Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


NDIME ZA PEMPHERO

NDIME ZA PEMPHERO

Atate wathu wakumwamba watilangiza kuti tizipemphera nthawi zonse. Ndi m’pemphero momwe timayanjana ndi Mulungu wathu. Pemphero ndi njira yolankhulirana ndi Mulungu. Ndi m’pemphero momwe timaperekera mapempho athu onse pamapazi a Mlengi wathu. Ndi komwe timapita zinthu zikavuta, tili ndi nkhawa, kapena titakhala achisoni.

Mulungu amadziwa kale zosowa zathu, ndipo ankadziwa miyoyo yathu tisanabadwe. Koma amafuna kuti tizilankhula naye, kuti timufunefune. Mukapemphera, mumayamba kulimbitsa ubwenzi wanu ndi Mulungu. Mumapanga ubale wolimba naye. Pemphero ndi chida champhamvu kwa ife okhulupirira Yesu. Ndi chida chodzitetezera pa nkhondo iliyonse. Ndi m’pemphero momwe mumapezera chipambano pa chilichonse.

Mphamvu ya pemphero sichokera kwa inu, koma kwa Yesu. Iye ndiye amayankha mapemphero ndi kuchititsa zinthu zomwe sizingatheke kwa anthu. Mukapemphera ndi mtima wonse, mumapeza chitonthozo, mtendere, ndi chikondi cha Atate. Yandikirani kwa Mulungu ndi mtima wodzichepetsa ndi wachisoni, ndipo sadzakukanani. (Aefeso 6:18)

Pemphani mwa Mzimu nthawi zonse, ndi mapempho osiyanasiyana. Khalani maso, ndipo pempherani nthawi zonse chifukwa cha oyera mtima onse. Mukapemphera, yambani ndi kuyamika Mulungu. Osangopereka mapempho anu okha, komanso khalani chete pamaso pake. (Atesalonika 1 5:16-18) Khalani okondwa nthawi zonse, pempherani nthawi zonse, ndipo yamikani Mulungu pa chilichonse, pakuti ichi ndi chifuniro chake kwa inu mwa Khristu Yesu.




Yobu 22:27

Ukadzapemphera kwa Iye adzakumvera, udzapereka kwa Iye zija udalumbira kuti udzaperekazi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 21:36

Muzikhala maso tsono, ndipo muzipemphera nthaŵi zonse, kuti mukhale ndi mphamvu zopulumukira ku zonsezi zimene ziti zidzachitike, ndiponso kuti mukaimirire pamaso pa Mwana wa Munthu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 143:1

Imvani pemphero langa, Inu Chauta. Tcherani khutu kuti mumve kupemba kwanga. Mundiyankhe chifukwa cha kukhulupirika kwanu ndi kulungama kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 1:27

Mwana uyu ndidachita kupempha, ndipo Chauta wandipatsa chopempha changacho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 9:38

Nchifukwa chake mupemphe Mwini dzinthu kuti atume antchito okatuta dzinthu dzakedzo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yona 2:1

Tsono Yona ali m'mimba mwa chinsomba chija, adayamba kutama Chauta mopemba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 18:7

Nanga Mulungu, angaleke kuŵaweruzira mlandu wao osankhidwa ake, amene amamdandaulira usana ndi usiku? Kodi adzangoŵalekerera?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 25:4

Mundidziŵitse njira zanu, Inu Chauta, mundiphunzitse kuchita kufuna kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 9:11

Apo Ambuye adamuuza kuti, “Nyamuka, upite ku mseu wa mumzindamu umene amati, ‘Njira Yolunjika.’ Ndipo ku nyumba ya Yudasi ukafune munthu wina wa ku Tariso, dzina lake Saulo. Panopa akupemphera,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:16

Nchifukwa chake sindilekeza kuthokoza Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani m'mapemphero anga,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 4:12

Akukupatsani moni Epafra, amene ali mmodzi mwa inu, ndiponso mtumiki wa Khristu Yesu. Nthaŵi zonse iyeyo amalimbikira kukukumbukirani m'mapemphero ake. Amatero pofuna kuti inuyo mukhale okhazikika, angwiro, ndipo kuti muzichilimikira kuchita zonse zimene Mulungu afuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:5-6

Uzikhulupirira Chauta ndi mtima wako wonse, usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu. Pa ntchito zako zonse uzivomera kuti kuli Mulungu, choncho njira zako Iye adzazilungamitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:2

Mumalakalaka zinthu, koma zimakusoŵani, nchifukwa chake mumapha munthu. Mumasirira zinthu, koma simungathe kuzipeza, nchifukwa chake mumamenyana, nkumachita nkhondo. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 10:4

Iye adayang'anitsitsa mngeloyo mantha atamgwira, ndipo adamufunsa kuti, “Nkwabwino, Ambuye?” Mngeloyo adati, “Mulungu wakondwera nawo mapemphero ako ndipo wakumbukira ntchito zako zachifundo zako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 42:8

Komabe Chauta amaonetsa chikondi chake chosasinthika tsiku ndi tsiku, Nchifukwa chake nthaŵi zonse ndimamuimbira nyimbo, ndi kumpemphera Mulungu wondipatsa moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:41

Khalani maso inu ndi kumapemphera, kuti mungagwe m'zokuyesani. Mtima ndiye ukufunitsitsadi, koma langokhala lofooka ndi thupi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:12

Masiku amenewo Yesu adapita ku phiri kukapemphera, ndipo adachezera usiku wonse akupemphera kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 6:4

Koma ife tidzadzipereka ku ntchito ya kupemphera ndi kulalika mau a Mulungu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 15:7

Ngati mukhala mwa Ine, ndipo mau anga akhala mwa inu, mupemphe chilichonse chimene mungachifune, ndipo mudzachilandiradi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 2:8

Ndikufuna kuti paliponse amuna popemphera azikweza manja ao kwa Mulungu momchitira ulemu, mopanda mkwiyo kapena kukangana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:42

Anthuwo ankasonkhana modzipereka kuti amve zimene atumwi ankaphunzitsa. Ankayanjana, ndipo ankadya Mgonero wa Ambuye ndi kupemphera pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 4:1

Ndikamaitana, mundiyankhe Inu Mulungu, Mtetezi wanga. Mudabwera kudzandithandiza pamene ndinali m'mavuto. Mundichitire chifundo, ndi kumvera pemphero langa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 14:23

Tsono atatsazikana nawo anthu aja, Iye adakwera ku phiri yekha kukapemphera. M'mene kunkayamba kuda, nkuti ali komweko yekhayekha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 5:7

Yesu, pa nthaŵi imene anali munthu pansi pano, mofuula ndi molira misozi, adapereka mapemphero ndi madandaulo kwa Mulungu, amene anali nazo mphamvu zompulumutsa ku imfa. Ndiye popeza kuti Yesu adaadzipereka modzichepetsa, Mulungu adamvera mapemphero ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 17:6

Ndikupemphera kwa Inu Mulungu, chifukwa mudzandiyankha. Tcherani khutu kuti mumve mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 55:6

“Mufunefune Chauta pamene angathe kupezeka, mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 42:10

Choncho Yobe ataŵapempherera abwenzi ake aja, Chauta adambwezera chuma chake. Adampatsa moŵirikiza kuposa zimene adaali nazo kale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 5:16

Koma Iye adapita kumalo kosapitapita anthu, namakapemphera kumeneko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 141:2

Pemphero langa likwere kwa Inu ngati lubani, kukweza kwa manja anga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 6:21

Muzimva mapemphero opemba a mtumiki wanu ndiponso a anthu anu Aisraele, akamapemphera ku malo ano. Ndithu mumve kumwambako kumene mumakhala, ndipo mukamva, mutikhululukire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 1:4

Nthaŵi zonse pamene ndikukupemphererani nonsenu, ndimapemphera mokondwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yuda 1:20

Koma inu okondedwa, muzithandizana kuti uzikulirakulira moyo wanu, umene udakhazikika pa maziko a chikhulupiriro chanu changwiro. Muzipemphera ndi mphamvu za Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:9

Mulungu ndi mboni yanga. Ndimamtumikira ndi mtima wanga wonse, pakulalika Uthenga Wabwino wonena za Mwana wake. Akudziŵa kuti ndimakukumbukirani kosalekeza m'mapemphero anga onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 16:25

Koma pakati pa usiku Paulo ndi Silasi ankapemphera ndi kuimba nyimbo zolemekeza Mulungu, akaidi anzao nkumamvetsera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 6:9

Chauta wamva pemphero langa ndipo wandiyankha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:41

Tsono adapatukana nawo kadera, kutalika kwake ngati pamene mwala ungafike munthu atauponya. Apo adagwada pansi nayamba kupemphera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 65:24

Ndidzaŵayankha asanatsirize nkomwe kupemphera, ndidzaŵamva akulankhula kumene.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:2

Adaŵauza kuti, “Dzinthu ndzambiri, koma antchito ngochepa. Nchifukwa chake pemphani Mwini dzinthu kuti atume antchito kukatuta dzinthudzo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:13

Koma ine ndimapemphera kwa Inu Chauta. Mundiyankhe pa nthaŵi yabwino, Inu Mulungu, chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, ndi chithandizo chanu chokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 8:28

Komabe Inu Chauta, Mulungu wanga, imvani pemphero la ine mtumiki wanu ndi kupemba kwanga. Mverani kulira kwanga ndiponso pemphero limene ine mtumiki wanu ndikupemphera pamaso panu lero lino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 3:10

Ndi mtima wonse timapemphera usana ndi usiku kuti tiwonane nanunso maso ndi maso, kuti tikakwaniritse zimene zikusoŵa pakuwonetsa chikhulupiriro chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 1:11

Nchifukwa chake timakupemphererani nthaŵi zonse, kuti Mulungu wathu akusandutseni oyenera moyo umene Iye adakuitanirani. Timapemphanso kuti ndi mphamvu zake akulimbikitseni kuchita zabwino zonse zimene mumalakalaka kuzichita, ndiponso ntchito zotsimikizira chikhulupiriro chanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:32

Koma Ine ndakupempherera, kuti usaleke kundikhulupirira. Ndipo iweyo utatembenuka mtima, ukaŵalimbitse abale akoŵa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 12:5

Motero Petro ankasungidwa m'ndende. Koma Mpingo unkamupempherera kwa Mulungu kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 61:1

Inu Mulungu, imvani kulira kwanga, mverani pemphero langa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 33:11

Choncho Chauta ankalankhula ndi Mose pamasompamaso, monga momwe munthu amalankhulira ndi bwenzi lake. Tsono pambuyo pake Mose ankabwerera kumahema komweko. Koma mnyamata wina, dzina lake Yoswa, mwana wa Nuni, amene anali mtumiki wa Mose, sankachoka kuchihemako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 13:9

Timakondwa pamene ife tili ofooka koma inu muli amphamvu. Chimene tikupempha Mulungu nchakuti mudzasanduke angwiro.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 13:3

Tsono atasala zakudya ndi kupemphera adaŵasanjika manja naŵatuma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 11:6

Ndipotu popanda chikhulupiriro nkosatheka kukondweretsa Mulungu. Paja aliyense wofuna kuyandikira kwa Mulungu, ayenera kukhulupirira kuti Mulunguyo alipodi, ndipo kuti amaŵapatsa mphotho anthu omufunafuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:17

Muzipemphera kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:7

Chimalizo cha zonse chayandikira. Nchifukwa chake khalani ochenjera ndi odziletsa, kuti muthe kupemphera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 4:16

Tiyeni tsono, tiyandikire mopanda mantha ku mpando wachifumu wa Mulungu wokoma mtima. Kumeneko tidzalandira chifundo, ndipo mwa kukoma mtima kwa Mulungu tidzapeza thandizo pa nthaŵi yake yeniyeni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 21:22

Ngati mukhala ndi chikhulupiriro, zonse zimene mungapemphe kwa Mulungu mudzalandira.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 18:6

Ndidaitana Chauta m'zovuta zanga. Ndidafuulira Mulungu wanga kuti andithandize. Iye ali m'Nyumba mwake, adamva liwu langa, kulira kwanga kofuna chithandizo kudamveka kwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 16:24

Mpaka tsopano simunapemphe kanthu potchula dzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikhale chathunthu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:29

Chauta amakhala kutali ndi anthu oipa mtima, koma amamva pemphero la anthu achilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:8

Yandikirani kwa Mulungu, ndipo Iye adzayandikira kwa inu. Muzisamba m'manja, inu anthu ochimwa. Chotsani maganizo onyenga m'mitima mwanu, inu anthu okayikakayika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 2:1

Tsono choyamba ndikukupemphani kuti pakhale mapemphero opempherera anthu onse. Mapemphero ake akhale opemba, opempha ndi othokoza Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 102:17

Adzayankha pemphero la anthu ake otayika, sadzanyoza kupemba kwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 4:2

Muzipemphera mosafookera, ndipo pamene mukupemphera, muzikhala tcheru ndiponso oyamika Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 18:1

Yesu adaŵaphera fanizo pofuna kuŵaphunzitsa kuti azipemphera nthaŵi zonse, osataya mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 6:18

Chitani zonse mopemphera, ndi kupempha chithandizo cha Mulungu nthaŵi zonse. Nthaŵi iliyonse muzipemphera motsogoleredwa ndi Mzimu Woyera. Nchifukwa chake muchezere kupemphera mosalekeza, kupempherera anthu onse a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:6

Musade nkhaŵa ndi kanthu kalikonse, koma m'mapemphero anu onse muzipempha Mulungu zimene zikusoŵani, ndipo nthaŵi zonse muzipemphe ndi mtima woyamika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:6

Koma iwe, pamene ukuti upemphere, loŵa m'chipinda chako, tseka chitseko, ndipo upemphere kwa Atate ako amene ali osaoneka. Tsono Atate ako amene amaona zobisika adzakupatsa mphotho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 29:12

Nthaŵi imeneyo mudzandiitana ndi kumanditama mopemba, ndipo ine ndidzakumverani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:7

“Pemphani ndipo adzakupatsani. Funafunani ndipo mudzapeza, gogodani, ndipo adzakutsekulirani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:18

Chauta ali pafupi ndi onse amene amamutama mopemba. Ali pafupi ndi onse amene amamutama mokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:13-14

Chilichonse chomwe mudzachipemphe potchula dzina langa ndidzachita, kuti Atate adzalemekezedwe mwa Mwana. Ngati mudzandipempha kanthu potchula dzina langa ndidzakachitadi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 5:14

Ndipo timalimba mtima pamaso pa Mulungu, popeza kuti amatimvera tikapempha kanthu kalikonse komukomera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 5:16

Muziwululirana machimo anu, ndipo muzipemphererana kuti muchire. Pemphero la munthu wolungama limakhala lamphamvu, ndipo silipita pachabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:12

Muzikhala okondwa chifukwa cha chiyembekezo chanu. Muzipirira pakati pa masautso, ndipo muzipemphera nthaŵi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 11:24

Nchifukwa chake ndikukuuzani kuti, m'mapemphero mwanu mukapempha Mulungu chinthu chilichonse, muzikhulupirira kuti mwalandira, ndipo mudzachilandiradi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:5

Wina mwa inu akasoŵa nzeru, apemphe kwa Mulungu, ndipo adzalandira, pakuti Mulungu amapereka kwa onse mwaufulu ndi mosatonzera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 5:3

M'maŵa, Inu Chauta, mumamva mau anga. M'maŵa ndimapemphera kwa Inu, ndi kudikira kuti mundiyankhe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 33:3

Akuti: Unditame mopemba, ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziŵa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:40

Pamene adafika kumeneko, Yesu adaŵauza kuti, “Pempherani, kuti mungagwe m'zokuyesani.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 5:20

Mulungu adaŵathandiza pomenya nkhondoyo, ndipo Ahagiriwo pamodzi ndi onse amene adaaphatikana nawo, adaperekedwa m'manja mwao. Ankalira kwa Mulungu pomenya nkhondoyo, tsono Mulungu adaŵapatsa zimene ankapemphazo, popeza kuti adaamkhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 1:11

Inu Chauta, tcherani khutu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu ena amene amakonda kulemekeza dzina lanu. Lolani kuti ine mtumiki wanu zinthu zindiyendere bwino lero, ndipo kuti mfumu indichitire chifundo.” Pa nthaŵi imeneyo nkuti ine ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:1-2

Ndimakonda Chauta chifukwa amamva mau anga omupemba. Ndidakhulupirirabe ngakhale pamene ndinkati, “Ndazunzika koopsa.” Pamene ndinkachita mantha, ndidati, “Anthu ndi osakhulupirika.” Ndidzambwezera chiyani Chauta pa zabwino zonse zimene adandichitira? Ndidzakweza chikho cha chipulumutso, ndidzapemphera potchula dzina la Chauta. Ndidzachita zimene ndidalumbira kwa Chauta pamaso pa anthu ake onse. Imfa ya anthu oyera mtima a Chauta, ndi yamtengowapatali pamaso pake. Chauta, ine ndine mtumiki wanu, mtumiki wanu weniweni, mwana wa mdzakazi wanu. Inu mwamasula maunyolo anga. Ndidzapereka kwa Inu nsembe yothokozera, ndidzapemphera potchula dzina la Inu, Chauta. Ndidzachita zimene ndidalumbira kwa Chauta pamaso pa anthu ake onse. Ndidzazipereka m'mabwalo a Nyumba ya Mulungu, mu mzinda wa Yerusalemu. Tamandani Chauta! Iye amatchera khutu kuti andimve, nchifukwa chake ndidzampempha nthaŵi zonse pamene ndili moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:31

Atatha kupemphera, nyumba imene adasonkhanamo ija idayamba kugwedezeka. Onse adadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kulankhula mau a Mulungu molimba mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 55:17

Madzulo, m'maŵa ndi masana ndikudandaula ndi kulira, ndipo Iye adzamva mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:9

Nchifukwa chake, kuyambira tsiku limene tidamva zimenezi, sitileka kukupemphererani. Timapempha Mulungu kuti akudzazeni ndi nzeru ndi luntha, zimene Mzimu Woyera amapatsa, kuti mumvetse zonse zimene Iye afuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 1:35

M'mamaŵa ndithu, kusanache, Yesu adadzuka napita kumalo kosapitapita anthu. Kumeneko adakapemphera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:12

Popeza kuti timakhulupirira Iyeyu, tingathe kulimba mtima kuyandikira kwa Mulungu mosakayika konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:15

Ngati mumvera Chauta, adzakuyang'anirani ndipo adzayankha kupempha kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:22

Ndipo chilichonse chimene timpempha, amatipatsa, chifukwa timatsata malamulo ake, ndipo timachita zomkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 16:11

Muzidalira Chauta ndi mphamvu zake. Muziyesetsa kukhala pamaso pake kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 12:23

Komanso kunena za ine, sindifuna kuchimwira Chauta, pakuleka kukupemphererani. Ndidzakuphunzitsani zimene zili zabwino ndi zolungama kuti muzizichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 18:20

Pajatu pamene aŵiri kapena atatu asonkhana m'dzina langa, Ineyo ndili nao pomwepo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 1:14

Onseŵa ankalimbikira kupemphera ndi mtima umodzi, pamodzi ndi akazi ena, ndi Maria amai ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:26

Momwemonso Mzimu Woyera amatithandiza. Ndife ofooka, osadziŵa m'mene tiyenera kupempherera. Nchifukwa chake Mzimu Woyera mwiniwake amatipempherera ndi madandaulo osafotokozeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:19-20

Koma zoonadi, Mulungu wandimvera, wasamala mau a pemphero langa. Imbani nyimbo zoyamika dzina lake laulemerero, mumtamande mwaulemu. Mulungu atamandike chifukwa sadakane pemphero langa, sadachotse chikondi chake chosasinthika kwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 5:13

Kodi wina mwa inu ali m'mavuto? Apemphere. Kodi wina wakondwa? Aimbe nyimbo zotamanda Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:7

“Pamene mukupemphera, musamangobwerezabwereza mau monga amachitira anthu akunja. Iwowo amayesa kuti akachulukitsa mau choncho, ndiye pamene Mulungu aŵamvere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 7:14

ndipo anthu anga amene amatchedwa dzina langa akadzichepetsa, napemphera, ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zao zoipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwambako. Choncho ndidzaŵakhululukira zoipa zao ndi kupulumutsa dziko lao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:15

Pajatu Mzimu amene mudalandira, sakusandutsani akapolo, kuti muzikhalanso amantha ai. Koma Mzimuyo amakusandutsani ana a Mulungu, ndipo mwa mphamvu yake, popemphera kwa Mulungu timati, “Abba! Atate!”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Zikomo Ambuye, Dokotala wanga, Mpatsi wanga, ndi Mlonda wanga. Ndinu amene mumalowerera nkhondo zanga, ndi kunditsogolera kuchoka pa ulemerero kupita pa ulemerero wina. M'dzina lamphamvu la Yesu, ndikupempherani Mulungu wanga wakumwamba, chifukwa mumakwaniritsa malonjezano anu, ndipo simusintha mawu anu. Zikomo chifukwa mudalonjeza kundithandiza, kunditeteza, kukhala mtendere wanga, chitonthozo changa, ndi kukhala nane masiku onse kufikira chimaliziro cha dziko lapansi. Ambuye, malonjezano anu sakhala chabe, ndipo mwakwaniritsa lililonse. Ambuye, zikomo chifukwa mwamva pemphero langa, ndipo mwalowerera nkhondo zanga, ndi kundilanditsa ku ziwembu za mdani. Ndaona dzanja lanu nthawi za kutopa, chifukwa mwamva kulira kwanga, ndipo mwanditsitsimutsa ngati mmene mbalame ya chiwombankhanga imatsitsimutsira. Zikomo chifukwa simuli munthu wongonama, kapena mwana wa munthu woti angasinthe maganizo ake. Atate, ndinu Wamphamvuyonse, simunandisiye ine ndekha. Zikomo chifukwa mwayankha pemphero langa, ndipo nthawi za mavuto mwakhala Mpatsi wanga ndi wa banja langa. Munditeteze kuti ndisamvere mawu a mdani, ndi kundilanditsa ku lilime lachinyengo ndi loipa lomwe likufuna kundikayikitsa zimene mudandilonjeza. Mawu anu amati, "Ndipo chilichonse chimene mudzapempha Atate m'dzina langa, ndidzachita, kuti Atate alemekezedwe mwa Mwana. Ngati mupempha kanthu m'dzina langa, Ine ndidzachita." Ndikukuthokozani chifukwa cha zimene mudzachita pa moyo wanga ndi wa banja langa. Zikomo chifukwa cha mphamvu yanu ndi Mzimu Woyera, amene ndi lonjezo labwino kwambiri ndi mnzathu amene munasiyira anthu anu. Pakuti tsiku la chisoni Iye wandilimbikitsa, ndipo ngakhale usiku wakuda bwanji, mwanena kuti, "Usachite mantha kapena kutaya mtima, limbika mtima ndipo ukhale wolimba mtima." Mundiphunzitse mmene ndiyenera kupemphera pamavuto onse a moyo wanga, pakuti sindikudziwa choti ndipemphe monga momwe ndiyenera, koma Mzimu yekha amandipempherera ndi kugwedezeka. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa