Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -



NDIME ZA ZOCHITIKA ZAPADERA

NDIME ZA ZOCHITIKA ZAPADERA

Timatamanda Mulungu chifukwa cha tsiku lililonse lapadera limene timakumana nalo, ndi masiku osangalala ndi kukondwerera. Mulungu amasangalala tikamayenda mu mtendere ndi chimwemwe. Muzimutamanda Yehova m'masiku amenewa ndipo musaiwale kuti ndi Mulungu amene amakuchititsani kukhala ndi nthawi zapadera.

Masalimo 30:11-12 amati, “Munasintha kulira kwanga kukhala kuvina; Munandichotsa chiguduli, n’kundiveka chokondwerera; kuti moyo wanga uziyimba nyimbo zotamanda Inu, osakhala chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzakutamandani nthawi zonse.” M’Baibulo muli mavesi ambiri okhudza zochitika zapadera.




Hoseya 9:5

Kodi pa tsiku la chikondwerero, tsiku lolemekeza Chauta, anthuwo adzachitapo chiyani?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 30:23

Pambuyo pake msonkhano wonse udavomerezana zopitiriza chikondwererocho masiku asanu ndi aŵiri ena. Choncho adachitadi chikondwerero masiku asanu ndi aŵiri ena mosangalala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 34:18

“Muzichita chikondwerero cha buledi wosafufumitsa monga ndidakulamulirani. Muzidzadya buledi wosafufumitsa pa masiku asanu ndi aŵiri pa mwezi wa Abibu, chifukwa ndi mwezi umenewu pamene inu mudachokako ku Ejipito kuja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:15

Muzikhala ndi tsiku la chikondwerero cha Buledi Wosatupitsa. Monga ndidakulamulirani, muzidya Buledi Wosatupitsa masiku asanu ndi aŵiri pa mwezi wa Abibu, pa nthaŵi yake, chifukwa mudatuluka ku Ejipito mwezi umenewo. Munthu asadzaonekere pamaso panga ali chimanjamanja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 31:16

Aisraele azisunga tsiku la Sabatalo, ndipo mibadwo yonse yakutsogoloko izidzalisunga ngati pangano losatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:24

Lero ndiye tsiku limene Chauta adalipanga. Tiyeni tikondwe ndi kusangalala pa tsiku limeneli.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 8:14-15

Tsono adapeza kuti m'buku la Malamulo mudalembedwa kuti Chauta adalamula kudzera mwa Mose kuti Aisraele azikhala m'zithando nthaŵi yonse ya chikondwerero cha pa mwezi wachisanu ndi chiŵiri. Motero adafalitsa ndi kulengeza m'midzi yao yonse ndiponso m'Yerusalemu, kuti, “Pitani ku mapiri, mukatengeko nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wakuthengo, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa, ndiponso za mitengo ina ya masamba ambiri, kuti mumangire misasa monga momwe zidalembedwera.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 2:11

Ndidzathetsa chimwemwe chake chonse, zikondwerero zake za pokhala mwezi, za masabata ndi za masiku ena onse opatulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 1:13-14

Musabwere nazonso nsembe zanu zachabechabe. Utsi wake umandinyansa. Sindingapirire misonkhano yanu yamapemphero, kapenanso zikondwerero za pokhala mwezi ndi za Sabata, sindingapirire mapemphero oipitsidwa ndi machimo. Zikondwerero zanu za pokhala mwezi ndi masiku anu oyera ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera, ndatopa nako kuŵapirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 32:5

Aroniyo ataona zimenezi, adapanga guwa patsogolo pa mwanawang'ombe wagolideyo. Tsono adalengeza kuti, “Maŵa padzakhala chikondwerero cholemekeza Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 66:23

Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala mwezi, ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 15:3

mwina muzidzapereka ng'ombe kapena nkhosa kwa Chauta kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, kapena yopsereza, kapena yopembedzera, kuti mukwaniritse zimene mudalonjeza molumbira. Mwina mudzazipereka kuti zikhale nsembe yaufulu kapena nsembe yopereka pa nthaŵi ya zikondwerero zosankhidwa, kuti zikhale nsembe zotulutsa fungo lokomera Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 31:10-11

Adaŵalamula onsewo kuti, “Kamodzi pa zaka zisanu ndi ziŵiri zilizonse, pamene chaka cha kumasulidwa chafika, muŵerenge malamuloŵa pa chikondwerero cha misasa. Muŵaŵerenge kwa Aisraele onse, pamene adzabwere kudzapembedza Chauta pa malo oŵasankha Iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:18

“Mukamapereka magazi a nyama ngati nsembe kwa Ine, musapereke pamodzi ndi buledi wofufumitsa, ndipo mafuta a nyama yopereka pa tsiku langa lachikondwerero asakhale mpaka m'maŵa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 14:22-23

Chachikhumi muziika padera, ndiye kuti limodzi mwa magawo khumi a zokolola zanu za chaka ndi chaka. Tsono pitani mukakhale pa malo amodzi amene Chauta, Mulungu wanu, adzasankhula kuti anthu azidzampembedzerapo. Ndipo magawo achachikhumi ameneŵa mudyere pa malo amenewo, pamaso pa Mulungu wanu. Magawo ameneŵa ndi a tirigu, vinyo ndi mafuta aolivi, ndiponso ana oyamba kubadwa a ng'ombe ndi a nkhosa. Muzichita zimenezi masiku onse, kuti motero muphunzire kuwopa Chauta, Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 8:10

Zikondwerero zanu ndidzazisandutsa kulira, nyimbo zanu ndidzazisandutsa zamaliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu pathupi panu, ndipo mitu yanu yonse idzachita dazi. Mudzakhala ngati anakubala olira mwana wao mmodzi yekha. Tsiku limenelo lidzakhaladi loŵaŵa mpaka kutha kwake.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:8-9

“Muziŵerenga masabata asanu ndi aŵiri a zaka, zaka zisanu ndi ziŵiri kuchulukitsa kasanunkaŵiri, kuti nyengo ya masabata asanu ndi aŵiri a zakayo ikwanire zaka 49 pamodzi. Tsono pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiŵiri, mulize lipenga mokweza. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo, ndilo tsiku limene mulize lipengalo m'dziko lanu lonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:6

Ndipo tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku la chikondwerero cha buledi wosafufumitsa, lolemekezera Chauta. Pa masiku asanu ndi aŵiri muzidya buledi wosafufumitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 45:25

“Tsono mfumu ichitenso chimodzimodzi pa tsiku la khumi ndi chisanu la mwezi wachisanu ndi chiŵiri. Chikondwerero chimenecho chizichitika masiku asanu ndi aŵiri. Izipereka nsembe za mtundu womwewonso, zopepesera machimo, nsembe zopsereza, ndiponso nsembe zaufa ndi zamafuta zomwe.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 45:21

“Pa tsiku la khumi ndi chinai la mwezi woyamba, muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi aŵiri. Masiku amenewo muzidya buledi wosatupitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezara 3:4

Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe kudalembedwera. Masiku onse ankaperekanso nsembe zopsereza potsata chiŵerengero chake chofunika tsiku ndi tsiku, monga kudalembedwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 30:21

Tsono anthu a ku Israele amene analipo ku Yerusalemu kuja, adachita chikondwerero cha buledi wosafufumitsa masiku asanu ndi aŵiri, ndipo adasangalala kwambiri. Alevi pamodzi ndi ansembe ankatamanda Chauta tsiku ndi tsiku, akumuimbira ndi mphamvu zao zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 8:13

monga momwe zinkafunikira pa tsiku lililonse. Ankapereka potsata malamulo a Mose okhudza masiku a Sabata, masiku a pokhala mwezi watsopano, ndiponso masiku achikondwerero atatu a chaka ndi chaka: Chikondwerero cha buledi wosafufumitsa, chikondwerero cha masabata ndiponso chikondwerero cha mahema.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:16

Anthu aamuna onse a mtundu wanu azidzabwera kudzapembedza Chauta, Mulungu wanu, ku malo achipembedzo, katatu pa chaka. Azidzafika pa nthaŵi ya Paska, pa nthaŵi ya chikondwerero cha kholola ndiponso pa nthaŵi ya chikondwerero cha misasa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 28:16

“Tsiku la 14 la mwezi woyamba, ndi la Paska ya Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 9:2-3

“Aisraele azichita Paska pa nthaŵi yake. Nthaŵi zina mtambowo unkaphimba masiku oŵerengeka, ndipo Aisraele ankakhalabe m'mahema potsata malamulo a Chauta. Tsono ankanyamuka ulendo Chauta akaŵalamula. Nthaŵi zina mtambowo unkangophimba chihemacho kuyambira madzulo mpaka m'maŵa. M'maŵa mwake mtambowo ukachoka, iwo ankanyamuka ulendo wao. Mwina mtambowo unkaphimba chihema chija tsiku lonse ndi usiku womwe, koma ukangochokapo, iwowo ankanyamuka ulendo wao. Ngakhale mtambowo uphimbe pamwamba pa chihema cha Mulungu nkumakhala pomwepo masiku aŵiri kapena mwezi, kapena chaka, kapena nthaŵi yopitirirapo, Aisraele ankakhalabe m'mahema, ndipo sankanyamuka. Koma mtambowo ukangochokapo, iwo ankanyamuka ulendo. Aisraele ankamanga mahema ao Chauta akaŵalamula, ndipo ankanyamuka ulendo wao Chauta akaŵalamula. Ankasunga lamulo la Chauta, loŵafikira kudzera mwa Mose. Muzichita Paska tsiku la 14 la mwezi uno, madzulo ake. Muzichita Paskayo potsata malamulo ake ndi malangizo ake onse.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:39

“Pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiŵiri, mutakolola dzinthu m'dziko mwanu, muchite chikondwerero cha Chauta pa masiku asanu ndi aŵiri. Tsiku loyamba likhale tsiku lalikulu lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu likhalenso tsiku lalikulu lopumula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:34

“Uza Aisraele kuti, ‘Kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiŵiri, pa masiku asanu ndi aŵiri, pazikhala chikondwerero chamisasa cholemekeza Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:27

‘Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiŵiri ndi tsiku lochita mwambo wopepesera machimo. Imeneyo ikhale nthaŵi yanu yochita msonkhano wopatulika. Musale zakudya, ndipo mupereke nsembe yopsereza kwa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:24

“Uza Aisraele kuti, ‘Pa mwezi wachisanu ndi chiŵiri, tsiku loyamba la mweziwo, muzilisunga kuti likhale tsiku lalikulu lopumula, tsiku lachikumbutso, lolengezedwa ndi malipenga, tsiku la msonkhano wopatulika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:15-16

“Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, pamene mudadzapereka mtolo wanu uja wa chopereka choweyula pamaso pa Chauta, muŵerenge milungu isanu ndi iŵiri yathunthu, ndiye kuti masiku asanu mpaka tsiku lotsatana ndi la Sabata lachisanu ndi chiŵiri. Patapita masiku amenewo, mupereke chopereka cha chakudya chatsopano kwa Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:10-11

“Uza Aisraele kuti, ‘Mukakaloŵa m'dziko limene ndikukupatsanilo ndi kukakolola za m'minda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa zoyambirira kucha mwa zokolola zanu. Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Chauta, kuti inuyo mulandiridwe. Auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:5

pa mwezi woyamba, tsiku la 14 la mweziwo, madzulo ake, ndi tsiku la Paska ya Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:4

“Masiku achikondwerero osankhidwa a Chauta, masiku oyera amisonkhano amene mudzaŵalengeza pa nthaŵi yake, ndi aŵa:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:2

“Uza Aisraele kuti, ‘Masiku achikondwerero osankhidwa olemekeza Chauta, amene mudzaŵalengeza kuti akhale masiku oyera amisonkhano, masiku achikondwerero amene Ine ndaŵasankha, ndi aŵa:

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 13:10

Musunge malangizo ameneŵa pa nthaŵi yake chaka ndi chaka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 12:24-27

Muziŵamvera malamulo ameneŵa inuyo ndi ana anu mpaka muyaya. Ndipo mukadzaloŵa m'dziko limene Chauta akukupatsanilo, monga momwe adalonjezera, muzidzasunga mwambo umenewu. Ana anu azidzakufunsani kuti, ‘Kodi mwambo umenewu umatanthauza chiyani?’ Pamenepo inu muzidzayankha kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Chauta, chifukwa chakuti adapitirira nyumba za Aisraele ku Ejipito; pamene ankapha Aejipito, nyumba zathu adazisiya.’ ” Atamva zimenezi, anthu adaŵerama pansi, napembedza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 28:17-18

Ndipo pa tsiku la 15 la mwezi umenewu, ndi tsiku lachikondwerero. Azidya buledi wosafufumitsa masiku asanu ndi aŵiri. Pa tsiku loyamba pazikhala msonkhano wopatulika. Musagwire ntchito yotopetsa,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 29:1

“Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiŵiri, muzichita msonkhano wopatulika. Musagwire ntchito zotopetsa. Tsiku limeneli muziliza malipenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 12:14

“Tsiku limeneli muzidzalisunga. Tsiku limeneli muzidzalikumbukira, ndipo muzidzachita chikondwerero, kupembedza Chauta. Mibadwo yonse izidzakumbukira tsikuli, kuti likhale lamulo lamuyaya, lakuti muzidzachita chikondwerero pa tsiku limenelo.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:1

Muzilemekeza Chauta, Mulungu wanu, pakuchita chikondwerero cha Paska pa mwezi wa Abibu. Chifukwa usiku wina mwezi umenewu, mpamene Chauta adakutulutsani ku Ejipito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 34:22

Muzichita chikondwerero cha masabata, ndi chikondwerero cha kukolola tirigu woyambirira, ndi chikondwerero cha kututa zokolola zonse pakutha pake pa chaka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 23:14-16

“Muzikhala ndi tsiku lachikondwerero katatu pa chaka, kuti mundilemekeze Ine. Muzikhala ndi tsiku la chikondwerero cha Buledi Wosatupitsa. Monga ndidakulamulirani, muzidya Buledi Wosatupitsa masiku asanu ndi aŵiri pa mwezi wa Abibu, pa nthaŵi yake, chifukwa mudatuluka ku Ejipito mwezi umenewo. Munthu asadzaonekere pamaso panga ali chimanjamanja. Muzikhalanso ndi tsiku la chikondwerero cha Masika pokolola mbeu zoyamba zochokera ku zobzala zanu. Muzikhalanso ndi tsiku la chikondwerero cha kututa zokolola zonse pakutha pa chaka, pamene muika m'nkhokwe dzinthu dzanu dzonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:13-14

Mutatuta tirigu wanu yense, ndiponso mutafinya mphesa zanu, muzidzachita chikondwerero cha misasa masiku asanu ndi aŵiri. Musangalale pa chikondwererocho, inuyo pamodzi ndi mwana wanu wamwamuna, mwana wanu wamkazi, mtumiki wanu wamwamuna, mdzakazi wanu, Alevi amene ali m'mizinda mwanu, alendo, ana amasiye ndi akazi amasiye, amene amakhala nanu m'mizinda mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 16:10

Tsono muchite chikondwerero cha kholola, cholemekeza Chauta, Mulungu wanu, pakumpatsa chopereka chaufulu, molingana ndi madalitso amene Iye wakupatsani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 14:16

Zitatha zimenezi anthu onse otsala mwa adani amene ankamenyana ndi Yerusalemu, azidzabwera chaka ndi chaka kudzapembedza Mfumu, Chauta Wamphamvuzonse, ndiponso kudzachita chikondwerero chamisasa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 7:2

Nthaŵiyo nkuti chikondwerero cha Misasa chili pafupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 2:13

Itayandikira nthaŵi ya Paska, chikondwerero cha Ayuda, Yesu adanyamuka kupita ku Yerusalemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 6:4

Chikondwerero chija chachipembedzo chotchedwa Paska chidaayandikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:1

Pamene tsiku la chikondwerero cha Pentekoste lidafika, iwo onse anali pamodzi m'nyumba imodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 12:3-4

Ndipo ataona kuti zimenezi zidakondweretsa Ayuda, adapitiriza ndithu nkugwiranso Petro. Zimenezi zidachitika pa masiku a Paska, chikondwerero cha mikate yosafufumitsa. Atamgwira, adamtsekera m'ndende, nampereka kwa magulu anai a asilikali kuti azimlonda, gulu lililonse asilikali anai. Tsono Herode ankafuna kuzenga mlandu wake pamaso pa anthu onse, chikondwerero cha Paska chitapita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:10

Mupatule chaka cha 50, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu m'dziko lonselo kwa onse amene ali m'menemo. Kwa inu chaka chimenecho chidzakhale chokondwerera zaka 50, pamene aliyense adzayenera kubwerera pa mtunda wake, ndipo aliyense mwa inu abwerere ku banja lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 33:20

Onani Ziyoni, mzinda wa zokondwerera zathu zachipembedzo. Maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, hema losasunthika. Zikhomo zake sizidzazuka, ndipo zingwe zake sizidzaduka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 11:55

Chikondwerero cha Paska chija chinkayandikira. Choncho anthu ambiri ochokera ku midzi adapita ku Yerusalemu kukachita mwambo wa kudziyeretsa, Paska isanayambe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:44

Umu ndimo m'mene Mose adafotokozera kwa Aisraele za masiku achikondwerero osankhidwa, olemekeza Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 29:12

“Pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiŵiri womwewo, muchite msonkhano wopatulika. Musagwire ntchito zotopetsa, ndipo muchite chikondwerero cholemekeza Chauta masiku asanu ndi aŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezara 6:22

Motero pa masiku asanu ndi aŵiri adasangalala pa chikondwerero cha buledi wosatupitsa. Zidatero chifukwa Chauta adaŵakondweretsa, ndipo adaatembenuza mtima wa mfumu ya ku Asiriya, kotero kuti idaŵakomera mtima niŵathandiza pa ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu, Mulungu wake wa Aisraele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 10:22

Ku Yerusalemu kunali chikondwerero chokumbukira kuperekedwanso kwa Nyumba ya Mulungu. Inali nyengo yozizira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 10:10

Pa tsiku lanu losangalala, pa masiku osankhidwa a zikondwerero zanu, ndi pa masiku oyamba a miyezi, mulize malipenga pamene mukupereka nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu zachiyanjano. Malipengawo adzakuthandizani kumkumbukira Mulungu wanu. Ine ndine Chauta, Mulungu wanu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 29:7

“Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiŵiri womwewo, muchite msonkhano wopatulika, ndipo musale zakudya. Musagwire ntchito iliyonse,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 35:2

Muzigwira ntchito zanu pa masiku asanu ndi limodzi. Koma tsiku lachisanu ndi chiŵiri, lidzakhala la Sabata, tsiku lanu lopumula, loperekedwa kwa Chauta. Munthu aliyense wogwira ntchito pa tsiku limenelo, adzaphedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 20:6

Koma ife tidayenda pa chombo kuchokera ku Filipi, itatha Paska, chikondwerero cha mikate yosafufumitsa. Ndipo patapita masiku asanu, tidakumana nawo ku Troasi. Kumeneko tidakhalako masiku asanu ndi aŵiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 23:21

Tsono mfumu Yosiya adalamula anthu onse kuti, “Muchite chikondwerero cha Paska, kulemekeza Chauta, Mulungu wanu, potsata zimene zidalembedwa m'buku lachipangano.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:32

Likhale ngati tsiku lalikulu la Sabata lopumula kwa inu, ndipo musale zakudya. Pa tsiku lachisanu ndi chinai la mwezi, kuyambira madzulo ake mpaka madzulo ena otsatira, musunge tsikulo monga ngati la Sabata.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 12:17

Chikondwerero chimenechi cha buledi wosafufumitsa, mudzachisunge ndithu, chifukwa pa tsiku limeneli mpamene ndidzatulutse magulu anu onse kuchoka m'dziko la Ejipito. Tsono muzidzasunga tsiku limeneli pa mibadwo yanu yonse, ngati lamulo lamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 7:37

Tsiku lotsiriza la chikondwerero chija linali lalikulu. Pa tsikulo Yesu adaimirira nkunena mokweza kuti, “Ngati pali munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 8:19

Kusala zakudya pa mwezi wachinai, wachisanu, wachisanu ndi chiŵiri ndi wakhumi, kudzakhala nthaŵi yachimwemwe ndi yachisangalalo ku banja la Yuda. Muzikonda zoona ndiponso mtendere.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 9:13

Koma munthu amene sadadziipitse ndipo sali paulendo, komabe akana kuchita Paska, ameneyo achotsedwe pakati pa Aisraele, chifukwa sadabwere ndi zopereka zake kwa Chauta pa nthaŵi yake. Ameneyo adzalangidwa chifukwa cha tchimo lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 35:17

Choncho Aisraele amene anali pamenepo adachita Paska nthaŵi imeneyo, ndipo pa masiku asanu ndi aŵiri adachita chikondwerero cha buledi wosafufumitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 25:6

Pa phiri ili la Ziyoni Chauta Wamphamvuzonse adzakonzera anthu a mitundu yonse phwando la zakudya zokoma ndi la vinyo wabwino, phwando la nyama yonona ndi la vinyo amene wafikapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:29

Koma inu anthu a Mulungu, mudzakondwa ndi kuimba monga m'mene mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika. Mudzasangalala ngati anthu opita naimba toliro ku phiri la Chauta, thanthwe la Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 30:26

Choncho kunali chikondwerero chachikulu ku Yerusalemu, pakuti kuyambira nthaŵi ya Solomoni, mwana wa Davide, mfumu ya Israele, sizidachitikepo zotere ku Yerusalemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 122:1

Ndidasangalala pamene adandiwuza kuti, “Tiyeni tipite ku Nyumba ya Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 42:4

Mtima wanga umaŵawa ndikamakumbukira m'mene ndinkayendera ndi chinamtindi cha anthu, poŵatsogolera ku Nyumba ya Mulungu. Panali khwimbi la anthu ofuula mosangalala, akuimba nyimbo zothokoza ndipo akuchita chikondwerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 27:9

Nthaŵi yaikulu idapita, ndipo ngakhale nthaŵi yosala zakudya inali itapita kale. Nthaŵiyo ulendo wapamadzi unali woopsa. Pamenepo Paulo adaŵachenjeza kuti,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 7:8

Inuyo pitani kuchikondwereroko. Ine sindipitako ku chikondwerero chimenechi, chifukwa nthaŵi yanga yoyenera siinafike.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:5

Koma ankati, “Zimenezi tisadzachite pa nthaŵi ya chikondwerero ai, pangadzachitike chipolowe pakati pa anthu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 5:1

Pambuyo pake kunali chikondwerero chachipembedzo cha Ayuda, ndipo Yesu adapitako ku Yerusalemuko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 46:9

“Pa masiku achikondwerero, anthu am'dzikomo akabwera kudzapembedza Chauta, munthu woloŵera pa chipata chakumpoto azidzatulukira pa chipata chakumwera. Munthu woloŵera pa chipata chakumwera, azidzatulukira pa chipata chakumpoto. Munthu aliyense asadzatulukire pomwe waloŵera, koma azipita chakutsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 23:37

“Ameneŵa ndi masiku achikondwerero osankhidwa olemekeza Chauta, amene muziŵalengeza kuti ndi nthaŵi ya msonkhano wopatulika. Masiku ameneŵa muzipereka kwa Chauta nsembe zapamoto, monga nsembe zopsereza, nsembe zaufa, nsembe zanyama, ndi zopereka za chakumwa, iliyonse pa tsiku lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 81:3

Imbani lipenga mwezi ukaoneka chatsopano, ukaoneka kwathunthu, pa tsiku lathu lachikondwerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Nehemiya 8:18

Tsiku ndi tsiku kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lotsiriza, Ezara ankaŵerenga buku la Malamulo a Mulungu. Anthu adachita chikondwerero masiku asanu ndi aŵiri, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu padachitika mwambo wotseka msonkhano, potsata buku la Malamulo lija.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:11

Chaka chimenecho cha 50 chikhale chaka chachikondwererodi. Pa chaka chimenechi musabzale kanthu, kapena kukolola mphulumukwa, kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosathenera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 10:2

“Upange malipenga aŵiri asiliva, uchite kusula. Uziimba malipengawo poitana mpingo, ndi pochoka pa mahema.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 12:32

Ndipo Yerobowamu adakhazikitsa tsiku lachikondwerero, pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, lofanafana ndi tsiku lachikondwerero limene ankachita ku Yuda, napereka nsembe pa guwa nthaŵi imeneyo. Adachita zimenezi ku Betele, namapereka nsembe kwa mafano a anaang'ombe, amene iyeyo adapanga. Ndipo ku Beteleko adaikako ansembe pa malo achipembedzo amene adamanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 45:17

Ndipo mfumu izipereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe zatirigu ndi nsembe zazakumwa pa masiku achikondwerero, ndi a pokhala mwezi, masiku a Sabata, ndiponso pa masiku ena amene Aisraele amaŵasunga. Mfumuyo ipereke zofunikira ku nsembe zopepesera machimo, nsembe zatirigu, nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kuti zonsezo zikhale zopepesera machimo a Aisraele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoweli 2:15

Lizani lipenga ku Ziyoni. Lengezani mwambo wa kusala zakudya. Muitanitse msonkhano waukulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 25:12

Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka 50. Chikhale chaka chopatulika kwa inu ndipo mudye zam'likale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 14:12

Pa tsiku loyamba la masiku a buledi wosafufumitsa, tsiku lomwe anthu ankapha mwanawankhosa wochitira phwando la Paska, ophunzira a Yesu adamufunsa kuti, “Kodi tikakukonzereni kuti malo okadyerako phwando la Paska?”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:7

Tsiku la buledi wosafufumitsa lidafika, ndiye kuti tsiku limene anthu ankapha mwanawankhosa wochitira phwando la Paska.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 22:1

Nthaŵi yochitira chikondwerero cha buledi wosafufumitsa inkayandikira. Chikondwererocho chimatchedwa Paska.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 26:17

Pa tsiku loyamba la masiku a buledi wosafufumitsa, ophunzira aja adadza nafunsa Yesu kuti, “Kodi tikakukonzereni kuti malo okadyerako phwando la Paska?”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga Wamuyaya, Wamkulu ndi Wamphamvu, Inu nokha ndinu Woyenera ulemerero ndi ulemu wonse! Pa tsiku lapaderali kwa ambiri a ife omwe tiri pano, ndikukuthokozani chifukwa cha thanzi ndi mtendere umene mutipatse kuti tisangalale ndi anansi ndi abale. Dalitsani onse omwe tidzakhala m'msonkhano uno, kuti tidziwane kumverana, kumvana, kukambirana, ndi kulemekezana maganizo, kuti ntchito iyi ikhale yaulemerero wanu ndipo Mzimu Woyera wanu udzioneke m'mitima mwathu ndipo tilandire kuchokera m'dzanja lanu chimene mukufuna kuti tikhale nacho. Mawu anu amati: "Taona, ndikulamula kuti ulimbike mtima ndi kukhala wolimba; usachite mantha kapena kuzengereza, pakuti Yehova Mulungu wako adzakhala nawe kulikonse kumene upita." Titumizireni, Ambuye, chisomo ndi mphamvu zanu kuti chikondi chanu chitsogolere mapazi athu onse; kuti tithe kuyika luso lathu kukutumikirani Inu. Bwerani, Ambuye, ndipo mutenge ulamuliro wa miyoyo yathu ndi maluso athu. Dalitsani ndi kubwezeretsa mphamvu za omwe adachita nawo pakukonzekera msonkhano uno, sungani mitima yawo ndi kuwapatsa chitukuko. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa