Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


122 Mau a m'Baibulo Okhudza Kudzikuza

122 Mau a m'Baibulo Okhudza Kudzikuza

Mtima wanga, dziwani kuti dyera ndi chinthu chomwe chimatigwira tonse, mosasamala kanthu za msinkhu wathu, kapena kuti ndife ndani.

M’Baibulo, muli nkhani zambiri zomwe zimatithandiza kuzindikira kuopsa kwa dyera. M’buku la Mlaliki, Mfumu Solomoni inalankhula za kufupika kwa moyo ndi kupanda pake kwa chuma ndi ulemerero wa dziko lapansi. Iye amatilimbikitsa kuyika chiyembekezo chathu mwa Mulungu, chifukwa zonse zomwe tili nazo ndi zomwe tinakwanitsa zidzatha.

Yesu, m’Chipangano Chatsopano, anatiphunzitsa kufunika koika maganizo athu pa zinthu zosatha, osati kufuna kuvomerezedwa ndi anthu. Mawu ake amatipatsa njira yopezera cholinga chenicheni cha moyo wathu, moyo wodzaza ndi chikondi cha Mulungu ndi cha anansi athu.

Dyera limatiletsa kukhala odzichepetsa ndipo limatipangitsa kufuna kudzikweza tokha, kuiwala chikondi ndi chifuniro cha Mulungu. Tiyeni tichenjere zimenezi.




Yobu 35:13

Ndithudi, Mulungu saamva kupempha kopanda pake, Mphambe sasamalako zimenezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:16

Paja zonse zapansipano, zilakolako zathupi, zinthu zimene maso amakhumbira, ndiponso kunyadira za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku mkhalidwe woipa wa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:11

Chuma chochipeza mofulumira chidzanka chitha pang'onopang'ono, koma chochipeza pang'onopang'ono chidzanka chichulukirachulukira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 31:30

Nkhope yachikoka ndi yonyenga, kukongola nkosakhalitsa, koma mkazi woopa Chauta ndiye woyenera kumtamanda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 5:10

Anthu okonda ndalama sakhutitsidwa nazo ndalamazo. Chimodzimodzinso anthu okonda chuma, sakhutitsidwa nalo phindu. Zimenezinso nzachabechabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 11:10

Choncho muchotseretu zokusautsani mu mtima mwanu, mupewe zokupwetekani m'thupi mwanu. Pajatu unyamata ndi ubwana, zonse nzopandapake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:8

Musalole kuti ndikhale wabodza kapena wonama. Ndisakhale mmphaŵi kapena khumutcha. Muzindidyetsa chakudya chondiyenera,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:19-21

“Musadziwunjikire chuma pansi pano, pamene njenjete ndi dzimbiri zimaononga, ndiponso mbala zimathyola ndi kuba. “Nchifukwa chake pamene mukupereka zachifundo, musachite modziwonetsera, monga amachitira anthu achiphamaso aja m'nyumba zamapemphero ndiponso m'miseu yam'mizinda. Iwoŵa amachita zimenezi kuti anthu aŵatame. Ndithu ndikunenetsa kuti amenewo alandiriratu mphotho yao. Koma mudziwunjikire chuma Kumwamba, kumene njenjete kapena dzimbiri siziwononga, ndiponso mbala sizithyola ndi kuba. Pajatu kumene kuli chuma chako, mtima wakonso kokhala nkomweko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 4:4

Tsono ndidazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Zimenezinso nzopanda phindu, ndipo kuyesa kuzimvetsa nkungodzivuta chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 3:3-4

Kudzikongoletsa kwanu kusangokhala kwa maonekedwe akunja pakuluka tsitsi, ndi kuvala zamakaka zagolide ndi zovala zamtengowapatali. Koma kudzikongoletsa kwanu kukhale kwa moyo wam'kati, kukongola kosatha kwa mtima wofatsa ndi wachete. Moyo wotere ngwamtengowapatali pamaso pa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 4:2

Anthu inu, mudzaleka liti kunyoza ulemu wanga? Bwanji mukukondabe zinthu zachabechabe? Bwanji mukulakalakabe zinthu zonama?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 16:13

chifukwa cha zoipa zake ndi za Ela mwana wake, zimene onse aŵiriwo adaachita. Iwo adachimwitsa anthu a ku Israele, naputa mkwiyo wa Chauta, Mulungu wa Aisraele, chifukwa cha mafano ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 31:6

Inu mumadana ndi opembedza mafano achabechabe. Koma ine ndimakhulupirira Inu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:22

Momwe chimaonekera chipini chagolide chikakhala pa mpuno wa nkhumba, ndi momwenso kumakhalira kukongola kwa mkazi wam'kamwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 17:15

Iwowo adanyoza malamulo a Chauta ndi chipangano cha Chauta chimene Iye adachita ndi makolo ao. Adanyozanso zochenjeza za Chauta. Adatsata milungu yachabechabe, ndipo iwo omwe adasanduka achabechabe. Ankatsata zitsanzo za anthu a mitundu ina okhala nawo pafupi, ngakhale Chauta anali atalamula kuti asamachite mofanana ndi mitundu imeneyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 7:16

Ndatopa nawo moyo wanga, sindingakonde kukhala moyo nthaŵi zonse. Ingondisiyani, poti moyo wanga uli ngati mpweya chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 39:5

“Onani, mwandipatsa masiku ochepa chabe, nthaŵi ya moyo wanga siili kanthu pamaso panu. Ndithudi, munthu aliyense ndi mpweya chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 16:26

Nanga ndiye kuti munthu angapindulenji atapata zonse zapansipano, iyeyo nkutaya moyo wake? Munthu angalipire chiyani choti aombolere moyo wake?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 15:31

Asadzinyenge pokhulupirira zinthu zoipa zachabe, poti zinthu zachabezo ndizo zidzakhale malipiro ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 39:11

Inu mumalanga munthu pakumdzudzula chifukwa cha uchimo wake. Mumaonongeratu zimene iye amazikonda, monga m'mene chimachitira chifukufuku. Zoonadi, munthu aliyense ndi mpweya chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:6-7

Nzoonadi, kupembedza Mulungu kumapindulitsa kwambiri, malinga munthu akakhutira ndi zimene ali nazo. Sitidatenge kanthu poloŵa m'dziko lino lapansi, ndipo sitingathenso kutenga kanthu potulukamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:9

Anthu otsika ndi mpweya chabe, ngakhale anthu okwera ndi nthunzi chabe, onsewo ndi oluluka pa sikelo, ndi opepuka kupambana mpweya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:2

Akutame ndi wina, osati pakamwa pako pomwe, wosadziŵana naye akakutamanda, apo ndipo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 78:33

Choncho Mulungu adadula masiku ao kuti azimirire ngati mpweya, adadula zaka zao kuti zithere m'zoopsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 9:23-24

Chauta akunena kuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, munthu wamphamvu asanyadire mphamvu zake, ndipo munthu wolemera asanyadire chuma chake. Koma ngati wina afuna kunyadira, anyadire ichi chakuti amamvetsa za Ine, ndipo amandidziŵa. Amadziŵa kuti Ine ndine Chauta wokonda chifundo, chilungamo, ndi ungwiro pa dziko lapansi. Ndithudi, pazimenezi ndipo pali mtima wanga.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:11

Chauta amadziŵa maganizo a anthu kuti ndi mpweya chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:37

Letsani maso anga kuti asamayang'ane zachabe, mundipatse moyo monga momwe mudalonjezera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:11

Kudzikuza kwa anthu kudzatha, kudzitama kwa anthu kudzaonongedwa. Chauta yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 144:4

Munthu ali ngati mpweya, masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 144:8

amene amalankhula zabodza, ndipo amalumbira zonama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 12:15

Atatero adauza anthu aja kuti, “Chenjerani, ndipo mupewe khumbo lililonse lofuna zambiri. Pajatu ngakhale munthu akhale ndi chuma chochuluka chotani, chumacho sichingatchinjirize moyo wake.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:3

Musamachita kanthu ndi mtima wodzikonda, kapena wodzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa, ndipo aliyense aziwona anzake kuti ngomuposa iyeyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 144:11

Landitseni kwa adani ankhalwe, mundipulumutse m'manja mwa akunja, amene amalankhula zabodza, ndipo amalumbira zonama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:6-8

Kudamveka mau akuti, “Lengeza.” Ine ndidafunsa kuti, “Kodi ndilengeze chiyani?” Mau aja adati, “Ulengeze kuti anthu onse ali ngati udzu. Kukongola kwao kuli ngati maluŵa akuthengo. Udzu umauma, maluŵa amafota, Chauta akaziwuzira mpweya wake. Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu. Udzu umauma, maluŵa amafota, koma mau a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:3

Popeza kuti mwa kukoma mtima kwake Mulungu adandiitana kuti ndikhale mtumwi, ndikukuuzani inu nonse kuti musadziyese anzeru koposa m'mene muliri. Makamaka maganizo anu akhale odzichepetsa, molingana ndi kukula kwa chikhulupiriro chimene Mulungu wapatsa aliyense mwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 1:2

Zonse nzopanda phindu, akutero Mlaliki. Zonse nzachabechabe! Ndithudi zonse nzopandapake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 1:31

Nchifukwa chake, monga Malembo anenera, “Wofuna kunyada, anyadire Ambuye.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 1:14

Zonse zochitika pansi pano ndaziwona. Zonsezo nzopandapake, ndipo kuzifunafuna nkungodzivuta chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 2:1

Nthaŵi zina mumtima mwangamu ndinkati, “Ah! Tsopano ndiyesepo zokondweretsa, ndidzisangalatse.” Koma ai, zimenezinso zinali zopanda phindu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:3

Ngati munthu adziyesa kanthu, pamene chikhalirecho sali kanthu konse, amangodzinyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 2:15

Ndiye ine ndidayamba kulingalira kuti, “Kani zimene zimagwera chitsiru nanenso zidzandigwera zomwezo! Nanga tsono ineyo nzeru zambiri chotere nzanji?” Pamenepo ndidaona kuti zimenezinso nzopanda phindu!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 2:11

Tsono ndidayamba kulingalira zonse zimene ndidazichita, ntchito zolemetsa zonse zimene ndidazigwira, nkuwona kuti zonsezo zinali zopanda phindu. Kunali kungodzivuta chabe. Ndithu panalibe choti nkupindulapo pa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:18

Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wa mtima wodzikuza adzagwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 2:17

Motero moyo wanga ndidaipidwa nawo, chifukwa chakuti zonse zochitika pansi pano zimandimvetsa chisoni. Ndithudi, zonsezo nzopandapake, ndipo kuyesa kuzimvetsa nkungodzivuta chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 5:7

Maloto akachuluka pamachulukanso zokamba zachabechabe. Koma iwe uzilemekeza Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 12:8

Nkuwonatu Mlaliki akuti, “Zonse nzopanda phindu. Ndithudi, zonse nzopandapake.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 6:9

Kuli bwino kumangopenya zinthu ndi maso kupambana kumazilakalaka chamumtima. Zimenezinso nzopanda phindu, ndipo kuyesa kuzimvetsa nkungodzivuta chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:12

Pajatu aliyense wodzikuza adzamchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamkuza.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 5:18

Tsoka kwa amene amadzikokera machimo ambiri ndi kunama kwao, amene amalephera kudzimasula ku machimo awo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 16:7

Koma Chauta adauza Samuele kuti, “Usayang'ane maonekedwe ake, ngakhale kutalika kwa msinkhu wake, poti ndamkana ameneyo. Chauta sapenya monga m'mene apenyera anthu. Anthu amapenya zakunja, koma Chauta amapenya zamumtima.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 24:10

Mu mzinda wachisokonezo uja zonse zaonongedwa, nyumba iliyonse yatsekedwa, kotero kuti palibe wotha kuloŵamo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 29:21

Mulungu adzalanga anthu osinjirira anzao, ndiponso ophophonyetsa anthu ozengedwa mlandu. Adzalanganso amene amapereka umboni wonama, kuti anzao osalakwa asaweruzidwe molungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 1:24-25

Paja mau a Mulungu amanena kuti, “Anthu onse ali ngati udzu, ulemerero wao uli ngati duŵa lakuthengo. Udzu umauma, ndipo duŵa limathothoka, koma mau a Ambuye ngokhala mpaka muyaya.” Mau ameneŵa ndi Uthenga Wabwino umene walalikidwa kwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:24

Inuyo sindinu kanthu konse, ndipo zochita zanu nzopandapake. Amene amakupembedzaniyo amandinyansa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:26

Samvazaanzake nchitsiru, koma wotsata nzeru za ena adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 41:29

Ndithudi, milungu yonseyi njachabe, zochita zake si kanthu konse. Mafano ake osungunula ali ngati mphepo yachabechabe.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 8:5-6

Anthu omvera khalidwe loipalo, amaika mtima pa zilakolako zathupi. Koma anthu omvera Mzimu Woyera, amaika mtima pa zimene Mzimu Woyerayo afuna. Kuika mtima pa khalidwe lopendekera ku zoipa, ndi imfa yomwe, koma kuika mtima pa zimene Mzimu Woyera afuna, kumabweretsa moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 3:23

Kupembedza pa magomo sikuthandiza, kuchita maphwando pa mapiri kulibenso ntchito. Zoonadi, mwa Chauta, Mulungu wathu ndiye muli chipulumutso cha Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 3:19-20

Zimene zimachitikira anthu, zomwezonso zimachitikira nyama. Monga chinacho chimafa, chinacho chimafanso. Zonsezo zimapuma mpweya umodzimodzi, munthu saposa nyama. Zonsezi nzopandapake. pali nthaŵi yobadwa ndi nthaŵi yomwalira, pali nthaŵi yobzala ndi nthaŵi yozula zobzalazo. Zonse zimapita kumodzimodzi. Zonsezo nzochokera ku dothi, ndipo zimabwerera kudothi komweko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:3

Ndithudi, miyambo ya anthu a mitundu inayo nzopanda pake. Iwo aja amakadula mtengo ku nkhalango, munthu waluso namausema ndi nsompho.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 3:2

Muzifunafuna za Kumwamba, osati zapansipano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 10:15

Mafanowo ngachabechabe, ayenera kuŵaseka, ndipo pamene anthuwo adzalangidwe, mafanowo adzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 51:18

Mafanowo ngachabechabe, oyenera kuŵaseka, ndipo pamene anthuwo adzalangidwe, mafanowo adzaonongedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 90:10

Zaka za moyo wathu nzokwanira makumi asanu ndi aŵiri, tikakhala amphamvu, ndiye makumi asanu ndi atatu. Koma zaka zonsezo ndi za nkhaŵa ndi mavuto. Zakazo zimatha msanga, ife nkumapita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 4:7

Nanga adakusiyanitsa ndi anthu ena ndani? Kaya uli ndi chiyaninso chimene sudachite kuchilandira? Tsono ngati udachita kuzilandira, ukunyadiranji ngati kuti sudangozilandira chabe?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Maliro 2:14

Zinthu zimene aneneri ako adakuwonera m'masomphenya zinali zabodza ndi zonyenga. Iwo sadaonetse uchimo wako, kuti ukhalenso pabwino. Mau amene adakutengeraniwo anali abodza ndi osokeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:31

Tsono, kaya mulikudya, kaya mulikumwa, kaya mukuchita chilichonse, muzichita zonse kuti mulemekeze Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:21-22

Inde ankamudziŵa Mulungu, koma m'malo mwa kumtamanda kapena kumthokoza, maganizo ao adasanduka opanda pake, ndipo m'mitima yao yopusa mudadzaza mdima. Iwo amadziyesa anzeru, koma chikhalirecho ndi opusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 5:15

Monga momwe munthu adabadwira m'mimba mwa mai wake opanda kanthu, chonchonso adzapita maliseche. Pa zonse zimene adakhetsera thukuta, palibe nchimodzi chomwe chimene adzatenge m'manja mwake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:7

Wina amadziyesa wolemera, m'menemo alibe nkanthu komwe. Wina amadziyesa wosauka, m'menemo ali nchuma chochuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 9:25

Nanga ndiye kuti munthu wapindulanji atapata zonse zapansipano, iyeyo nkutaya moyo wake kapena kuuwononga?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 2:5

Iye akukufunsani kuti, “Kodi makolo anu adandipeza ncholakwa chanji kuti andithaŵe? Adatsata milungu yachabechabe, iwonso nkusanduka achabechabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:14

m'menemo inuyo zamaŵa simukuzidziŵa. Kodi moyo wanu ngwotani? Pajatu inu muli ngati utsi chabe, umene umangooneka pa kanthaŵi, posachedwa nkuzimirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 5:21

Tsoka kwa amene amadziwona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:15-16

Samalirani bwino mayendedwe anu. Musayende monga anthu opanda nzeru, koma monga anthu anzeru. Mukhale achangu, osataya nthaŵi yanu pachabe, pakuti masiku ano ngoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:16

Muzimvana bwino, ndipo musamadzikweze, koma muziyanjana nawo anthu wamba. Musamadziyese anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 14:11

Pajatu aliyense wodzikuza adzamchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamkuza.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:23

Kunyada kwa munthu kudzamtsitsa, koma amene ali wodzichepetsa adzalandira ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:17-18

Tsono m'dzina la Ambuye ndikukuuzani, ndipo ndikunenetsa, kuti musayendenso monga amachitira akunja potsata maganizo ao achabe. Nzeru zao zidachita chidima, sangalandire nao konse moyo wa Mulungu chifukwa cha umbuli umene udadza mwa iwo kaamba ka kuuma mtima kwao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:6

Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mbiya. Zimenezinso nzachabechabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 49:10-12

Zoonadi, aliyense atha kuwona kuti ngakhale anthu anzeru amafa. Chimodzimodzi, anthu opusa ndi opulukira ayenera kufa ndi kusiyira ena chuma chao. Manda ao ndiye kwao mpaka muyaya, ndi malo odzakhalako pa mibadwo yonse, ngakhale akadali moyo ankatcha maiko maina ao. Ngakhale munthu akhale wolemera chotani, komabe adzafa chabe ngati nyama zakuthengo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:24

“Munthu sangathe kutumikira mabwana aŵiri, pakuti kapena adzadana ndi mmodzi nkukonda winayo, kapena adzadzipereka kwa mmodzi nkumanyoza winayo. Simungathe kutumikira onse aŵiri, Mulungu ndi chuma.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:27

Si kwabwino kudya uchi wambiri, tsono muchenjere nawo mau oyamikira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:4

Chikondi ncholeza mtima ndiponso nchofatsa. Chikondi chilibe kaduka, ndipo sichidzitamanda kapena kudzikuza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 57:13

Mukamafuula kufuna chithandizo, mafano anuwo akupulumutseni! Mphepo idzaiyalula milunguyo, mpweya udzaiwulutsa. Koma amene amakhulupirira Ine, adzalandira dziko lokhalamo, ndi kumapembedza pa phiri langa loyera.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 13:14

Ambuye Yesu Khristu mwini akhale chida chanu chankhondo. Lekani mtima wofunafuna zosangalatsa thupi, musagonjere zilakolako zake zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 10:17-18

Paja Malembo akuti, “Wofuna kunyada, anyadire Ambuye.” Pakuti munthu wovomerezeka, si amene amadzichitira yekha umboni, koma amene Ambuye amamchitira umboni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 6:11-12

Mau akachuluka, zopandapake zimachulukanso. Nanga munthu apindulapo chiyani? Ndani amadziŵa zomkomera munthu kwenikweni pa nthaŵi yochepa imene munthuyo ali ndi moyo? Moyo wake ndi wa masiku ochepa, ndi wopandapake, umangopitirira ngati mthunzi. Ndani angathe kumufotokozera munthuyo zimene zidzachitike pansi pano iyeyo atafa?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:6

Koma amatikomera mtima koposa. Nchifukwa chake Malembo akuti, “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma odzichepetsa amaŵakomera mtima.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:6-7

Nchifukwa chake amavala kunyada ngati mkanda wam'khosi. Amavala nkhanza ngati malaya. Maso ao ndi otupa ndi kunenepa. Mitima yao ndi yodzaza ndi maganizo ofuna kuchita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 3:7-8

Koma chifukwa cha Khristu, zomwe kale ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziwona kuti nzosapindula. Zoonadi, zonse ndikuziwona kuti nzosapindulitsa poziyerekeza ndi phindu lopambana la kudziŵa Khristu Yesu, amene ndi Ambuye anga. Chifukwa cha Khristuyo ndidalolera kutaya zonse, nkumaziyesa zinyalala, kuti potero phindu langa likhale Khristu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 8:14-15

Pali chinthu china chachabechabe chimene chimachitika pansi pano. Chinthucho ndi ichi: mwina anthu abwino amalangidwa ngati ochita zoipa, pamene oipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino. Ndikuti zimenezinso nzachabechabe. Nchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinthu chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake, amene Mulungu wampatsa pansi pano.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:26

Tisakhale odzitukumula, oputana, kapena ochitirana dumbo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:33

Kuwopa Chauta kumaphunzitsa nzeru, ndipo ndi kudzichepetsa ndi ulemu, chili patsogolo nkudzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 127:1

Chauta akapanda kumanga nawo nyumba, omanga nyumbayo angogwira ntchito pachabe. Chauta akapanda kulonda nawo mzinda, mlonda angochezera pachabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:5

Inunso anyamata, muzimvera akulu. Ndipo nonsenu, khalani okonzeka kutumikirana modzichepetsa. Paja mau a Mulungu akuti. “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma amaŵakomera mtima anthu odzichepetsa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 9:11-12

Ndidaonanso pansi pano kuti opambana pa kuthamanga si aliŵiro okhaokha, opambana pa nkhondo si amphamvu okhaokha, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru okhaokha. Olemera si odziŵa zambiri okhaokha, ndipo si anthu aluso okhaokha amene anzao amaŵakomera mtima. Onsewo mwai umangoŵagwera pa nthaŵi yake. Kungoti munthu saidziŵa nthaŵi yake. Monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, monga momwenso mbalame zimakodwera mu msampha, anthunso nchimodzimodzi. Amachita ngati kukodwa mu msampha pa nthaŵi yoipa, pamene tsoka laŵagwera mwadzidzidzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:4

Maso odzikuza ndi mtima wonyada zimatsogolera anthu oipa ngati nyale, nchifukwa chake amachimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 4:18

Mitima yathu siili pa zinthu zooneka, koma pa zinthu zosaoneka. Paja zooneka nzosakhalitsa, koma zosaoneka ndiye zamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:17

Kudzikuza kwa anthu kudzatha, kudzitama kwao konse kudzaonongedwa. Chauta yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 13:5

Mtima wanu usakangamire pa ndalama, ndipo zimene muli nazo, mukhutire nazo. Paja Mulungu adati, “Sindidzakusiyani kapena kukutayani konse.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 49:16-17

Usavutike munthu wina akamalemera, pamene chuma cha m'nyumba mwake chikukulirakulira. Chifukwa pamene munthuyu amwalira, sadzatengapo kanthu. Chuma chake sichidzapita naye limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 40:15-17

Mitundu ya anthu ili ngati kadontho ka madzi mu mtsuko, ilinso ngati fumbi chabe pa sikelo. M'manja mwa Chauta zilumba nzopepuka ngati fumbi. Nkhalango ya ku Lebanoni siingakwanitse nkhuni zosonkhera moto, nyama zam'menemo sizingakwanire kuperekera nsembe yootcha. Mitundu yonse ya anthu si kanthu konse pamaso pa Chauta, Iye amaziyesa zachabe ndi zopandapake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:8-9

Musalole kuti ndikhale wabodza kapena wonama. Ndisakhale mmphaŵi kapena khumutcha. Muzindidyetsa chakudya chondiyenera, kuwopa kuti ndikakhuta kwambiri, ndingayambe kukukanani nkumanena kuti, “Chauta ndiye yaninso?” Kuwopanso kuti ndikakhala mmphaŵi, ndingayambe kuba, potero nkuipitsa dzina la Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 1:17

Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera Kumwamba, kwa Atate a zounikira zonse zakuthambo. Iwo sasinthika konse, ndipo kuŵala kwao sikutsitirika mpang'ono pomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 52:7

“Muwoneni munthu amene sadafune kudalira Mulungu, koma adakhulupirira chuma chake chochuluka, nalimbikira kuchita zoipa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 1:4

Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo adatipatsa madalitso aakulu ndi amtengowapatali amene Iye adatilonjeza. Adatero kuti mulandireko moyo wake wa Mulungu, mutapulumuka ku chivunde chimene chili pa dziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 15:58

Tsono abale anga okondedwa, limbikani, khalani osagwedezeka, gwirani ntchito ya Ambuye mwachangu masiku onse, podziŵa kuti ntchito zimene mumagwirira Ambuye sizili zopanda phindu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 2:8-9

Ndi kukoma mtima kwa Mulungu kumene kudakupulumutsani pakukhulupirira. Simudapulumuke chifukwa cha zimene inuyo mudaachita ai, kupulumuka kwanu ndi mphatso ya Mulungu. Munthu sapulumuka chifukwa cha ntchito zake, kuwopa kuti angamanyade.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:17

Ndipotu dziko lapansi likupita, pamodzi ndi zake zonse zimene anthu amazilakalaka. Koma munthu wochita zimene Mulungu afuna, amakhalapo mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 49:4

Koma ndidati, “Ndagwira ntchito yopanda phindu. Ndangoononga mphamvu zanga pachabe.” Komabe zondiyenerera zili m'manja mwa Chauta, mphotho yanga ili m'manja mwa Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:96

Ndazindikira kuti zabwino zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe konse malire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 16:13

“Palibe wantchito amene angathe kutumikira mabwana aŵiri, pakuti kapena adzadana ndi mmodzi nkukonda winayo, kapena adzadzipereka kwa mmodzi nkunyoza winayo. Simungathe kutumikira onse aŵiri, Mulungu ndi chuma.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:21-23

“Si munthu aliyense womangonditi ‘Ambuye, Ambuye’ amene adzaloŵe mu Ufumu wakumwamba ai. Koma adzaloŵe ndi wochita zimene Atate anga akumwamba afuna. Pa tsiku lachiweruzo anthu ambiri azidzanena kuti, ‘Ambuye, Ambuye, kodi suja ife tinkalalika mau a Mulungu m'dzina lanu? Suja tinkatulutsa mizimu yonyansa potchula dzina lanu? Suja tinkachita ntchito zamphamvu zambiri m'dzina lanu?’ Apo Ine ndidzaŵauza poyera kuti, ‘Sindidaakudziŵani konse. Chokani apa, anthu ochita zoipa.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 3:2-4

Anthu adzakhala odzikonda, okonda ndalama, onyada, odzikuza, onyoza Mulungu, osamvera anakubala ao, osayamika, ndi oipitsa zinthu za Mulungu. Adzakhala opanda chifundo, osapepeseka, ndi osinjirira anzao. Adzakhala osadzigwira, aukali, odana ndi zabwino, opereka anzao kwa adani ao. Adzakhala osaopa chilichonse, odzitukumula, okonda zosangalatsa m'malo mokonda Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:4

Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Chauta, ndi chuma, ulemu ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 4:16

Mfumu ikhoza kulamulira anthu osaŵerengeka, komabe itamwalira, palibe aliyense amene adzayamikire zomwe mfumuyo idachita. Ndithudi, zimenezinso nzopandapake, ndipo kuyesa kuzimvetsa nkungodzivuta chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 7:18

Ndikudziŵa kuti mwa ine simukhala kanthu kabwino. Ndikamati, “ine”, ndikunena khalidwe langa lokonda zoipa. Ngakhale ndimafuna kuchita zabwino, komabe sindizichita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 103:15-16

Kunena za munthu, masiku ake sakhalitsa, ali ngati a udzu, munthuyo amakondwa ngati duŵa lakuthengo. Koma mphepo ikaombapo, duŵalo pamakhala palibe, siliwonekanso pa malo ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 12:13-14

Basi, zonse zamveka. Mfundo yeniyeni ya zonsezi ndi iyi: Uzimvera Mulungu, ndipo uzitsata malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wake wonse wa munthu. Pajatu Mulungu adzaweruza zonse zimene timachita, zabwino kapena zoipa, ngakhale ndi zam'chinsinsi zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Yesu wanga wodabwitsa, Mpulumutsi wa moyo wanga, landirani ulemerero ndi ulemu, ndinu Woyera, Wamuyaya ndipo ndinena kuti ndinu woyenera kutamandidwa konse. Zikomo chifukwa chondiwonetsa chifundo chanu pa moyo wanga, zikomo chifukwa chondigula ndi Magazi anu amtengo wapatali ndipo mukupitirizabe kukonza ntchito yanu mwa ine. Lero ndidzipereka pamaso panu kuti ndikupempheni kuti mufufuze mtima wanga, ngati mupeza njira yoipa ndikupemphani chikhululukiro, ngati mupeza kudzikuza ndi zolinga zoyipa mwa ine ndikupemphani kuti mundisambitse ndi Magazi anu ndipo mulungamitse njira yanga. Mundikhululukire chifukwa cha zochita zanga zoyipa, ndithandizeni kusunga mawu anu ndikukhala nthawi zonse pamaso panu, kuti ndisagonjedwe ndi mzimu wanga kapena ndi malingaliro anga, koma ndi chifuniro chanu changwiro. Ndili m'manja mwanu achikondi Mulungu, ndikudziwa kuti sindine wangwiro ndipo inu mukuzidziwa bwino zimenezo, mundipange tsiku lililonse m'chifaniziro chanu chifukwa ndikufuna kukhala nsembe yokondweretsa kwa inu. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa