Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

119 Mau a Mulungu Okhudza Kupanduka

Mulungu ndi wapamwamba komanso woyenera ulemu, woyenera kutamandidwa konse. Pamaso pake, mapiri amanjenjemera, ndipo palibe wopanduka amene adzaperekedwa chilango. Dzina la Wamuyaya silitha; ali ndi mphamvu zosayerekezeka.

Chifukwa chake, konza zomwe zikuoneka zopindika mumtima mwako. Ngati pali choipa mumtima mwako, funa chikhululukiro kwa Mulungu, pakuti iye ndi wolungama komanso wachifundo. Usatsutse mawu ake kapena chifuniro chake, chifukwa sudzapila padziko lapansi ngati uchita zinthu mosemphana ndi zimene iye akufuna.

Lero ndi tsiku loyanjanirana naye, lotsegula mtima wako ndikudzitukumula pamaso pake, chifukwa mtima wodzichepetsa sudzatayidwa naye. Muzindikire m'njira zanu zonse ndipo musadzione ngati wanzeru pa maganizo anu, koma m'malo mwake, dalirani Mulungu ndipo musamadzikulitse; chifukwa, ngati simutero, moyo wanu udzawonongeka ndipo mudzapandukira amene anakulengani ndi kukupatsani moyo.

Njira za Mulungu ndi zangwiro ndipo zimatsogolera ku moyo wosatha, pomwe njira za munthu ndi zoyipa ndipo zimatsogolera ku imfa.


Yeremiya 28:16

Nchifukwa chake Chauta akunena kuti, ‘Chenjera, ndidzakuchotsa pa dziko lapansi. Ufa chaka chino chisanathe, chifukwa chakuti wakhala ukulalikira zopandukira Chauta.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 68:6

Anthu osiyidwa, Mulungu amaŵapatsa malo okhalamo, am'ndende amaŵatulutsa kuti akhale pa ufulu, koma anthu oukira, amaŵapirikitsira ku nthaka yoguga.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 15:22-23

Koma Samuele adati, “Kodi Chauta amakondwa ndi chiti: nsembe zopsereza ndi nsembe zina, kapena kumvera mau ake? Ndithu, ndi kumvera ndi kupereka nsembe kwabwino kwambiri nkumvera. Ndi kutchera khutu ndi kupereka mafuta ankhosa kwabwino kwambiri nkutchera khutu.

Kugalukira kuli ngati tchimo loombeza, kukhala wokanika kuli ngati tchimo lopembedza mafano. Popeza kuti mwakana mau a Chauta, Iyenso wakukanani kuti musakhalenso mfumu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 5:23

Koma anthu ameneŵa ndi okanika ndiponso a mtima waupandu. Adapatuka ndipo adapitiratu.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 13:5

Koma aphedwe mneneri aliyense kapena womasulira maloto aliyense amene akuuzani kuti muukire Chauta, Mulungu wanu, amene adakutulutsani ku Ejipito ndi kukuwombolani m'dziko laukapolo. Munthu wotero ndi woipa, chifukwa akufuna kukusiyitsani njira imene Chauta akufuna kuti muitsate. Aphedwe, ndipo pakutero mudzachotsa choipa chimenechi pakati panu.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 20:24

“Aroni saloŵa nao m'dziko limene ndidapatsa Aisraele. Adzafa, chifukwa choti nonse aŵirinu simudamvere lamulo langa ku madzi a ku Meriba kuja.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 12:14-15

Mukamaopa Chauta ndi kumamtumikira ndi kumamvera mau ake, osakana malamulo ake, ndiponso ngati nonsenu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Chauta, Mulungu wanu, zonse zidzakuyenderani bwino.

Koma mukapanda kumvera mau a Chauta nkumakana malamulo ake, ndiye kuti Iye adzakulangani inu ndi mfumu yanu yomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:1

Chauta akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira Ine! Amachita zodzikonzera okha osati zokonza Ine. Amachita chipangano chaochao, chosatsata chifuniro changa, ndipo amanka nachimwirachimwira.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 32:9

Ndipo Chauta adaonjeza kuti, “Anthu ameneŵa ndikuŵadziŵa, ngokanika kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 14:9

Koma musagalukire Chauta. Musaope anthu a m'dzikolo chifukwa tidzaŵaononga. Iwowo alibe oŵatchinjiriza, koma ife Chauta ali nafe, musaŵaope.”

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 9:7

Musaiŵale m'mene mudakwiyitsira Chauta, Mulungu wanu, m'chipululu muja. Kuyambira tsiku lija mudatuluka ku Ejipito kuja, mpaka tsiku limene mudafika kuno, mwakhala mukuukira Chauta, Mulungu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 5:10

Asenzetseni tchimo lao, Inu Mulungu. Upo wao woipa uŵagwetse iwo omwe, muŵachotse pamaso panu chifukwa cha zochimwa zao zambirimbiri, chifukwa akuukirani Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 63:10

Komabe iwo adampandukira, namkwiyitsa Mulungu. Motero Chauta adasanduka mdani wao, ndipo adamenyana nawo nkhondo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:24

“Akamachoka, adzaona mitembo ya anthu amene adandipandukira. Mphutsi zimene zidzaŵadya sizidzafa, ndipo moto umene udzaŵatentha sudzazima. Anthu a mitundu yonse poŵaona adzanyansidwa nawo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 2:19

Mudzalangidwa ndi machimo anu omwe: poti mwandikana, ndidzakuimbani mlandu. Muganizire bwino za kuipa kwake kwa kundisiya Ine, Chauta, Mulungu wanu. Mulingalire kuŵaŵa kwake kwa kukhala osandiwopa,” akuterotu Ambuye, Chauta Wamphamvuzonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:8

Asakhale ngati makolo ao, anthu oukira ndi osamvera aja, mbadwo wa anthu amene mitima yao inali yosakhazikika, amene moyo wao unali wosakhulupirika kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 1:18

Pamenepo Chauta wakhoza, chifukwa ndine ndidapandukira malamulo ake. Imvani, inu anthu a mitundu yonse, onani kuvutika kwanga. Anamwali anga ndi anyamata anga atengedwa ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 3:42

Ifeyo tachimwa, ndipo tapanduka, tsono Inu simudakhululuke.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 4:17

Akuzinga Yerusalemu ngati alonda a munda, chifukwa choti anthu andipandukira,” akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 59:2

Machimo anu adakulekanitsani ndi Mulungu wanu, ndipo Iye wakufulatirani chifukwa cha machimo anuwo. Choncho saamva zimene inu mumanena.

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 13:16

A ku Samariya adzalangidwa chifukwa choti adapandukira Mulungu wao. Adzaphedwa ndi lupanga, ana ao adzaphedwa moŵakankhanthitsa pansi. Akazi ake apathupi adzang'ambidwa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 33:8

Ndidzaŵayeretsa pochotsa machimo ao onse ondichimwira. Ndidzaŵakhululukira zoipa zonse zimene adachita pondipandukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 31:27

Ndikudziŵa kukanika kwanu ndiponso uchigaŵenga wanu. Ngati mugalukira Chauta, ndikadali moyo, nanji ndikadzafa, ndiye mudzaposa kugaluka kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 2:3

Musalole kuti wina akupusitseni mwa njira iliyonse. Pajatu lisanafike tsikulo, kudzayamba kwachitika zoti anthu ochuluka akupandukira Mulungu, ndipo kudzaoneka Munthu Woipitsitsa uja, woyenera kutayikayu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 5:25

Koma zolakwa zanu zaletsetsa zonsezi, ndipo machimo anu akumanitsani zokoma.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:11

pakuti adaatsutsa mau a Mulungu, adaakana monyoza malangizo a Wopambanazonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 13:2

Motero munthu wokana kumvera olamulira, akukana dongosolo limene adaliika Mulungu. Ndipo ochita zimenezi, adzadzitengera okha chilango.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 3:13

Ungovomera kulakwa kwako. Vomera kuti udaukira Chauta Mulungu wako, kuti udapembedza nao milungu yachilendo patsinde pa mitengo yogudira, ndiponso kuti sudamvere mau anga,’ ” akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 15:23

Kugalukira kuli ngati tchimo loombeza, kukhala wokanika kuli ngati tchimo lopembedza mafano. Popeza kuti mwakana mau a Chauta, Iyenso wakukanani kuti musakhalenso mfumu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 20:8

Koma adandipandukira, adakana kundimvera. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adasiya zonyansa zake zimene ankasangalala nazo. Palibe amene adasiya mafano a ku Ejipito. Tsono ndidaganiza zoŵaonetsa ukali ndi mkwiyo wanga ku Ejipito komwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 59:13

Takupandukirani, takukanani, Inu Chauta, ndipo takana kukutsatani. Tapanikiza anzathu, takupandukirani Inu. Maganizo athu ndi abodza, mau athu ndi onama.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:11

Munthu woipa mtima amangofuna zoukira. Tsono adzamtumira wamthenga wankhalwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 20:13

Koma Aisraele adandipandukira m'chipululumo. Sadatsate malangizo anga ndipo adakana malamulo anga, amene amakhalitsa moyo anthu oŵamvera. Anthuwo adaipitsa kotheratu masiku anga a Sabata. Motero Ine ndidaganiza zoŵalanga mwaukali m'chipululu momwemo ndi kuŵaononga kotheratu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 2:3

Adandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, ndikukutuma kwa Israele, mtundu wa anthu aupandu amene andipandukira. Iwowo ndi makolo ao akhala akundichimwira mpaka lero lino.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 106:43

Nthaŵi zambiri Iye ankaŵapulumutsa, koma iwo ankamuukirabe osaleka, namamira m'machimo ao,

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:7

Anthu oika mtima pa khalidwe lokonda zoipa, amadana ndi Mulungu. Anthu otere sagonjera Malamulo a Mulungu, ndipo kunena zoona, sangathedi kuŵagonjera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 65:2

Nthaŵi zonse ndakhala wokonzeka kuŵalandira mwaufulu anthu ondipandukiraŵa, amene amachita zoipa namatsata njira zao chifukwa cha kuuma mitu kwao.

Mutu    |  Mabaibulo
Nehemiya 9:26

“Komabe iwowo sankamvera, ndipo adakuukirani. Adaŵataya kunkhongo Malamulo anu, napha aneneri anu amene ankaŵadzudzula kuti abwerere kwa Inu. Adachita zinthu zoipitsitsa zokunyozani.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 1:26-27

Koma inu simudafune kupita, mudaukira ulamuliro wa Chauta, Mulungu wanu.

Inu munkangodandaula m'mahema mwanu nkumati, “Chauta amadana nafe. Nchifukwa chake adatitulutsa ku dziko la Ejipito, natipereka kwa Aamori kuti atiphe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:2

Chauta adati, “Tamvera, iwe mlengalenga, tchera khutu, iwe dziko lapansi, Ine Chauta ndikulankhula. Ndidabereka ana ndi kuŵalera, koma andigalukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 44:16-17

“Ife sitidzamvera zimene watiwuza m'dzina la Chauta.

Koma tidzachitadi zonse zimene tidalumbira. Tidzaifukizira ndithu lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuiperekera nsembe zazakumwa, monga tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akalonga athu, m'mizinda ya ku Yuda ndi m'miseu ya mu Yerusalemu. Nthaŵi imeneyo tinali ndi chakudya chambiri, ndipo tinkakhuta, osapeza zovuta.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 2:4

Pakuti Mulungu sadaŵalekerere angelo amene adachimwa aja, koma adaŵaponya m'ng'anjo yamoto, m'maenje amdima momwe ali omangidwa kudikira chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 36:16

Koma anthuwo ankapeputsabe amithengawo, namanyoza mau a Mulungu. Ndipo ankaŵaseka aneneri ake, mpaka Chauta adakwiyira anthu ake, ndipo panalibenso mankhwala ochiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 2:29

Chauta akuti, “Kodi mukundiimbiranji mlandu? Nonsenu mwandipandukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 4:6

Anthu anga akuwonongeka chifukwa Ine sandidziŵa. Ndidzakukanani kuti musanditumikire ngati ansembe, chifukwa choti mwakana kuphunzitsa za Ine. Mwaiŵala malamulo a Mulungu wanu, tsono Inenso Mulungu wanu ndidzaiŵala ana anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 8:5

Chifukwa chiyani nanga anthu ameneŵa akupitirirabe kulakwa, osabwereranso? Akangamira ndithu machimo ao, akukana kubwerera.

Mutu    |  Mabaibulo
Oweruza 2:19

Koma nthaŵi zonse mtsogoleri akafa, anthuwo ankayambanso kuchita zoipa, nkusanduka oipa kupambana makolo ao, namatsata milungu ina, kumaitumikira ndi kumaigwadira. Sankaleka kuchita zimene adaazoloŵera ndiponso sankaleka kukhala ouma mitu.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 33:3

Pitani ku dziko lamwanaalirenji. Koma Ine sindidzapita nanu chifukwa ndinu anthu okanika, ndipo ndingathe kukuwonongani panjira.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 81:11-12

“Koma anthu anga sadamvere mau anga. Israele adandinyoza.

Choncho ndidaŵasiya ndi mitima yao yosamverayo, kuti atsate zimene ankafuna.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 7:24

Koma anthuwo sadamvere, sadasamaleko, ndipo adapitirira kukhala osamvera ndi mitima yao yoipa. Adayang'ana zam'mbuyo osati zakutsogolo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mafumu 17:14-15

Koma anthuwo sankamva, anali ouma mitu monga momwe analiri makolo ao amene sadakhulupirire Chauta Mulungu wao.

Iwowo adanyoza malamulo a Chauta ndi chipangano cha Chauta chimene Iye adachita ndi makolo ao. Adanyozanso zochenjeza za Chauta. Adatsata milungu yachabechabe, ndipo iwo omwe adasanduka achabechabe. Ankatsata zitsanzo za anthu a mitundu ina okhala nawo pafupi, ngakhale Chauta anali atalamula kuti asamachite mofanana ndi mitundu imeneyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 48:8

Chikhalire sudamve chikhalire sudadziŵe, nkale lonse makutu ako sanali otsekuka. Chifukwa ndidaadziŵa kuti ndiwe wachiwembu, ndipo kuti chiyambire cha ubwana wako adakutchula waupandu.

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 7:13

“Tsoka kwa iwo pakuti andisiya Ine. Aonongeke chifukwa chakuti andipandukira. Ndimafuna kuŵapulumutsa, koma amangolankhula zabodza za Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 20:21

“Koma ana ao nawonso adandipandukira. Sadatsate malangizo anga, sadamvere malamulo anga, amene amakhalitsa moyo anthu oŵamvera. Ndiponso adaipitsa masiku anga a Sabata. Tsono ndidaganiza zoŵalanga mokwiya ndi kuŵalipsira m'chipululu momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:9

Wina akamakana kumvera malamulo, ngakhale mapemphero ake amanyansira Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 11:10

Abwereranso ku machimo a makolo ao amene adakana kundimvera. Akutsata milungu ina ndi kumaipembedza. A ku Israele ndi a ku Yuda aphwanya chipangano chimene ndidapangana ndi makolo ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 31:29

Ndikudziŵa kuti ine ndikadzafa, nonse mudzaipa ndipo mudzakana zimene ndakuuzanizi. Koma pambuyo pake kutsogoloko, mudzakomana ndi masoka, chifukwa chochita zoipa pamaso pa Chauta ndi kuputa mkwiyo wake pakuchulukitsa machimo anu. Mwakwiyitsa Chauta pochita zimene Iyeyo amakana.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:28

Koma opanduka ndi ochimwa adzaŵaonongera pamodzi, osiya Chauta adzatheratu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 25:4-5

Inu simudamvere kapena kutchera khutu, ngakhale kuti Chauta sadaleke kukutumirani aneneri, atumiki ake.

Aneneriwo ankati, ‘Aliyense mwa inu akaleka makhalidwe ake oipa ndi ntchito zake zoipa, ndiye kuti mudzakhala m'dziko limene Chauta adakupatsani inu ndi makolo anu mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:40

Kaŵirikaŵiri ankamuukira m'chipululu, ankamumvetsa chisoni.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 50:5

Ambuye Chauta anditsekula makutu, ndipo sindidaŵanyoze kapena kuŵapandukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 13:10

Anthu oipaŵa akana kumvera mau anga. Atsata milungu ina, namaitumikira nkumaipembedza. Iwowo adzakhala ngati mpango wopanda ntchitowu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 23:35

“Nchifukwa chake Ine Ambuye Chauta ndikuti, Chifukwa chakuti wandiiŵala Ine ndi kundifulatira, uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi zigololo zako.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 9:13-14

Apo Chauta adayankha kuti, “Nchifukwa chakuti anthu angawo sadatsate malamulo amene ndidaŵapatsa, ndipo sadamvere mau anga ndi kuŵasamala.

Koma ankangotsata zolakwa za mitima yao yokanika. Ankapembedza Abaala monga momwe makolo ao adaŵaphunzitsira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 106:7

Pamene makolo athu anali ku Ejipito, sadasamale ntchito zanu zodabwitsa. Sadakumbukire kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, koma adaukira Mulungu Wopambanazonse ku Nyanja Yofiira kuja.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:9

Ameneŵa ndi anthu opandukira Mulungu, ana onama, okana kumvera malangizo a Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Malaki 3:7

Kuyambira masiku a makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga, simudaŵatsate konse. Ngati mubwerera kwa Ine, Inenso ndidzabwerera kwa inu. Ndikutero Ine Chauta Wamphamvuzonse. Komabe inu mumati, ‘Kodi tingathe kubwerera bwanji?’

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 15:6

Ine mudandikana, mukupitirirabe kundifulatira. Motero ndidakweza mkono wanga nkukukanthani. Ndidatopa nako kukhululuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 14:1

Mumtima mwake munthu wopusa amati, “Kulibe Mulungu.” Anthu otereŵa ndi oipa, amachita zonyansa, palibe ndi mmodzi yemwe wochita zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
Nehemiya 9:17

Adakana kumvera, ndipo sankakumbuka zodabwitsa zimene Inu mudaazichita pakati pao. Adakhala okanika, nadzisankhira mtsogoleri woti aŵatsogolere kubwerera ku Ejipito ku dziko laukapolo lija. Koma Inu ndinu Mulungu wokhululuka, wokoma mtima, wachifundo, wosakwiya msanga, wokhala ndi chikondi chachikulu chosasinthika, motero iwowo simudaŵasiye.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:24-26

Paja ine ndidaakuitanani, inu nkukana kumvera, ndidaati ndikuthandizeni, koma popanda wosamalako.

Uphungu wanga simudaulabadire, kudzudzula kwanga simudakusamale.

Ndiye inenso ndidzakusekani, mukadzagwa m'mavuto, ndidzakunyodolani, mukadzazunguzika ndi mantha,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 12:19

Motero Aisraele akumpoto adakhala akupandukira banja la Davide mpaka lero lino.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 29:13

Ambuye adati, “Anthu aŵa amati amapemphera kwa Ine, koma mau ao ndi opanda tanthauzo, ndipo mitima yao ili kutali ndi Ine. Chipembedzo chao ndi kungotsata chabe malamulo ongoŵaloŵeza pamtima, malamulo ochokera kwa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 32:33

Andifulatira kotheratu. Ngakhale ndidavutikira kumaŵaphunzitsa, sadamve kapena kutolapo nzeru iliyonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Zekariya 7:11-12

“Koma iwowo adakana kumvera, adandifulatira ndi mtima wokanika. Adatseka makutu ao kuti asamve.

Mitima yao adaiwumitsa kwambiri, kuti asamve malamulo ndi mau amene Ine Chauta Wamphamvuzonse ndidaŵaphunzitsa ndi Mzimu wanga kudzera mwa aneneri amakedzana. Nchifukwa chake Ine Chauta Wamphamvuzonse ndidaŵakwiyira kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 5:24

Nchifukwa chake monga momwe moto umaonongera chiputu, monga momwenso udzu wouma umapsera m'malaŵi a moto, momwemonso muzu wao udzaola, ndipo maluŵa ao adzafota ndi kuuluka ngati fumbi, chifukwa adakana malamulo a Chauta Wamphamvuzonse, adanyoza mau a Woyera uja wa Israele.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 44:4-5

Komabe ine ndidakhala ndikutuma atumiki anga aneneri kuti adzakuuzeni kuti, ‘Musamachita zoipa zimene Ine ndimadana nazo.’

Koma makolo anuwo sadamvere, sadasamaleko nkomwe. Sadaleke kuchita zoipa zao, sadasiye kuifukizira lubani milungu ina.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:2-4

Anthu adzakhala odzikonda, okonda ndalama, onyada, odzikuza, onyoza Mulungu, osamvera anakubala ao, osayamika, ndi oipitsa zinthu za Mulungu.

Adzakhala opanda chifundo, osapepeseka, ndi osinjirira anzao. Adzakhala osadzigwira, aukali, odana ndi zabwino,

opereka anzao kwa adani ao. Adzakhala osaopa chilichonse, odzitukumula, okonda zosangalatsa m'malo mokonda Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 16:12

Komanso inu mudachimwa koposa kupambana makolo anu: aliyense mwa inu akutsata zoipa ndi mtima wake wokanika, m'malo momandimvera Ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 3:7

Koma Aisraele sadzakumvera, chifukwa safuna kundimvera Ine. Onsewo ngaliwuma ndi a mtima wosamvera.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 18:12

“Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nzopanda pake. Tidzachita monga m'mene tifunira, ndipo aliyense mwa ife azidzangotsata zoipa za mtima wake wokanika.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:21-23

Inde ankamudziŵa Mulungu, koma m'malo mwa kumtamanda kapena kumthokoza, maganizo ao adasanduka opanda pake, ndipo m'mitima yao yopusa mudadzaza mdima.

Iwo amadziyesa anzeru, koma chikhalirecho ndi opusa.

Adaleka kulemekeza Mulungu wosafa, nkumapembedza mafano ooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame ndi nyama zina, kapena zokwaŵa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:12

Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kopherezera kwake nku imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 3:15

Paja Malembo akuti, “Lero lino mukamva mau a Mulungu, musaumitse mitima yanu monga muja zidaachitikira poukira Mulungu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:32

Amalidziŵa lamulo la Mulungu lakuti anthu ochita zotere ndi oyenera kufa, komabe iwo omwe amachita zomwezo, ndiponso amavomerezana ndi anthu ena ozichita.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:3-4

“Koma pali ena amene amangochita zoŵakomera. Kwa iwo nchimodzimodzi kupereka ng'ombe yamphongo ngati nsembe kapena kupha munthu, kupha mwanawankhosa kuti aperekere nsembe kapena kupha galu, kupereka chopereka cha chakudya kapena kupereka magazi a nkhumba, kupereka lubani ku nsembe yachikumbutso kapena kupembedza fano. Anthu ameneŵa mtima wao umakondwera nazo zonyansa zao.

Ine tsono ndidzaŵagwetsera chilango ndipo ndidzaŵachititsa mantha, chifukwa nditaŵaitana, palibe amene adandiyankha, kapena kutchera khutu pamene ndinkalankhula. Adachita zoipa pamaso panga, adasankhula kuchita zimene zimandinyansa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 23:17

Saleka kuŵauza amene amandinyoza Ine kuti, ‘Zinthu zidzakuyenderani bwino.’ Ndipo amene amaumirira kutsata zofuna za mtima wao amaŵauza kuti, ‘Simudzaona vuto ai.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:26-27

Pakuti tikamachimwirachimwira mwadala, kwina tikudziŵa choona, palibenso nsembe ina iliyonse ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.

Pamenepo chotitsalira si china ai, koma kumangodikira ndi mantha chiweruzo, ndiponso moto woopsa umene udzaononga otsutsana ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 13:21-22

ndipo iyeyo adafuulira mneneri wa Mulungu, wochokera ku Yuda uja kuti, “Imvani mau a Chauta, akuti chifukwa choti simudamvere mau a Chauta, ndipo simudatsate lamulo lake limene adakulamulani,

koma mwabwerera, ndipo mwadya ndi kumwa madzi pa malo amene Chauta adakuuzani kuti musakadye chakudya kapena kumwako madzi, mtembo wanu sadzauika m'manda a makolo anu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 32:15

Yesuluni, anthu ake a Chauta adakulupala, koma iwowo adamuukira, adanenepa ndi kukula thupi, ndipo adakhuta zedi, kenaka adasiya Mulungu Mlengi wao, nanyoza mtetezi ndi mpulumutsi wao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 2:2-3

Mafumu ao akuchita upo, olamula ao akhala pamodzi kuti apangane zoipa, zoukira Chauta ndi mfumu yake yodzozedwa.

Akuti, “Tiyeni timasule maunyolo aoŵa, tichokeretu mu ulamuliro wao.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 50:17

Iwe sufuna kulangizidwa, umaponya mau anga ku nkhongo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 24:5

Anthu aipitsa dziko lapansi posatsata malamulo a Mulungu, ponyoza mau ake, ndipo pophwanya chipangano chamuyaya chimene Iye adapangana nawo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 22:21

Ndidaakuchenjezani pamene zinthu zinkakuyenderani bwino. Koma inu mudati, ‘Sitidzamvera.’ Ndi m'mene mwakhala mukuchitira kuyambira muli ana aang'ono, simudamvere mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 33:11

Uŵauze kuti Ine Ambuye Chauta ndikuti, Ndithudi, pali Ine ndemwe, sindikondwa ndikaona munthu woipa alikufa. Ndikadakonda kuti aleke kuchimwako kuti akhale ndi moyo. Inu Aisraele, muferanji? Tembenukani, lekani zoipa zimene mukuchita.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 24:20

Tsono mzimu wa Mulungu udaloŵa mwa Zekariya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye adaimirira pakati pa anthu naŵauza kuti, “Chauta akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mukuchimwira malamulo a Chauta? Ndithu simudzapindula kanthu?’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:10

sadasunge chipangano cha Mulungu, koma adakana kutsata malamulo ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 5:3

Kodi Inu Chauta, suja mumafuna anthu onena zoona? Inu mudaŵakantha anthuwo, koma iwo sadamve kuŵaŵa. Mudaŵatswanya, koma sadafune kutembenuka mtima. Adaumitsa mitima yao ngati mwala, adakana kwamtuwagalu kulapa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 16:8

Ndipo Mose adati, “Ndi Chauta amene adzakupatsani madzulo nyama yoti mudye, ndi m'maŵa buledi woti nkukhuta, chifukwa choti wamva madandaulo anu onse omuŵiringulira aja. Ife ndife yani? Madandaulo anu simudaŵiringulire ife ai, koma Chauta.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 7:13

Munkachita zoipa zonsezi, mudakana kundimvera nditakulankhulani kosalekeza, ndipo simudayankhe pamene ndidakuitanani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:16-19

Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Chauta amadana nazo, makamaka zisanu ndi ziŵiri ndithu zimene zimamunyansa:

maso onyada, pakamwa pabodza, manja opha munthu wosalakwa,

mtima wokonzekera kuchita zoipa, mapazi othamangira msangamsanga ku zoipa,

mboni yonama yolankhula mabodza, ndi munthu woutsa chidani pakati pa abale.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 24:13

Dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako, poti nditakutsuka sudayere. Tsono sudzayeranso mpaka mkwiyo wanga utakwaniratu pa iwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 2:13

Anthu anga achita machimo aŵiri: andisiya Ine kasupe wa madzi opatsa moyo, adzikumbira okha zitsime, zitsime zake zong'aluka, zosatha kusunga madzi.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 12:14

Koma Rehobowamuyo adachita zoipa, popeza kuti mtima wake sudafunitsitse Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 1:5

Kodi ndi pati ndingakumenyeninso, popeza kuti mukupandukirapandukira? Aliyense mutu wake uli ndi mabala kale, ndipo mtima wake wafookeratu.

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 9:9

Anthu aipiratu monga zidachitikira ku Gibea. Nchifukwa chake Mulungu sadzaiŵala kuipa kwao, ndipo adzalanga machimo ao.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 57:17

“Ndidaŵakwiyira chifukwa anali okonda chuma dziŵi. Tsono ndidaŵalanga, ndi kuŵafulatira mokwiya. Koma iwowo adakhalabe ouma mitu, ndipo adapitirira kuchita ntchito zao zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Amosi 4:6-8

“Ndine amene ndidakusendetsani milomo m'mizinda yanu yonse. Ndine amene ndidagwetsa njala konse kumene munkakhala. Komabe simudabwerere kwa Ine.” Akutero Chauta.

“Ndinenso amene ndidamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndine amene ndinkagwetsa mvula pa mudzi wina, koma pa mudzi wina ai. Mvula inkagwa pa munda wina, koma munda wina nkumakhala gwa, chifukwa chosoŵa mvula.

Motero midzi iŵiri kapena itatu inkapita ku mudzi umodzi kuti ikamwe madzi, koma osaŵakwanira. Komabe simudabwerere kwa Ine.” Akutero Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 20:38

Ndidzakuchotserani anthu amene amandipandukira ndi kundichimwira. Ndidzaŵatulutsa m'dziko limene akukhalamolo, koma sadzapondamo m'dziko la Israele. Motero mudzadziŵa kuti Ine ndine Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 19:15

“Chauta Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israele, akunena kuti, Ndidzagwetsa tsoka pa mzinda uwu pamodzi ndi pa midzi yake yonse monga ndidaanenera, chifukwa choti anthu ake ndi okanika, ndipo akukana kumvera mau anga.”

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 8:9

Anthu anzeru adzachita manyazi, adzatha nzeru, ndipo adzagwidwa. Akana mau a Chauta, nanga nzeru zao nzotani?

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 25:7

Komabe simudandimvere. Mudaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene mudapanga ndi manja anu, motero mudadziwononga nokha,” akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 28:15

Komatu mukapanda kumvera bwino mau a Chauta, Mulungu wanu, ndi kutsata malamulo ndi malangizo amene ndikukupatsani lero lino, adzakugwerani matemberero aŵa:

Mutu    |  Mabaibulo
2 Mbiri 30:8

Musati muumitse makosi anu monga m'mene ankachitira makolo anu, koma mudzipereke kwa Chauta, ndipo muzibwera ku Nyumba yake imene Chautayo waiyeretsa mpaka muyaya. Ndipo muzitumikira Chauta, Mulungu wanu, kuti mkwiyo wake woopsa ukuchokeni.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 10:6

Ndikumtuma kwa mtundu wosasamala za Mulungu, ndipo ndikumlamula kuti apite kwa anthu amene ndaŵakwiyira, kuti akafunkhe ndi kukalanda chuma chao chonse, ndi kuŵaponderezera pansi ngati matope am'miseu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mika 3:4

“Nthaŵi ikubwera pamene mudzalira kwa Chauta, koma sadzakuyankhani. Nthaŵi imeneyo adzakufulatirani chifukwa ntchito zanu nzoipa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Amosi 2:4

Zimene akunena Chauta ndi izi: “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, sindileka kuŵalanga. Iwo anyoza malamulo a Ine Chauta, ndipo sadatsate malangizo anga. Milungu yabodza imene makolo ao ankaipembedza yaŵasokeretsa.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Mtima wanga ukukutamandani Mulungu Wamuyaya, manja anu andilenga ndipo munapatsa mpweya moyo wanga. Ulamuliro wanu ndi waukulu, zonse zakumwamba ndi zapadziko lapansi zili pansi pa mphamvu zanu. Chifukwa cha ichi, ndikupatsani ulemerero wonse chifukwa ndinu woyenera kutamandidwa. Mulungu wanga, lero ndimayimirira pamaso panu ndi mtima wodzichepetsa. Ndikufuna mundisanthule mkati mwanga ndi kunditsuka ku zoipa zanga zonse. Ngati ndakhala ndi malingaliro kapena zochita zonditsutsa inu, ndikupempha chikhululukiro. Sindikufuna kuchita chilichonse chotsutsana ndi chifuniro chanu. Chonde wongolani mapazi anga ndi kundionetsa njira yoyenera kuyendamo. Musandilole kudzidalira kwambiri kapena mtima wanga ukukutsutsani. Ndidzimasula ku malingaliro onse akundikopa kuchita zoipa. Mu dzina la Yesu, ndikukuthokozani chifukwa cha mtima woyera womwe mwandipatsa. M'dzina la Yesu, Ameni.