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:8

“Ine Chauta ndimakonda chilungamo, ndimadana ndi zakuba ndi zoipa. Anthu anga ndidzaŵapatsa mphotho mokhulupirika, ndidzapangana nawo chipangano chosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:5

Imvani mau a Chauta, inu amene mumanjenjemera akamalankhula. Iye akuti, “Abale anu omwe amene amadana nanu nakukanani chifukwa cha dzina langa, amati, ‘Chauta alemekezeke, kuti ife tiwone chimwemwe chanu.’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 12:8

Anthu anga osankhidwa asanduka ngati mikango yakuthengo, amandidzumira mwaukali. Nchifukwa chake ndimadana nawo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 44:4

Komabe ine ndidakhala ndikutuma atumiki anga aneneri kuti adzakuuzeni kuti, ‘Musamachita zoipa zimene Ine ndimadana nazo.’

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 9:15

Chauta akuti, “Kuipa kwao konse kudaoneka makamaka ku Giligala. Ndidayamba kudana nawo kumeneko. Ndidzaŵapirikitsa m'dziko mwanga, chifukwa makhalidwe ao ndi oipa. Sindidzaŵakondanso, atsogoleri ao onse andiwukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Amosi 5:10

Inu mumadana ndi muweruzi wodzudzula zosalungama, mumanyansidwa ndi wokamba zoona pa bwalo lamilandu.

Mutu    |  Mabaibulo
Amosi 5:15

Muzidana ndi zoipa, muzikonda zabwino. Mukhazikitse chilungamo m'mabwalo a milandu. Mwina mwake Chauta, Mulungu Wamphamvuzonse, adzakukomerani mtima inu anthu otsala a m'banja la Yosefe.

Mutu    |  Mabaibulo
Mika 3:2

Mumadana ndi zabwino, mumakonda zoipa. Anthu anga mumaŵasenda amoyo, ndi kukangadzula mnofu wao.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 8:17

Musamachitirane chiwembu, musamakonde kulumbira zonama, pakuti zonsezi ndimadana nazo.” Ndikutero Ine Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Malaki 1:2-3

Chauta akuti, “Ndakukondani inu.” Koma inu mumati. “Kodi mwatikonda motani?” Chauta akunena kuti, “Kodi suja Esau ndi mbale wake wa Yakobe?

Komabe ndakonda Yakobe, koma Esau ndadana naye. Dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu, dziko limene ndidampatsa ndalisandutsa la nkhandwe zam'chipululu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:43-44

“Mudamva kuti anthu akale aja adaaŵalamula kuti, ‘Ukonde mnzako, ndi kudana ndi mdani wako.’

Chabwino, koma Ine ndikukuuzani kuti muzikonda adani anu ndipo muziŵapempherera amene amakuzunzani.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 6:24

“Munthu sangathe kutumikira mabwana aŵiri, pakuti kapena adzadana ndi mmodzi nkukonda winayo, kapena adzadzipereka kwa mmodzi nkumanyoza winayo. Simungathe kutumikira onse aŵiri, Mulungu ndi chuma.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 13:13

Anthu onse adzadana nanu chifukwa cha Ine. Koma yemwe adzalimbikire mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.”

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:71

Adaalonjeza kuti adzatipulumutsa kwa adani athu, ndi kwa onse odana nafe.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:22

“Ndinu odala anthu akamadana nanu, akamakusalani ndi kukuchitani chipongwe, ndipo akamaipitsa dzina lanu chifukwa cha Ine Mwana wa Munthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 21:17

Anthu onse adzadana nanu chifukwa cha Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 7:7

Anthu ongokonda zapansipano sangadane nanu, koma amadana ndi Ine, chifukwa ndimapereka umboni wosonyeza kuti ntchito zao nzoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 8:44

Inu ndinu ana a Satana. Iye ndiye tate wanu, ndipo mukufuna kumachita zimene tate wanuyo amalakalaka. Iye uja chikhalire ngwopha anthu. Sadakhazikike m'zoona, chifukwa mwa iye mulibe zoona. Kunena bodza ndiye khalidwe lake, pakuti ngwabodza, nkukhalanso chimake cha mabodza onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:18-19

“Ngati anthu odalira zapansipano adana nanu, kumbukirani kuti adadana ndi Ine asanadane nanu.

Mukadakhala a mkhalidwe wao, akadakukondani chifukwa cha kukhala anzao. Koma amadana nanu, chifukwa Ine ndidakusankhani pakati pa iwo, motero sindinu anzao.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 15:23-25

Munthu wodana ndi Ine, amadana ndi Atate anganso.

Ndikadapanda kuchita pakati pao zimene wina aliyense sadazichite, sibwenzi atakhala ndi mlandu. Koma tsopano adaziwonadi, komabe akudana nane ndiponso ndi Atate anga.

Koma zatere kuti zipherezere zimene zidalembedwa m'buku lao la Malamulo kuti, ‘Adadana nane popanda chifukwa.’

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 17:14

Ndaŵaphunzitsa mau anu. Anthu odalira zapansipano amadana nawo, chifukwa iwo sali anzao, monga Inenso sindili mnzao.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:30

amasinjirira, ndipo amadana ndi Mulungu. Ndi achipongwe, odzikuza, ndi onyada. Amafunafuna njira zatsopano zochitira zoipa, samvera makolo ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:7

Anthu oika mtima pa khalidwe lokonda zoipa, amadana ndi Mulungu. Anthu otere sagonjera Malamulo a Mulungu, ndipo kunena zoona, sangathedi kuŵagonjera.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:9

Chikondi chizikhala chopanda chiphamaso. Muzidana ndi zoipa, nkumaika mtima pa kuchita zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:17-19

Munthu akakuchitani choipa, musamubwezere choipa. Yesani kuchita zimene anthu onse amaziwona kuti nzabwino.

Ngati nkotheka, khalani ndi mtendere ndi anthu onse, monga momwe mungathere.

Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:10

Ngati munthu akonda mnzake, sangamchite choipa ai. Nchifukwa chake amene amakonda mnzake, wasunga zonse zimene Malamulo a Mulungu akunena.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:4-5

Chikondi ncholeza mtima ndiponso nchofatsa. Chikondi chilibe kaduka, ndipo sichidzitamanda kapena kudzikuza.

Chikondi chilibe matama kapena chipongwe, sichidzikonda, sichikwiya, sichisunga mangaŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 4:16

Monga ndasanduka mdani wanu popeza kuti ndakuuzani zoona?

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:19-21

Zochita za khalidwe lokonda zoipa zimaonekera poyera. Ndi izi: Dama, kuchita zonyansa, kusadziletsa,

Ndiye mvetsani, ine Paulo ndikukuuzani kuti mukalola kukuumbalani, Khristu simupindula nayenso konse ai.

kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko,

dumbo, kuledzera, kudakwa pa maphwando achipembedzo, ndi zina zotere. Ndikukuchenjezani tsopano, monga ndidaachitanso kale, kuti anthu amene amachita zotere, sadzalandirako Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:26-27

Inde mwina nkupsa mtima, koma musachimwe, ndipo musalole kuti dzuŵa likuloŵereni muli chikwiyire.

Musampatse mpata Satana woti akugwetseni.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:31

Muchotseretu pakati panu kuzondana, kukalipa, ndiponso kupsa mtima. Musachitenso chiwawa, kapena kulankhula mau achipongwe, tayani kuipa konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:11

Musayanjane nawo anthu ochita zopanda pake za mdima, koma muŵatsutse.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:15

Alipodi ena amene amalalika Khristu chifukwa cha kaduka ndi kukonda mikangano. Koma aliponso ena amene amamlalika ndi mtima woona.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:3

Musamachita kanthu ndi mtima wodzikonda, kapena wodzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa, ndipo aliyense aziwona anzake kuti ngomuposa iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:8

Koma tsopano musachitenso zonsezi, monga kukalipa, kukwiya, kuipa mtima, ndi mijedu. Pakamwa panu pasamatulukenso mau otukwana kapena onyansa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:15

Onetsetsani kuti wina aliyense mnzake akamchita choipa, asabwezere choipacho. Koma nthaŵi zonse muziyesetsa kuchitira zabwino anzanu ndi anthu ena onse.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 1:6-8

Paja Mulungu mwa chilungamo chake, adzaŵalanga ndi masautso anthu amene amakusautsani inu.

Koma inu amene mukusauka tsopano, adzakupatsani mpumulo pamodzi ndi ife tomwe. Adzachita zimenezi, Ambuye Yesu akadzabwera kuchokera Kumwamba pamodzi ndi angelo ake amphamvu.

Adzabwera ndi moto woyaka, nadzalanga anthu amene sadziŵa Mulungu, ndi amene sadamvere Uthenga Wabwino wa Ambuye athu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:3

Adzakhala opanda chifundo, osapepeseka, ndi osinjirira anzao. Adzakhala osadzigwira, aukali, odana ndi zabwino,

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 3:3

Pajatu kale ifenso tinali opusa, osamvera, ndi osokezedwa. Tinali akapolo a zilakolako zoipa ndi zisangalatso zamitundumitundu. Masiku onse tinkakhalira kuchita zoipa ndi kaduka, anthu kudana nafe, ndipo ife tomwe kumadana.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 1:9

Mudakonda chilungamo nkudana ndi zosalungama. Nchifukwa chake Ine, Mulungu wanu, ndakukwezani nkukudzozani ndi mafuta osonyeza chimwemwe, kupambana anzanu ena onse.”

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:26-27

Pakuti tikamachimwirachimwira mwadala, kwina tikudziŵa choona, palibenso nsembe ina iliyonse ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.

Pamenepo chotitsalira si china ai, koma kumangodikira ndi mantha chiweruzo, ndiponso moto woopsa umene udzaononga otsutsana ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:14-15

Yesetsani kukhala ndi mtendere ndi anthu onse, ndi kukhala oyera mtima, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe amene adzaona Ambuye popanda kuyera mtimako.

Chenjerani kuti wina aliyense asabwerere m'mbuyo nkutaya madalitso a Mulungu. Chenjerani kuti wina aliyense asakhale ngati muzu woŵaŵa, umene umaphuka nkuvuta ena ambiri ndi ululu wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:19-20

Abale anga okondedwa, gwiritsani mau aŵa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma kulankhula asamafulumira, ndipo kukwiya asamafulumiranso.

Abale anga, muzikondwa ndithu mukamayesedwa ndi mavuto amitundumitundu.

Paja munthu wokwiya safikapo pa chilungamo chimene amafuna Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:1-2

Kodi nkhondo zimachokera kuti? Kukangana pakati panu kumachokera kuti? Kodi suja zimachokera ku zilakolako zanu zathupi, zimene zimachita nkhondo mwa inu?

Mudzichepetse pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

Abale, musamasinjirirana. Wosinjirira mbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo a Mulungu. Koma ukaweruza Malamulo a Mulungu, ndiye kuti sukuchita zimene Malamulowo akunena, ukudziyesa woweruza.

Mulungu yekha ndiye wopanga Malamulo ndiponso woweruza. Ndiyenso wotha kupulumutsa ndi kuwononga. Nanga iwe ndiwe yani kuti uziweruza mnzako?

Onani tsono, inu amene mukuti, “Lero kapena maŵa tipita ku mzinda wakutiwakuti, ndipo tikachitako malonda chaka chimodzi kuti tikaphe ndalama,”

m'menemo inuyo zamaŵa simukuzidziŵa. Kodi moyo wanu ngwotani? Pajatu inu muli ngati utsi chabe, umene umangooneka pa kanthaŵi, posachedwa nkuzimirira.

Kwenikweni muyenera kumanena kuti, “Ambuye akalola, tikakhala ndi moyo, tidzachita chakutichakuti.”

Koma monga zilirimu, mumanyada ndi kudzitama. Kunyada konse kotere nkoipa.

Munthu akadziŵa zabwino zimene ayenera kuchita, napanda kuzichita, ndiye kuti wachimwa.

Mumalakalaka zinthu, koma zimakusoŵani, nchifukwa chake mumapha munthu. Mumasirira zinthu, koma simungathe kuzipeza, nchifukwa chake mumamenyana, nkumachita nkhondo. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:4

Inu anthu osakhulupirikanu, kodi simudziŵa kuti kuchita chibwenzi ndi zapansipano nkudana ndi Mulungu? Choncho munthu wofuna kukhala bwenzi la zapansipano, ameneyo amadzisandutsa mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:1

Nchifukwa chake tayani choipa chonse, kunyenga konse, chiphamaso, kaduka ndi masinjiriro onse.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:9

Anthu okuchitani choipa, osaŵabwezera choipa, okuchitani chipongwe osaŵabwezera chipongwe. Koma inu muziŵadalitsa, pakuti inuyo Mulungu adakuitanirani mkhalidwe wotere, kuti mulandire madalitso ake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:8

Chachikulu nchakuti muzikondana mosafookera, popeza kuti chikondi chimaphimba machimo ochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:13

Motero musadabwe abale, anthu odalira zapansipano akamadana nanu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:7-8

Inu okondedwa, tizikondana, pakuti chikondi nchochokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi, ndi mwana wa Mulungu, ndipo amadziŵa Mulungu.

Koma munthu wopanda chikondi sadziŵa Mulungu, pakuti Mulungu ndiye chikondi chimene.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:20-21

Wina akamanena kuti, “Ndimakonda Mulungu”, komabe nkumadana ndi mbale wake, ndi wonama ameneyo. Pakuti munthu wosakonda mbale wake amene wamuwona, sangathe kukonda Mulungu amene sadamuwone.

Lamulo limene Iye adatipatsa ndi lakuti, wokonda Mulungu azikondanso mbale wake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:3

Paja kukonda Mulungu ndiye kuti kutsata malamulo ake, ndipo malamulo ake si olemetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Yohane 1:6

Chikondi chimene ndikunenachi nchakuti tikhale omvera malamulo a Mulungu. Lamulo limene ndikukulemberanilo, monga mudamva kuyambira pa chiyambi, ndi lakuti moyo wanu uzikhala wachikondi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yuda 1:10

Koma anthu ameneŵa amachita chipongwe zinthu zimene sazidziŵa. Ndipo zinthu zimene amazidziŵa ndi nzeru zachibadwa, zonga za nyama, ndizo zimene zimaŵaononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yuda 1:17-19

Koma inu okondedwa, muzikumbukira mau amene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu adaneneratu.

Paja adakuuzani kuti, “Pa masiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsata zilakolako zao zoipa.”

Anthu ameneŵa ndi oyambitsa mipatuko. Amangotsata zapansipano, ndipo mumtima mwao alibe Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 2:6

Komabe chokomera chanu ndi ichi chakuti, mumadana ndi zochita za Anikolai, zimene inenso ndimadana nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 2:15

Chimodzimodzi inuyo, muli nawonso anthu ena otsata chiphunzitso cha Anikolai.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 12:11

Abale athuwo adamgonjetsa ndi magazi a Mwanawankhosa uja, ndiponso ndi mau amene iwo ankaŵachitira umboni. Iwo adadzipereka kotheratu, kotero kuti sadaope ngakhale kufa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 12:17

Apo chinjokacho chidamupsera mtima kwambiri mai uja, nkungochokapo kuti chikayambane ndi ana ena onse a maiyo, ndiye kuti anthu otsata malamulo a Mulungu ndi kuchitira Yesu umboni. Motero chidakaimirira pambali pa nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 17:16

Tsono nyanga khumi unaona zija, pamodzi ndi chilombo chija, zidzadana naye mkazi wadamayo. Zidzamlanda zake zonse ndi kumsiya maliseche. Zidzadyako mnofu wake, kenaka nkumuponya pa moto kuti apserere.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 18:2

Adafuula mokweza mau ndi kunena kuti, “Wagwa, wagwa Babiloni wotchuka uja! Wasanduka malo okhalamo mizimu yoipa, malo othaŵiramo mizimu yonse yonyansa, malo othaŵiramo mbalame zonse zonyansa ndi zodedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 22:15

Koma ochita zautchisi, zaufiti, zadama, zopha anzao, zopembedza mafano, ndi okonda zabodza nkumazichita, adzakhala kunja kwa mzindawo.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga wachilungamo, ndinu thandizo langa ndi moyo wanga, amene amasunga moyo wanga, amatsitsimutsa mzimu wanga ndi kuchiritsa mtima wanga. Atate Woyera, ndinu nokha amene muli ndi mphamvu yomasula ine ku chidani ndi mkwiyo, chifukwa ndikudziwa kuti mkumbukidwe ndi kuwawa zikundidyetsa pang'onopang'ono. Ndithandizeni kudula maunyolo ndi zomangira za kale, kundilekanitsa ndi maganizo onse a chidani omwe amangobweretsa poizoni wakufa mwa ine kuti ndidziwononge ndekha. Ndikupemphani kuti Mzimu wanu Woyera undipatse mphamvu yosiya chilichonse chomwe chikundilepheretsa kupita patsogolo, kuti ndikhoze kukonzanso ndi kuchiritsa mtima wanga, kuti ndikhulitsa aliyense amene mwanjira ina wandipweteka. Chomwe ndapeza nthawi yonseyi ndi khalidwe loipa, ndikuchotsa anthu omwe amandizungulira. Tsegulani nzeru zanga, ndimvetse choonadi chanu ndi kundiphunzitsa kuyenda molingana ndi mawu anu. Chifukwa zoonadi: "Iye amene akunena kuti ali mumdima, ndipo amadana ndi m'bale wake, ali mumdimabe." Ambuye, kuyambira pano, ndikusiya chidani, mkwiyo, mkumbukidwe ndi kusakhululuka. M'dzina la Yesu. Amen!