Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

100 Mau a m'Baibulo Okhudza Gehena

Ndikufuna ndikufotokozereni za malo amene akufa amapita, osiyana ndi chilango chomaliza cha oipa. Ngakhale kuti mawuwa achokera ku nkhani zakale zachikunja, tanthauzo lake lenileni lachokera ku mawu achihebri akuti Sheol. Mawuwa amapezeka nthawi makumi asanu ndi limodzi mphambu zisanu m’Malemba Achihebri, ndipo ngakhale kuti m’ma Baibulo ena amawamasulira kuti gehena, manda, kapena dzenje, Baibulo la Chichewa limagwiritsa ntchito mawu akuti Sheol. Mofanana ndi momwe mawu akuti Hades amagwiritsidwira ntchito m’Malemba Achigiriki.

Chofunika kwambiri apa ndichakuti Yesu anauza Petro kuti zipata za Hades sizidzalimbana ndi mpingo. Izi zikutanthauza kuti Yesu wapatsa mpingo mphamvu zoposa mphamvu zonse za mdani kuti tilengeze moyo pamene mdani walengeza imfa. Choncho, tifunika nthawi zonse kuima m’malo mwa anthu, kulankhula Mawu a Mulungu, ndikupemphera kuti chifuniro cha Mulungu chichitike padziko lapansi.


Machitidwe a Atumwi 2:27

Pakuti simudzasiya moyo wanga ku dziko la akufa, kapena simudzapereka Woyera wanu aone chivunde,

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 16:18

Ndiponso Ine ndinena kwa iwe, kuti iwe ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe ili ndidzakhazika Mpingo wanga; ndipo makomo a dziko la akufa sadzagonjetsa uwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 2:31

iye pakuona ichi kale, analankhula za kuuka kwa Khristu, kuti sanasiyidwe m'dziko la akufa, ndipo thupi lake silinaone chivunde.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 10:15

Ndipo iwe, Kapernao, kodi udzakwezedwa kufikira Kumwamba? Udzatsitsidwa kufikira ku dziko la akufa.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 16:23

Ndipo m'dziko la akufa anakweza maso ake, pokhala nao mazunzo, naona Abrahamu patali, ndi Lazaro m'chifuwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 1:18

ndi Wamoyoyo; ndipo ndinali wakufa, ndipo taona, ndili wamoyo kufikira nthawi za nthawi, ndipo ndili nazo zofungulira za imfa ndi dziko la akufa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 20:13

Ndipo nyanja inapereka akufawo anali momwemo, ndipo imfa ndi dziko la akufa zinapereka akufawo anali m'menemo; ndipo anaweruzidwa yense monga mwa ntchito zake.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:22

koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wokwiyira mbale wake wopanda chifukwa adzakhala wopalamula mlandu; ndipo amene adzanena ndi mbale wake, Wopanda pake iwe, adzakhala wopalamula mlandu wa akulu: koma amene adzati, Chitsiru iwe: adzakhala wopalamula Gehena wamoto.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 11:23

Ndipo iwe, Kapernao, udzakwezedwa kodi kufikira kuthambo? Udzatsika kufikira ku dziko la akufa! Chifukwa ngati zamphamvu zimene zachitidwa mwa iwe zikadachitidwa mu Sodomu, uyo ukadakhala kufikira lero.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 6:8

Ndipo ndinapenya, taonani, kavalo wotumbuluka; ndipo iye womkwera, dzina lake ndiye Imfa; ndipo dziko la akufa linatsatana naye; ndipo anawapatsa ulamuliro pa dera lachinai la dziko, kukapha ndi lupanga, ndi njala, ndi imfa, ndi zilombo za padziko.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:28

Ndipo musamaopa amene akupha thupi, koma moyo sangathe kuupha; koma makamaka muope Iye, wokhoza kuononga moyo ndi thupi lomwe muGehena.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 20:13-14

Ndipo nyanja inapereka akufawo anali momwemo, ndipo imfa ndi dziko la akufa zinapereka akufawo anali m'menemo; ndipo anaweruzidwa yense monga mwa ntchito zake.

Ndipo imfa ndi dziko la akufa zinaponyedwa m'nyanja yamoto. Iyo ndiyo imfa yachiwiri, ndiyo nyanja yamoto.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 23:33

Njoka inu, obadwa inu a mamba, mudzatha bwanji kuthawa kulanga kwake kwa Gehena?

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 16:24

Ndipo anakweza mau nati, Atate Abrahamu, mundichitire chifundo, mutume Lazaro, kuti aviike nsonga ya chala chake m'madzi, naziziritse lilime langa; pakuti ndizunzidwadi m'lawi ili la moto.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 16:26

Ndipo pamwamba pa izi, pakati pa ife ndi inu pakhazikika phompho lalikulu, kotero kuti iwo akufuna kuoloka kuchokera kuno kunka kwa inu sangathe, kapena kuchokera kwanuko kuyambuka kudza kwa ife, sangathenso.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 16:28

pakuti ndili nao abale asanu; awachitire umboni iwo kuti iwonso angadze kumalo ano a mazunzo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 6:23

Pakuti mphotho yake ya uchimo ndi imfa; koma mphatso yaulere ya Mulungu ndiyo moyo wosatha wa mwa Khristu Yesu Ambuye wathu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:10

Pakuti ife tonse tiyenera kuonetsedwa kumpando wakuweruza wa Khristu, kuti yense alandire zochitika m'thupi, monga momwe anachita, kapena chabwino kapena choipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:7

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 3:19

chitsiriziro chao ndicho kuonongeka, mulungu wao ndiyo mimba yao, ulemerero wao uli m'manyazi ao, amene alingirira za padziko.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 9:27

Ndipo popeza kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi, ndipo atafa, chiweruziro;

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:27

koma kulindira kwina koopsa kwa chiweruziro, ndi kutentha kwake kwa moto wakuononga otsutsana nao.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:6

Ndipo lilime ndilo moto; ngati dziko la chosalungama mwa ziwalo zathu laikika lilime, ndili lodetsa thupi lonse, niliyatsa mayendedwe a chibadwidwe, ndipo liyatsidwa ndi Gehena.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:19

m'menemonso anapita, nalalikira mizimu inali m'ndende,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:6

Pakuti chifukwa cha ichi walalikidwa Uthenga Wabwino kwa iwonso adafawo, kuti akaweruzidwe monga mwa anthu m'thupi, koma akakhale ndi moyo monga mwa Mulungu mumzimu.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 2:11

Iye wokhala nalo khutu amve chimene Mzimu anena kwa Mipingo. Iye amene apambana sadzachitidwa choipa ndi imfa yachiwiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 20:10

Ndipo mdierekezi wakuwasokeretsa anaponyedwa m'nyanja ya moto ndi sulufure, kumeneko kulinso chilombocho ndi mneneri wonyengayo; ndipo adzazunzidwa usana ndi usiku kunthawi za nthawi.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 20:14

Ndipo imfa ndi dziko la akufa zinaponyedwa m'nyanja yamoto. Iyo ndiyo imfa yachiwiri, ndiyo nyanja yamoto.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 21:8

Koma amantha, ndi osakhulupirira, ndi onyansa, ndi ambanda, ndi achigololo, ndi olambira mafano, ndi onse a mabodza, cholandira chao chidzakhala m'nyanja yotentha ndi moto ndi sulufure; ndiyo imfa yachiwiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 14:9

Kunsi kwa manda kugwedezeka, chifukwa cha iwe, kukuchingamira podza pako; kukuutsira iwe mizimu, ngakhale onse akuluakulu a dziko lapansi; kukweza kuchokera m'mipando yao mafumu onse a amitundu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 14:15

Koma udzatsitsidwa kunsi kumanda, ku malekezero a dzenje.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 66:24

Ndipo iwo adzatuluka ndi kuyang'ana mitembo ya anthu amene andilakwira Ine, pakuti mphutsi yao sidzafa, pena moto wao sudzazimidwa; ndipo iwo adzanyansa anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 32:21

Amphamvu oposa ali m'kati mwa manda adzanena naye, pamodzi ndi othandiza ake, Anatsikira, agonako osadulidwawo, ophedwa ndi lupanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 32:27

Koma sagona pamodzi ndi amphamvu osadulidwa adagwawo amene anatsikira kumanda ndi zida zao za nkhondo, amene anawatsamiritsa malupanga ao; ndi mphulupulu zao zili pa mafupa ao; pakuti anaopsetsa amphamvu m'dziko la amoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 12:2

Ndipo ambiri a iwo ogona m'fumbi lapansi adzauka, ena kunka kumoyo wosatha, ndi ena kumanyazi ndi mnyozo wosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 8:12

koma anawo a Ufumu adzatayidwa kumdima wakunja; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 22:13

Pomwepo mfumu inati kwa atumiki, Mumange iye manja ndi miyendo, mumponye kumdima wakunja; komweko kudzali kulira ndi kukukuta mano.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 24:51

nadzamdula, nadzaika pokhala pake ndi anthu onyenga; pomwepo padzakhala kulira ndi kukukuta mano.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 25:30

Ndipo ponyani kapoloyo wopanda pake kumdima wakunja; kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:5

Koma ndidzakulangizani amene muzimuopa; taopani Iye amene atatha kupha ali ndi mphamvu yakutaya ku Gehena, inde, ndinena ndinu opani ameneyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 13:28

Kudzakhala komweko kulira ndi kukukuta mano, pamene mudzaona Abrahamu, ndi Isaki, ndi Yakobo, ndi aneneri onse, mu Ufumu wa Mulungu, koma inu nokha mutulutsidwa kunja.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 16:19

Ndipo panali munthu mwini chuma amavala chibakuwa ndi nsalu yabafuta, nasekera, nadyerera masiku onse;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:18

Pakuti mkwiyo wa Mulungu, wochokera Kumwamba, uonekera pa chisapembedzo chonse ndi chosalungama cha anthu, amene akanikiza pansi choonadi m'chosalungama chao;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 2:8

koma kwa iwo andeu, ndi osamvera choonadi, koma amvera chosalungama, adzabwezera mkwiyo ndi kuzaza,

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 2:9

nsautso ndi kuwawa mtima, kwa moyo wa munthu aliyense wakuchita zoipa, kuyambira Myuda, komanso Mgriki;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 1:9

amene adzamva chilango, ndicho chionongeko chosatha chowasiyanitsa kunkhope ya Ambuye, ndi kuulemerero wa mphamvu yake,

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 14:11

ndipo utsi wa kuzunza kwao ukwera kunthawi za nthawi; ndipo sapuma usana ndi usiku iwo akulambira chilombocho ndi fano lake, ndi iye aliyense akalandira lemba la dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 20:15

Ndipo ngati munthu sanapezedwe wolembedwa m'buku la moyo, anaponyedwa m'nyanja yamoto.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 9:17

Oipawo adzabwerera kumanda, inde amitundu onse akuiwala Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:15

Imfa iwagwere modzidzimutsa, atsikire kumanda ali amoyo, pakuti m'mokhala mwao muli zoipa pakati pao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 86:13

Pakuti chifundo chanu cha pa ine nchachikulu; ndipo munalanditsa moyo wanga kunsi kwa manda.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:24

Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera, kuti apatuke kusiya kunsi kwa manda.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 27:20

Kunsi kwa manda ndi kuchionongeko sikukhuta; ngakhale maso a munthu sakhutai.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 5:14

Ndipo manda akuza chilakolako chake, natsegula kukamwa kwake kosayeseka; ndi ulemerero wao, ndi unyinji wao, ndi phokoso lao, ndi iye amene akondwerera mwa iwo atsikira mommo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 28:15

Chifukwa inu munati, Ife tapangana pangano ndi imfa, tavomerezana ndi kunsi kwa manda; pakuti mliri wosefukira sudzatifikira ife; pakuti tayesa mabodza pothawirapo pathu, ndi kubisala m'zonyenga;

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 30:33

Pakuti Tofeti wakonzedwa kale, inde chifukwa cha mfumu wakonzedweratu; Iye wazamitsapo, nakuzapo; mulu wakewo ndi moto ndi nkhuni zambiri; mpweya wa Yehova uuyatsa ngati mtsinje wa sulufure.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 3:55

Ndinaitana dzina lanu, Yehova, ndili m'dzenje lapansi;

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 18:30

Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 33:11

Uziti nao, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, sindikondwera nayo imfa ya woipa, koma kuti woipa aleke njira yake, nakhale ndi moyo; bwererani, bwererani, kuleka njira zanu zoipa, muferenji inu nyumba ya Israele?

Mutu    |  Mabaibulo
Hoseya 13:14

Ndidzawaombola kumphamvu ya kumanda, ndidzawaombola kuimfa; imfa, miliri yako ili kuti? Kulekerera kudzabisika pamaso panga.

Mutu    |  Mabaibulo
Mika 1:5

Chichitika ichi chonse chifukwa cha kulakwa kwa Yakobo, ndi machimo a nyumba ya Israele. Kulakwa kwa Yakobo nkotani? Si ndiko Samariya? Ndi misanje ya Yuda ndi iti? Si ndiyo Yerusalemu?

Mutu    |  Mabaibulo
Habakuku 3:14

Munapyoza ndi maluti ake mutu wa ankhondo ake; anadza ngati kamvulumvulu kundimwaza; kukondwerera kwao kunanga kufuna kutha ozunzika mobisika.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:13

Lowani pa chipata chopapatiza; chifukwa chipata chili chachikulu, ndi njira yakumuka nayo kukuonongeka ili yotakata; ndipo ali ambiri amene alowa pa icho.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 13:42

ndipo adzawataya iwo m'ng'anjo yamoto; kumeneko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 13:50

nadzawataya m'ng'anjo yamoto; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 25:41

Pomwepo Iye adzanena kwa iwo a kudzanja lamanzere, Chokani kwa Ine otembereredwa inu, kumoto wa nthawi zonse wokolezedwera mdierekezi ndi angelo ake:

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 9:25

Pakuti munthu apindulanji, akadzilemezera dziko lonse lapansi nadzitayapo, kapena kulipapo moyo wake?

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 3:36

Iye amene akhulupirira Mwanayo ali nao moyo wosatha; koma iye amene sakhulupirira Mwanayo sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu ukhala pa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 8:24

Chifukwa chake ndinati kwa inu, kuti mudzafa m'machimo kwa inu, kuti mudzafa m'machimo anu, pakuti ngati simukhulupirira kuti Ine ndine, mudzafa m'machimo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:1

Chifukwa chake tsopano iwo akukhala mwa Khristu Yesu alibe kutsutsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 6:9

Kapena simudziwa kuti osalungama sadzalandira ufumu wa Mulungu? Musasocheretsedwe; adama, kapena opembedza mafano, kapena achigololo, kapena olobodoka ndi zoipa, kapena akudziipsa ndi amuna,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 15:22

Pakuti monga mwa Adamu onse amwalira, choteronso mwa Khristu onse akhalitsidwa ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:19-21

Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,

Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu.

kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:5

Pakuti ichi muchidziwe kuti wadama yense, kapena wachidetso, kapena wosirira, amene apembedza mafano, alibe cholowa mu ufumu wa Khristu ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:6

chifukwa cha izi zomwe ukudza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera;

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 6:4-6

Pakuti sikutheka kuwakonzanso, atembenuke mtima, iwo amene anaunikidwa pa nthawi yake, nalawa mphatso ya Kumwamba, nakhala olandirana naye Mzimu Woyera,

nalawa mau okoma a Mulungu, ndi mphamvu ya nthawi ilinkudza,

koma anagwa m'chisokero; popeza adzipachikiranso okha Mwana wa Mulungu, namchititsa manyazi poyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 12:29

Pakuti Mulungu wathu ndiye moto wonyeketsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:12

Woika lamulo ndi woweruza ndiye mmodzi, ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuononga; koma iwe woweruza mnzako ndiwe yani?

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 2:15-17

Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko lapansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, chikondi cha Atate sichili mwa iye.

Pakuti chilichonse cha m'dziko lapansi, chilakolako cha thupi ndi chilakolako cha maso, matamandidwe a moyo, sizichokera kwa Atate, koma kudziko lapansi.

Ndipo dziko lapansi lipita, ndi chilakolako chake; koma iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala kunthawi yonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 3:5

Iye amene apambana adzamveka motero zovala zoyera; ndipo sindidzafafaniza ndithu dzina lake m'buku la moyo, ndipo ndidzamvomereza dzina lake pamaso pa Atate wanga, ndi pamaso pa angelo ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 3:16

Kotero, popeza uli wofunda, wosati wotentha kapena wozizira, ndidzakulavula m'kamwa mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:20

Pakuti oipa adzatayika, ndipo adani ake a Yehova adzanga mafuta a anaankhosa; adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 49:14

Aikidwa m'manda ngati nkhosa; mbusa wao ndi imfa. Ndipo m'mawa mwake oongoka mtima adzakhala mafumu ao; ndipo maonekedwe ao adzanyekera kumanda, kuti pokhala pake padzasowa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:27

Pakuti, taonani, iwo okhala patali ndi Inu adzaonongeka; muononga onse akupembedza kwina, kosiyana ndi Inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:18

Ndipo mwamunayo sadziwa kuti akufa ali konko; omwe achezetsa utsiru ali m'manda akuya.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:7

Amayesa wolungama wodala pomkumbukira; koma dzina la oipa lidzavunda.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 9:10

Chilichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 57:21

Palibe mtendere, ati Mulungu wanga, kwa oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 7:34

Ndipo ndidzaletsa m'mizinda ya Yuda, ndi m'miseu ya Yerusalemu, mau akukondwa ndi mau akusekera, ndi mau a mkwati ndi mau a mkwatibwi; pakuti dziko lidzasanduka bwinja.

Mutu    |  Mabaibulo
Maliro 2:22

Mwaitana zondiopsa mozungulira ngati tsiku la msonkhano; panalibe wopulumuka ndi wotsala tsiku la mkwiyo wa Yehova; omwe ndinawaseweza ndi kuwalera, adaniwo anawatsiriza.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 31:17

Iwonso anatsika naye kumanda kwa iwo ophedwa ndi lupanga, ndiwo amene adakhala dzanja lake okhala mumthunzi mwake pakati pa amitundu.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 32:11

Pakuti atero Ambuye Yehova, Lupanga la mfumu ya ku Babiloni lidzakudzera.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:36

Ndipo ndinena kwa inu, kuti mau onse opanda pake, amene anthu adzalankhula, adzawawerengera mlandu wake tsiku la kuweruza.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 13:30

Kazilekeni zonse ziwiri, zikulire pamodzi kufikira pakututa; ndimo m'nyengo yakututa ndidzauza akututawo, Muyambe kusonkhanitsa namsongole, mummange uyu mitolo kukamtentha, koma musonkhanitse tirigu m'nkhokwe yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 8:31

Ndipo zinampempha Iye, kuti asazilamulire zichoke kulowa ku chiphompho chakuya.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:32

amene ngakhale adziwa kuweruza kwake kwa Mulungu, kuti iwo amene achita zotere ayenera imfa, azichita iwo okha, ndiponso avomerezana ndi iwo akuzichita.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 2:12

kuti aweruzidwe onse amene sanakhulupirire choonadi, komatu anakondwera ndi chosalungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:31

Kugwa m'manja a Mulungu wamoyo nkoopsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 19:20

Ndipo chinagwidwa chilombocho, ndi pamodzi nacho mneneri wonyenga amene adachita zizindikiro pamaso pake, zimene anasokeretsa nazo iwo amene adalandira lemba la chilombo, ndi iwo akulambira fano lake; iwo awiri anaponyedwa ali moyo m'nyanja yamoto yakutentha ndi sulufure:

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga, dzina lanu ndi lolemekezeka ndi loopsa, palibe chofanana ndi chiyero chanu. Lero ndikulapa machimo anga ndipo ndikupempha chikhululukiro, ndikudziwa kuti kukhalapo kwanu kokha kunganditsuke kuti ndikhale wopanda kuipa ndi mantha. Mundipatse kukhala mwana wanu wakhama ndi wodalirika pa nkhani ya chipulumutso changa, kuti moyo wanga ukhale wonunkhira bwino pamaso panu ndipo mapazi anga atsogoleredwe ndi mawu anu. Ambuye Yesu, lero ndikudzitukumula pamaso panu, ndikuvomereza tchimo langa, chonde, Ambuye ndikupemphani kuti mundibwezeretse, mundisinthe ndi kuchiritsa mabala omwe ulendo wandipatsa, musalole kuti moyo wanga uzunzidwe kwamuyaya ku Hade. Ndithandizeni kukuyembekezerani tsiku lililonse Yesu ndi lingaliro lakuti munabwera dzulo ndipo mudzabweranso mawa, musalole Ambuye kuti zonyansa, kuipitsidwa, kapena kudzikuza zindichotse maso anga kwa inu. Mawu anu akuti: "Pakuti simudzasiya moyo wanga ku Hade, Kapena kulola kuti Woyera wanu aone chivundi." M'dzina la Yesu. Ameni.