Ukunena sikuli bwino konse. Pamaso pa Mulungu, kunena bodza n’koipa ndipo kumabweretsa mavuto aakulu kwa amene akuchita zimenezi akapezeka. Usaname pothawa udindo wako kapena kuti ukondweretse munthu wina, chifukwa kunena bodza kumakupanga munthu wosakhulupirika.
Ukamabodza, umadziwa bwino zomwe ukuchita, ndipo ngati chikumbumtima chako sichikukuvutitsa, ndiye kuti waopa Mulungu ndipo wazolowela bodza. Ngati ukhoza kunena bodza ukuyang’ana munthu m’maso, uli pa njira yolakwika, osati chifukwa cha zimene ukuchitira munthuyo, koma chifukwa chakuti suganizira momwe Mulungu amakuonera.
Munthu akayamba kunena bodza, amakhala munthu wopanda komanso wozizira. Poyamba ungaganize kuti kunena bodza kamodzi sikuli koipa kwenikweni, koma ukabwerezanso ukuchita kutsegula khomo, ndipo ukazindikira, zidzakhala mochedwa, sungathe kusiya ndipo watsegula chibowo chachikulu. Bodza lingakulekanitse ndi Mulungu ndikupangitsa kuti utayitse mabwenzi ofunika komanso maubwenzi.
Wabodza amadzinyenga yekha, akutaya ulemu, kuyamikiridwa ndi chitetezo. Tsopano popeza wadziwa zonsezi, samala ndi mawu otuluka pakamwa pako ndipo usakhale kapolo wa mizimu yoipa yomwe ikufuna kuti usanene zoona. Bodza limakhala msampha womwe ungatulukemo pokhapokha ngati wavomereza machimo ako kwa Khristu, kutaya zoipa ndi kukhala ndi mtima wowona nthawi zonse.
Kunena bodza kumakulekanitsa ndi Mulungu, usadziloŵetse m’moyo wopanda kukhalapo kwake. Ulipobe nthawi yoti uwongolere njira yako ndikuchita zoyenera.
Koma ochita zautchisi, zaufiti, zadama, zopha anzao, zopembedza mafano, ndi okonda zabodza nkumazichita, adzakhala kunja kwa mzindawo.
Musamauzana mabodza, pakuti mwachita ngati mwavula moyo wanu wakale, pamodzi ndi zochitachita zake zoipa,
Munthu wokonda Mulungu amadana ndi bodza, koma zochita za munthu woipa zimanyansa ndipo zimachititsa manyazi.
Ndimadana ndi anthu abodza, zoonadi, ndimanyansidwa nawo, koma ndimakonda malamulo anu.
Koma anthu amantha, osakhulupirika, okonda zonyansa, opha anzao, ochita zadama, ochita zaufiti, opembedza mafano, ndi anthu onse onama, malo ao ndi m'nyanja yodzaza ndi moto ndi miyala ya sulufure woyaka. Imeneyi ndiyo imfa yachiŵiri.”
Koma Petro adamufunsa kuti, “Iwe Ananiya, chifukwa chiyani walola mtima wako kugwidwa ndi Satana mpaka kumanamiza Mzimu Woyera pakupatula ndalama zina za munda wako?
Malamulo amaŵaika chifukwa cha anthu adama, ochimwa ndi amuna anzao, oba anthu, amabodza, olumbira monama, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona.
Palibe munthu wochita zonyenga amene adzakhale m'nyumba mwanga. Palibe munthu wolankhula zabodza amene adzakhale pafupi ndi ine.
Kulankhula kwabwino sikuyenerana ndi chitsiru. Nanji kulankhula kwabodza, kodi kungayenerane ndi mfumu?
Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Chauta amadana nazo, makamaka zisanu ndi ziŵiri ndithu zimene zimamunyansa: maso onyada, pakamwa pabodza, manja opha munthu wosalakwa, mtima wokonzekera kuchita zoipa, mapazi othamangira msangamsanga ku zoipa, mboni yonama yolankhula mabodza, ndi munthu woutsa chidani pakati pa abale.
Otsala a mu Israeleŵa sadzalakwanso, sadzalankhulanso zabodza, sadzachitanso zonyenga, Adzakhala pabwino mwamtendere, popanda wina woŵaopsa.”
Aweruziwo adzafufuze za mlanduwo. Akapeza kuti munthu uja ndi mboni yachabe ndipo kuti waneneza mnzake monama, amlange pomchita choipa chimene iyeyo anati achite mnzake. Mwa njira imeneyi, mudzachotsa choipa chimenechi pakati pa inu.
Pakamwa pabodza pamamnyansa Chauta. Koma anthu ochita zinthu mokhulupirika amamkondweretsa.
Tsono lekani kunama. Aliyense azilankhula zoona zokhazokha ndi mkhristu mnzake, pakuti tonse pamodzi mogwirizana ndife ziwalo za thupi la Khristu.
M'kamwa mwao m'moopsa ngati manda apululu, ndi lilime lao amalankhula zonyenga, pamilomo pao pamatuluka mau aululu, ululu wake wonga wa mamba. M'kamwa mwao m'modzaza ndi matemberero, mumatuluka mau oŵaŵa.
Inu ndinu ana a Satana. Iye ndiye tate wanu, ndipo mukufuna kumachita zimene tate wanuyo amalakalaka. Iye uja chikhalire ngwopha anthu. Sadakhazikike m'zoona, chifukwa mwa iye mulibe zoona. Kunena bodza ndiye khalidwe lake, pakuti ngwabodza, nkukhalanso chimake cha mabodza onse.
Paja mau a Mulungu akuti. “Yemwe afuna kukondwera ndi moyo, ndi kuwona masiku abwino, aletse lilime lake kulankhula zoipa, ndiponso milomo yake kunena mabodza.
Tsiku lonse umakhalira kusinkhasinkha za kuwononga ena, lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nkunyenga. Umakonda zoipa kupambana zabwino, umakonda kunama kupambana kulankhula zoona. Umakonda kulankhula mau ovutitsa ena, iwe wabodzawe.
Muzichita izi: muzikambirana zoona, muziweruza moona ndi mwamtendere m'mabwalo a milandu.
Koma ngati muli ndi mtima wakaduka ndi wodzikonda, musamanyada ndi kutsutsana ndi choona pakunena mabodza. Nzeru zotere si zochokera Kumwamba, koma ndi nzapansipano, ndi za anthu chabe, ndiponso nzochokera ku mizimu yoipa.
Inu mumaŵaononga anthu olankhula zonama. Inu Chauta mumanyansidwa nawo anthu onyenga ndi opha anzao.
Mitima yao idadzaza ndi zosalungama zamitundumitundu, monga kuipa, umbombo ndi dumbo. Amangolingalira za kaduka, za kupha anthu, za ndeu, za kunyenga, ndi za njiru. Amachita ugogodi,
Chifukwa m'kati mwa mitima ya anthu ndiye mumatuluka maganizo oipa, za kuphana, za chigololo, za chiwerewere, za kuba, maumboni onama, ndiponso zachipongwe.
Musalole kuti ndikhale wabodza kapena wonama. Ndisakhale mmphaŵi kapena khumutcha. Muzindidyetsa chakudya chondiyenera,
Munthu akamati, “Ine ndimadziŵa Mulungu”, koma chikhalirecho satsata malamulo ake, angonama ameneyo, ndipo mwa iye mulibe choona.
Koma Isaki adayankha kuti, “Mng'ono wako anabwera, ndipo wandinyenga. Iyeyo ndiye amene watenga madalitso ako onse.”
Munthu akakuchitani choipa, musamubwezere choipa. Yesani kuchita zimene anthu onse amaziwona kuti nzabwino.
“Usatchule pachabe dzina la Chauta, Mulungu wako, chifukwa Mulunguyo sadzamleka aliyense wotchula pachabe dzina lakelo.
Anthu oipa ndi osokera kuyambira ali m'mimba mwa mai ao, anthu amabodza ndi otayika kuyambira tsiku la kubadwa kwao.
Usamafulumira kulankhula, ndipo usamalumbira msanga kwa Mulungu mumtima mwako. Paja Mulungu ali Kumwamba, iwe uli pansi pano, tsono usamachulukitsa mau ai.
Chuma chomachipeza monyenga chimangoti wuzi ngati nthunzi, ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
Akulu a ansembe aja ndi onse a m'Bwalo Lalikulu la Ayuda ankafunafuna umboni wonama woneneza Yesu kuti amuphe. Tsiku lina Yesu anali ku Betaniya, m'nyumba ya Simoni wotchedwa Wakhate. Koma sadaupeze ngakhale padaabwera mboni zambiri zabodza. Potsiriza padabwera anthu aŵiri.
Mundichotse m'njira zondisokeza, kuti ndisayendemo. Mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Munthu wochitira mnzake umboni wonama, amapweteka mnzakeyo ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
Takaniratu njira zonse zochititsa manyazi zimene anthu amatsata mobisika. Sitichita kanthu monyenga kapena kupotoza mau a Mulungu; koma pakulankhula zoona poyera pamaso pa Mulungu, tifuna kuti anthu onse ativomereze m'mitima mwao.
Ndidzatsata njira yopanda cholakwa. Nanga mudzabwera liti kwa ine? Ndidzakhala ndi mtima wangwiro m'nyumba mwanga. Sindidzaika maso anga pa chinthu chilichonse chachabechabe. Ndimadana ndi zochita za anthu okusiyani, sizindikomera konse.
Tsono iwe wophunzitsa ena, bwanji sukudziphunzitsa wekha? Iwe wolalika kuti, “Osamaba,” bwanji iwenso umaba?
Ungwiro wa anthu olungama umaŵatsogolera, koma makhalidwe okhota a anthu onyenga ngoononga.
Koma tsopano musachitenso zonsezi, monga kukalipa, kukwiya, kuipa mtima, ndi mijedu. Pakamwa panu pasamatulukenso mau otukwana kapena onyansa.
Musadzinyenge, nkosatheka kupusitsa Mulungu. Zimene munthu amabzala, adzakolola zomwezo.
Zophunzitsa zimenezi nzochokera ku chinyengo cha anthu onama, amene mumtima mwao adalembedwa chizindikiro ndi chitsulo chamoto.
Munthu wina aliyense asakupusitseni ndi mau onyenga, pakuti zinthu zotere ndizo zimadzetsa ukali wa Mulungu pa anthu omupandukira.
Chauta amakonda chilungamo, sadzaŵasiya okha anthu ake okhulupirika. Iye adzawasunga mpaka muyaya, koma adzaononga ana a anthu oipa.
Ndikunenetsa kuti pa tsiku la chiweruzo, anthu adzazengedwa mlandu chifukwa cha mau aliwonse opanda pake amene adaalankhula.
Tikanena kuti timayanjana naye, pamene tikuyendabe mu mdima, tikunama, ndipo zochita zathu nzosagwirizana ndi zoona.
Mkwiyo wa Mulungu ukuwoneka kuchokera Kumwamba. Amakwiyira anthu chifukwa cha kusalungama kwao konse ndi kusamchitira ulemu. Kusalungama kwaoko kumaŵalepheretsa kudziŵa zoona.
Ngati wina akudziyesa woika mtima pa zopembedza Mulungu, koma nkukhala wosasunga pakamwa, chipembedzo chakecho nchopanda pake, ndipo amangodzinyenga.
“Munthu akaba ng'ombe kapena nkhosa, nkuipha kapena kuigulitsa, alipire ng'ombe zisanu pa ng'ombe imodzi, kapena nkhosa zinai pa nkhosa imodzi.
Ndi munthu amene amayenda mosalakwa, amene amachita zolungama nthaŵi zonse, amene amalankhula zinthu ndi mtima woona. Ndi amene sasinjirira ndipo sachita anzake zoipa, kapena kumafalitsa mbiri yoipa ya anzake.
Ine ndidaaona kuti iwo sakuyenda molunjika, sakutsata choona cha Uthenga Wabwino. Tsono ndidauza Petro pamaso pa onse kuti, “Iwe ndiwe Myuda, komabe ukukhala ngati munthu wa mtundu wina, osati Myuda. Nanga ungakakamize bwanji anthu a mitundu ina kukhala ngati Ayuda?”
Nchifukwa chake tayani choipa chonse, kunyenga konse, chiphamaso, kaduka ndi masinjiriro onse.
Sindidzaika maso anga pa chinthu chilichonse chachabechabe. Ndimadana ndi zochita za anthu okusiyani, sizindikomera konse.
Takupandukirani, takukanani, Inu Chauta, ndipo takana kukutsatani. Tapanikiza anzathu, takupandukirani Inu. Maganizo athu ndi abodza, mau athu ndi onama.
“Nchifukwa chake Ine Ambuye Chauta ndikuti, Aisraele inu, aliyense mwa inu ndidzamuweruza molingana ndi ntchito zake. Lapani, tembenukani mtima, kuti machimo anu asakuwonongeni.
Tilimbikire kuvomereza mosafookera zimene timaziyembekeza, pakuti Iye amene adatilonjeza zimenezi ngwokhulupirika.
Wobisa machimo ake sadzaona mwai, koma woulula ndi kuleka machimo, adzalandira chifundo.
Kodi mumagamuladi molungama, inu akuluakulu oweruza? Kodi mumaweruzadi anthu mwachilungamo? Munthu wangwiro adzakondwera poona kulipsirako. Adzasamba mapazi ake m'magazi a anthu oipawo. Motero anthu adzati, “Zoona, olungama amalandiradi mphotho. Alipodi Mulungu amene amaweruza pa dziko lapansi.” Iyai, mitima yanu imangolingalira zoipa, kuweruza kwanu kosalungama kumadzetsa chiwawa.
Kwa anthu oyera mtima mumadziwonetsa okoma mtima, koma kwa anthu oipa mtima mumadziwonetsa ochenjera koposa.
Ndithudi ndikunena zoona ine amene ndili wake wa Khristu, ndipo sindikunama ai. Mtima wanga, umene Mzimu Woyera amautsogolera, ukundichitira umboni kuti
Ndikadazindikira choipa chilichonse mumtima mwanga ndi kuchibisa, Ambuye sakadandimvera.
Ananu, chikondi chathu chisamangokhala cha nkhambakamwa chabe, koma chiziwoneka pa zochita zathu.
Ulewe zabodza, zosinjirira. Usaphe munthu wosalakwa ndi wosapalamula, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.
Chauta amayang'anira bwino anthu odziŵa zinthu, koma mau a anthu osakhulupirika, Iye amaŵalepheretsa.
Chikondi chizikhala chopanda chiphamaso. Muzidana ndi zoipa, nkumaika mtima pa kuchita zabwino.
“Chenjera nawoni aneneri onyenga. Amadza kwa inu ali ndi maonekedwe ofatsa ngati nkhosa, koma m'kati mwao ndi mimbulu yolusa.
Paja mau a Mulungu akuti. “Yemwe afuna kukondwera ndi moyo, ndi kuwona masiku abwino, aletse lilime lake kulankhula zoipa, ndiponso milomo yake kunena mabodza. Alewe zoipa, azichita zabwino. Afunefune mtendere ndi kuyesetsa kuupeza.
Musandichotsere kumodzi ndi anthu oipa, anthu amene amachita zonyenga, amene amalankhula zamtendere ndi anzao, koma mitima yao ndi yodzaza ndi chidani.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wokhoza ndiye, mpaka mnzake atabwera nadzamufunsitsa bwino.
Ndidzatsata njira yopanda cholakwa. Nanga mudzabwera liti kwa ine? Ndidzakhala ndi mtima wangwiro m'nyumba mwanga.
Ndithudi ndikunena zoona ine amene ndili wake wa Khristu, ndipo sindikunama ai. Mtima wanga, umene Mzimu Woyera amautsogolera, ukundichitira umboni kuti Ndipo si pokhapo ai. Ana aŵiri a Rebeka aja bambo wao anali mmodzi, kholo lathu Isaki. Ngakhale anawo asanabadwe, ndiye kuti tsono asanachite chilichonse chabwino kapena choipa, Mulungu adaafunabe kuti cholinga chake chosankhira munthu aliyense chipitirire. Izi adachita osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifukwa chakuti Mulungu adamuitana munthuyo. Motero Mulungu adauza Rebeka kuti, “Wamkuluyu adzatumikira wamng'onoyu.” Paja Malembo akuti, “Yakobe ndidaamukonda, koma Esau ndidaadana naye.” Pamenepo tinganene chiyani tsono? Kodi tinganene kuti Mulungu ngwosalungama? Iyai, sitingatero. Pajatu Iye adaauza Mose kuti, “Ndidzachitira chifundo amene ndifuna kumchitira chifundo, ndidzamvera chisoni amene ndifuna kumumvera chisoni.” Motero chachikulu si zimene munthu azifuna, kapena zimene munthu amayesetsa kuchita, koma chachikulu ndi chifundo cha Mulungu. Ndi monga m'Malembo timaŵerenga kuti Mulungu adaauza Farao kuti, “Ndidakulonga ufumu, kuti mwa iwe ndiwonetse mphamvu zanga, ndiponso kuti ndimveketse dzina langa pa dziko lonse lapansi.” Motero timaona kuti Mulungu amachitira chifundo munthu amene Iye afuna kumchitira chifundo, ndipo amamsandutsa wokanika munthu amene Iye afuna kumsandutsa wokanika. Tsono kapena wina nkundifunsa kuti, “Ngati zili choncho, chifukwa chiyani Mulungu akuŵadzudzulabe anthu? Nanga ndani angaletse Mulungu kuchita zimene Iye afuna?” ndili ndi chisoni chachikulu. Ndipo ukundipweteka kosalekeza chifukwa cha abale anga, anthu a mtundu wangaŵa. Koma iwe, munthu chabe, ndiwe yani kuti nkumatsutsana ndi Mulungu? Kodi mbiya nkufunsa woiwumba kuti, “Bwanji mwandiwumba motere?” Kodi kapena woumba sangathe kuumba mbiya ziŵiri ndi dothi lomwelo, ina ya masiku apadera ina ya masiku onse? Mulungunso ndi momwemo. Adaafuna kuwonetsa mkwiyo wake, nafunanso kuti mphamvu zake zidziŵike. Komabe adapirira moleza mtima kwambiri zochita za anthu amene Iye adaaŵakwiyira, ndipo amene adaayeneradi kuwonongedwa. Mulungu adaafunanso kuti udziŵike ulemerero wake waukulu pa ife, amene Iye adatichitira chifundo, natikonzeratu kuti tilandire ulemerero. Pajatu ife ndife amene Mulungu adatiitana, osati kuchokera kwa Ayuda okha ai, komanso kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Ndi monga momwe Mulungu akunenera m'buku la mneneri Hoseya kuti, “Amene sanali anthu anga, ndidzaŵatcha ‘Anthu anga’. Mtundu umene sindinkaukonda, ndidzautcha ‘Wokondedwa wanga’. Ndipo kumalo komwe iwo adauzidwa kuti, ‘Sindinu mtundu wanga’, kumeneko adzatchedwa ‘Ana a Mulungu wopatsa moyo.’ ” Ndipo mneneri Yesaya adaanena mokweza mau za Aisraele kuti, “Ngakhale Aisraele achuluke ngati mchenga wakunyanja, koma oŵerengeka okha adzapulumuka. Pakuti Ambuye adzagamula milandu ya anthu pa dziko lapansi. Ndipo adzachita zimenezi mofulumira ndi mwachidule.” Izi zili monga momwe Yesaya adaaneneratunso kale kuti, “Ambuye amphamvuzonse akadapanda kutisiyirako zidzukulu zina, tikadafafanizidwa ngati Sodomu ndi Gomora.” Ndikadakonda kuti m'malo mwao, ineineyo ndikhale wotembereredwa, osakhalanso wake wa Khristu.
Anthu anga amadzasonkhana kwa iwe nakhala pansi kuti amve zimene iweyo unene. Koma akazimva, sazitsata zimenezo. Zokamba zao zimaonetsa chikondi, m'menemo mitima yao imangokonda phindu chabe.
Munthu wosauka amene amayenda mwaungwiro amaposa kwambiri munthu wolemera amene ali wonyenga.
Ndakulemberani, osati chifukwa chakuti simudziŵa choona, koma chifukwa chakuti mumachidziŵa, ndipo mukudziŵanso kuti bodza silichokera ku choona.
Ndikukupemphani abale, chenjera nawoni anthu amene amapatutsa anzao naŵachimwitsa. Iwo amaphunzitsa zosiyana ndi zimene inu mudaphunzira. Muziŵalewa,
Inunso muli chimodzimodzi: pamaso pa anthu mumaoneka olungama, pamene m'kati mwanu m'modzaza ndi chiphamaso ndi zoipa zina.
Motero musaweruziretu munthu aliyense, Ambuye asanabwere. Iwo ndiwo adzaunika pa zonse zobisika mu mdima, ndipo adzaulula maganizo a m'mitima mwa anthu. Pamenepo aliyense adzalandira kwa Mulungu chiyamiko chomuyenerera.
Inu Chauta, kodi ndani angathe kukhala m'Nyumba mwanu? Ndani angathe kukhala pa phiri lanu loyera? Ndi munthu amene amayenda mosalakwa, amene amachita zolungama nthaŵi zonse, amene amalankhula zinthu ndi mtima woona.