Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


104 Mau a M'Baibulo Okhudza Kudzoza Manja

104 Mau a M'Baibulo Okhudza Kudzoza Manja

Mawu a Mulungu amatiphunzitsa mu 1 Timoteo 5:22 kuti tisamafulumire kuyika manja pa wina aliyense, kapena kutenga nawo mbali mu machimo a ena. Tiyenera kudzisunga oyera. Kuyika manja sikuyenera kuchitika chifukwa cha kutengeka maganizo kapena chifundo, koma chiyenera kuchitika motsogoleredwa ndi Mzimu Woyera. Choncho, tiyenera kuchita izi moganizira bwino kwambiri kuti moyo wa munthuyo udalitsidwe.

Kuyika manja kumachitika popereka madalitso, mphamvu zauzimu, kapena pochiza. M’Chikhristu, ndi chizindikiro chosonyeza kupereka Mzimu Woyera ndi kugwirizana ndi Mulungu. Timaona kuyika manja m’mavesi ambiri a m’Baibulo. Mwachitsanzo, m’Chipangano Chakale, Mose anayika manja pa Yoswa asanatsogolere Aisraeli kulowa m’dziko lolonjezedwa. M’Chipangano Chatsopano, Yesu nayenso anaika manja pochiza odwala ndi kutulutsa ziwanda.

Komabe, nthawi zonse tiyenera kukumbukira kuti mphamvu yeniyeni imachokera kwa Mulungu, ndipo kuyika manja ndi njira imodzi yokha imene tingagwiritsire ntchito kukhala chida cha Mulungu pa moyo wa wina. Choncho, n’kofunika kuti amene akuyika manja adzipereke kwa Mulungu ngati nsembe yolandirika, kuti agwiritsidwe ntchito ngati chida cholemekezeka m’manja mwake.




1 Timoteyo 4:14

Usanyalapse mphatsoyo ili mwa iwe, yopatsidwa kwa iwe mwa chinenero, pamodzi ndi kuika kwa manja a akulu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 5:22

Usafulumira kuika manja pa munthu aliyense, kapena usayanjana nazo zoipa za eni; udzisunge wekha woyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 19:6

Ndipo pamene Paulo anaika manja ake pa iwo, Mzimu Woyera anadza pa iwo; ndipo analankhula ndi malilime, nanenera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 4:40

Ndipo pakulowa dzuwa anthu onse amene anali nao odwala ndi nthenda za mitundumitundu, anadza nao kwa Iye; ndipo Iye anaika manja ake pa munthu aliyense wa iwo, nawachiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 10:16

Ndipo Iye anatiyangata, natidalitsa, ndi kuika manja ake pa ito.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 8:17

Pamenepo anaika manja pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:17

Ndipo pamene ndinamuona Iye, ndinagwa pa mapazi ake ngati wakufa; ndipo anaika dzanja lake lamanja pa ine, nati, Usaope, Ine ndine Woyamba ndi Wotsiriza,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 6:2

a chiphunzitso cha ubatizo, a kuika manja, a kuuka kwa akufa, ndi a chiweruziro chosatha.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 1:4

Ndipo aike dzanja lake pamutu pa nsembe yopsereza; ndipo idzalandiridwa m'malo mwake, imtetezere.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 27:18-23

Ndipo Yehova anati kwa Mose, Utenge Yoswa mwana wa Nuni, ndiye munthu mwa iye muli mzimu, nuike dzanja lako pa iye; numuimike pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse; numlangize pamaso pao. Ndipo anaima pamaso pa Mose, ndi pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa akalonga; ndi khamu lonse, pakhomo pa chihema chokomanako, ndi kuti, Ndipo umuikirepo ulemerero wako, kuti khamu lonse la ana a Israele ammvere. Ndipo aime pamaso pa Eleazara wansembe, amene amfunsire monga mwa chiweruzo cha Urimu pamaso pa Yehova; ponena iye azituluka, ndi ponena iye azilowa, ndi iye ndi ana onse a Israele pamodzi naye, ndiwo khamu lonse. Ndipo Mose anachita monga Yehova adamuuza; natenga Yoswa namuimitsa pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse; namuikira manja ake, namlangiza monga Yehova adanena ndi dzanja la Mose.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 8:10

nubwere nao Alevi pamaso pa Yehova; ndi ana a Israele aike manja ao pa Alevi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:13-15

Pamenepo anadza nato tiana kwa Iye, kuti Iye aike manja ake pa ito, ndi kupemphera: koma ophunzirawo anawadzudzula. Koma Yesu anati, Tilekeni tiana, musatikanize kudza kwa Ine: chifukwa Ufumu wa Kumwamba uli wa totere. Ndipo Iye anaika manja ake pa ito, nachokapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Deuteronomo 34:9

Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anadzala ndi mzimu wanzeru; popeza Mose adamuikira manja ake; ndi ana a Israele anamvera iye, nachita monga Yehova adauza Mose.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 27:18

Ndipo Yehova anati kwa Mose, Utenge Yoswa mwana wa Nuni, ndiye munthu mwa iye muli mzimu, nuike dzanja lako pa iye;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 1:6

Chifukwa chake ndikukumbutsa iwe ukoleze mphatso ya Mulungu, ili mwa iwe mwa kuika kwa manja anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 6:6

amenewo anawaika pamaso pa atumwi; ndipo m'mene adapemphera, anaika manja pa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 28:8

Ndipo kunatero kuti atate wake wa Publioyo anagona wodwala nthenda ya malungo ndi kamwazi. Kwa iyeyu Paulo analowa, napemphera, naika manja pa iye, namchiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 48:14

Ndipo Israele anatambalitsa dzanja lake lamanja, naliika pamutu wa Efuremu, amene ndiye wamng'ono, ndi dzanja lake lamanzere pamutu wa Manase, anapingasitsa manja ake dala; chifukwa Manase anali woyamba.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 19:15

Ndipo Iye anaika manja ake pa ito, nachokapo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 13:3

Pamenepo, m'mene adasala chakudya ndi kupemphera ndi kuika manja pa iwo, anawatumiza amuke.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 6:5

Ndipo kumeneko sanakhoze Iye kuchita zamphamvu konse, koma kuti anaika manja ake pa anthu odwala owerengeka, nawachiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 16:18

adzatola njoka, ndipo ngakhale akamwa kanthu kakufa nako, sikadzawapweteka; adzaika manja ao pa odwala, ndipo adzachira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 13:13

Ndipo anaika manja ake pa iye; ndipo pomwepo anaongoledwa, nalemekeza Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 9:17

Ndipo anachoka Ananiya, nalowa m'nyumbayo; ndipo anaika manja ake pa iye, nati, Saulo, mbale, Ambuye wandituma ine, ndiye Yesu amene anakuonekerani panjira wadzerayo, kuti upenyenso, ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 9:18

M'mene Iye analikulankhula nao zinthu zimenezo, onani, anadza munthu mkulu, namgwadira Iye, nanena, Wamwalira tsopanoli mwana wanga wamkazi, komatu mudze muike dzanja lanu pa iye, ndipo adzakhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 14:3

Chifukwa chake anakhala nthawi yaikulu nanenetsa zolimba mtima mwa Ambuye, amene anachitira umboni mau a chisomo chake, napatsa zizindikiro ndi zozizwa kuti zichitidwe ndi manja ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 29:10

Ndipo ubwere nayo ng'ombe yamphongo patsogolo pa chihema chokomanako; ndipo Aroni ndi ana ake aamuna aike manja ao pamutu pa ng'ombe yamphongoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 4:4

Ndipo adze nayo ng'ombeyo ku khomo la chihema chokomanako pamaso pa Yehova; naike dzanja lake pamutu pa ng'ombeyo, naiphe ng'ombeyo pamaso pa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 5:23

nanena, kuti, Kamwana kanga kabuthu kalinkutsirizika; ndikupemphani Inu mufikeko, muike manja anu pa iko, kuti kapulumuke, ndi kukhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 8:3

Ndipo Yesu anatambalitsa dzanja lake, namkhudza iye, nati, Ndifuna; takonzedwa. Ndipo pomwepo khate lake linachoka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 8:23-25

Ndipo anamgwira dzanja munthu wakhunguyo, natulukira naye kunja kwa mudzi; ndipo atamthira malovu m'maso mwake, naika manja pa iye, anamfunsa, Uona kanthu kodi? Ndipo anakweza maso, nanena, Ndiona anthu; pakuti ndiwapenya ayendayenda ngati mitengo. Pamenepo anaikanso manja m'maso mwake; ndipo anapenyetsa, nachiritsidwa, naona zonse mbee.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 6:19

ndi khamu lonse lija linafuna kumkhudza Iye; chifukwa munatuluka mphamvu mwa Iye, nkuchiritsa onsewa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 7:32-35

Ndipo anadza naye kwa Iye munthu wogontha, ndi wachibwibwi; ndipo anampempha Iye kuti aike dzanja pa iye. Ndipo anampatula pa khamu la anthu pa yekha, nalonga zala zake m'makutu mwake, nalavula malovu, nakhudza lilime lake: nagadamira kumwamba, nausa moyo, nanena naye, Efata, ndiko, Tatseguka. Ndipo makutu ake anatseguka, ndi chomangira lilime lake chinamasulidwa, ndipo analankhula chilunjikire.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 8:18-19

Koma pakuona Simoni kuti mwa kuika manja a atumwi anapatsidwa Mzimu Woyera, anawatengera ndalama, nanena, Ndipatseni inenso ulamuliro umene, kuti aliyense amene ndikaika manja pa iye, alandire Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Genesis 48:14-15

Ndipo Israele anatambalitsa dzanja lake lamanja, naliika pamutu wa Efuremu, amene ndiye wamng'ono, ndi dzanja lake lamanzere pamutu wa Manase, anapingasitsa manja ake dala; chifukwa Manase anali woyamba. Ndipo anadalitsa Yosefe, nati, Mulungu, pamaso pake anayenda makolo anga Abrahamu ndi Isaki, Mulungu amene anandidyetsa ine nthawi zonse za moyo wanga kufikira lero,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:1

Ndipo pamene Iye anadziitanira ophunzira ake khumi ndi awiri, anapatsa iwo mphamvu pa mizimu yoipa, yakuitulutsa, ndi yakuchiza nthenda iliyonse ndi zofooka zonse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 9:1

Ndipo Iye anaitana pamodzi khumi ndi awiriwo nawapatsa mphamvu ndi ulamuliro pa ziwanda zonse, ndi zakuchiritsa nthenda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:38

Koma Petro anati kwa iwo, Lapani, batizidwani yense wa inu m'dzina la Yesu Khristu kuloza ku chikhululukiro cha machimo anu; ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 4:30

m'mene mutambasula dzanja lanu kukachiritsa; ndi kuti zizindikiro ndi zozizwa zichitidwe mwa dzina la Mwana wanu wopatulika Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 5:12

Ndipo mwa manja a atumwi zizindikiro ndi zozizwa zambiri zinachitidwa pa anthu; ndipo anali onse ndi mtima umodzi m'khonde la Solomoni.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 6:8

Ndipo Stefano, wodzala ndi chisomo ndi mphamvu, anachita zozizwa ndi zizindikiro zazikulu mwa anthu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 11:21

Ndipo dzanja la Ambuye linali nao; ndi unyinji wakukhulupirira unatembenukira kwa Ambuye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 19:11

Ndipo Mulungu anachita zamphamvu za pazokha ndi manja a Paulo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 28:9

Ndipo patachitika ichi, enanso a m'chisumbu, okhala nazo nthenda, anadza, nachiritsidwa;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 12:13

Pomwepo ananena Iye kwa munthuyo, Tansa dzanja lako. Ndipo iye analitansa, ndipo linabwezedwa lamoyo longa linzake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 14:14

Ndipo Iye anatuluka, naona khamu lalikulu la anthu, nachitira iwo chifundo, nachiritsa akudwala ao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 20:34

Ndipo Yesu anagwidwa ndi chifundo, nakhudza maso ao; ndipo pomwepo anapenyanso, namtsata Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 1:41

Ndipo Yesu anagwidwa chifundo, natansa dzanja namkhudza iye, nanena naye, Ndifuna; khala wokonzedwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 5:13

Ndipo Iye anatambalitsa dzanja lake, namkhudza, nanena, Ndifuna, takonzeka. Ndipo pomwepo khate linachoka kwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 9:6-7

Pamene ananena izi, analavula pansi, nakanda thope ndi malovuwo, napaka thopelo m'maso, nati kwa iye, Muka, kasambe m'thamanda la Siloamu (ndilo losandulika, Wotumidwa). Pamenepo anachoka, nasamba, nabwera alikuona.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 3:7

Ndipo anamgwira iye kudzanja lake lamanja, namnyamutsa; ndipo pomwepo mapazi ake ndi mfundo za kumapazi zinalimbikitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 5:15-16

kotero kuti ananyamulanso natuluka nao odwala kumakwalala, nawaika pamakama ndi pamphasa, kuti, popita Petro, ngakhale chithunzi chake chigwere wina wa iwo. Komanso unasonkhana pamodzi unyinji wa anthu ochokera kumidzi yozungulira Yerusalemu, alikutenga odwala, ndi ovutika ndi mizimu yonyansa; ndipo anachiritsidwa onsewa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Eksodo 40:15

nuwadzoze, monga unadzoza atate wao, kuti andichitire ntchito ya nsembe; ndi kudzozedwa kwao kuwakhalire unsembe wosatha mwa mibadwo yao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Levitiko 8:12

Ndipo anatsanulirako mafuta odzoza pamutu pa Aroni, namdzoza kumpatula.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 19:19

Tsono anachokako, napeza Elisa mwana wa Safati alikukoketsa chikhasu ng'ombe ziwiriziwiri magoli khumi ndi awiri, iye yekha anakhala pa goli lakhumi ndi chiwiri; ndipo Eliya ananka kunali iyeyo, naponya chofunda chake pa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 58:11

ndipo Yehova adzakutsogolera posalekai, ndi kukhutitsa moyo wako m'chilala, ndi kulimbitsa mafupa ako; ndipo udzafanana ndi munda wothirira madzi, ndi kasupe wamadzi amene madzi ake saphwa konse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 10:38

za Yesu wa ku Nazarete, kuti Mulungu anamdzoza Iye ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu; amene anapitapita nachita zabwino, nachiritsa onse osautsidwa ndi mdierekezi, pakuti Mulungu anali pamodzi ndi Iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 4:24

Ndipo mbiri yake inabuka ku Siriya konse: ndipo anatengera kwa Iye onse akudwala, ogwidwa ndi nthenda ndi mazunzo a mitundumitundu, ndi ogwidwa ndi ziwanda, ndi akhunyu, ndi amanjenje; ndipo Iye anawachiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 15:30-31

Ndipo makamu ambiri a anthu anadza kwa Iye, ali nao opunduka miyendo, akhungu, osalankhula, opunduka ziwalo, ndi ena ambiri, nawakhazika pansi pa mapazi ake: ndipo Iye anawachiritsa; kotero kuti khamulo linazizwa, pakupenya osalankhula nalankhula, opunduka ziwalo nachira, ndi opunduka miyendo nayenda, ndi akhungu napenya, ndipo iwo analemekeza Mulungu wa Israele.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 21:14

Ndipo anadza kwa Iye ku Kachisiko akhungu ndi opunduka miyendo, nachiritsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 7:21-22

Nthawi yomweyo Iye anachiritsa anthu ambiri nthenda zao, ndi zovuta, ndi ziwanda; napenyetsanso anthu akhungu ambiri. Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Mukani, muuze Yohane zimene mwaziona, nimwazimva; anthu akhungu alandira kuona kwao, opunduka miyendo ayenda, akhate akonzedwa, ogontha akumva, akufa aukitsidwa, kwa aumphawi ulalikidwa Uthenga Wabwino.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 9:6

Ndipo iwo anatuluka, napita m'midzi yonse, ndi kulalikira Uthenga Wabwino, ndi kuchiritsa ponse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 10:9

ndipo chiritsani odwala ali momwemo nimunene nao, Ufumu wa Mulungu wayandikira kwa inu. Koma kumudzi uliwonse mukalowako,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:12

Indetu, indetu, ndinena kwa inu, Wokhulupirira Ine, ntchito zimene ndichita Ine adzazichitanso iyeyu; ndipo adzachita zoposa izi; chifukwa ndipita Ine kwa Atate.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 17:18

Monga momwe munandituma Ine kudziko lapansi, Inenso ndinatuma iwo kudziko lapansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 1:8

Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ndi mu Yudeya monse, ndi mu Samariya, ndi kufikira malekezero ake a dziko.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:4

Ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nayamba kulankhula ndi malilime ena, monga Mzimu anawalankhulitsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 9:12

ndipo anaona mwamuna dzina lake Ananiya, alikulowa, namuika manja, kuti apenyenso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 19:12

kotero kuti anamuka nazo kwa odwala nsalu zopukutira ndi za pantchito, zochokera pathupi pake, ndipo nthenda zinawachokera, ndi ziwanda zinatuluka.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 15:19

mu mphamvu ya zizindikiro ndi zozizwitsa, mu mphamvu ya Mzimu Woyera; kotero kuti ine kuyambira ku Yerusalemu ndi kuzungulirako kufikira ku Iliriko, ndinakwanitsa Uthenga Wabwino wa Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 12:9

kwa wina chikhulupiriro, mwa Mzimu yemweyo; ndi kwa wina mphatso za machiritso, mwa Mzimu mmodziyo;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 12:12

Zizindikirotu za mtumwi zinachitika pakati pa inu, m'chipiriro chonse, ndi zizindikiro, ndi zozizwa, ndi zamphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 3:5

Ndipo iye amene akuonjezerani inu Mzimuyo, nachita zimphamvu mwa inu, atero kodi ndi ntchito za lamulo, kapena ndi kumva kwa chikhulupiriro?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 1:17-19

kuti Mulungu wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa ulemerero, akupatseni inu mzimu wa nzeru, ndi wa vumbulutso kuti mukamzindikire Iye; ndiko kunena kuti maso a mitima yanu awalitsike, kuti mukadziwe inu chiyembekezo cha kuitana kwake nchiyani; chiyaninso chuma cha ulemerero wa cholowa chake mwa oyera mtima, ndi chiyani ukulu woposa wa mphamvu yake ya kwa ife okhulupirira, monga mwa machitidwe a mphamvu yake yolimba,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 3:20

Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 4:13

Ndikhoza zonse mwa Iye wondipatsa mphamvuyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 1:5

kuti Uthenga Wabwino wathu sunadze kwa inu m'mau mokha, komatunso mumphamvu, ndi mwa Mzimu Woyera, ndi m'kuchuluka kwakukulu; monga mudziwa tinakhala onga otani mwa inu chifukwa cha inu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 1:7

Pakuti Mulungu sanatipatse mzimu wa mantha; komatu wa mphamvu ndi chikondi ndi chidziletso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 2:4

pochita umboni pamodzi nao Mulungunso ndi zizindikiro, ndi zozizwitsa ndi mphamvu za mitundumitundu ndi zogawira za Mzimu Woyera, monga mwa chifuniro chake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 2:24

amene anasenza machimo athu mwini yekha m'thupi mwake pamtanda, kuti ife, titafa kumachimo, tikakhale ndi moyo kutsata chilungamo; ameneyo mikwingwirima yake munachiritsidwa nayo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Marko 6:13

Ndipo anatulutsa ziwanda zambiri, nadzoza mafuta anthu ambiri akudwala, nawachiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:7

Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo chidzatsegulidwa kwa inu;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 11:13

Potero, ngati inu, okhala oipa, mudziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, koposa kotani nanga Atate wanu wa Kumwamba adzapatsa Mzimu Woyera kwa iwo akumpempha Iye?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yohane 14:13-14

Ndipo chimene chilichonse mukafunse m'dzina langa, ndidzachichita, kuti Atate akalemekezedwe mwa Mwana. Ngati mudzapempha kanthu m'dzina langa, ndidzachita.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 3:6

Koma Petro anati, Siliva ndi golide ndilibe; koma chimene ndili nacho, ichi ndikupatsa, M'dzina la Yesu Khristu Mnazarayo, yenda.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 5:16

Komanso unasonkhana pamodzi unyinji wa anthu ochokera kumidzi yozungulira Yerusalemu, alikutenga odwala, ndi ovutika ndi mizimu yonyansa; ndipo anachiritsidwa onsewa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 9:40-41

Koma Petro anawatulutsa onse, nagwada pansi, napemphera; ndipo potembenukira kumtembo anati, Tabita, uka. Ndipo anatsegula maso ake; ndipo pakuona Petro, anakhala tsonga. Ndipo Petro anamgwira dzanja, namnyamutsa; ndipo m'mene adaitana oyera mtima ndi amasiye, anampereka iye wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 2:4-5

Ndipo mau anga ndi kulalikira kwanga sanakhale ndi mau okopa a nzeru, koma m'chionetso cha Mzimu ndi cha mphamvu; kuti chikhulupiriro chanu chisakhale m'nzeru ya anthu, koma mu mphamvu ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Akorinto 1:21-22

Koma Iye wakutikhazika pamodzi ndi inu kwa Khristu, natidzoza ife, ndiye Mulungu; amenenso anatisindikiza chizindikiro, natipatsa chikole cha Mzimu mu mitima yathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Agalatiya 5:22-23

Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro, chifatso, chiletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 5:18

Ndipo musaledzere naye vinyo, m'mene muli chitayiko; komatu mudzale naye Mzimu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Afilipi 2:13

pakuti wakuchita mwa inu kufuna ndi kuchita komwe, chifukwa cha kukoma mtima kwake, ndiye Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Akolose 1:29

kuchita ichi ndidzivutitsa ndi kuyesetsa monga mwa machitidwe ake akuchita mwa ine ndi mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Atesalonika 2:13

Koma tiyenera ife tiziyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu, abale okondedwa ndi Ambuye, kuti Mulungu anakusankhani inu kuyambira pachiyambi, mulandire chipulumutso mwa chiyeretso cha Mzimu ndi chikhulupiriro cha choonadi;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Timoteyo 6:12

Limba nayo nkhondo yabwino ya chikhulupiriro, gwira moyo wosatha, umene adakuitanira, ndipo wavomereza chivomerezo chabwino pamaso pa mboni zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Timoteyo 4:5

Koma iwe, khala maso m'zonse, imva zowawa, chita ntchito ya mlaliki wa Uthenga Wabwino, kwaniritsa utumiki wako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Tito 1:5

Chifukwa cha ichi ndinakusiya iwe mu Krete, kuti ukalongosole zosowa, nukaike akulu m'midzi yonse, monga ndinakulamulira;

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ahebri 10:24-25

ndipo tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino, osaleka kusonkhana kwathu pamodzi, monga amachita ena, komatu tidandaulirane, ndiko koposa monga momwe muona tsiku lilikuyandika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yakobo 5:14-15

Pali wina kodi adwala mwa inu? Adziitanire akulu a Mpingo, ndipo apemphere pa iye, atamdzoza ndi mafuta m'dzina la Ambuye: ndipo pemphero la chikhulupiriro lidzapulumutsa wodwalayo, ndipo Ambuye adzamuukitsa; ndipo ngati adachita machimo adzakhululukidwa kwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Petro 4:10-11

monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo okoma a chisomo cha mitundumitundu cha Mulungu; akalankhula wina, alankhule ngati manenedwe a Mulungu; wina akatumikira, achite ngati mu mphamvu imene Mulungu ampatsa, kuti m'zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Khristu, amene ali nao ulemerero ndi mphamvu kunthawi za nthawi. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Yohane 3:22

ndipo chimene chilichonse tipempha, tilandira kwa Iye, chifukwa tisunga malamulo ake, ndipo tichita zomkondweretsa pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
3 Yohane 1:2

Wokondedwa, ndipemphera kuti pa zonse ulemere, nukhale bwino, monga mzimu wako ulemera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani

Pemphero kwa Mulungu

Wamkulu ndi wodabwitsa Mulungu wanga, woyenera ulemerero ndi kutamandidwa konse. Zikomo chifukwa cha kukoma mtima kwanu ndi chikondi chimene mukusonyeza pa moyo wanga. Zikomo chifukwa chondilimbitsa ndi kukhala thandizo langa nthawi zonse. Chisomo chanu ndi kukoma mtima kwanu kwakhala kwabwino kwa ine. Simundisiya kapena kunditaya; nthawi zonse mumakhalapo kuti mundithandize, kundilimbitsa, kundiphunzitsa, ndi kundilanga. Pa nthawi ino, ndikupemphani kuti mundithandize kukhala wolimba pamavuto, kuti palibe chilichonse chomwe chingandichotse pamaziko a mawu amene mwandipatsa. Ndithandizeni kuti ndisanyalanyaze mphatso imene munapereka mwa ine pamene anandiika manja. Ndikufuna kukhala ndi moyo woyaka ndi moto wa Mzimu wanu Woyera, ndi kuti njala yosatha ya kukhala nanu ikhale mkati mwanga. Mundidzaze tsiku lililonse ndi inu, kuti ndikhale ndi moyo wokulemekezani ndi kuchita chifuniro chanu. M'dzina la Yesu, Ameni.
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa