Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


114 Mauvesi a M’Baibulo Ponena za Kupanduka

114 Mauvesi a M’Baibulo Ponena za Kupanduka

Ndikufuna ndikuuzeni nkhani yofunika kwambiri. Munthu akamakana kumvera ndi kutsata malamulo, zimenezo zimatchedwa kupanduka. Zimaonetsa mtima wosasamala, wonyoza, komanso wopanda chifundo. Ambiri amene amachita zinthu monyadira, mwadyera, komanso osamvera akuluakulu awo, ali ndi mzimu wopanduka, womwe Mulungu sawukonda.

Ngati umati ndiwe mwana wa Atate Wathu wakumwamba, koma ukuchita zinthu zopanduka, suli paubwenzi wabwino ndi Mzimu Woyera. M'malo mwake, mizimu yoipa ndiyo ikukutsogolera. Kupanduka ndi chifukwa chachikulu chomwe anthu ambiri amathawa Mulungu. Amakana kulandira uphungu ndi kutsata malamulo ake, m'malo mwake amasankha kutsata zilakolako zawo ndi maganizo awo, akuchimwira Mulungu Wamphamvuyonse.

Wopanduka amadziona ngati wanzeru, koma sakudziwa kuti akulowera m'mavuto, kutanthauza chilango chosatha ku gehena. Buku la Deuteronomo 1:43-45 limati: "Ndinakuuzani, koma simunamvere; munapandukira lamulo la Yehova, ndipo monyadira munakwera phiri. Koma Aamori amene anakhala m’phirilo anatuluka kukakumana nanu, anakulondolani monga momwe njuchi zimachitira, ndipo anakugonjetsani ku Seiri, kufikira ku Horima. Pamenepo munabwerera ndi kulira pamaso pa Yehova, koma iye sanamvere mawu anu, kapena kukuyang’anirani.”

Kumbukirani kuti Yesu sakonda anthu opanduka. Amakukondani ndipo akufuna kukupulumutsani, koma sakonda kuti simukulapa machimo anu. Mukadali ndi nthawi yopeza chifundo cha Mulungu. Ingotsegula mtima wanu, dzichepetse pamaso pa Ambuye, pemphani chikhululukiro, ndi kuvomereza zolakwa zanu modzichepetsa. Musamadzilungamitse, ndipo landirani chilango chimene mukuyenera kuti musinthe mkati mwanu.

Yandikirani Mzimu Woyera, muuzeni kuti mukumufuna, ndipo musamakhale popanda chikondi chake changwiro. Mukatero, mudzapeza chisomo pamaso pa Mulungu ndi anthu. Pemphani chikhululukiro kwa akuluakulu anu ndi kuyambiranso moyo watsopano.




Masalimo 68:23

kuti musambe mapazi anu m'magazi, kuti agalu anu anyambiteko magazi a adaniwo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:1-2

Munthu aliyense azimvera akulu olamulira, chifukwa palibe ulamuliro umene sudachokere kwa Mulungu. Ndipo olamulira amene alipo, adaŵaika ndi Mulungu. Ngati munthu akonda mnzake, sangamchite choipa ai. Nchifukwa chake amene amakonda mnzake, wasunga zonse zimene Malamulo a Mulungu akunena. Muchite zimenezi chifukwa mukudziŵa kuti yafika kale nthaŵi yakuti mudzuke kutulo. Pakuti chipulumutso chili pafupi tsopano kuposa pamene tidayamba kukhulupirira. Usiku uli pafupi kutha, ndipo mbandakucha wayandikira. Tiyeni tsono tileke ntchito za mdima, tivale zida zomenyera nkhondo kutayera. Mayendedwe athu akhale oyenera, ngati a anthu oyenda usana. Pasakhale dyera kapena kuledzera, dama kapena zonyansa, ndeu kapena nsanje. Ambuye Yesu Khristu mwini akhale chida chanu chankhondo. Lekani mtima wofunafuna zosangalatsa thupi, musagonjere zilakolako zake zoipa. Motero munthu wokana kumvera olamulira, akukana dongosolo limene adaliika Mulungu. Ndipo ochita zimenezi, adzadzitengera okha chilango.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:12-13

Abale, mchenjere, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woipa ndi wosakhulupirira, womlekanitsa ndi Mulungu wamoyo. Kwenikweni muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku ikadalipo nthaŵi, imene m'mau a Mulungu imatchedwa kuti, “Lero”. Muzichita zimenezi, kuwopa kuti wina aliyense mwa inu angaumitsidwe mtima ndi chinyengo cha uchimo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:1

Chauta akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira Ine! Amachita zodzikonzera okha osati zokonza Ine. Amachita chipangano chaochao, chosatsata chifuniro changa, ndipo amanka nachimwirachimwira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-21

Zochita za khalidwe lokonda zoipa zimaonekera poyera. Ndi izi: Dama, kuchita zonyansa, kusadziletsa, Ndiye mvetsani, ine Paulo ndikukuuzani kuti mukalola kukuumbalani, Khristu simupindula nayenso konse ai. kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko, dumbo, kuledzera, kudakwa pa maphwando achipembedzo, ndi zina zotere. Ndikukuchenjezani tsopano, monga ndidaachitanso kale, kuti anthu amene amachita zotere, sadzalandirako Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:8

Asakhale ngati makolo ao, anthu oukira ndi osamvera aja, mbadwo wa anthu amene mitima yao inali yosakhazikika, amene moyo wao unali wosakhulupirika kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 2:3-4

Adandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, ndikukutuma kwa Israele, mtundu wa anthu aupandu amene andipandukira. Iwowo ndi makolo ao akhala akundichimwira mpaka lero lino. Anthu ake ndi okanika ndiponso achipongwe. Ndikukutuma kuti ukanene zimene Ine Ambuye Chauta ndikuŵauza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:118

Inu mumaŵakana anthu onse osamvera malamulo anu, zoonadi, kuchenjera kwao nkopandapake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:30

“Munthu wosavomerezana ndi Ine, ndiye kuti ndi wotsutsana nane. Ndipo wosandithandiza kusonkhanitsa, ndiye kuti ameneyo ndi womwaza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 34:37

Pa tchimo lao aonjezerapo upandu, akunyadira zochita zao, ndipo akuchulukitsa mau onyoza Mulungu ife tilikumva.” Mulungu amasamalira zochitika pa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:5-6

Komabe ambirimbiri mwa iwo Mulungu sadakondwere nawo, kotero kuti adafera m'chipululu. Tsono zimene zidachitikazi ndi zitsanzo zotichenjeza ife, kuti tisamasirira zoipa monga adaachitira iwowo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 2:19

Mudzalangidwa ndi machimo anu omwe: poti mwandikana, ndidzakuimbani mlandu. Muganizire bwino za kuipa kwake kwa kundisiya Ine, Chauta, Mulungu wanu. Mulingalire kuŵaŵa kwake kwa kukhala osandiwopa,” akuterotu Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 8:5

Chifukwa chiyani nanga anthu ameneŵa akupitirirabe kulakwa, osabwereranso? Akangamira ndithu machimo ao, akukana kubwerera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:23

Nchifukwa chake adaŵauza kuti akadaŵaononga, pakadapanda Mose wosankhidwa wake kuima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usaŵaononge.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:1

Munthu wochita liwuma kwina atamdzudzula, adzaonongeka mwadzidzidzi osachiranso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:15

Paja Malembo akuti, “Lero lino mukamva mau a Mulungu, musaumitse mitima yanu monga muja zidaachitikira poukira Mulungu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 31:6

Inu Aisraele, bwererani kwa Iye amene mudampandukira kwakukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 24:13

“Pali ena amene amakana kuŵala, safuna kuyenda m'kuŵalako, ndipo sadziŵa njira zake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 9:23

Ndipo Chauta atakutumani kuchokera ku Kadesi-Baranea kuti mupite kukalandira dziko limene adakupatsanilo, inu mudakana malamulo a Chauta, Mulungu wanu, ndipo simudamkhulupirire kapena kumumvera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:2-3

Chauta adati, “Tamvera, iwe mlengalenga, tchera khutu, iwe dziko lapansi, Ine Chauta ndikulankhula. Ndidabereka ana ndi kuŵalera, koma andigalukira. Koma mukakana ndi kumapanduka, mudzaphedwa ndi lupanga. Ine Chauta ndatero.” Taonanitu! Mzinda umene kale udaali wokhulupirika ndi wachilungamo, tsopano ukuchita zadama. Mzinda umene kale udaali ndi anthu aungwiro, tsopano wadzaza ndi anthu opha anzao. Iwe Yerusalemu, unali ngati siliva, koma tsopano wasanduka wopandapake. Unali ngati vinyo wabwino, koma tsopano uli ngati vinyo wosakanizika ndi madzi. Atsogoleri ako apanduka, ndipo amagwirizana ndi mbala. Aliyense amakonda chiphuphu, ndipo amathamangira mphatso. Satchinjiriza ana amasiye, ndipo samvera madandaulo a akazi amasiye. Nchifukwa chake Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse, Wamphamvu uja wa Israele, akunena kuti: “Ha! Olimbana nane ndidzaŵatha, adani anga ndidzaŵalipsira. Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe. Ndidzasungunula machimo ako nkuŵachotsa, monga m'mene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala. Aweruzi ako ndidzaŵakhazikitsanso ngati pa masiku akale aja. Aphungu akonso ndidzaŵakhazikitsanso ngati poyamba paja. Pambuyo pake iweyo udzatchedwa mzinda waungwiro, mzinda wokhulupirika.” Chauta ndi wolungama, adzaombola Ziyoni. Chauta ndi waungwiro, adzaombolanso anthu olapa amumzindamo. Koma opanduka ndi ochimwa adzaŵaonongera pamodzi, osiya Chauta adzatheratu. Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani, mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene mudaipatula. Ng'ombe imadziŵa mwini wake, bulu amadziŵa kumene mwini wake amamdyetsera, koma Aisraele sadziŵa, anthu anga samvetsa konse.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 21:28-31

“Kodi inu, mukuganiza bwanji? Munthu wina anali ndi ana aamuna aŵiri. Adapita kwa woyamba, nakamuuza kuti, ‘Mwana wanga, pita ukagwire ntchito m'munda wamphesa lero.’ Iyeyo adati, ‘Toto ine.’ Koma pambuyo pake adasintha maganizo, napitadi. Wina akakakufunsani kanthu, inu mukati, ‘Ambuye ali nawo ntchito, akangothana nawo aŵatumiza nthaŵi yomweyo.’ ” Bambo uja adapita kwa mwana wina uja, nakamuuza mau omwe aja. Iyeyo adati, ‘Chabwino atate,’ koma sadapite. Kodi mwa aŵiriwo, yemwe adachita zimene bambo wake ankafuna ndi uti?” Iwo adati, “Woyamba uja.” Yesu adaŵauza kuti, “Ndithu ndikunenetsa kuti okhometsa msonkho ndi akazi adama akuloŵa mu Ufumu wa Mulungu inu nkumakusiyani m'mbuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 7:11

“Koma iwowo adakana kumvera, adandifulatira ndi mtima wokanika. Adatseka makutu ao kuti asamve.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:25

Chenjerani tsono kuti musakane kumvera amene akulankhula nanu. Anthu amene adakana kumvera iye uja amene adaaŵachenjeza pansi pano, sadapulumuke ku chilango ai. Nanji tsono ifeyo, tidzapulumuka bwanji ngati timufulatira wotilankhula kuchokera Kumwambaku?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:21-22

Inde ankamudziŵa Mulungu, koma m'malo mwa kumtamanda kapena kumthokoza, maganizo ao adasanduka opanda pake, ndipo m'mitima yao yopusa mudadzaza mdima. Iwo amadziyesa anzeru, koma chikhalirecho ndi opusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:13-14

Chifukwa cha Ambuye, muzimvera akulu onse olandira ulamuliro. Ngati ndi mfumu yaikulu koposa ija, imvereni chifukwa ili ndi ulamuliro pa mafumu ena onse. Ngati ndi nduna, zimvereni chifukwa zidachita kutumidwa ndi mfumu kuti zizilanga ochita zoipa ndi kuyamikira ochita zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:16

Koma Chauta amaŵakwiyira anthu ochita zoipa, anthuwo sadzakumbukikanso pansi pano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:1

Woipa mtima amangodzithaŵira popanda wina wompirikitsa, koma wochita zabwino amalimba mtima ngati mkango.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 11:4-6

Ndipo adati, “Tsopano tiyeni timange mzinda wathu, ndipo nsanja yake italike mpaka kukafika kumwamba. Tikatero tidzatchuka ndithu, ndipo sitidzamwazikanso pa dziko lapansi.” Tsono Chauta adatsika kudzaona mzindawo, pamodzi ndi nsanja imene anthu ankamanga. Ndipo adati, “Tsopano anthu onseŵa ndi amodzi, ndipo akulankhula chilankhulo chimodzi. Zinthu akuchitazi ndi chiyambi chabe cha zimene adzachite. Kenaka iwoŵa adzachita chilichonse chimene afuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:7

Tsono muzigonjera Mulungu. Satana muzilimbana naye, ndipo adzakuthaŵani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:3

Kupusa kwake kwa munthu kukamgwetsa m'chiwonongeko, mtima wake umadzakwiyira Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:37

Mtima wao sunali wokhulupirika kwa Iye. Sadasunge chipangano chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:24

“Akamachoka, adzaona mitembo ya anthu amene adandipandukira. Mphutsi zimene zidzaŵadya sizidzafa, ndipo moto umene udzaŵatentha sudzazima. Anthu a mitundu yonse poŵaona adzanyansidwa nawo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:113

Ndimadana nawo anthu apaŵiripaŵiri, koma ndimakonda mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:10-12

Ngodala anthu ozunzidwa chifukwa cha kuchita chilungamo, pakuti Ufumu wakumwamba ndi wao. “Ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani ndi kukunyengezerani zoipa zamitundumitundu chifukwa cha Ine. Sangalalani, kondwerani, chifukwa mphotho yanu ndi yaikulu Kumwamba. Paja ndi m'menenso anthu ankazunzira aneneri amene analipo kale inu musanabadwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 53:6

Tonse tidaasokera ngati nkhosa. Aliyense mwa ife ankangodziyendera. Ndipo Chauta adamsenzetsa iyeyo machimo athu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:11

pakuti adaatsutsa mau a Mulungu, adaakana monyoza malangizo a Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:4

Wolamula akakukwiyira, usachoke pa ntchito yako, pakuti kufatsa kumakonza ngakhale zolakwa zazikulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:17

Nsembe imene Inu Mulungu mumailandira, ndi mtima wotswanyika. Mtima wachisoni ndi wolapa, Inu Mulungu simudzaunyoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 59:12

Akodwe ndi kunyada kwao, chifukwa cha uchimo wa m'kamwa mwao, ndi mau a pakamwa pao. Chifukwa chakuti amatemberera ndipo amanama,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 7:14

ndipo anthu anga amene amatchedwa dzina langa akadzichepetsa, napemphera, ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zao zoipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwambako. Choncho ndidzaŵakhululukira zoipa zao ndi kupulumutsa dziko lao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:10

Kusiyana kwake pakati pa ana a Mulungu ndi ana a Satana kumaoneka motere: aliyense wosachita chilungamo, ndiponso wosakonda mnzake, sali mwana wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:8-9

Musaumitse mitima yanu monga ku Meriba kuja, monganso tsiku lija ku Masa m'chipululu muja, pamene makolo anu adandiputa mondiyesa ngakhale anali ataona ntchito zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:16

Mukudziŵa paja kuti mukadzipereka kuti mukhale akapolo a munthu nkumamumvera, ndiye kuti ndinu akapolo a munthu womumverayo. Tsono ngati ndinu akapolo a uchimo, mudzafa. Koma ngati ndinu akapolo a Mulungu, mudzakhala olungama pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 11:28

Koma matemberero kwa inu, mukapanda kumvera malamulo ameneŵa, nkusiya njira imene ndikukulamulani lero, kuti mutembenukire kwa milungu ina ndi kumaipembedza, milungu imene nkale lonse simudaipembedzepo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 65:2

Nthaŵi zonse ndakhala wokonzeka kuŵalandira mwaufulu anthu ondipandukiraŵa, amene amachita zoipa namatsata njira zao chifukwa cha kuuma mitu kwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:104

Ndimakhala ndi nzeru za kumvetsa chifukwa cha malamulo anu. Nchifukwa chake ndimadana ndi njira iliyonse yonyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:7

Musadzinyenge, nkosatheka kupusitsa Mulungu. Zimene munthu amabzala, adzakolola zomwezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:21-22

Mwana wanga, uziwopa Chauta ndiponso mfumu, usagwirizane ndi anthu okonda kuŵachitira mwano. Ameneŵa amatha kugwetsa tsoka mwadzidzidzi, ndani angadziŵe kuwopsa kwa chiwonongeko chochokera kwa aŵiriŵa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 58:3

Anthu oipa ndi osokera kuyambira ali m'mimba mwa mai ao, anthu amabodza ndi otayika kuyambira tsiku la kubadwa kwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:155

Chipulumutso chili kutali ndi anthu oipa, pakuti safunafuna malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 5:23

Koma anthu ameneŵa ndi okanika ndiponso a mtima waupandu. Adapatuka ndipo adapitiratu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:14-15

Koma munthu aliyense amayesedwa ndi zinyengo pamene chilakolako cha mwiniwakeyo chimkopa ndi kumkola. Pamenepo chilakolakocho chimachita ngati chatenga pathupi nkubala uchimo. Tsono uchimowo utakula msinkhu, umabala imfa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:2

Musamatsanzira makhalidwe a anthu odalira zapansipano, koma Mulungu asinthe moyo wanu wonse pakukupatsani mitima yatsopano. Pamenepo mudzatha kudziŵa zimene Mulungu afuna, ndipo mudzazindikira zimene zili zabwino, zangwiro ndi zomkondwetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:15

Chilungamo chikachitika, nzika zabwino zimakondwera, koma zimadederetsa atambwali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 19:13

Musalole kuti ine mtumiki wanu ndizichimwa dala, kulakwa koteroku ndisakutsate. Tsono ndidzakhala wangwiro wopanda mlandu wa uchimo waukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 3:6-7

Tsono mkaziyo adaona kuti mtengowo ndi wokongola, ndiponso kuti zipatso zake zingakhale zokoma kudya. Pompo adayamba kukhumbira kuti adyeko zipatsozo, adzakhale wanzeru. Motero adathyolako zipatso zina za mtengowo, naadya. Tsono zina adapatsako mwamuna wake, ndipo iyenso adadya. Atangodya choncho, adazindikira kuti ali maliseche. Choncho adasoka masamba a mkuyu navala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 82:5

Iwo sadziŵa kanthu ndiponso alibe nzeru, amangoyenda m'chimbulimbuli. Maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 18:30

“Nchifukwa chake Ine Ambuye Chauta ndikuti, Aisraele inu, aliyense mwa inu ndidzamuweruza molingana ndi ntchito zake. Lapani, tembenukani mtima, kuti machimo anu asakuwonongeni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:26-27

Pakuti tikamachimwirachimwira mwadala, kwina tikudziŵa choona, palibenso nsembe ina iliyonse ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo. Pamenepo chotitsalira si china ai, koma kumangodikira ndi mantha chiweruzo, ndiponso moto woopsa umene udzaononga otsutsana ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 48:8

Chikhalire sudamve chikhalire sudadziŵe, nkale lonse makutu ako sanali otsekuka. Chifukwa ndidaadziŵa kuti ndiwe wachiwembu, ndipo kuti chiyambire cha ubwana wako adakutchula waupandu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:21

Simungathe kumwera m'chikho cha Ambuye nkumweranso m'chikho cha Satana. Simungathe kudyera pa tebulo la Ambuye nkudyeranso pa tebulo la Satana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:21

“Si munthu aliyense womangonditi ‘Ambuye, Ambuye’ amene adzaloŵe mu Ufumu wakumwamba ai. Koma adzaloŵe ndi wochita zimene Atate anga akumwamba afuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:14

Adadzilekerera potsata zilakolako zao m'chipululu muja, adayesa Mulungu m'chipululumo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:8

Koma ochita zaupandu, namatsutsa zoona nkumachita zosalungama, Mulungu adzaŵakwiyira ndi kuŵazazira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 57:17

“Ndidaŵakwiyira chifukwa anali okonda chuma dziŵi. Tsono ndidaŵalanga, ndi kuŵafulatira mokwiya. Koma iwowo adakhalabe ouma mitu, ndipo adapitirira kuchita ntchito zao zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 1:19

uli ndi chikhulupiriro ndiponso ndi mtima wopanda kanthu koutsutsa. Ena sadamvere pamene mtima wao unkaŵatsutsa, motero chikhulupiriro chao chidaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 86:14

Inu Mulungu, anthu achipongwe andiwukira. Anthu opanda chifundo akufunafuna moyo wanga ndipo sasamala za Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:15

Kupusa kumakhala mumtima mwa mwana, koma ndodo yomlangira mwanayo idzachotsa kupusako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:16-17

Koma kwa munthu woipa Mulungu amati, “Ukuvutikiranji ndi kutchula malamulo anga? Bwanji pakamwa pako pakulankhula za chipangano changa? Iwe sufuna kulangizidwa, umaponya mau anga ku nkhongo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:16

Chimene ndikufuna kunena ndi ichi: Mulole Mzimu Woyera kuti azikutsogolerani. Mukatero, pamenepo simudzachita zimene khalidwe lanu lokonda zoipa limalakalaka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:115

Chokereni inu, anthu ochita zoipanu, kuti ine ndizitsata malamulo a Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:4

pakuti iyeyo ndi mtumiki wa Mulungu wokutsogolera kuchita zabwino. Koma ngati ukuchita zoipa uwope, pakuti ali ndi mphamvu ndithu zokulanga. Iye ndi mtumiki wa Mulungu wogwetsa mkwiyo wa Mulungu pa wochita zoipa, pomulanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 3:16

Pajatu pamene pali kaduka ndi kudzikonda, pomweponso pali chisokonezo ndi ntchito yoipa ya mtundu uliwonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 59:2

Pulumutseni kwa anthu ochita zoipa, landitseni kwa anthu okhetsa magazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:15

Zimene amachita munthu wopusa mwiniwakeyo amaziyesa zolungama, koma munthu wanzeru amamvetsera malangizo a ena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 15:9

Mdani uja adati, ‘Ndidzaŵalondola nkuŵagwira. Chuma chao ndidzachigaŵagaŵa, ndipo mtima wanga udzakhutira nacho. Ndidzasolola lupanga, ndipo ndidzaŵaononga ndi dzanja langa.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:10-12

Pa nthaŵi imeneyo ambiri adzataya chikhulupiriro chao, azidzaperekana nkumadana. Kudzaoneka aneneri onama ambiri, amene azidzasokeza anthu ambiri. Tsono popeza kuti zoipa zizidzachulukirachulukira, chikondi chizidzacheperachepera pakati pa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 14:1

Mumtima mwake munthu wopusa amati, “Kulibe Mulungu.” Anthu otereŵa ndi oipa, amachita zonyansa, palibe ndi mmodzi yemwe wochita zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 14:12-14

“Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe Nthanda, mwana wa Mbandakucha? Wagwetsedwa pansi bwanji, iwe amene unkagonjetsa mitundu ya anthu? Mumtima mwako unkati, ‘Ndidzakwera mpaka kumwamba. Ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu. Ndidzakhala pampandopo pa phiri la kumpoto kumene imasonkhanako milungu yonse. Ndidzakwera pamwamba pa mitambo, ndidzafanafana naye Wopambanazonse.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 2:3-4

Musalole kuti wina akupusitseni mwa njira iliyonse. Pajatu lisanafike tsikulo, kudzayamba kwachitika zoti anthu ochuluka akupandukira Mulungu, ndipo kudzaoneka Munthu Woipitsitsa uja, woyenera kutayikayu. Ameneyu ndi mdani, ndipo adzadziika pamwamba pa chilichonse chimene anthu amachitcha mulungu kapena amachipembedza, kotero kuti mwiniwakeyo adzadzikhazika m'Nyumba ya Mulungu ndi kudzitcha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:29

Nanji tsono munthu wonyoza Mwana wa Mulungu, munthu woyesa chinthu chachabe magazi achipangano amene adamuyeretsa, munthu wonyoza Mzimu wotipatsa madalitso a Mulungu! Chilango cha munthu wotere chidzakhala choopsa kopambana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:7

Anthu oika mtima pa khalidwe lokonda zoipa, amadana ndi Mulungu. Anthu otere sagonjera Malamulo a Mulungu, ndipo kunena zoona, sangathedi kuŵagonjera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:17

Usachite kunyanyanso kuipa, usanyanye nawonso uchitsiru. Nanga uferenji nthaŵi yako isanakwane?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:20

kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:26

Samvazaanzake nchitsiru, koma wotsata nzeru za ena adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 89:30-32

“Koma ngati ana ake asiya lamulo langa, ndipo satsata malangizo anga, ngati aphwanya malamulo anga, ndipo sasunga malangizo anga, “ndidzaŵalanga ndi ndodo, chifukwa cha zolakwa zao, ndidzaŵakwapula ndi zikoti chifukwa cha machimo ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:20

Nchifukwa chake ndikukuuzani kuti ngati kukhulupirika kwanu sikuposa kukhulupirika kwa aphunzitsi a Malamulo ndi kwa Afarisi, simudzaloŵa konse mu Ufumu wakumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:9

pamene makolo anu adandiputa mondiyesa ngakhale anali ataona ntchito zanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:28-32

Tsono popeza kuti iwo sadalabadireko za kumvera Mulungu, Mulunguyo adaŵasiya m'maganizo ao opusa, kotero kuti amachita zosayenera. Mitima yao idadzaza ndi zosalungama zamitundumitundu, monga kuipa, umbombo ndi dumbo. Amangolingalira za kaduka, za kupha anthu, za ndeu, za kunyenga, ndi za njiru. Amachita ugogodi, Umasimba za Mwana wake, Yesu Ambuye athu. Poyang'anira umunthu wake, kholo lake ndi Davide, amasinjirira, ndipo amadana ndi Mulungu. Ndi achipongwe, odzikuza, ndi onyada. Amafunafuna njira zatsopano zochitira zoipa, samvera makolo ao. Ndi opusa, osakhulupirika, okhakhala moyo, ndi opanda chifundo. Amalidziŵa lamulo la Mulungu lakuti anthu ochita zotere ndi oyenera kufa, komabe iwo omwe amachita zomwezo, ndiponso amavomerezana ndi anthu ena ozichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:21-22

Kodi sindidana nawo anthu odana nanu, Inu Chauta? Kodi sindinyansidwa nawo anthu okuukirani? Ndimadana nawo ndi chidani chenicheni. Ndimaŵayesa adani anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 15:8-9

“ ‘Anthu aŵa amangondilemekeza ndi pakamwa chabe, koma mtima wao uli kutali ndi Ine. Amandipembedza inde, koma kupembedza kwaoko nkopanda phindu, chifukwa zimene amaphunzitsa ngati zophunzitsa zenizeni ndi malamulo a anthu chabe.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 3:19

Motero tikuwona kuti anthuwo sadathe kuloŵa, chifukwa cha kusakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 5:20

Mulungu adapereka Malamulo kuti anthu azindikire kuchuluka kwa machimo ao. Koma pamene uchimo udachuluka, kukoma mtima kwa Mulungu kudachuluka koposa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:1-2

Chauta akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira Ine! Amachita zodzikonzera okha osati zokonza Ine. Amachita chipangano chaochao, chosatsata chifuniro changa, ndipo amanka nachimwirachimwira. Amauza oona zobisika kuti, ‘Musaonenso.’ Amauza aneneri kuti, ‘Musatiloserenso zoona. Mutiwuze zotikomera, mutilosere zam'mutu chabe. Chokani apa, osakhala pa njira. Sitifuna kumvanso za Woyera uja wa Israele.’ ” Nchifukwa chake Woyera uja wa Israele akunena kuti, “Inu mumanyozera zimene ndimakuuzani, mumakhulupirira zopsinja anzanu ndipo mumadalira mabodza. Nchifukwa chake tchimo lanuli lidzakhala ngati mng'ankha pa chipupa chachitali choŵinuka, chimene kugwa kwake nkwadzidzidzi. Zidzakhala ngati kuphwanyika kwa mbiya, imene ili yotekedzekeratu, popanda ndi phale lomwe lopalira moto, kapena lotungira madzi m'chitsime.” Tsono Ambuye Chauta, Woyera uja wa Israele adati, “Ngati mutembenuka ndi kubwerera, mudzapulumuka. Ngati mudzinga ndi kukhulupirira, mudzakhala amphamvu.” Koma inu mudakana kutero. Mudati, “Tidzathamanga pa akavalo.” Chabwino, mudzathaŵe! Mudatinso, “Tidzakwera pa magareta aliŵiro.” Chabwino, koma okuthamangitsani adzakhalanso aliŵiro. Anthu chikwi chimodzi mwa inu adzathaŵa poona mdani mmodzi. Asilikali asanu okha adzakwanira kukuthamangitsani. Otsalira mwa inu adzakhala ngati mtengo wa mbendera wapaphiri, ngati chizindikiro chapagomo. Komabe Chauta akufunitsitsa kuti akukomereni mtima. Ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo, chifukwa Chauta ndi Mulungu wachilungamo. Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye! Ndithudi, inu anthu a ku Ziyoni, okhala ku Yerusalemu, simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu, ndipo akadzangomva, pompo adzakuyankhani. Amapita ku Ejipito kukapempha chithandizo, Ine osandifunsa. Amathaŵira kwa Farao kuti aŵatchinjirize, amakafuna malo opulumukirako ku Ejipito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:4

Inu anthu osakhulupirikanu, kodi simudziŵa kuti kuchita chibwenzi ndi zapansipano nkudana ndi Mulungu? Choncho munthu wofuna kukhala bwenzi la zapansipano, ameneyo amadzisandutsa mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 11:5

Chauta amayesa anthu olungama namakondwera nawo, mtima wake umadana ndi anthu oipa okonda zachiwawa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:5

Munthu aliyense wodzikuza amanyansa Chauta, ndithu ameneyo sadzalephera kulangidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 3:23

popeza kuti onse adachimwa, nalephera kufika ku ulemerero umene Mulungu adaŵakonzera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:20

Onse amene amakonda Chauta, amaŵasunga, koma Chauta adzaononga oipa onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 15:23

Kugalukira kuli ngati tchimo loombeza, kukhala wokanika kuli ngati tchimo lopembedza mafano. Popeza kuti mwakana mau a Chauta, Iyenso wakukanani kuti musakhalenso mfumu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 17:11

Munthu woipa mtima amangofuna zoukira. Tsono adzamtumira wamthenga wankhalwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 68:6

Anthu osiyidwa, Mulungu amaŵapatsa malo okhalamo, am'ndende amaŵatulutsa kuti akhale pa ufulu, koma anthu oukira, amaŵapirikitsira ku nthaka yoguga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 2:2

Mafumu ao akuchita upo, olamula ao akhala pamodzi kuti apangane zoipa, zoukira Chauta ndi mfumu yake yodzozedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 20:24

“Aroni saloŵa nao m'dziko limene ndidapatsa Aisraele. Adzafa, chifukwa choti nonse aŵirinu simudamvere lamulo langa ku madzi a ku Meriba kuja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:7

Iye amalamula ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amalonda mitundu ina ya anthu. Anthu oukira asadzikweze.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 12:14

Mukamaopa Chauta ndi kumamtumikira ndi kumamvera mau ake, osakana malamulo ake, ndiponso ngati nonsenu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Chauta, Mulungu wanu, zonse zidzakuyenderani bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 14:9

Koma musagalukire Chauta. Musaope anthu a m'dzikolo chifukwa tidzaŵaononga. Iwowo alibe oŵatchinjiriza, koma ife Chauta ali nafe, musaŵaope.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 5:10

Asenzetseni tchimo lao, Inu Mulungu. Upo wao woipa uŵagwetse iwo omwe, muŵachotse pamaso panu chifukwa cha zochimwa zao zambirimbiri, chifukwa akuukirani Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 13:5

Koma aphedwe mneneri aliyense kapena womasulira maloto aliyense amene akuuzani kuti muukire Chauta, Mulungu wanu, amene adakutulutsani ku Ejipito ndi kukuwombolani m'dziko laukapolo. Munthu wotero ndi woipa, chifukwa akufuna kukusiyitsani njira imene Chauta akufuna kuti muitsate. Aphedwe, ndipo pakutero mudzachotsa choipa chimenechi pakati panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 28:16

Nchifukwa chake Chauta akunena kuti, ‘Chenjera, ndidzakuchotsa pa dziko lapansi. Ufa chaka chino chisanathe, chifukwa chakuti wakhala ukulalikira zopandukira Chauta.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Maliro 3:42

Ifeyo tachimwa, ndipo tapanduka, tsono Inu simudakhululuke.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu, ndinu nokha woyenera ulemerero, ulemu, chitamando ndi kulambira. Ndikubwera kwa inu kudzera mwa Ambuye wathu Yesu Khristu kukuthokozani chifukwa cha kukhulupirika kwanu, chikondi chanu ndi kundikhululukira nthawi zonse ndikalakwitsa. Ndimakukhulupirirani Ambuye wanga ndipo ndikudziwa kuti munditeteza ku choipa, maso anu anaona mwana wanga ali m'mimba, ndinu amene mukudziwa zobisika mumtima mwanga ndipo ndisanayambe kulankhula mukudziwa zomwe ndinganene. Lero ndikupempherera mtima wanga kuti ukukondweretseni ndipo muuyeretse, ndikupempha chisomo chanu chifukwa ndikudziwa kuti ndinali wopanduka kwa inu, kwa banja langa, abale ndi anzanga, ndinayesa kuiwala mawu anu ndipo ndinachita zomwe mdani anandiuza, koma ndimakhulupirira ndi mtima wonse kuti ndinu chishango changa ndi woteteza wanga, pakuti kwalembedwa: "Ife tinapanduka, ndipo sitinakhale okhulupirika; inu simunatikhululukire". Atate wokondedwa, ndikupemphani kuti mubisire moyo wanga chifukwa ndayesedwa kuti ndichoke m'njira yanu, ndilanditseni Mulungu wokondedwa ku mitsinje ya dziko lino, ku lilime lonyenga ndi lonama, sungani makutu ndi maso anga ku zokopa za satana. Ndikusiya mkwiyo, chidani, kudzidalira, kunyada ndi dyera m'dzina la Yesu. Mundichitire chifundo Mulungu, sungani pakamwa panga kuti pasatuluke mawu otsutsana nanu, mundibisire pamaso pa mdani, ndikudziwa kuti sindidzagwedezeka chifukwa muli kudzanja langa lamanja. Onetsani mphamvu yanu Ambuye, pakuti mwakhala pothawirapo panga ndi chitetezo changa pa tsiku la masautso anga. Zikomo m'dzina la Yesu chifukwa chondilanditsa ku imfa. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa