Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

104 Mau a m'Baibulo Pa Nkhani

Buku la Aefeso limandiphunzitsa kuti ndisamanene mawu alionse oipa, koma mawu anga onse akhale opatsa mphamvu kwa anthu ondizungulira, kuti ndiwadalitse pamavuto alionse amene akukumana nawo.

Lilime langa linalengedwa kuti likhale chitoliro cha madalitso chimene Mulungu amafuna kugwiritsa ntchito pofalitsa uthenga ndi kumanga anthu ambiri. Ndiye chifukwa chake, ndikofunikira kwambiri kuchotsa chilichonse chimene sichichokera kwa Mulungu ndipo sichithandiza pakumanga.

Ndiyenera kusamala kwambiri ndi mawu anga, chifukwa ndidzaweruzidwa malinga ndi zimene ndimanena. Ndiyenera kukhala wofulumira kudalitsa m'malo motemberera mnzanga kapena kufalitsa miseche, chifukwa miseche siyabwino pamaso pa Mulungu.

Ndiyenera kuyesetsa kukhala wolankhula wamawu a Mulungu mwachangu, kuti chisomo chake ndi chifundo chake zikhale nane nthawi zonse. Ndikumbukire kusunga lilime langa ku zoipa ndi milomo yanga kuti isanene bodza, chifukwa munthu woipa amabweretsa ndewu zoopsa, koma woteteza mnzake amapulumutsa moyo.


Miyambo 11:13

Amene amanka nachita ukazitape, amaulula zinsinsi. Koma wa mtima wokhulupirika, amasunga pakamwa pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:28

Munthu woipa mtima amafalitsa mkangano, kazitape amadanitsa anthu okhala pa chibwenzibwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:29

M'kamwa mwanu musatuluke mau aliwonse oipa, koma muzinena mau okhaokha abwino ndi olimbitsa mtima monga kungafunikire, kuti mupindulitse anzanu omva mau anuwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Levitiko 19:16

Musamangoyendayenda uku ndi uku kumachita ukazitape pakati pa anthu a mtundu wanu. Musachite kanthu kalikonse kamene kangathe kudzetsa imfa ya munthu wina. Ine ndine Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:9

Munthu wosalabadirako za Mulungu amaononga mnzake ndi pakamwa pake; munthu wochita chilungamo amapulumuka chifukwa cha kudziŵa zinthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:11

“Ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani ndi kukunyengezerani zoipa zamitundumitundu chifukwa cha Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:13

Ngati ufunadi moyo, usalankhule zoipa, pakamwa pako pasakambe zonyenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:19

Amene amanka nachita ugogodi, amaulula zinsinsi. Nchifukwa chake usamagwirizane naye wolankhula zopusayo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 15:2-3

Ndi munthu amene amayenda mosalakwa, amene amachita zolungama nthaŵi zonse, amene amalankhula zinthu ndi mtima woona.

Ndi amene sasinjirira ndipo sachita anzake zoipa, kapena kumafalitsa mbiri yoipa ya anzake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:1

Nchifukwa chake tayani choipa chonse, kunyenga konse, chiphamaso, kaduka ndi masinjiriro onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:20

Moto umazima pakasoŵa nkhuni, chonchonso kumene kulibe kazitape, kulibenso ndeu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:8

Mau a kazitape ali ngati chakudya chokoma, anthu amaŵameza onse mokondwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 141:3

Muike mlonda pakamwa panga, Inu Chauta. Mulonde pa khomo la milomo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Tito 3:2

Uŵauze kuti asamakamba zoipa za wina aliyense, apewe kukangana, akhale ofatsa, ndipo nthaŵi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:36

Ndikunenetsa kuti pa tsiku la chiweruzo, anthu adzazengedwa mlandu chifukwa cha mau aliwonse opanda pake amene adaalankhula.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 23:1

“Usachite umboni wonama. Munthu wolakwa usamthandize pakumchitira umboni wonama.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:5-6

Chimodzimodzinso lilime: ndi kachiwalo kakang'ono, komabe limadzitama kuti nkuchita zazikulu. Tangoganizani kukula kwake kwa nkhalango imene ingayatsidwe ndi kalilaŵi kakang'ono ka moto.

Tsonotu lilime limatentha ngati moto. Chifukwa chokhala pakati pa ziwalo zathu limawanditsa zoipa m'thupi monse. Limaipitsa khalidwe lonse la munthu. Limayatsa moto moyo wathu wonse kuyambira pobadwa mpaka imfa; ndipo moto wake ngwochokera ku Gehena.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:11

Abale, musamasinjirirana. Wosinjirira mbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo a Mulungu. Koma ukaweruza Malamulo a Mulungu, ndiye kuti sukuchita zimene Malamulowo akunena, ukudziyesa woweruza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:26

Ngati wina akudziyesa woika mtima pa zopembedza Mulungu, koma nkukhala wosasunga pakamwa, chipembedzo chakecho nchopanda pake, ndipo amangodzinyenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:4

Ndiponso musamalankhule zolaula, zopusa, kapena zopandapake, koma muzilankhula zoyamika Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:29-30

Mitima yao idadzaza ndi zosalungama zamitundumitundu, monga kuipa, umbombo ndi dumbo. Amangolingalira za kaduka, za kupha anthu, za ndeu, za kunyenga, ndi za njiru. Amachita ugogodi,

Umasimba za Mwana wake, Yesu Ambuye athu. Poyang'anira umunthu wake, kholo lake ndi Davide,

amasinjirira, ndipo amadana ndi Mulungu. Ndi achipongwe, odzikuza, ndi onyada. Amafunafuna njira zatsopano zochitira zoipa, samvera makolo ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:16-19

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Chauta amadana nazo, makamaka zisanu ndi ziŵiri ndithu zimene zimamunyansa:

maso onyada, pakamwa pabodza, manja opha munthu wosalakwa,

mtima wokonzekera kuchita zoipa, mapazi othamangira msangamsanga ku zoipa,

mboni yonama yolankhula mabodza, ndi munthu woutsa chidani pakati pa abale.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:23

Amene amagwira pakamwa ndi kusamala zokamba zake, sapeza mavuto.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 5:13

Kuwonjezera pamenepo, amagwa m'chizoloŵezi cha kungokhala khale, motero amangoyendayenda ku nyumba za anthu. Tsonotu samangokhala khale chabe ai, amachitanso miseche nkumaloŵera za eni, ndi kukhala omalankhula zimene samayenera kulankhula.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 20:16

“Usachite umboni womnamizira mnzako.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 15:1-3

Inu Chauta, kodi ndani angathe kukhala m'Nyumba mwanu? Ndani angathe kukhala pa phiri lanu loyera?

Ndi munthu amene amayenda mosalakwa, amene amachita zolungama nthaŵi zonse, amene amalankhula zinthu ndi mtima woona.

Ndi amene sasinjirira ndipo sachita anzake zoipa, kapena kumafalitsa mbiri yoipa ya anzake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:19

Mau akachuluka, zolakwa sizisoŵa, koma amene amasunga pakamwa ndi wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 41:6

Amene amabwera kudzandiwona, ndi wosakhulupirika, mumtima mwake amaganiza zoipa za ine, ndipo akatuluka, amakaziwanditsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:27

Munthu wopandapake amakonzekera kuchita zoipa, mau ake ali ngati moto wopsereza.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:8

Koma tsopano musachitenso zonsezi, monga kukalipa, kukwiya, kuipa mtima, ndi mijedu. Pakamwa panu pasamatulukenso mau otukwana kapena onyansa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:15

“Mbale wako akakuchimwira, pita ukamdzudzule muli aŵiri nokha. Akakumvera, wamkonza mbale wakoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:31

Zomwe mukufuna kuti anthu akuchitireni, inuyo muŵachitire zomwezo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:18

Wobisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo wochita ugogodi nchitsiru.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 2:1

Tsono woweruza enawe, kaya ndiwe yani, ulibe pozembera. Pakutitu pamene ukuweruza mnzako, ukudzitsutsa wekha, popeza kuti iweyo woweruzawe umachita zokhazokhazo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 4:11

Yesetsani kukhala ndi moyo wabata. Aliyense asamale ntchito yakeyake ndi kumagwira ntchito ndi manja ake. Chitani zimenezi, monga tidakulangizirani muja,

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:8

Potsiriza, abale, muziika mtima pa zilizonse zabwino kwambiri ndi zotamandika, monga izi: zinthu zoona ndi zolemekezeka, zinthu zolungama, zoyera, zokongola, ndi zaulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:9

Wokhululukira cholakwa amafunafuna chikondi, koma wosunga nkhani kukhosi amapha chibwenzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:22

Mau a kazitape ali ngati zakudya zokoma, zimene zimatsikira m'mimba msanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 14:19

Nchifukwa chake tsono tizifunafuna zimene zingathandize kuti pakhale mtendere ndiponso kugwirizana pakati pathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:18

Wofulumira kulankhula, zonena zake zimalasa ngati mpeni, koma mau a munthu wanzeru amachiza anzake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:31-32

Muchotseretu pakati panu kuzondana, kukalipa, ndiponso kupsa mtima. Musachitenso chiwawa, kapena kulankhula mau achipongwe, tayani kuipa konse.

Muzikomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, ndipo muzikhululukirana monga momwe Mulungu mwa Khristu adakukhululukirani inunso.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 101:5

Munthu wosinjirira mnzake kuseri ndidzamcheteketsa. Wooneka wonyada ndi wodzikuza sindidzamulekerera.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 12:20

Ndikuwopa kuti ndikadzabwera kwanuko, mwina nkudzakupezani muli osiyana ndi m'mene ndikadafunira. Ndikuwopa kuti mwina inunso nkudzandipeza ine wosiyana ndi m'mene mukadafunira. Ndikuwopanso kuti mwina ine nkudzapeza kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusinjirirana, ugogodi, kudzitukumula, ndiponso chisokonezo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:10

Paja mau a Mulungu akuti. “Yemwe afuna kukondwera ndi moyo, ndi kuwona masiku abwino, aletse lilime lake kulankhula zoipa, ndiponso milomo yake kunena mabodza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:24

Mau okometsera ali ngati chisa cha uchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 4:6

Nthaŵi zonse mau anu akhale okoma, opindulitsa ena, kuti potero mudziŵe m'mene muyenera kuyankhira munthu aliyense.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:28

Munthu wonama amadana ndi amene iye adaŵapweteka, pakamwa poshashalika mpoononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:9

Ngodala anthu odzetsa mtendere, pakuti Mulungu adzaŵatcha ana ake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:20

Wina akamanena kuti, “Ndimakonda Mulungu”, komabe nkumadana ndi mbale wake, ndi wonama ameneyo. Pakuti munthu wosakonda mbale wake amene wamuwona, sangathe kukonda Mulungu amene sadamuwone.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:3

Nchifukwa chake zonse zimene mwalankhula pa mdima, zidzamveka poyera, ndipo zonse zimene mwanong'oneza anthu m'kati mwa nyumba, adzazilengeza pa bwalo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 25:23

Mphepo ya mpoto ndiyo imadza ndi mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 52:2-4

Tsiku lonse umakhalira kusinkhasinkha za kuwononga ena, lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nkunyenga.

Umakonda zoipa kupambana zabwino, umakonda kunama kupambana kulankhula zoona.

Umakonda kulankhula mau ovutitsa ena, iwe wabodzawe.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 13:4-7

Chikondi ncholeza mtima ndiponso nchofatsa. Chikondi chilibe kaduka, ndipo sichidzitamanda kapena kudzikuza.

Chikondi chilibe matama kapena chipongwe, sichidzikonda, sichikwiya, sichisunga mangaŵa.

Sichikondwerera zosalungama, koma chimakondwerera choona.

Chikondi chimakhululukira zonse, chimakhulupirira nthaŵi zonse, sichitaya mtima, ndipo chimapirira onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:14-15

Paja Malamulo onse a Mulungu amaundidwa mkota pa lamulo limodzi lija lakuti, “Uzikonda mnzako monga momwe umadzikondera iwe wemwe.”

Koma ngati muyamba kulumana ndi kukadzulana, muchenjere kuti mungaonongane kotheratu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:1

Kuyankha kofatsa kumazimitsa mkwiyo, koma mau ozaza amakolezera ukali.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:18

Ngati nkotheka, khalani ndi mtendere ndi anthu onse, monga momwe mungathere.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:21

Zimene umanena zingathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo, munthu wolankhulalankhula adzapeza bwino kapena tsoka.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 14:13

Tsono tiyeni tileke kumaweruzana. Makamaka mutsimikize kuti musachite kanthu kalikonse kophunthwitsa mbale wanu, kapena komchimwitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 4:5

Motero musaweruziretu munthu aliyense, Ambuye asanabwere. Iwo ndiwo adzaunika pa zonse zobisika mu mdima, ndipo adzaulula maganizo a m'mitima mwa anthu. Pamenepo aliyense adzalandira kwa Mulungu chiyamiko chomuyenerera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:23

Pa ntchito iliyonse pali phindu lake, koma kumangolakatika kumabweretsa umphaŵi.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:1-2

“Musamaweruza anthu ena kuti ndi olakwa, kuwopa kuti Mulungu angakuweruzeni.

Kapena atampempha nsomba, iye nkumupatsa njoka?

Tsono ngati inu, nkuipa kwanuku, mumadziŵa kupatsa ana anu mphatso zabwino, nanji Atate anu amene ali Kumwamba, angalephere bwanji kupereka zinthu zabwino kwa amene aŵapempha?

Zomwe mukufuna kuti anthu akuchitireni, inuyo muŵachitire zomwezo. Izi ndiye zimene Malamulo a Mose ndiponso aneneri amaphunzitsa.

“Loŵerani pa chipata chophaphatiza. Pajatu chipata choloŵera ku chiwonongeko nchachikulu, ndipo njira yake ndi yofumbula, nkuwona anthu amene amadzerapo ndi ambiri.

Koma chipata choloŵera ku moyo nchophaphatiza, ndipo njira yake ndi yosautsa, nkuwona anthu amene amaipeza ndi oŵerengeka.

“Chenjera nawoni aneneri onyenga. Amadza kwa inu ali ndi maonekedwe ofatsa ngati nkhosa, koma m'kati mwao ndi mimbulu yolusa.

Mudzaŵadziŵira zochita zao. Kodi mitengo yaminga nkubala mphesa? Kodi mitula nkubala nkhuyu?

Chonchonso mtengo uliwonse wabwino umabala zipatso zabwino, koma mtengo woipa umabala zipatso zoipa.

Mtengo wabwino sungabale zipatso zoipa, kapena mtengo woipa kubala zipatso zabwino ai.

Mtengo uliwonse wosabala zipatso zabwino, amaudula nkuuponya pa moto.

M'mene inu mumaweruzira ena, ndi m'menenso Mulungu adzakuweruzirani inuyo. Ndipo muyeso womwe mumagwiritsa ntchito poweruza ena, Mulungu adzagwiritsa ntchito womwewo pokuweruzani inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:19-21

Zochita za khalidwe lokonda zoipa zimaonekera poyera. Ndi izi: Dama, kuchita zonyansa, kusadziletsa,

Ndiye mvetsani, ine Paulo ndikukuuzani kuti mukalola kukuumbalani, Khristu simupindula nayenso konse ai.

kupembedza mafano, ufiti, chidani, kukangana, kaduka, kupsa mtima, kudzikonda, kusagwirizana, kuchita mipatuko,

dumbo, kuledzera, kudakwa pa maphwando achipembedzo, ndi zina zotere. Ndikukuchenjezani tsopano, monga ndidaachitanso kale, kuti anthu amene amachita zotere, sadzalandirako Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 29:20

Ngakhale chitsiru chomwe nkuti ndiponi pali chikhulupiriro, koma osati munthu wodziyesa wanzeru pamene ali wopusa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:11

Nchifukwa chake muzilimbitsana mtima ndi kumathandizana, monga momwe mukuchitiramu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:10

Muzikondana kwenikweni monga abale, ndipo muzichita ngati kupikisana poonetsana ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:37

“Musamaweruza anthu ena kuti ngolakwa, ndipo Mulungu sadzakuweruzani. Musamaimba ena mlandu, ndipo Mulungu sadzakuimbani mlandu. Muzikhululukira ena, ndipo Mulungu adzakukhululukirani.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:2

Paja tonsefe timalakwa pa zinthu zambiri. Ngati alipo amene salakwa pakulankhula, ndiye kuti ndi wangwirodi ameneyo, mwakuti angathe kulamuliranso thupi lake lonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:3

Amene amagwira pakamwa pake amasunga moyo wake, koma amene amangolakatika amaonongeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:2-3

Muzikhala odzichepetsa, ofatsa ndi opirira nthaŵi zonse. Muzilezerana mtima mwachikondi,

Koma umu si m'mene inu mudaphunzirira za Khristu ai,

ngatitu mudamva za Iyeyo, ngatinso mudaphunzitsidwa za Iye, motsata choona chimene chili mwa Yesu.

Mudaphunzira kuti muleke mayendedwe anu akale, muvule moyo wanu wakale uja umene unkadziwononga ndi zilakolako zake zonyenga.

Mtima wanu, umene uli gwero la maganizo anu, usanduke watsopano.

Ndipo muvale moyo watsopano, umene Mulungu adaulenga, wofanafana naye. Apo mudzakhala olungama ndi oyera mtima kwenikweni.

Tsono lekani kunama. Aliyense azilankhula zoona zokhazokha ndi mkhristu mnzake, pakuti tonse pamodzi mogwirizana ndife ziwalo za thupi la Khristu.

Inde mwina nkupsa mtima, koma musachimwe, ndipo musalole kuti dzuŵa likuloŵereni muli chikwiyire.

Musampatse mpata Satana woti akugwetseni.

Amene ankaba, asabenso, koma makamaka azigwira ntchito kolimba ndi kumachita zolungama ndi manja ake, kuti akhale nkanthu kopatsa osoŵa.

M'kamwa mwanu musatuluke mau aliwonse oipa, koma muzinena mau okhaokha abwino ndi olimbitsa mtima monga kungafunikire, kuti mupindulitse anzanu omva mau anuwo.

ndipo muziyesetsa kusunga umodzi mwa Mzimu Woyera pa kulunzana mu mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 50:20

“Umakhala pansi nkumachitira mbale wako miseche, inde, umasinjirira mbale wako weniweni.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:10

Ngati munthu akonda mnzake, sangamchite choipa ai. Nchifukwa chake amene amakonda mnzake, wasunga zonse zimene Malamulo a Mulungu akunena.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:18-19

Monga munthu wopenga amene amangoponya nsakali zamoto, kapena mivi yoopsa,

ndimonso amakhalira munthu wonyenga mnzake, amene amati, “Ai, ndi zoseka chabe!”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 27:2

Akutame ndi wina, osati pakamwa pako pomwe, wosadziŵana naye akakutamanda, apo ndipo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:13

Ukayankha usanamve nkhani yonse, umaoneka wopusa ndipo umachita manyazi.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 5:9

Abale musamanenerana zoipa pakati panu, kuwopa kuti Mulungu angakuweruzeni. Onani, woweruza waima pa khomo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:28

Munthu wabwino amaganizira za m'mene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woipa pamatuluka mau oipa okhaokha.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:34

Ana a njoka inu, mungathe bwanji kulankhula zabwino pamene muli oipa? Pajatu pakamwa pamalankhula zimene zadzaza mu mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:22

Pakamwa pabodza pamamnyansa Chauta. Koma anthu ochita zinthu mokhulupirika amamkondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:14-15

Muzichita zonse mosanyinyirika ndi mosatsutsapo,

kuti mukhale angwiro ndi osalakwa, ana a Mulungu opanda chilema chilichonse pakati pa anthu onyenga ndi osokeretsa anzao. Pakati pa anthu otere mumaŵala monga momwe zimaonekera nyenyezi pa dziko lapansi,

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:2

Aliyense mwa ife azikondweretsa mnzake, ndi kumchitira zabwino, kuti alimbikitse chikhulupiriro chake.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 2:16

Koma nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, uzipewe, pakuti anthu olankhula zotere adzanka nanyozeranyozera Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:24

Ulekeretu kulankhula zokhotakhota, usiyiretu kukamba zopotoka.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:15

Pakati panu pasakhale ndi mmodzi yemwe wogwa m'mavuto chifukwa choti wapha munthu, kapena waba, kapena wachita choipa, kapena waloŵerera za eniake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:14

Mau anga ndi maganizo anga avomerezeke pamaso panu, Inu Chauta, thanthwe langa ndi mpulumutsi wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:18

Ananu, chikondi chathu chisamangokhala cha nkhambakamwa chabe, koma chiziwoneka pa zochita zathu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:7

Tsono muzilandirana monga momwe Khristu adakulandirirani inu, kuti Mulungu alemekezedwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:22

Chabwino, koma Ine ndikukuuzani kuti aliyense wopsera mtima mbale wake adzayenera kuzengedwa ku bwalo lamilandu. Aliyense wonena mnzake kuti, ‘Wopandapake iwe,’ adzayenera kuzengedwera ku Bwalo Lapamwamba. Ndipo aliyense wonena mnzake kuti, ‘Chitsiru,’ adzayenera kukaponyedwa ku moto wa Gehena.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 64:2-3

Tchinjirizeni ku upo wachiwembu wa anthu oipa, tetezeni ku chiwawa cha anthu ochita zoipa.

Iwo amanola lilime lao ngati lupanga, amaponya mau obaya ngati mivi.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:45

Munthu wabwino amatulutsa zabwino m'chuma chabwino cha mumtima mwake. Nayenso munthu woipa amatulutsa zoipa m'chuma choipa cha mumtima mwake. Pajatu pakamwa pamalankhula zimene zadzaza mu mtima.”

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:28

Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, pakamwa pako pasamanena zonama.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:9

Musamauzana mabodza, pakuti mwachita ngati mwavula moyo wanu wakale, pamodzi ndi zochitachita zake zoipa,

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:1-2

Tsono popeza kuti ndinu ana okondedwa a Mulungu, muziyesa kumtsanzira.

Muziyesa kudziŵa kwenikweni zimene zingakondweretse Ambuye.

Musayanjane nawo anthu ochita zopanda pake za mdima, koma muŵatsutse.

Paja zimene iwo amachita mobisa, ngakhale kuzitchula komwe kumachititsa manyazi.

Koma kuŵala kumaunika zinthu, ndipo zonse zimaonekera poyera.

Motero chilichonse choonekera poyera, chimasanduka kuŵala. Nchifukwa chake amati, “Dzuka wam'tulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuŵalira.”

Samalirani bwino mayendedwe anu. Musayende monga anthu opanda nzeru, koma monga anthu anzeru.

Mukhale achangu, osataya nthaŵi yanu pachabe, pakuti masiku ano ngoipa.

Nchifukwa chake musakhale opusa, koma dziŵani zimene Ambuye afuna kuti muchite.

Musaledzere vinyo, kumeneko nkudzitaya, koma mudzazidwe ndi Mzimu Woyera.

Muzichezerana ndi mau a masalimo ndi a nyimbo za Mulungu ndi zauzimu. Ndipo muziimbira Ambuye mopolokezana ndi mtima wanu wonse.

Muzikondana, monga Khristu adatikonda ife, nadzipereka kwa Mulungu chifukwa cha ife. Adadzipereka ngati chopereka ndi nsembe ya fungo lokondweretsa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:5

Mboni yokhulupirika siinama, koma mboni yonyenga imalankhula zabodza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 26:18-20

Monga munthu wopenga amene amangoponya nsakali zamoto, kapena mivi yoopsa,

ndimonso amakhalira munthu wonyenga mnzake, amene amati, “Ai, ndi zoseka chabe!”

Monga imachitira mpheta yokhalira kuuluka, monga amachitira namzeze kumangoti zwezwezwe, ndimonso limachitira temberero lopanda chifukwa, silitha.

Moto umazima pakasoŵa nkhuni, chonchonso kumene kulibe kazitape, kulibenso ndeu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 13:34-35

Ndikukupatsani lamulo latsopano, lakuti muzikondana. Monga momwe Ine ndidakukonderani, inunso muzikondana.

Mukamakondana, anthu onse adzadziŵa kuti ndinudi ophunzira anga.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:3

Popeza kuti mwa kukoma mtima kwake Mulungu adandiitana kuti ndikhale mtumwi, ndikukuuzani inu nonse kuti musadziyese anzeru koposa m'mene muliri. Makamaka maganizo anu akhale odzichepetsa, molingana ndi kukula kwa chikhulupiriro chimene Mulungu wapatsa aliyense mwa inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 2:12-13

Tsono muzilankhula ndi kuchita zinthu monga anthu oti Mulungu adzaŵaweruza potsata lamulo loŵapatsa ufulu.

Paja munthu woweruza mopanda chifundo, nayenso Mulungu adzamuweruza mopanda chifundo. Koma wochita chifundo alibe chifukwa choopera chiweruzo cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:5

Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, wolankhula mabodza sadzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:16

Muzimvana bwino, ndipo musamadzikweze, koma muziyanjana nawo anthu wamba. Musamadziyese anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 6:4

Munthu wotere ndi wodzitukumula ndi kunyada, sadziŵa kanthu. Mtima wake ngwodwala, wongofuna zotsutsanatsutsana ndi kukangana pa mau chabe. Zimenezi zimabweretsa kaduka, kusamvana, kusinjirirana, kuganizirana zoipa,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 25:18

Munthu wochitira mnzake umboni wonama, amapweteka mnzakeyo ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:1

Abale, wina akagwa m'tchimo lililonse, inu amene Mzimu Woyera amakutsogolerani, mumthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe ndi zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga, Wamkulukulu woyenera kutamandidwa, ndikukutamandani chifukwa cha chifundo chanu chachikulu ndi kukoma mtima kwanu kosatha. Palibe tsiku limene simusonyeza kukhulupirika kwanu pa moyo wanga. Mumadziwa zoyenda zanga zonse, kuyambira m'mawa mpaka usiku. Ndikukupemphani tsopano, Ambuye, kuti mufufuze mtima wanga. Ngati mupeza njira yolakwika mwa ine, ndikhululukireni. Ndisambitseni ku zoipa zanga ndi kundikonza. Sindikufuna kuti mawu oipa atuluke pakamwa panga, koma ndikufuna kulankhula choonadi chanu. Ndilanditseni ku chinyengo chilichonse. Sindikufuna kukhala munthu wopanda chifundo kwa mnzanga. Ndithandizeni kusunga ulemu wa m'bale wanga ndi kupewa miseche, chifukwa ndikudziwa kuti simukukondwera nazo. Ikani moto woyera pakamwa panga kuti muchotse chodetsa chilichonse, chifukwa ndikufuna kukhala chotengera cholemekezeka m'manja mwanu. Ndikupempha kuti nthawi zonse ndikatsegula pakamwa panga, ndikhale kudalitsa miyoyo ya ena. Zikomo chifukwa cha zonse, Yesu wokondedwa wanga. M'dzina la Yesu, Ameni.