Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


ZIKOMO VERSE

ZIKOMO VERSE

Ambuye watipatsa madalitso ambiri, tsiku lililonse tili ndi zambiri zoti tiyamike. Mulungu ndi wabwino ndipo amatidzaza ndi madalitso ake tsiku lililonse. Mu Mulungu timawona ndi kusangalala ndi madalitso amenewa monga: kukhala ndi pogona, kukhala ndi thanzi labwino, kukhala ndi banja, kukhala ndi ntchito. Pali zinthu zambiri zomwe timawona madalitso a Mulungu, kotero nthawi zonse padzakhala chifukwa choyamikira Mulungu. Nthawi zina timaganizira kwambiri mavuto athu kapena zinthu zomwe tilibe m'malo motamanda ndi kuyamikira Mulungu pazinthu zonse zabwino zomwe zili m'miyoyo yathu.

Mulungu wathu ndiye wopereka zinthu zonse zabwino! Yambani chizolowezi choyamika Mulungu tsiku lililonse chifukwa cha ubwino wake wonse. Conco, popeza tilandira ufumu wosagwedezeka, tiyeni tikhale oyamikira. Ndi chiyamiko chimenechi, tiyeni tilambire Mulungu momusangalatsa, ndi mantha ndi ulemu. (Ahebri 12:28) Apa mupeza mavesi ambiri oyamika Mulungu.




Masalimo 136:1

hokozani Chauta chifukwa ngwabwino, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:18

Muzithokoza Mulungu pa zonse. Paja zimene Mulungu amafuna kuti muzichita mwa Khristu Yesu nzimenezi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:1

Thokozani Chauta chifukwa ngwabwino, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:15

Mtendere wa Khristu uzikutsogolerani m'mitima mwanu. Mulungu adakuitanani kuti mukhale nawo mtendere umenewu, popeza kuti ndinu ziwalo za thupi limodzi. Muzikhala oyamika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:2

Tiyeni, tikafike pamaso pake, tikamthokoze, tiyeni tifuule kwa Iye ndi chimwemwe, timuimbire nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:4

Loŵani pa zipata zake mukuthokoza, pitani m'mabwalo a Nyumba yake mukutamanda. Yamikani Chauta, lemekezani dzina lake!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:20

Muziyamika Mulungu Atate nthaŵi zonse chifukwa cha zonse, m'dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:1

Thokozani Chauta chifukwa ngwabwino, ndipo chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:6

Musade nkhaŵa ndi kanthu kalikonse, koma m'mapemphero anu onse muzipempha Mulungu zimene zikusoŵani, ndipo nthaŵi zonse muzipemphe ndi mtima woyamika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 34:1

Ndidzayamika Chauta nthaŵi zonse, pakamwa panga padzatamanda Iye kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:2

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, ndipo usaiŵale zabwino zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:21

Inde ankamudziŵa Mulungu, koma m'malo mwa kumtamanda kapena kumthokoza, maganizo ao adasanduka opanda pake, ndipo m'mitima yao yopusa mudadzaza mdima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:12

Choncho ndisakhale chete, koma ndikutamandeni ndi mtima wonse. Choncho mtima wanga udzakuimbirani mosalekeza, Chauta, Mulungu wanga, ndidzakuthokozani mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 69:30

Ndidzatamanda dzina la Mulungu pomuimbira nyimbo, ndidzalalika ukulu wake pomuthokoza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:29

Thokozani Chauta pakuti ngwabwino, ndipo chikondi chake chosasinthika nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:12

Ndipo timapemphera kuti muziyamika Atate, amene adakuyenerezani kuti mudzalandire nao madalitso onse amene amasungira anthu ao mu ufumu wa kuŵala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 16:34

Thokozani Chauta, pakuti ngwabwino, chikondi chake chosasinthika nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:10

Zamoyo zonse zidzakuthokozani, Inu Chauta, anthu anu onse oyera mtima adzakutamandani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 92:1

Nkwabwino kuthokoza Chauta, kuimba nyimbo zotamanda dzina lanu, Inu Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 15:36

Kenaka adatenga buledi msanu ndi muŵiri uja, ndi nsomba zija, adathokoza Mulungu, nazinyemanyema nkuzipereka kwa ophunzira ake, iwowo nakazigaŵira anthu aja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 86:12

Inu Ambuye, Mulungu wanga, ndikukuthokozani ndi mtima wanga wonse, ndidzalemekeza ukulu wanu mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 136:26

Thokozani Mulungu wakumwamba, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:1

Ndidzakuthokozani, Inu Chauta, ndi mtima wanga wonse. Ndidzasimba za ntchito zanu zonse zodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 9:15

Tiyamike Mulungu chifukwa cha mphatso yake yosaneneka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 50:14

“Koma perekani nsembe zanu zothokozera kwa Mulungu, ndipo muchite zimene mudalumbira kwa Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:21

Ndikukuyamikani popeza kuti mwandiyankha, ndipo mwasanduka Mpulumutsi wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:1

Fuulani kwa Chauta ndi chimwemwe, inu maiko onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 126:3

Ndithudi, Chauta watichitira zazikulu, ndipo tasangalala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 13:6

Ndidzaimbira Chauta, popeza kuti wandichitira zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:17

Ndidafuula kwa Iye, ndipo ndidamtamanda ndi pakamwa panga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:14

Koma ine ndidzakhulupirira Inu nthaŵi zonse, ndipo ndidzapitirizabe kukutamandani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:62

Ndimadzuka pakati pa usiku kuti ndikutamandeni, chifukwa cha malangizo anu olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 1:2

Timathokoza Mulungu nthaŵi zonse chifukwa cha inu nonse ndi kumakutchulani m'mapemphero athu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:7

Imbirani Chauta mothokoza, imbirani Mulungu wathu nyimbo yokoma ndi pangwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 42:11

Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika choncho m'kati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamtamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:15

Nchifukwa chake, kudzera mwa Yesu tiyeni tipereke kosalekeza mayamiko athu kwa Mulungu ngati nsembe. Ndiye kunena kuti tipereke ngati nsembe mau athu ovomereza dzina lake poyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:2

Tamandani Chauta ndi pangwe. Muimbireni nyimbo ndi zeze wa nsambo khumi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 8:1

Chauta, Ambuye athu, dzina lanu ndi lotchuka pa dziko lonse lapansi. Kumwamba amaimba nyimbo zotamanda ulemerero wanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 118:14

Chauta amene ndimamuimbira ndiye mphamvu zanga. Ndiye mpulumutsi wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 149:1

Tamandani Chauta! Imbirani Chauta nyimbo yatsopano, imbani nyimbo yomtamanda pa msonkhano wa anthu ake oyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:7

Adzasimba za ubwino wanu, adzaimba nyimbo zotamanda kulungama kwanu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 32:11

Sangalalani ndi kukondwa inu nonse okonda Mulungu, chifukwa cha zimene Chautayo adakuchitirani. Inu anthu ake onse, fuulani ndi chimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:5

Mudzandikhutitsa ndi zonona, ndipo ndidzakutamandani ndi mau osangalala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 29:13

Tsopano tikukuthokozani, Inu Mulungu wathu, ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 51:15

Ambuye, tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalankhula zotamanda Inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 104:33

Ndidzaimbira Chauta moyo wanga wonse. Ndidzaimba nyimbo zotamanda Chauta, nthaŵi zonse pamene ndili moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:4

Muzikondwa mwa Ambuye nthaŵi zonse. Ndikubwerezanso kuti, “Muzikondwa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:20-21

Tamandani Chauta, inu angelo ake, inu amphamvu amene mumamva mau ake, amene mumachita zimene amalamula. Tamandani Chauta, inu magulu a ankhondo ake onse, atumiki ake ochita zimene Iye afuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:2

Ndidzakondwa ndi kusangalala chifukwa cha Inu, ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu, Inu Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 75:1

Tikukuthokozani Inu Mulungu, ndithu tikukuthokozani. Tikutchula dzina lanu mopemphera ndipo tikulalika ntchito zanu zodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:2

Ndikugwada moŵerama kumaso kwa Nyumba yanu yoyera. Ndikutamanda dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika, chifukwanso cha kukhulupirika kwanu. Mwakweza dzina lanu ndiponso malonjezo anu kupambana chinthu china chilichonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 33:1

Kondwerani mwa Chauta, inu anthu ake. Zoonadi ochita zolungama azitamanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 147:1

Tamandani Chauta! Nkwabwino kuimba nyimbo zotamanda Mulungu wathu, nkokondwetsa mtima kumtamanda moyenera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:17

Ndidzapereka kwa Inu nsembe yothokozera, ndidzapemphera potchula dzina la Inu, Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 111:1

Tamandani Chauta. Ndidzathokoza Chauta ndi mtima wanga wonse pa msonkhano wa anthu olungama mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:28

Koma ine kukhala pafupi ndi Mulungu kumandikomera. Ndatsimikiza zoti Ambuye ndiwo kothaŵira kwanga ndipo ndidzalalika ntchito zao zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 7:17

Ine ndidzathokoza Chauta chifukwa cha kulungama kwake, ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina la Chauta, Wopambanazonse uja.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 12:28

Popeza kuti talandira ufumu wosagwedezeka, tizithokoza Mulungu, ndipo pakutero timpembedze moyenera, mwaulemu ndi mwamantha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:8

Lemekezani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthunu, mau omtamanda Iye amveke.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:22

Tamandani Chauta, inu zolengedwa zake zonse, ku madera onse a ufumu wake. Nawenso mtima wanga, tamanda Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 105:1

Thokozani Chauta, tamandani dzina lake, lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 9:11

Imbani nyimbo zotamanda Chauta amene amakhala ku Ziyoni. Lalikani za ntchito zake kwa anthu a mitundu yonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 106:1

Tamandani Chauta. Thokozani Chauta chifukwa ngwabwino, pakuti chikondi chake nchamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 27:6

Ndidzapambana adani anga ondizungulira, ndipo ndidzapereka nsembe m'Nyumba mwake ndili kufuula ndi chimwemwe. Ndidzaimba nyimbo yotamanda Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 28:7

Chauta ndiye mphamvu zanga, ndiyenso chishango changa chonditeteza. Ndaika mtima wanga wonse pa Iye. Wandithandiza, choncho mtima wanga ukusangalala, ndipo ndimamthokoza ndi nyimbo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:3

Ndidzakutamandani chifukwa chikondi chanu nchabwino kupambana moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 12:4

Tsiku limenelo mudzati: “Thokozani Chauta, tamandani dzina lake. Mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 111:2

Ntchito za Chauta nzazikulu, onse okondwera nazo amazilingalira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:5

Uzikhulupirira Chauta ndi mtima wako wonse, usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:164

Ndimakutamandani kasanunkaŵiri pa tsiku, chifukwa cha malangizo anu olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 45:17

Ndidzamveketsa mbiri ku mibadwo yonse, nchifukwa chake mitundu ya anthu idzakutamandani mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:4

Anthu onse a pa dziko lapansi amakupembedzani, amaimba nyimbo zotamanda Inu, amaimba nyimbo zotamanda dzina lanu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:12

Ndidzambwezera chiyani Chauta pa zabwino zonse zimene adandichitira?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:7

Ndidzakutamandani ndikuchita zoyenera, ndikaphunzira malangizo anu olungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 29:10

Nchifukwa chake Davide adatamanda Chauta pamaso pa msonkhano wonse. Adati, “Mutamandike mpaka muyaya Inu Chauta, Mulungu wa Israele, kholo lathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:1

Ndikukuthokozani Inu Chauta ndi mtima wanga wonse. Ndikuimba nyimbo zokutamandani pamaso pa milungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 25:1

Inu Chauta, ndinu Mulungu wanga. Ndidzakulemekezani ndi kutamanda dzina lanu. Pakuti mwachita zinthu zodabwitsa mokhulupirika ndi motsimikiza, zinthu zimene mudakonzeratu kalekale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:1

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:1

Ndidzakuyamikani, Inu Mulungu wanga, mfumu yanga, ndidzalemekeza dzina lanu nthaŵi zonse mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 92:2

Nkwabwino m'maŵa kulalika za chikondi chanu chosasinthika, ndipo usiku kusimba za kukhulupirika kwanu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:3

Dziŵani kuti Chauta ndiye Mulungu. Ndiye amene adapanga ife, ndipo ifeyo ndife ake. Ndife anthu ake, nkhosa za busa lake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:16-17

Khalani okondwa nthaŵi zonse. Muzipemphera kosalekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 30:4

Imbani nyimbo zotamanda Chauta, inu anthu ake oyera mtima, mumthokoze chifukwa cha dzina lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:4

Mafumu onse a m'dziko adzakutamandani, Inu Chauta, chifukwa amva mau a pakamwa panu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:19

Ndidzazipereka m'mabwalo a Nyumba ya Mulungu, mu mzinda wa Yerusalemu. Tamandani Chauta!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 22:27

Anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi adzakumbukira nadzatembenukira kwa Chauta, mabanja a mitundu ina ya anthu adzampembedza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 48:1

Chauta ndi wamkulu, ndi woyenera kumutamanda kwambiri. Timuyamike mu mzinda wake, pa phiri lake loyera,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 67:3

Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu, mitundu yonse ya anthu ikuyamikeni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 98:4

Fuulirani Chauta ndi chimwemwe, inu dziko lonse lapansi. Muimbireni mokondwa nyimbo zotamanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:11

Ndiponso akuti, “Inu nonse a mitundu ina, tamandani Ambuye, anthu a mitundu yonse amtamande.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:1

Ndimakonda Chauta chifukwa amamva mau anga omupemba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mbiri 16:8

Thokozani Chauta, tamandani dzina lake, lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 41:13

Atamandike Chauta, Mulungu wa Israele, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Inde momwemo. Inde momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 100:5

Paja Iye ndi wabwino. Chikondi chake nchamuyaya, kukhulupirika kwake nkosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:1

Tamandani Mulungu ndi chimwemwe mokweza mau, inu anthu onse a pa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 139:14

Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 47:1

Ombani m'manja inu anthu a mitundu yonse. Fuulani kwa Mulungu poimba nyimbo zachimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 6:13

Musapereke chiwalo chilichonse cha thupi lanu ku uchimo, kuti chigwire ntchito zotsutsana ndi chilungamo. Inu mudzipereke kwa Mulungu, monga anthu amene anali akufa, koma tsopano ali amoyo. Ndipo mupereke ziwalo zanu zonse kwa Mulungu, kuti zigwire ntchito zachilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 95:6

Bwerani, timpembedze ndi kumlambira. Tiyeni tigwade pamaso pa Chauta Mlengi wathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 149:5

Okhulupirika akondwerere chigonjetso chopambanachi, aziimba mokondwa ali gone pa mabedi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:5

Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zake nzodabwitsa pakati pa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 91:15

Akadzandiitana, ndidzamuyankha, ndidzakhala naye pa nthaŵi yamavuto. Ndidzamlanditsa ndi kumlemekeza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 107:8

Athokoze Chauta chifukwa cha chikondi chake chosasinthika, chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa kwa anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:28

Ndipo tikudziŵa kuti Mulungu amayendetsa zinthu mwa njira yoti zonse ziŵakomere anthu omukonda ndipo apindulepo. Anthuwo ndi amene Iye amaŵaitana monga momwe Iye adazikonzera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 71:23

Pakamwa panga padzafuula ndi chimwemwe, pamene ndikukuimbirani nyimbo zotamanda. Nawonso mtima wanga umene mwauwombola, udzaimba moyamika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 145:2

Ndidzakuthokozani tsiku ndi tsiku, ndidzatamanda dzina lanu mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 63:4

Choncho ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga. Ndidzakweza manja anga kwa Inu mopemphera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 116:2

Iye amatchera khutu kuti andimve, nchifukwa chake ndidzampempha nthaŵi zonse pamene ndili moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:23

Tilimbikire kuvomereza mosafookera zimene timaziyembekeza, pakuti Iye amene adatilonjeza zimenezi ngwokhulupirika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye, ndinu Alfa ndi Omega! Atate, Mlengi wa thambo ndi dziko lapansi, ndinu woyamba ndi wotsiriza, chiyambi ndi chimaliziro. Zikomo chifukwa chondikokera ndi dzanja lanu ndipo ndimatha kuyenda molimba mtima pamodzi nanu, ndithandizeni kukhala ndi mtima woyamikira nthawi zonse osayang'ana zomwe ndikusowa, koma kuyamikira ndi chimwemwe zomwe mwandipatsa kale. Lero ndikufuna kukuwonetsani kuyamikira kwanga chifukwa cha chikondi chanu chachikulu ndi chifundo, chifukwa mwandipulumutsa ndi kundikhululukira. Zikomo Ambuye, chifukwa mwawonjezera madalitso pa moyo wanga ndipo pakati pa mavuto simunandileke kapena kundisiya. Mawu anu amati: "Mundionetsa njira ya moyo; Pamaso panu pali chimwemwe chochuluka; Zokondweretsa kudzanja lanu lamanja kwamuyaya." Zikomo chifukwa cha zokumana nazo zoipa chifukwa zakhala aphunzitsi abwino ndipo zandiphunzitsa kuti ndiyenera kukumbukira nthawi zonse kuti usiku wakuda kwambiri, umatuluka nyenyezi zowala kwambiri. Zikomo chifukwa cha zabwino zanu, chifukwa ndinu amene mumakhululukira mphulupulu zanga zonse, amene muchiritsa matenda anga onse, amene mupulumutsa moyo wanga ku dzenje ndi kundiveka korona wachisomo ndi chifundo. Ambuye Yesu, zikomo chifukwa munali inu amene munabwezeretsa chiyembekezo cha moyo wosatha mwa ine ndipo kuchokera pa mtanda mwandiwonetsa chikondi chachikulu ndi chowona mtima, kundipatsa chikhululukiro chanu ndi chipulumutso kumeneko. Ndikukuthokozani chifukwa mwasunga moyo wanga ndi wa banja langa ku ziwembu ndi misampha ya mdani. M'dzina la Yesu. Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa