Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


MAVESI OKHUDZA CHILENGEDWE

MAVESI OKHUDZA CHILENGEDWE

Mulungu ndiye analenga zonsezi. Dziko, thambo, zonse zomwe zili mmenemu, ndi zake. Iye ndiye anazipanga. Monga mmene Baibulo limanenera pa Ekisodo 20:11, Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zomwe zili mmenemu m’masiku asanu ndi limodzi, ndipo anapumula pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. N’chifukwa chake tsiku la Sabata ndi lopatulika. Zonse zimene Mulungu analenga zinali zangwiro, ndipo tiyenera kumutamanda chifukwa cha zodabwitsa zimene anachita.

Tiyeni tiope Mulungu ndi kumupatsa ulemu, chifukwa nthawi ya chiweruzo chake yafika. Tiyeni tilambire iye amene analenga kumwamba, dziko, nyanja, ndi akasupe a madzi. Tiyeni timupatse Mulungu ulemu wonse. Ukakhala pa gombe, ukayang’ana mitengo, kapena mapiri, kumbukira kuti Mlengi wako ndiye anazipanga zokongola ndi zangwiro. Usaleke kupatsa Mulungu ulemu.




Miyambo 12:10

Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziŵeto zake, koma munthu woipa mtima chifundo chake nchankhwidzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:9

Chauta ndi wabwino kwa onse, amachitira chifundo zamoyo zonse zimene adazilenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:26

Zitatha izo Mulungu adati, “Tiyeni tipange munthu m'chifanizo chathu, adzakhale wonga Ifeyo. Adzalamulire nsomba zam'nyanja, mbalame zamumlengalenga, nyama zoŵeta, ndi zokwaŵa zonse za pa dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:14

Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:26

Onani mbalame zamumlengalenga. Sizifesa kapena kukolola kapena kututira m'nkhokwe ai. Komabe Atate anu akumwamba amazidyetsa. Nanga inu sindinu amtengowapatali kuposa mbalame?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 25:4

Ng'ombe imene ikupuntha tirigu, musaimange pakamwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:23

Uzidziŵe bwino nkhosa zako m'mene ziliri, ndipo usamalire ziŵeto zako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:9

Amapereka chakudya kwa nyama ndi kwa ana a khungubwi pamene akulira chakudya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:5

Bulu wa mdani wako akagwa ndi katundu, usabzole ndi kumsiya, koma umthandize kuti adzuke.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 36:6

Kulungama kwanu kumaonekera ngati mapiri aatali, kuweruza kwanu nkozama ngati nyanja yakuya, Inu Chauta, mumasamalira anthu ndi nyama zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 20:10

Koma tsiku lachisanu ndi chiŵiri ndi la Sabata loperekedwa kwa Chauta, Mulungu wako. Usamagwira ntchito pa tsiku limenelo iweyo, kapena ana ako, kapena antchito ako, kapena zoŵeta zako, kapena mlendo amene amakhala m'mudzi mwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 65:25

Mimbulu ndi anaankhosa zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ng'ombe. Fumbi ndiye lidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa loyera la Ziyoni sipadzakhala chinthu chopweteka kapena choononga,” akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 6:6-8

Pita kwa nyerere, mlesi iwe. Kapenyetsetse makhalidwe ake, ukaphunzireko nzeru. Ilibe ndi mfumu yomwe, ilibe kapitao kapena wolamulira. Komabe imakonzeratu chakudya chake m'malimwe, ndipo imatuta chakudyacho m'masika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:6

“Suja amagulitsa atimba asanu tindalama tiŵiri? Komabe Mulungu saiŵala ndi mmodzi yemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:24

Inu Chauta ntchito zanu nzambiri, zonse mwazipanga mwanzeru, ndipo dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 2:18

Nthaŵi imeneyo ndidzachita chipangano ndi nyama zakuthengo, mbalame zamumlengalenga, ndi zokwaŵa pansi, kuti ziyanjane ndi anthu anga. Tsono ndidzathyola uta, lupanga, ndi zida zina zonse zankhondo, ndipo ndidzazichotsa m'dzikomo, kuti iwo apeze moyo wamtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yona 4:11

Nanga Ine, kodi sindiyenera kuumvera chisoni mzinda waukulu wa Ninive? M'mene mujatu muli anthu opitirira zikwi 120, amene sadziŵa kusiyanitsa kuti zabwino nziti, zoipa nziti, mulinso ziŵeto zochuluka.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 22:6-7

Ngati mupeza chisa cha mbalame mu mtengo kapena pansi, make ali pa mazira, kapena ali ndi tiana take, musaitenge mbalameyo pamodzi ndi tiana take. Tianato mungathe kutenga, koma makeyo mloleni apite, kuti mukakhale ndi moyo wabwino ndi wautali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:12

“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi, koma pa tsiku lachisanu ndi chiŵiri musamagwira ntchito, kuti ng'ombe zanu zipume pamodzi ndi abulu anu omwe, kutinso akapolo anu ndi alendo omwe apezenso mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 2:15

Tsono Chauta adamtenga munthuyo, namukhazika m'munda wa Edeni uja kuti azilima ndi kumausamala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:6

Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwanawankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwanawambuzi, mwanawang'ombe ndi mwanawamkango adzadyera limodzi, mwana wamng'ono nkumaziŵeta zonsezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:7

Ng'ombe zanu ndi nyama za m'dziko mwanu zizidzadya zimene nthaka idzabereka.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 38:41

Kodi khwangwala amampatsa chakudya chake ndani, pamene maunda ake akulirira kwa Mulungu, namadzandira chifukwa chosoŵa chakudya?”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 148:10

Inu nyama zakutchire ndi zoŵeta zonse, inu zinthu zokwaŵa ndi mbalame zouluka!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:11

Koma chaka chachisanu ndi chiŵiri mudzaipumuze mindayo. Anthu osauka a mtundu wanu ndiwo adzadye zomera m'mindamo, ndipo nyama zakuthengo zidzadya zotsala. Muzidzachita chimodzimodzi ndi minda yamphesa ndi yaolivi yomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 14:21

Nyama iliyonse yofa yokha, musadye. Alendo okha amene mumakhala nawo, alekeni adye, kapena mungogulitsa nyamayo kwa alendo ena. Pajatu inu ndinu opatulika a Chauta, Mulungu wanu. Musaphike mwanawankhosa kapena mwanawambuzi mu mkaka wa make.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:10-11

“Popeza kuti nyama iliyonse yam'nkhalango ndi yanga, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku mapiri ochuluka. Mbalame zonse zamumlengalenga, zamoyo zonse zoyenda ku thengo ndi zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:11

Adzasamala nkhosa zake ngati mbusa. Adzasonkhanitsa anaankhosa ndi kuŵakumbatira. Ndipo adzatsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 8:6-8

Mudampatsa ulamuliro pa ntchito za manja anu. Mudamgonjetsera zolengedwa zonse, nkhosa, ng'ombe ndi nyama zakuthengo, mbalame zamumlengalenga, nsomba zam'nyanja, ndi zonse zoyenda pansi pa nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 22:28

Make akakhala ng'ombe kapena nkhosa, musaphe makeyo pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 14:5

Kenaka adaŵafunsa kuti, “Ndani mwa inu, bulu wake kapena ng'ombe yake itagwa m'chitsime pa tsiku la Sabata, sangaitulutse pa Sabata pomwepo?”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:1

Munthu wokonda mwambo amakonda kudziŵa zinthu, koma wodana ndi chidzudzulo ngwopusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 43:20

Nyama zakuthengo zidzandilemekeza, nkhandwe ndi nthiŵatiŵa zidzanditamanda, chifukwa ndidzayendetsa madzi m'chipululu ndipo ndidzayendetsa mitsinje m'dziko louma, kuti ndiŵapatse madzi anthu anga osankhidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:34

Adabwera kwa wovulalayo, nathira mafuta ndi vinyo pa mabala ake, nkuŵamanga. Atatero adamkweza pa bulu wake, nkupita naye ku nyumba ya alendo, namsamalira bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 9:9

Paja timaŵerenga m'Malamulowo kuti, “Usaimange pakamwa ng'ombe pamene ikupuntha tirigu.” Kodi pamene adanena zimenezi, Mulungu adangosamala za ng'ombe zokha?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:8-9

“Sindikudzudzulani chifukwa cha nsembe zanu, popeza kuti mumapereka nsembe zanu zopsereza kwa Ine nthaŵi zonse. Ndithudi, sindilandira ng'ombe kapena mbuzi iliyonse ya m'makola anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 3:19

Zimene zimachitikira anthu, zomwezonso zimachitikira nyama. Monga chinacho chimafa, chinacho chimafanso. Zonsezo zimapuma mpweya umodzimodzi, munthu saposa nyama. Zonsezi nzopandapake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 34:15

Akadzidzi adzamangako zisa zao, nkuikirako mazira, ndi kuswa ana ao namaŵasamala. Adembo adzasonkhana kumeneko aŵiriaŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:11-12

Yesu adaŵayankha kuti, “Ndani mwa inu atakhala ndi nkhosa imodzi, nkhosayo nkugwa m'dzenje pa tsiku la Sabata, angapande kuigwira nkuitulutsa? Nanji munthu, amene amaposa nkhosa kutalitali! Ndiye kutitu Malamulo amalola kuchita zabwino pa tsiku la Sabata.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:27

Zonse zolengedwa zimayang'anira kwa Inu, kuti muzipatse chakudya pa nyengo yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 39:1

“Kodi iwe umaidziŵa nthaŵi imene zinkhoma zimaswera? Kodi udaziwonapo nswala zikubadwa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:11

Imapatsa nyama zonse zakuthengo madzi akumwa, mbidzi zimapherapo ludzu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:8

Amaphimba zakumwamba ndi mitambo, amapatsa nthaka mvula, amameretsa udzu pa magomo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:7

Ng'ombe yaikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ndipo ana ao adzagona pamodzi. Mkango udzadya udzu ngati ng'ombe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:26

anaankhosa adzakupatsa chovala, ndi ubweya wao, ndipo pogulitsa mbuzi udzapeza chogulira munda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 38:39

“Kodi iwe ungathe kuufunira chakudya mkango? Kodi ungathe kuipatsa chakudya misona yake ija,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 21:33-34

“Munthu akasiya dzenje lapululu, kapena akakumba dzenje, koma osaphimbira, tsono ng'ombe kapena bulu nkugweramo, ayenera kulipira chifukwa cha choŵetacho. Alipire ndalama kwa mwini choŵetacho, koma nyamayo atenge ikhale yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 34:14

Ndidzaziŵetera ku mabusa abwino, ndipo zizidzadya msipu wonenepetsa ku mapiri okwera a Israele. Kumeneko zidzapumula ku mabusa abwino amsipu. Zidzapezadi mabusa abwino ku mapiri a Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:15

Maso onse amayang'anira kwa Inu, ndipo mumaŵapatsa chakudya pa nthaŵi yake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 2:19

Chauta adatenga dothi naumba nyama zonse ndi mbalame zonse, nabwera nazo kwa Adamu kuti azitche maina. Mwakuti maina amene Adamu adazitcha, maina ake ndi omwewo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:12

“Ndikadakhala ndi njala sindikadakuuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zam'menemo, ndi zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:8

Munthu wosalankhula umlankhulire ndiwe. Anthu osiyidwa uŵalankhulire pa zoŵayenerera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:24

Onani makwangwala. Safesa, sakolola, alibe nyumba yosungiramo zinthu, kapena nkhokwe, komabe Mulungu amaŵadyetsa. Inu mumazipambana mbalamezo kutali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:16

Mumafumbatula dzanja lanu, ndipo mumapatsa chamoyo chilichonse zofuna zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:28

Adaŵadalitsa poŵauza kuti, “Mubereke ndi kuchulukana, mudzaze dziko lonse lapansi ndi kumalilamulira. Ndakupatsani ulamuliro pa nsomba, mbalame ndi nyama zonse zimene zikukhala pa dziko lapansi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 29:5

Ndidzakutaya ku chipululu, iweyo pamodzi ndi nsomba za m'mitsinje yako. Udzagwera ku thengo popanda wina wokutola kuti aike maliro ako. Ndidzakusandutsa chakudya cha zilombo ndi mbalame.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 11:9

Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena choononga pa phiri lopatulika la Mulungu. Ndipo anthu a pa dziko lonse lapansi adzakhala odzaza ndi nzeru ya kudziŵa Chauta, monga nyanja imadzazira ndi madzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 36:7

Chikondi chanu chosasinthika ndi chamtengowapatali. Nchifukwa chake anthu anu amathaŵira m'munsi mwa mapiko anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 35:11

amenenso amatiphunzitsa kupambana nyama zam'dziko ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zouluka.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:31

Koma amene amakhulupirira Chauta adzalandira mphamvu zatsopano, adzauluka ngati ziwombankhanga. Adzathamanga koma osatopa, adzayenda koma osalefuka konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 84:3

Ngakhale timba amapeza malo okhalapo, nayenso namzeze amamanga chisa chake m'mene amagonekamo ana ake, pafupi ndi maguwa anu, Inu Chauta Wamphamvuzonse, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 8:1

Tsono Mulungu adakumbukira Nowa pamodzi ndi nyama zonse zakuthengo ndi zoŵeta zimene zinali naye m'chombomo. Adalamula mphepo kuti iwombe pa dziko lapansi, pomwepo madzi adayamba kutsika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 22:32-33

Mngelo wa Chauta adamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani wamenya bulu wako chotere katatu? Ndabwera kudzakutsekera njira, chifukwa ulendo wakowu ukundiipira. Bulu wako anandiwona, ndipo anasiya njira katatu konse atandiwona. Akadapanda kusiya njira atandiwona, ndithu ndikadakuphera pomwepo, koma buluyo ndikadamleka kuti akhale moyo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 6:19-20

Ndipo udzatengenso nyama za mtundu uliwonse, yaimuna ndi yaikazi, kuti zisungidwe ndi moyo. Ana aamuna a Mulungu adaona kuti ana aakazi a anthu anali okongola, nayamba kukwatira amene ankaŵakonda. Mbalame za mtundu uliwonse ndi nyama zazikulu ndi zokwaŵa zomwe, zidzaloŵe m'chombo kuti zisungidwe ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 22:4

Bulu wa Mwisraele mnzanu akagona mu mseu, muutseni. Muchitenso chimodzimodzi ndi ng'ombe yake, musailekerere. Mthandizeni mnzanu kuti adzutse choŵetacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 22:30

Mundipatsenso ana oyamba kubadwa a ng'ombe zanu ndi nkhosa zanu. Mwana woyamba kubadwayo adzangokhala ndi mai wake masiku asanu ndi aŵiri, ndipo mudzampereka kwa Ine pa tsiku lachisanu ndi chitatu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:8-9

Amaphimba zakumwamba ndi mitambo, amapatsa nthaka mvula, amameretsa udzu pa magomo. Amapereka chakudya kwa nyama ndi kwa ana a khungubwi pamene akulira chakudya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 11:2-3

“Auzeni Aisraele kuti nyama zimene angathe kudya pakati pa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi izi: “Zonse za miyendo inai, zouluka, nzonyansa kwa inu. Komabe pakati pa zouluka zonse za miyendo inai, mungathe kudya zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira pa dothi. Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse. Koma zamapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inai nzonyansa kwa inu. “Tsono zimenezi mukazikhudza, zidzakuipitsani, ndipo aliyense wozikhudza zitafa, adzakhala woipitsidwa mpaka madzulo. Aliyense akanyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo, achape zovala zake, komabe akhala woipitsidwa mpaka madzulo. Nyama iliyonse yokhala ndi ziboda zogaŵikana, koma mapazi ake osagaŵikana, kapenanso yosabzikula, njonyansa imeneyo kwa inu, ndipo aliyense woikhudza, adzakhala woipitsidwa. Pakati pa nyama zonse za miyendo inai, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo ku mapazi, nzonyansa kwa inu, ndipo aliyense wozikhudza zitafa, adzakhala woipitsidwa mpaka madzulo. Ndipo munthu amene anyamula nyamazi zitafa, achape zovala zake, komabe akhala woipitsidwa mpaka madzulo. Zimenezi nzonyansa kwa inu. “Tsono zokwaŵa zonse zimene zili zonyansa kwa inu ndi izi: likongwe, mbeŵa, ng'azi za mitundu yonse, ‘Nyama zonse zokhala ndi ziboda zogaŵikana, ndi zobzikula, angathe kudya zimenezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 22:1

Mukaona ng'ombe kapena nkhosa ya Mwisraele mnzanu ikusokera, musailekerere. Itengeni, mukampatse mwiniwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:24-25

Pali zinthu zinai zing'onozing'ono pa dziko lapansi, koma ndi zochenjera kwambiri: Nyerere zili ngati anthu opanda nyonga, komabe zimakonzeratu chakudya chake m'chilimwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 17:4

Uzikamwa mumtsinjemo, ndipo ndalamula makwangwala kuti azikakudyetsa kumeneko.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 7:2-3

Tsono tenga magulu asanu ndi aŵiri a nyama, ziŵiriziŵiri, yaimuna ndi yaikazi, zimene amaperekera nsembe, ndipo utengenso nyama ziŵiriziŵiri, yaimuna ndi yaikazi, zosaperekera nsembe. Tsono adakwererakwerera ndithu mpaka kubzola nsonga za mapiriwo mamita asanu ndi aŵiri. Zamoyo zonse zokhala pa dziko lapansi zidafa, monga mbalame, zoŵeta, nyama zakuthengo, mtindiri wa tizilombo tosiyanasiyana, ndi anthu onse. Zamoyo zonse za pa dziko lapansi zidafa. Chauta adaononga zamoyo zonse za pa dziko: anthu, nyama, zokwaŵa ndi mbalame. Nowa yekha adapulumuka pamodzi ndi onse amene anali naye m'chombomo. Madziwo adakhala osaphwa konse pa dziko lapansi masiku 150. Utengekonso mbalame ziŵiriziŵiri za mtundu uliwonse, magulu asanu ndi aŵiri. Uchite zimenezi pofuna kuti nyama ndi mbalame za mitundu yonse zisungidwe ndi moyo, ndipo kuti zidzaswanenso pa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 13:12

muzidzapereka kwa Chauta chilichonse choyamba kubadwa. Zoŵeta zanu zamphongo zoyamba kubadwa nza Chauta zimenezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 5:14

Koma tsiku lachisanu ndi chiŵiri ndi la Sabata la Chauta, Mulungu wako. Pa tsiku limenelo, usagwire ntchito iliyonse iweyo, mwana wako wamwamuna, mwana wako wamkazi, wantchito wako wamwamuna, mdzakazi wako, ng'ombe yako, bulu wako, kaya choŵeta chako chilichonse, ngakhale mlendo wokhala m'mudzi mwako. Motero atumiki ako aamuna ndi aakazi azipumanso monga iwe wemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 2:7

ndipo adabala mwana wake wachisamba wamwamuna. Adamkulunga m'nsalu namgoneka m'chodyera cha zoŵeta, chifukwa adaasoŵa malo m'nyumba ya alendo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 22:10

Musamange ng'ombe ndi bulu kuti zilimire pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 8:4-8

ndimadzifunsa kuti, “Kodi munthu nchiyani kuti muzimkumbukira, mwana wa munthu nchiyani kuti muzimsamalira?” Ndiyetu mudamlenga mochepera pang'ono kwa Mulungu amene, mudampatsa ulemerero ndi ulemu wachifumu. Mudampatsa ulamuliro pa ntchito za manja anu. Mudamgonjetsera zolengedwa zonse, nkhosa, ng'ombe ndi nyama zakuthengo, mbalame zamumlengalenga, nsomba zam'nyanja, ndi zonse zoyenda pansi pa nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 9:3-4

Tsopano mungathe kudya nyama zonse, monga ndidakulolani kudya ndiwo zamasamba. Ndakupatsani zonsezi kuti zikhale chakudya chanu. Koma pali chinthu chimodzi chokha chimene simuyenera kudya, ndicho nyama imene ikali ndi magazi. Ndaletsa poti magaziwo ndiwo moyo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:9

Chauta amapha ludzu la munthu womva ludzu, amamudyetsa zinthu zabwino munthu womva njala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 39:19-25

“Kodi ndiwe amene umapatsa mphamvu kavalo? Nanga ndiwe amene umaveka chenjerere m'khosi mwake? Kodi ungathe kuŵerenga miyezi imene zimakhala ndi bele? Kodi nthaŵi imene nyamazi zimaswa iwe umaidziŵa? Kodi ndiwe amene umamlumphitsa ngati dzombe? Kavalo akamadzuma, mpweya wake ndi waukali ndiponso woopsa. Kavaloyo amalumphalumpha m'chigwa, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse. Sachita mantha, sachita nkhaŵa, ndipo sabwerera m'mbuyo akaona lupanga. Zida zankhondo za wokwerapo wake zimachita kwichikwichi m'phodo, ndipo mkondo ndi nthungo zimanyezemira pa dzuŵa. Akavalowo amanjenjemera ndi ukali nathamangira kutsogolo, ndipo akangomva lipenga sangathe kuima. Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali. Amamva kufuula kwa atsogoleri ankhondo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 19:19

“Muzitsata malamulo anga. Musalole kuti ng'ombe zanu zikwerane ndi zoŵeta za mtundu wina. Musafese mbeu za mitundu iŵiri m'munda mwanu, ndipo musavale chovala chopangidwa ndi nsalu za mitundu iŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:29-31

Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya. Pali zinthu zinai zimene zimayenda monyadira: Sindidaphunzire nzeru, ndipo Woyera uja sindimdziŵa. Mkango umene uli ndi mphamvu kupambana nyama zonse, ndipo suthaŵa kanthu kalikonse. Tambala woyenda chinyachinya, ndi tonde, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 3:21

Kodi ndani angatsimikize kuti mzimu wa munthu ndiwo umakwera kumwamba, koma mpweya wa nyama umatsikira kunsi kwa nthaka?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 1:24

Ndipo Mulungu adati, “Padziko pakhale mitundu yonse ya zamoyo potsata mitundu yake: zoŵeta, zokwaŵa, ndi nyama zakuthengo, potsata mitundu yake.” Ndipo zidachitikadi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 17:14

“Pajatu moyo wa cholengedwa chilichonse uli m'magazi mwake. Nchifukwa chake ndaŵauza Aisraele kuti, ‘Musadye magazi a cholengedwa chilichonse, pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli m'magazi mwakemo. Aliyense wodya magazi adzachotsedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:3

“Koma pali ena amene amangochita zoŵakomera. Kwa iwo nchimodzimodzi kupereka ng'ombe yamphongo ngati nsembe kapena kupha munthu, kupha mwanawankhosa kuti aperekere nsembe kapena kupha galu, kupereka chopereka cha chakudya kapena kupereka magazi a nkhumba, kupereka lubani ku nsembe yachikumbutso kapena kupembedza fano. Anthu ameneŵa mtima wao umakondwera nazo zonyansa zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 12:7

“Koma ufunse kwa nyama zakuthengo, zidzakuphunzitsa. Ufunse mbalame zamumlengalenga, zidzakuuza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:17

Chauta ndi wolungama m'zochita zake zonse, ndi wachifundo pa zonse zimene achita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:14-15

Mumameretsa udzu kuti ng'ombe zidye, ndi zomera kuti munthu azilima ndi kupeza chakudya m'nthaka. Amapezamo vinyo wosangalatsa mtima wake, mafuta odzola kuti thupi lake lisisire, ndiponso buledi kuti ampatse mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 65:17

Chauta akunena kuti, “Ndikulenga thambo lam'mwamba latsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zakale sadzazikumbukiranso, zidzaiŵalika kotheratu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 39:13-18

“Nthiŵatiŵa ikukupiza mapiko ake monyadira, koma nthenga zake ndi mapiko ake sizikuithandiza kuuluka monga amachitira kakoŵa. Nthiŵatiŵa imafotsera mazira ake pansi, kuti afundidwe m'nthaka. Koma imaiŵala kuti mapazi ake omwe angathe kuphwanya mazirawo, ndipo kuti nyama zakuthengo nkuŵapondereza. Nthiŵatiŵa imachita ana ake nkhalwe ngati si ake. Zakuti idaavutika poŵabereka imaiŵalako. Paja Mulungu adaimana nzeru, kotero kuti simvetsa kanthu kalikonse. Komabe nthiŵatiŵayo ikadzambatuka nkuyamba kuthaŵa, imamsiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:12

Mbalame zimamanga zisa pafupi ndi mitsinjeyo, zimaimba m'nthambi za mitengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 63:14

Mzimu wa Chauta udaŵapumitsa, monga m'mene ng'ombe zimapumulira ku dambo.” Motero Inu Chauta mudatsogolera anthu anu, kuti dzina lanu lilemekezeke.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse, ulemerero ndi ulemu zikhale kwa Inu! Inu Atate wabwino, Mlengi wa thambo ndi dziko lapansi. Ndikuthokoza kuchokera pansi pa mtima chifukwa cha chilengedwe, zikomo chifukwa chotipatsa chakudya patebulo lathu. Ikani mumtima mwanga chikondi ndi chisamaliro cha dziko lomwe munandipatsa, mundiphunzitse kusamalira chilengedwe chanu. Ndithandizeni kuyamikira ndi kulemekeza miyoyo ya nyama ndi nkhalango. Mawu anu amati: “Thambo ndi lanu, dziko lapansi ndi lanunso; dziko lonse ndi zonse zili mmenemo, inu munalizika.” Tisagwiritse ntchito molakwitsa chilengedwe. Ndikupemphani kuti mundipatse mphamvu zolamulira nyama ndi kusamalira chilengedwe chanu chifukwa ndidzayankha mlandu wake. Ndikupempherera anthu ogwira ntchito yoteteza nyama ndi zomera, amene amateteza zokongola zachilengedwe, mitundu ya nyama yomwe ikutha, ndi amene akugwira ntchito yochepetsa kuipitsidwa kwa dziko. Ndikupempheraninso kuti anthu onse azisangalala ndi chilengedwe ndi zinthu zomwe chimatipatsa mwanzeru ndi modziletsa. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa