Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


104 Mau a m'Baibulo Okhudza Kudzikuza

104 Mau a m'Baibulo Okhudza Kudzikuza

Baibulo limatiuza kuti Mulungu amaona kutali munthu wodzikuza. Kudzikuza ndi khalidwe lomwe silikondweretsa Mulungu, ndipo limapezeka mwa anthu ambiri, kumawapangitsa kudzidalira mopambanitsa ndikuganiza kuti angathe kulamulira chilichonse. Munthu wodzikuza sadziwa zolakwa zake, koma nthawi zonse amaona zolakwa za anzake, n’kunyalanyaza zake.

Njira yokha yothawa mtima umenewu womwe umawononga maganizo ndi mtima wanu, ndikuvomereza Mulungu pa chilichonse chimene muchita. Muziwerama pamaso pake ndi kuvomereza kuti mumadalira Iye, osati mphamvu kapena luso lanu. Koma chifukwa cha chikondi ndi chisomo chake. Ndikukutsimikizirani kuti mukachita izi, chikondi chake chochiritsa chidzakuphimbani, chidzasintha maganizo anu, ndi kukupangani munthu watsopano m’chifaniziro chake.

Dzipumbitsitseni pansi pa dzanja lamphamvu la Yehova, ndipo nthawi yake ikadzakwana adzakukwezani ndi kukuyikani pamalo amene anakukonzerani kuyambira kalekale.




Miyambo 16:5

Munthu aliyense wodzikuza amanyansa Chauta, ndithu ameneyo sadzalephera kulangidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:12

Pajatu aliyense wodzikuza adzamchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamkuza.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 138:6

Ngakhale Chauta ndi wamphamvu, amasamalira anthu otsika, koma anthu odzikuza amaŵadziŵira chapatali.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 10:4

Munthu woipa sasamala Mulungu chifukwa cha kunyada kwake. Mumtima mwake amati, “Kulibe Mulungu.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 18:12

Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umadzikuza, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:18

Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wa mtima wodzikuza adzagwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 21:4

Maso odzikuza ndi mtima wonyada zimatsogolera anthu oipa ngati nyale, nchifukwa chake amachimwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:23

Kunyada kwa munthu kudzamtsitsa, koma amene ali wodzichepetsa adzalandira ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 3:7

Usamadziwona ngati wanzeru. Uziwopa Chauta, ndipo uleke zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 27:1

Usamanyadira zamaŵa, pakuti sudziŵa zimene zidzachitika pa tsikulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 11:2

Kunyada kukaloŵa, pamafikanso manyazi, koma pali kudzichepetsa, palinso nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:2

Dzambatukani, Inu Muweruzi wa dziko lapansi, apatseni anthu onyada zoŵayenerera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:16

Muzimvana bwino, ndipo musamadzikweze, koma muziyanjana nawo anthu wamba. Musamadziyese anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:11

Kudzikuza kwa anthu kudzatha, kudzitama kwa anthu kudzaonongedwa. Chauta yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 131:1

Chauta, mtima wanga ndi wosadzikuza, maso anga ndi osanyada. Sinditengeka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:3

Ngati munthu adziyesa kanthu, pamene chikhalirecho sali kanthu konse, amangodzinyenga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:3

Popeza kuti mwa kukoma mtima kwake Mulungu adandiitana kuti ndikhale mtumwi, ndikukuuzani inu nonse kuti musadziyese anzeru koposa m'mene muliri. Makamaka maganizo anu akhale odzichepetsa, molingana ndi kukula kwa chikhulupiriro chimene Mulungu wapatsa aliyense mwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:6

Koma amatikomera mtima koposa. Nchifukwa chake Malembo akuti, “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma odzichepetsa amaŵakomera mtima.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:5

Inunso anyamata, muzimvera akulu. Ndipo nonsenu, khalani okonzeka kutumikirana modzichepetsa. Paja mau a Mulungu akuti. “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma amaŵakomera mtima anthu odzichepetsa.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 10:17-18

Paja Malembo akuti, “Wofuna kunyada, anyadire Ambuye.” Pakuti munthu wovomerezeka, si amene amadzichitira yekha umboni, koma amene Ambuye amamchitira umboni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 73:6

Nchifukwa chake amavala kunyada ngati mkanda wam'khosi. Amavala nkhanza ngati malaya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 2:16

Paja zonse zapansipano, zilakolako zathupi, zinthu zimene maso amakhumbira, ndiponso kunyadira za moyo uno, zonsezi sizichokera kwa Atate, koma ku mkhalidwe woipa wa dziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:8-9

Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake. Mtima wopirira ndi wopambana mtima wodzikuza. Usamafulumira kukwiya, pakuti mkwiyo umakhalira zitsiru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 1:43

Ndidakuuzani zimene Chauta adanena, koma inu simudasamale. Mudaukira Chauta, ndipo mudakaloŵa m'dziko lamapirilo, muli tumbatumba kunyada.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 19:22

“Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira yani? Kodi ndani amene wamufuulira ndi kumuyang'ana monyada? Si wina ai, koma Woyera uja wa Israele!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:10

Mudzichepetse pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 1:30

amasinjirira, ndipo amadana ndi Mulungu. Ndi achipongwe, odzikuza, ndi onyada. Amafunafuna njira zatsopano zochitira zoipa, samvera makolo ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:12

Ngakhale chitsiru chomwe nkuti ndiponi, pali chikhulupiriro, koma osati munthu wodziyesa wanzeru pamene ali wopusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:8

Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake. Mtima wopirira ndi wopambana mtima wodzikuza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 101:5

Munthu wosinjirira mnzake kuseri ndidzamcheteketsa. Wooneka wonyada ndi wodzikuza sindidzamulekerera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:10

Chipongwe cha osasamala za anzao chimadzetsa mkangano, koma omvera malangizo a anzao ndiwo ali ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 10:12-13

Mau a pakamwa pa munthu wanzeru amakondweretsa, koma pakamwa pa chitsiru mpoononga. Chitsiru chimayamba ndi mau opusa, potsiriza zolankhula zake zimangokhala zamisala basi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:51

Anthu osasamala za Mulungu amandinyoza kwathunthu, komabe sindisiyana nawo malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:85

Anthu osasamala za Mulungu, osatsata malamulo anu, andikumbira mbuna.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 30:32

Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza, kapena wakhala ukukonzekera kuchita zoipa, yamba wati chete, uziganize bwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 10:12

Tsono amene akuganiza kuti waimirira molimba, achenjere kuti angagwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 13:11

Chauta akuti, “Ndidzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha kuipa kwao, ndidzalanga oipa chifukwa cha kuchimwa kwao. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 50:31

“Ndikukuthira nkhondo, mzinda wachipongwewe, pakuti yakwana nthaŵi yako, lafika tsiku lako la chilango,” akutero Chauta Wamphamvuzonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 2:19

Umakhulupirira kuti ndiwe mtsogoleri wa anthu akhungu, nyale younikira anthu amene ali mu mdima,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:26

Tisakhale odzitukumula, oputana, kapena ochitirana dumbo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:19

Kuli bwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu osauka, kupambana kumagaŵana chuma ndi anthu onyada.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 140:5

Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika, atchera ukonde wa zingwe, anditchera misampha m'mbali mwa njira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 12:15

Zimene amachita munthu wopusa mwiniwakeyo amaziyesa zolungama, koma munthu wanzeru amamvetsera malangizo a ena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 35:12-13

Ena amaitana Mulungu koma Iye saŵayankha, chifukwa cha kunyada ndi kuipa kwa anthuwo. Ndithudi, Mulungu saamva kupempha kopanda pake, Mphambe sasamalako zimenezo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 19:25

Ukamenya munthu wonyoza anzake, adzachenjererapo. Ukadzudzula munthu womvetsa bwino zinthu, adzapindulapo nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 59:12

Akodwe ndi kunyada kwao, chifukwa cha uchimo wa m'kamwa mwao, ndi mau a pakamwa pao. Chifukwa chakuti amatemberera ndipo amanama,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 14:13-14

Mumtima mwako unkati, ‘Ndidzakwera mpaka kumwamba. Ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu. Ndidzakhala pampandopo pa phiri la kumpoto kumene imasonkhanako milungu yonse. Ndidzakwera pamwamba pa mitambo, ndidzafanafana naye Wopambanazonse.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:17-18

Usamakondwerera kugwa kwa mdani wako, mtima wako usamasangalala iyeyo akaphunthwa. Ukatero Chauta adzaziwona zimenezo nadzaipidwa nazo, kenaka adzaleka kumkwiyira mdani wakoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 3:13

Ndani mwa inu ali wanzeru ndi womvetsa zinthu? Aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru zimaongoleradi zochita zake zofatsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:2

Muzikhala odzichepetsa, ofatsa ndi opirira nthaŵi zonse. Muzilezerana mtima mwachikondi,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 75:4-5

Ndimauza anthu odzitama kuti, “Musadzitame,” ndiponso anthu oipa kuti, “Musadzitukumule chifukwa cha mphamvu zanu. Musadzikuze chifukwa cha mphamvu zanu, kapena kumalankhula zamwano.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 5:5

Ngodala anthu ofatsa, pakuti Mulungu adzaŵapatsa dziko la pansi pano kuti likhale lao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:25

Munthu waumbombo amautsa mkangano, koma wokhulupirira Chauta adzalemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 66:7

Iye amalamula ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amalonda mitundu ina ya anthu. Anthu oukira asadzikweze.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 4:7

Nanga adakusiyanitsa ndi anthu ena ndani? Kaya uli ndi chiyaninso chimene sudachite kuchilandira? Tsono ngati udachita kuzilandira, ukunyadiranji ngati kuti sudangozilandira chabe?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 28:17

Unkanyada chifukwa cha kukongola kwako, udaipitsa nzeru zako chifukwa chofuna kukhala wotchuka. Motero ndidakugwetsa pansi kuti ukhale chenjezo kwa mafumu ena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 2:12

Chauta Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku, pamene adzatsitsa onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 12:3

Inu Chauta, tsekani pakamwa ponse pothyasika letsani lilime lililonse lolankhula modzikuza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 3:6

Asakhale munthu wolandiridwa mu mpingo chatsopano, kuwopa kuti angadzitukumule nkulangidwa monga momwe Satana adalangidwira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:25

Chauta amapasula nyumba ya munthu wonyada, koma amasamalira kadziko ka mkazi wamasiye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 14:4

Kodi iweyo ndiwe yani kuti uweruze wantchito wamwini kuti walakwa? Mbuye wake yekha ndiye aweruze ngati iye wakhoza kapena walephera pa ntchito yake. Ndipo adzakhoza, popeza kuti Ambuye angathe kumkhozetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 6:1

“Chenjerani, musachite ntchito zanu zabwino pamaso pa anthu ndi cholinga choti akuwoneni. Mukatero, simudzalandira mphotho kwa Atate anu amene ali Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 28:26

Samvazaanzake nchitsiru, koma wotsata nzeru za ena adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 119:119

Anthu onse oipa a pa dziko lapansi, mumaŵayesa ngati zakudzala, nchifukwa chake ndimakonda malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 40:4

Ngwodala munthu amene amadalira Chauta, munthu amene sapatukira ku mafano kapena kutsata milungu yonama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:8

Munthu wa mtima wanzeru adzasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 22:4

Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Chauta, ndi chuma, ulemu ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 11:20

Nzoona, iwo adakadzukadi chifukwa sadakhulupirire, ndipo inu pakukhulupirira, mukukhala mu mtengo tsopano. Komatu tsono musamadzitame, makamaka muzichita mantha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 5:6

Nchifukwa chake mudzichepetse pamaso pa Mulungu wamphamvu, kuti pa nthaŵi yake adzakukwezeni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:4

Iwo amamanga katundu wosautsa kunyamula nkusenzetsa anthu, koma iwowo samukhudzako mpang'ono pomwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 94:4-5

Amalankhula modzikuza ndipo amanyadira zoipa zao. Amatswanya anthu anu, Inu Chauta, amazunza anthu anu osankhidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 15:33

Kuwopa Chauta kumaphunzitsa nzeru, ndipo ndi kudzichepetsa ndi ulemu, chili patsogolo nkudzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 131:1-2

Chauta, mtima wanga ndi wosadzikuza, maso anga ndi osanyada. Sinditengeka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa. Koma ndautonthoza ndi kuukhalitsa chete mtima wanga, monga mwana amene mai wake amamtonthoza ndi bere. Momwemo mtima wanga uli phe m'kati mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 5:21

Tsoka kwa amene amadziwona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera!

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 14:3

Kulankhula kwa chitsiru kumamuitanira ndodo pa msana, koma mau a munthu wanzeru amamteteza.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 24:9

Kukonzekera zopusa nkuchimwa, munthu wonyoza amanyansa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:11

Koma anthu ofatsa adzalandira dziko kuti likhale lao, ndipo adzakhala pa mtendere wosaneneka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mlaliki 7:16-17

Ndiye usachite kunkitsa nako kulungama, kapena kunkitsa nazo nzeru. Nanga ufere ziti? Usachite kunyanyanso kuipa, usanyanye nawonso uchitsiru. Nanga uferenji nthaŵi yako isanakwane?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 25:6-7

Usamadzikuza ukakhala pamaso pa mfumu, usamakhala pa malo a anthu apamwamba. Pajatu kuli bwino kuchita kukuuza kuti, “Dzakhale pokwera pano”, koposa kuchita kukutsitsa chifukwa cha wina wokupambana. Zimene maso ako azipenya,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 6:4

Aliyense aziyesa yekha ntchito zake m'mene ziliri. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, osati chifukwa zapambana ntchito za mnzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 62:9

Anthu otsika ndi mpweya chabe, ngakhale anthu okwera ndi nthunzi chabe, onsewo ndi oluluka pa sikelo, ndi opepuka kupambana mpweya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 29:20

Ngakhale chitsiru chomwe nkuti ndiponi pali chikhulupiriro, koma osati munthu wodziyesa wanzeru pamene ali wopusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 37:12-13

Munthu woipa amachitira upo mnzake wabwino, namamtuzulira maso mwachidani. Koma Chauta amamseka munthu woipayo, poti amaona kuti tsiku lake la kuwonongeka likubwera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 8:13

Kuwopa Chauta nkudana ndi zoipa. Kunyada, kudzitama, kuchita zoipa ndi kulankhula zonyenga, zonsezo ndimadana nazo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 5:2

Ndipo inu mukudzitukumulabe! Kwenikweni mukadayenera kumva chisoni, ndi kumchotsa pakati panu munthu amene adachita zimeneziyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 13:6

Chilungamo chimatchinjiriza munthu wabwino, koma tchimo limagwetsa munthu woipa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 49:16-17

Usavutike munthu wina akamalemera, pamene chuma cha m'nyumba mwake chikukulirakulira. Chifukwa pamene munthuyu amwalira, sadzatengapo kanthu. Chuma chake sichidzapita naye limodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:3-5

Popeza kuti mwa kukoma mtima kwake Mulungu adandiitana kuti ndikhale mtumwi, ndikukuuzani inu nonse kuti musadziyese anzeru koposa m'mene muliri. Makamaka maganizo anu akhale odzichepetsa, molingana ndi kukula kwa chikhulupiriro chimene Mulungu wapatsa aliyense mwa inu. M'thupi lathu limodzi lomweli tili ndi ziwalo zambiri, ndipo ziwalozo zili ndi ntchito zosiyanasiyana. Momwemonso ife, ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, olumikizana mwa Khristu, ndipo tonse, aliyense pa mbali yake, ndife ziwalo zolumikizana.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:12

Kuchita zoipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 23:10-12

Anthu asatinso azikutchulani atsogoleri, popeza kuti Mtsogoleri wanu ndi mmodzi yekha, ndiye Khristu. Pakati panupa wamkulu akhale mtumiki wanu. Pajatu aliyense wodzikuza adzamchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamkuza.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 10:17

Wosamala malangizo amayenda pa njira ya moyo, koma wokana chidzudzulo amasokera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yobu 36:11

Ngati anthu amumvera ndi kumamtumikira, adzatsiriza masiku a moyo wao mwamtendere, adzatsiriza zaka zao mosangalala.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 76:4

Inu Mulungu, mukuwonetsa ulemerero ndi mphamvu kupambana mapiri a zofunkha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:19

Okondedwa anga, musabwezere choipa, koma alekeni, mkwiyo wa Mulungu ndiwo uŵalange. Paja Malembo akuti, “Kulipsira nkwanga. Ndidzaŵalanga ndine, akutero Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:24

Mau okometsera ali ngati chisa cha uchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Masalimo 109:28

Iwo atemberere, koma Inu mundidalitse. Ondiputa muŵachititse manyazi, koma ine mtumiki wanu ndisangalale.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:19-21

Zochita za khalidwe lokonda zoipa zimaonekera poyera. Ndi izi: Dama, kuchita zonyansa, kusadziletsa, Ndiye mvetsani, ine Paulo ndikukuuzani kuti mukalola kukuumbalani, Khristu simupindula nayenso konse ai. kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko, dumbo, kuledzera, kudakwa pa maphwando achipembedzo, ndi zina zotere. Ndikukuchenjezani tsopano, monga ndidaachitanso kale, kuti anthu amene amachita zotere, sadzalandirako Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 26:26

Ngakhale amabisa chidani mochenjera, kuipa kwakeko kudzaoneka poyera pakati pa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 57:15

Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthaŵi zonse, ndipo dzina lake ndi Woyera uja, akunena kuti, “Ndimakhala pa malo aulemu, oyera. Koma ndimakhalanso ndi anthu odzichepetsa ndi olapa mu mtima, kuti odzichepetsawo ndiŵachotse mantha, olapawo ndiŵalimbitse mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Miyambo 16:18-19

Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wa mtima wodzikuza adzagwa. Kuli bwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu osauka, kupambana kumagaŵana chuma ndi anthu onyada.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 13:4-5

Chikondi ncholeza mtima ndiponso nchofatsa. Chikondi chilibe kaduka, ndipo sichidzitamanda kapena kudzikuza. Chikondi chilibe matama kapena chipongwe, sichidzikonda, sichikwiya, sichisunga mangaŵa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 4:4

Inu anthu osakhulupirikanu, kodi simudziŵa kuti kuchita chibwenzi ndi zapansipano nkudana ndi Mulungu? Choncho munthu wofuna kukhala bwenzi la zapansipano, ameneyo amadzisandutsa mdani wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Yesu wanga wokondedwa, wodzala chifundo ndi wolekera kukwiya, ndikulambira dzina lanu ndi mtima wanga wonse, pakuti ndinu woyenera ulemerero ndi ulemu wonse. Ndikukutamandani Mulungu wanga wabwino, chifukwa cha chikondi chanu ndipo mwandiwombola moyo wanga ku imfa. Mwandipulumutsa ndi kundipatsa mwayi tsiku lililonse kuti ndikhale munthu wabwino. Mzimu Woyera, ndidzipereka pamaso panu podziwa kuti ndikukusowani. Sindikufuna kukhala moyo wodzikuza kapena kuchita chilichonse chomwe chingandisiyanitse ndi inu. Chonde munditsuke ku chilichonse chomwe chikudetsa mtima wanga ndi kundithandiza kukhala moyo woyera, kuti palibe choipa kapena chodzikweza chomwe chingakhale mkati mwanga. Ndikutsutsa kudzikuza konse lero ndipo ndikulengeza kuti ndine mfulu kwathunthu m'dzina la Yesu. Ndili m'manja mwanu, nditsogolereni nthawi zonse ndipo musalole kuti ndichoke pamaso panu. Mundilange ndi kundiphunzitsa njira yoyenera kuyenda. Zikomo chifukwa cha zonse Mulungu wanga wabwino, ndikukulambirani ndi kukukwezani kwamuyaya. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa