Mphamvu pa moyo ndi imfa zili mwa Mulungu. Ndi Iye amene amasankha zaka za munthu padziko lapansi ndi kupatsa mpweya m'moyo wake. Koma, kuyambira kale, pali mdani amene amatsutsa chifuniro cha Mulungu ndipo nthawi zonse amafunafuna njira yowonongera cholengedwa chake chokongola kwambiri: anthu.
Anthu ambiri anamwalira msanga, osati chifukwa chakuti Mulungu anakonza choncho, koma chifukwa anasiya cholinga chamuyaya. Gulu la mdani limakonza tsiku lililonse kulimbitsa mitima ya anthu, kufesa misempha yonse: nsanje, kaduka, ulesi, kusasamala, kufikira pokhala ozizira.
Palibe wobadwa kuti aphe. Mavuto amabuka munthu akasankha kukhala kutali ndi Mulungu. Uchimo wa aliyense umamukopa ku zoipa, ndipo akamakhala popanda Mulungu, moyo wake umasanduka chisokonezo, moti mitima yambiri imagalukira Mlengi wawo.
Atate Wakumwamba amaliritsa akaona anthu akuphedwerekana tsiku ndi tsiku, pomwe m'mawu ake amati "Usaphe" (Ekisodo 20:13). Kupha si njira yabwino. Yesu akufuna kukuthandiza musanachite tchimo ndikudzilimbana ndi chisoni pambuyo pake.
Pulumutsa moyo wako ku gehena, tsata malamulo a Mulungu ndipo udzalandira chifundo. Si udindo wako kuweruza; mkhalapakati yekha m'dziko lino ndi Yesu wa Nazareti. Dziwa kuti ukunamizidwa. Kupha munthu sikudzakupulumutsa ku imfa, koma kudzakutsogolera ku chiweruzo.
Mawu a Mulungu m'buku la Levitiko 24:17 amati: "Munthu akapha munthu mnzake, ayenera kuphedwa." Yesetsani kukhala mwamtendere, yendani molungama, ndipo musapatuke ku zoipa. Pangana mtendere ndi Mulungu lero, mupemphe chikhululukiro pa machimo anu onse ndipo mudzalandira moyo wosatha kumwamba, kupewa kuvutika ku gehena.
Mitima yao idadzaza ndi zosalungama zamitundumitundu, monga kuipa, umbombo ndi dumbo. Amangolingalira za kaduka, za kupha anthu, za ndeu, za kunyenga, ndi za njiru. Amachita ugogodi,
“Mudamva kuti anthu akale aja adaaŵalamula kuti, ‘Usaphe. Aliyense wopha mnzake adzayenera kuzengedwa ku bwalo lamilandu,’ Chabwino, koma Ine ndikukuuzani kuti aliyense wopsera mtima mbale wake adzayenera kuzengedwa ku bwalo lamilandu. Aliyense wonena mnzake kuti, ‘Wopandapake iwe,’ adzayenera kuzengedwera ku Bwalo Lapamwamba. Ndipo aliyense wonena mnzake kuti, ‘Chitsiru,’ adzayenera kukaponyedwa ku moto wa Gehena.
Pajatu malamulo amene amati, “Usachite chigololo, usaphe, usabe, usasirire”, ndiponso malamulo ena onse, amaundidwa mkota m'lamulo ili lakuti, “Uzikonda mnzako monga momwe umadzikondera iwe wemwe.”
“Aliyense wopha munthu, nayenso adzaphedwa, pakuti munthu adalengedwa muchifaniziro cha Mulungu.
Aliyense wodana ndi mnzake, ndi wopha anthu. Ndipo mukudziŵa kuti aliyense wopha anthu, alibe moyo wosatha mumtima mwake.
Adakhetsa magazi osachimwa, magazi a ana ao aamuna ndi aakazi, amene adaŵapereka nsembe kwa mafano a ku Kanani, choncho dzikolo adaliipitsa ndi imfa zimenezo.
Anthu oipa amasolola lupanga, ndipo amakoka mauta, kuti aphe anthu ovutika ndi osoŵa, amene amayenda molungama. Koma lupanga lao lidzalasa mitima ya eniake omwewo, ndipo mauta ao adzaŵathyokera m'manja.
Iye adati, “Malamulo ake oti?” Yesu adayankha kuti, “Usaphe, usachite chigololo, usabe, usachite umboni wonama,
Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Chauta amadana nazo, makamaka zisanu ndi ziŵiri ndithu zimene zimamunyansa: maso onyada, pakamwa pabodza, manja opha munthu wosalakwa,
Munthu amene wapalamula mlandu wopha mnzake, akhale womathaŵathaŵa mpaka kufa kwake. Wina aliyense asamthandize.
Si nsembe wamba imene Inu imakusangalatsani. Ndikadapereka nsembe yopsereza, sibwenzi Inu mutakondwera nayo. Nsembe imene Inu Mulungu mumailandira, ndi mtima wotswanyika. Mtima wachisoni ndi wolapa, Inu Mulungu simudzaunyoza.
Manja anu ali psuu ndi magazi a anthu amene mudapha. Mudadziipitsa ndi machimo anu ambiri. Pakamwa panu palankhula zabodza, pamanena zoipa.
Mumalakalaka zinthu, koma zimakusoŵani, nchifukwa chake mumapha munthu. Mumasirira zinthu, koma simungathe kuzipeza, nchifukwa chake mumamenyana, nkumachita nkhondo. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu.
Zochita za khalidwe lokonda zoipa zimaonekera poyera. Ndi izi: Dama, kuchita zonyansa, kusadziletsa, Ndiye mvetsani, ine Paulo ndikukuuzani kuti mukalola kukuumbalani, Khristu simupindula nayenso konse ai. kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko, dumbo, kuledzera, kudakwa pa maphwando achipembedzo, ndi zina zotere. Ndikukuchenjezani tsopano, monga ndidaachitanso kale, kuti anthu amene amachita zotere, sadzalandirako Ufumu wa Mulungu.
Koma munthu akapha mnzake mwadala mwa njira yonyenga, aphedwe ndithu ngakhale wathaŵira ku guwa langa.
Ndimanyansidwa ndikamayang'ana anthu osakhulupirika, chifukwa satsata malamulo anu.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wosalakwa, koma anthu angwiro amateteza moyo wake.
Mwina mwake munthu adana ndi mnzake, ndipo amkhalizira namupha mwadala, nkuthaŵira ku umodzi mwa mizinda imeneyi kuti apulumuke. Zikatero, akuluakulu akwao adzamuitanitse kuchokera ku mzinda wakewo, ndi kukampereka kwa woyenera kumlipsira uja kuti aphedwe ndithu. Musamchitire chifundo. Mchotseni pakati pa Aisraele munthu wopha mnzake wosalakwa, kuti zinthu zikuyendereni bwino.
Musandipereke m'manja mwa adani angawo. Mboni zonama zandiwukira, ndipo zimandiwopseza.
“Mudamva kuti anthu akale aja adaaŵalamula kuti, ‘Diso kulipa diso, dzino kulipa dzino.’ Chabwino, koma Ine ndikukuuzani kuti munthu woipa osalimbana naye. Ngati munthu akumenya pa tsaya la ku dzanja lamanja, upereke linalonso.
Adzati, “Tiye kuno, tikabisale kuti tiphe anthu, tiye tikalalire anthu osalakwa. Tiyeni tiŵameze amoyo ngati manda, tiŵameze athunthu ngati anthu otsikira ku manda.
Oweruza akamachedwetsa chilango cha anthu opalamula, anthu ena amalimba mtima nkumafuna kuti ayambe kuchita zoipa nawonso.
Pulumutseni, Inu Chauta, kwa anthu oipa. Tchinjirizeni kwa anthu ankhanza. Makala amoto aŵagwere, aponyedwe m'maenje ozama, asatulukemonso. Musalole kuti woononga mbiri ya mnzake akhazikike m'dziko. Choipa chimlondole munthu wankhanza mpaka kumuwononga. Ndimadziŵa kuti Inu Chauta mumateteza ozunzika, mumaweruza mwachilungamo anthu osoŵa. Zoonadi, anthu ochita zabwino adzatamanda dzina lanu. Anthu amenewo adzakhala pamaso panu. Iwo amalingalira mumtima mwao kuti achite zoipa, amautsa nkhondo nthaŵi zonse.
Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.”
Mukamatambasula manja anu popemphera, sindidzayang'anako. Ngakhale muchulukitse mapemphero anu chotani, sindidzasamalako, chifukwa manja anu ndi odzaza ndi magazi.
Apo Yesu adamuuza kuti, “Bwezera lupangalo m'chimake, pakuti onse ogwira lupanga adzaphedwa ndi lupanga.
Makolo asafere zolakwa za ana ao. Momwemonso ana asafere zolakwa za makolo ao. Munthu aphedwe chifukwa cha zoipa za iye mwini.
Khristu mwiniwake adasenza machimo athu m'thupi lake pa mtanda, kuti m'machimo tikhale ngati akufa, koma pakutsata chilungamo tikhale amoyo ndithu. Mudachiritsidwa ndi mabala ake.
Tsiku lina Sarai adauza Abramu kuti, “Cholakwa chimenechi chakuti Hagara akundinyoza, chili pa inu. Ine ndidakupatsani mdzakazi ameneyu, ndipo kuyambira paja adatenga pathupipa, wakhala akundinyoza. Chauta ndiye aweruze kuti tiwone wolakwa ndani pakati pathu.”
Mukonzekere kupha ana aamuna a mfumuyi, chifukwa cha kulakwa kwa atate ao, kuwopa kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda.”
Thetsani mphamvu za munthu woipa ndi wochimwa. Fufuzani kuipa kwake, ndipo mumlange kuti asadzabwerezenso.
“Atembereredwe aliyense wopha mnzake mwachinsinsi.” Ndipo anthu onse adzayankhe kuti, “Inde, momwemo!” “Atembereredwe onse olandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.” Ndipo anthu onse adzayankhe kuti, “Inde, momwemo!”
Zomwe mukufuna kuti anthu akuchitireni, inuyo muŵachitire zomwezo. Izi ndiye zimene Malamulo a Mose ndiponso aneneri amaphunzitsa.
Munthu wopsa mtima msanga amachita zauchitsiru, wa khalidwe lonyenga, anthu amadana naye.
Anthu onse oipa a pa dziko lapansi, mumaŵayesa ngati zakudzala, nchifukwa chake ndimakonda malamulo anu.
Chauta akubwera kuchokera kumene amakhala, akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo ao. Magazi okhetsedwa pa dziko lapansi adzaululuka, mitembo ya anthu ophedwa sidzabisikanso.
Ndikadakonda kuti muwononge anthu oipa, Inu Mulungu, ndipo kuti anthu okhetsa magazi andichokere. Inu mumadziŵa pamene ndikhala pansi, pamenenso ndidzuka, mumazindikira maganizo anga muli kutali. Anthuwo amakunenani zinthu zoipa, namakuukirani ndi mtima woipa. Kodi sindidana nawo anthu odana nanu, Inu Chauta? Kodi sindinyansidwa nawo anthu okuukirani? Ndimadana nawo ndi chidani chenicheni. Ndimaŵayesa adani anga.
“Munthu akamenya kapolo wake wamwamuna kapena wamkazi ndi ndodo, ndipo kapoloyo afera pomwepo, munthuyo adzalangidwa. Koma kapoloyo akakhala moyo tsiku lathunthu kapena masiku aŵiri, mbuyakeyo asalangidwe. Kapoloyo ndi chuma cha mbuyakeyo.
Koma Inu Mulungu mudzaŵaponya adani anga m'dzenje lozama lachiwonongeko. Anthu okhetsa magazi ndi onyenga sadzafika ngakhale theka la masiku ao. Koma ine ndidzadalira Inu.
Nzeru nzabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amatha kuwononga zabwino zambiri.
“Ndithu ngati mukhululukira anthu machimo ao, Atate anu akumwamba adzakukhululukirani inunso. Koma ngati simukhululukira anthu machimo ao, Atate anunso sadzakukhululukirani machimo anu.
Nzeru zotere si zochokera Kumwamba, koma ndi nzapansipano, ndi za anthu chabe, ndiponso nzochokera ku mizimu yoipa.
M'dziko limene Chauta, Mulungu wanu, akukupatsani kuti likhale lanulanu mwina mwake mungathe kupeza munthu wakufa m'munda, inu osadziŵa amene wamupha. Chauta, Mulungu wanu, akakupambanitsani pa nkhondo, mungathe kugwirapo akapolo kunkhondoko. Mwina pakati pa akapolowo inu nkuwona mkazi wokongola amene mwamkonda, ndipo mufuna kumkwatira. Pita nayeni kwanu, ndipo mkaziyo amete kumutu, ndi kutseteka makadabo ake, ndipo asinthe zovala. Akhale m'mudzi mwanu mwezi wathunthu, ndipo alire maliro kulira makolo ake. Tsono atatha zimenezi, mumkwatire. Pambuyo pake mutaona kuti simukumfunanso, mumleke, apite mwaufulu kumene akufuna. Simungathe kumuyesanso kapolo kapena kumgulitsa, chifukwa mudakhala naye malo amodzi. Tiyese kuti munthu ali ndi akazi aŵiri, wina wokondedwa kwambiri wina pang'ono, onsewo nkubala ana aamuna, mwana woyamba kubadwa nakhala wa mkazi amene amamkonda pang'ono. Munthuyo akatsimikiza zoti agaŵire ana akewo chuma chake, asakondere mwana wa mkazi wokondedwa koposayo, pakumpatsa gawo la mwana woyamba. Mwana wake woyamba kubadwa uja ampatse moŵirikiza, ngakhale kuti ndi mwana amene mai wake ndi wokondedwa pang'ono. Munthu ayenera kuvomera mwana wake woyamba, ndi kumpatsa gawo limene lili lake potsata lamulo. Tiyese kuti wina ali ndi mwana wokanika ndiponso wachipongwe, mwana woti bambo ndi mai ake saŵamvera konse, ngakhale amlange chotani. Makolo ake a mwanayo amgwire ndi kupita naye kwa akuluakulu amumzinda ku chipata cha mzindawo. Akuluakulu anu ndi aweruzi anu apiteko, ndipo akayese kutalika kwake kuchokera pamalo pamene pali munthu wakufayo mpaka ku mizinda yoyandikana ndi malowo. Makolowo auze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu ndi wokanika ndipo ndi wachipongwe safuna kutimvera, ndi wadyera ndiponso chidakwa. Pamenepo anthu amumzindawo amuphe pakumponya miyala, motero mudzachotsa choipa pakati panu. Anthu onse a mu Israele muno akadzamva zimene zachitikazi, adzakhala ndi mantha.” Munthu akaphedwa chifukwa cha mlandu, ndipo mtembo wake ndi wopachikidwa pa mtengo, mtembowo usagonere pamtengopo. Uikidwe tsiku lomwelo, chifukwa kuti mtembo ugonerere pamtengo ndi chinthu chobweretsa matemberero a Mulungu. Kwirirani mtembowo, kuwopa kuti mungaipitse dziko limene Chauta, Mulungu wanu, akukupatsanilo. Pamenepo akuluakulu a mudzi woyandikana kwambiri ndi pamene pali mtembopo, asankhe ng'ombe imene sidagwirepo ntchito, ndipo sidakokepo galeta. Ng'ombeyo apite nayo kudambo kumene kuli madzi oyenda. Malowo akhale akuti munthu sadalimepo nkale lonse kapena kubzalapo kanthu. Kumeneko akaithyole khosi ng'ombeyo. Ansembe Achilevi apitekonso kumeneko, chifukwa ndiwo amene ayenera kumaweruza milandu yonse ya ndeu ndi ya kupha. Chauta, Mulungu wanu, wasankha iwowo kuti akhale atumiki ake, ndiponso kuti azidalitsa m'dzina lake. Tsono atsogoleri onse ochokera ku mudzi wa pafupi ndi pamene panali munthu wophedwayo, asambe m'manja pamwamba pa ng'ombe ija imene adaithyola khosi m'dambo muja. Ndipo anene kuti, “Sindife tidamupha munthuyu, ndipo amene adamupha sitidamuwone. Inu Chauta, khululukirani anthu anu Aisraele amene mudaŵaombola. Tikhululukireni ndipo musaike pa ife tchimo la kupha munthu wosalakwayu.” Mukachita zimene Chauta afuna, Iyeyo sadzakuzengani mlandu woti mwapha munthu wosalakwa.
Munthu woipa amazonda munthu wabwino, amafunafuna kuti amuphe. Koma wolungamayo Chauta sadzamsiya yekha m'manja mwa mdani wake, sadzalola kuti pomuweruza, mlandu wake umuipire.
Tsono iwe wophunzitsa ena, bwanji sukudziphunzitsa wekha? Iwe wolalika kuti, “Osamaba,” bwanji iwenso umaba?
Yakwana nthaŵi yakuti Inu Chauta muchitepo kanthu, popeza kuti anthu aphwanya malamulo anu.
Amathamangira kukachita zoipa, sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo ao onse ali pa zoipa. Kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja, ndiponso amaononga. Kumene kuli iwowo, anthu sapeza mtendere. Zonse zimene amachita nzopanda chilungamo. Amayenda m'njira zokhotakhota, ndipo aliyense woyenda m'njira zimenezo sadzapeza mtendere.
“Inunsotu Atate anga akumwamba adzakuchitani zomwezo, aliyense mwa inu akapanda kukhululukira mbale wake ndi mtima wonse.”
Chifukwa chiyani anthu akunja akuti, “Kodi Mulungu wao ali kuti?” Mulole kuti tiwone Inu mukulipsira mitundu ina ya anthu, chifukwa chokhetsa magazi a atumiki anu.
kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko,
Ndikunenetsa kuti pa tsiku la chiweruzo, anthu adzazengedwa mlandu chifukwa cha mau aliwonse opanda pake amene adaalankhula.
Amafulumira kupweteka ndi kupha anzao. Amasakaza ndi kusautsa kulikonse kumene amapita, ndipo njira yamtendere saidziŵa.
Mzinda wa Babiloni, iwe woyenera kuwonongedwawe, adzakhala wodala munthu amene adzakubwezera zimene watichita ifezi. Adzakhala wodala munthu amene adzatenga makanda ako ndi kuŵakankhanthitsa ku thanthwe.
Mukuŵapsinjiranji anthu anga? Chifukwa chiyani mukuŵadyera masuku pamutu amphaŵi?” Akutero Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse.
Usachite kunyanyanso kuipa, usanyanye nawonso uchitsiru. Nanga uferenji nthaŵi yako isanakwane?
Inu mumaŵaononga anthu olankhula zonama. Inu Chauta mumanyansidwa nawo anthu onyenga ndi opha anzao.
Mundiwonetse njira zanu zachifundo, Inu Chauta, munditsogolere m'njira yosalala, chifukwa ndili ndi adani ambiri. Musandipereke m'manja mwa adani angawo. Mboni zonama zandiwukira, ndipo zimandiwopseza.
Angathe kutero ndi amene amachita zolungama ndi kulankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga, amene amakutumula manja ake kuti angagwire chiphuphu, amene amatseka makutu kuti angamve mau opangana za kupha anzao, amene amatsinzina kuti angaone zoipa.
“Uziyanjana msanga ndi mnzako wamlandu, mukali pa njira yopita ku bwalo lamilandu, kuwopa kuti angakakupereke kwa woweruza, woweruzayo angakakupereke kwa msilikali, ndipo msilikaliyo angakakuponye m'ndende. Ndithu ndikunenetsa kuti sudzatulukamo mpaka utalipira zonse.
Mumve kubuula kwa anthu am'ndende, muŵasunge ndi mphamvu zanu zazikulu anthu oyenera kuphedwa.
Musapereke chiwalo chilichonse cha thupi lanu ku uchimo, kuti chigwire ntchito zotsutsana ndi chilungamo. Inu mudzipereke kwa Mulungu, monga anthu amene anali akufa, koma tsopano ali amoyo. Ndipo mupereke ziwalo zanu zonse kwa Mulungu, kuti zigwire ntchito zachilungamo.
Pakuti munthuyo sadakumbukire kuchita chifundo, koma adazunza osauka, osoŵa ndi ovutika mu mtima, mpaka kuŵapha.
Uchimo umalankhula mu mtima wa munthu wosamvera Mulungu. Alibe mantha ndi Mulungu m'maganizo mwake. Musaleke kuŵakonda ndi chikondi chanu chosasinthika anthu okudziŵani, pitirizani kuŵachitira zokoma anthu olungama mtima. Musalole kuti mapazi a anthu odzikuza andipondereze, ndipo kuti manja a anthu oipa andipirikitse. Onani, ochita zoipa ali ngundangunda. Inu mwaŵagwetsa pansi ndipo sangathe kudzuka. Amadzinyenga m'maganizo mwake, kotero kuti tchimo lake sangathe kulizindikira ndi kudana nalo. Mau a pakamwa pake ndi oipa ndi onyenga. Sachita zanzeru kapena zabwino. Amaganiza zachiwembu akamagona usiku. Amayenda pa njira imene siili yabwino, sapewa zoipa.
“Chenjerani kuti musanyoze ndi mmodzi yemwe mwa anaŵa. Ndithu ndikunenetsa kuti angelo ao Kumwamba amakhala pamaso pa Atate anga amene ali Kumwambako nthaŵi zonse.” [
Ukonde wa kangaude sangauvale ngati nsalu, chimene anthu amapangacho sangafunde konse. Ntchito zao nzoipa ndipo amakonda kuchita zandeu ndi manja ao.
Koma Chauta adamuyankha kuti, “Iyai, aliyense wopha iwe Kaini adzalangidwa, ndipo Ineyo ndidzamulipsira kasanunkaŵiri.” Motero Chauta adaika chizindikiro pa Kaini kuchenjeza aliyense kuti asamuphe Kainiyo.
Munthu wangwiro adzakondwera poona kulipsirako. Adzasamba mapazi ake m'magazi a anthu oipawo.
Paja Malembo akuti, “Chifukwa cha Inu tsiku lonse akufuna kutipha, pamaso pao tili ngati nkhosa zimene akukazipha.”
Tsono popeza kuti zoipa zizidzachulukirachulukira, chikondi chizidzacheperachepera pakati pa anthu.
Woweruza munthu woipa mtima kuti ndi wosalakwa, amanyansa Chauta, nayenso wopasa mlandu munthu wosalakwa amaipira Chauta.
Chauta amayesa anthu olungama namakondwera nawo, mtima wake umadana ndi anthu oipa okonda zachiwawa.
Inu Chauta, tetezeni kwa anthu oipa, tchinjirizeni kwa anthu andeu, amene amaganiza zofuna kundigwetsa.
“Pambuyo pake Mfumuyo idzauzanso a ku dzanja lake lamanzere aja kuti, ‘Chokani apa, inu otembereredwa. Pitani ku moto wosatha, umene Mulungu adakonzera Satana ndi angelo ake.
Koma tsono anthu ameneŵa aŵalanda ndi kuŵafunkhira zinthu zao. Onseŵa adaŵakola m'mbuna, ndi kuŵabisa m'ndende. Adaŵafunkhira, popanda wina woŵapulumutsa, adaŵabera, popanda wina wonena kuti, “Bwezani!”
Anthu abwino akapambana, pamakhala chikondwerero chachikulu, koma oipa mtima akalandira ulamuliro, anthu amabisala.
Munthu wosinjirira mnzake kuseri ndidzamcheteketsa. Wooneka wonyada ndi wodzikuza sindidzamulekerera.
Ulewe zabodza, zosinjirira. Usaphe munthu wosalakwa ndi wosapalamula, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.
Kwa chitsiru kulakwa kumakhala ngati maseŵera, koma kwa munthu womvetsa zinthu kuchita zanzeru ndiye kumapatsa chimwemwe.
Koma anthu amantha, osakhulupirika, okonda zonyansa, opha anzao, ochita zadama, ochita zaufiti, opembedza mafano, ndi anthu onse onama, malo ao ndi m'nyanja yodzaza ndi moto ndi miyala ya sulufure woyaka. Imeneyi ndiyo imfa yachiŵiri.”
“Mudamva kuti anthu akale aja adaaŵalamula kuti, ‘Usaphe. Aliyense wopha mnzake adzayenera kuzengedwa ku bwalo lamilandu,’
“Ngati mbala ipezeka ikuthyola nyumba ndipo ikanthidwa nkufa, asalipsire magazi chifukwa cha mbalayo.
Aisraelewo adamenyana nkhondo ndi Amidiyani, monga momwe Chauta adaalamulira Mose, ndipo adapha amuna onse.
Nchifukwa chake tsono iphani mwana wamwamuna aliyense, ndi mkazi aliyense amene adadziŵapo ndi mwamuna.
Tisakhale ngati Kaini amene anali wake wa Woipa uja, ndipo adapha mbale wake. Chomuphera chinali chiyani? Chifukwa zochita zake zinali zoipa, koma za mbale wake zinali zolungama.