Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

58 Mau a m'Baibulo Okhudza Mzimu

Mulungu, m’chifundo Chake chopanda malire, anandipatsa moyo kuti ndikhale paubwenzi wolimba ndi Iye. Mawu a Mulungu amandiphunzitsa kuti moyo ndi mpweya wa Mulungu ndipo ndi mbali ya umunthu wanga, ndipo ndi chizindikiro choyamba cha munthu wamoyo.

M’buku la Genesis 2:7 limati, “Ndipo Yehova Mulungu anaumba munthu ndi dothi lapansi, nauzira mpweya wa moyo m’mphuno mwake; ndipo munthuyo anakhala wamoyo.” Choncho, ine ndikuyitanidwa kukhala pamaso pa Mulungu kuti ndidzaze ndi mtendere ndi chimwemwe.

Moyo wanga unachokera ku mphamvu ya Mzimu wa Mulungu (Genesis 2:7). Moyo ndi wauzimu chifukwa unachokera kwa Mulungu, komanso ndi wachibadwidwe chifukwa umaonekera m’thupi langa. Ndikofunika kuti ndisunge moyo wanga wolumikizana ndi Mzimu wa Mulungu, wopanda chodetsa chilichonse.

Ndiyenera kukhala m’chiyero kuti tsiku lina ndikadzasiya dziko lapansi, moyo wanga udzakhala ndi moyo wosatha Kumwamba pamodzi ndi Ambuye Yesu. Mulungu safuna kuti moyo wanga utaike. Ndiyenera kuyenda m’zipatso za Mzimu, osati kukhutiritsa zilakolako za thupi langa, kuti ndikapeze chipulumutso ndikakhale Kumwamba pamodzi ndi Khristu.


Marko 8:36

Nanga ndiye kuti munthu wapindulanji atapata zonse za pansi pano, iyeyo nkutaya moyo wake?

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 5:20

dziŵani kuti amene adzabweza munthu wochimwa ku njira yake yosokera, adzapulumutsa moyo wa munthuyo ku imfa, ndipo chifukwa cha iye machimo ochuluka adzakhululukidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 107:9

Chauta amapha ludzu la munthu womva ludzu, amamudyetsa zinthu zabwino munthu womva njala.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 94:19

Pamene nkhaŵa zikundichulukira, Inu mumasangalatsa mtima wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:2

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, ndipo usaiŵale zabwino zake zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 130:5

Ndimayembekeza chithandizo cha Chauta, ndimayembekeza ndi mtima wonse, ndipo ndimakhulupirira mau ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:1

Mtima wanga umakhala chete kuyembekezera Mulungu yekha, pakuti chipulumutso changa chimafumira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:7

Mau a Chauta ngangwiro, amapatsa munthu moyo watsopano. Umboni wa Chauta ndi wokhulupirika, umaŵapatsa nzeru amene alibe.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:28

Musamaŵaopa amene amapha thupi, koma mzimu sangathe kuupha. Makamaka muziwopa amene angathe kuwononga thupi ndi mzimu womwe m'Gehena.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:5

Mtima wanga umakhala chete kuyembekezera Mulungu yekha, pakuti chikhulupiriro changa nchofumira kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 22:37

Yesu adamuyankha kuti, “Uzikonda Chauta, Mulungu wako, ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:7

Iwe mtima wanga, bwerera ku malo ako opumulira, chifukwa Chauta wakuchitira zokoma.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:3

Pa tsiku limene ndidakuitanani, Inu mudandiyankha, mumandilimbitsa mtima ndi mphamvu zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 142:7

Tulutseni m'ndende kuti ndizitamanda dzina lanu. Anthu anu adzandizungulira, chifukwa Inu mwandichitira zabwino zambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:1-3

Chauta ndiye mbusa wanga, sindidzasoŵa kanthu.

Amandigoneka pa busa lamsipu. Amanditsogolera ku madzi odikha kokapumulirako.

Amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera m'njira za chilungamo malinga ndi ulemerero wa dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 71:23

Pakamwa panga padzafuula ndi chimwemwe, pamene ndikukuimbirani nyimbo zotamanda. Nawonso mtima wanga umene mwauwombola, udzaimba moyamika.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 16:26

Nanga ndiye kuti munthu angapindulenji atapata zonse zapansipano, iyeyo nkutaya moyo wake? Munthu angalipire chiyani choti aombolere moyo wake?

Mutu    |  Mabaibulo
3 Yohane 1:2

Wokondedwa, ndimapemphera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndipo kuti moyo wako wathupi ukhale wolimba, monga momwe uliri moyo wako wauzimu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 31:25

Ndidzatsitsimutsa anthu ofooka, ndipo anthu anjala ndidzaŵadyetsa chakudya nadzakhuta.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:11

Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika choncho m'kati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamtamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 63:1

Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, ndimakufunafunani. Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka Inu ngati dziko louma, loguga ndi lopanda madzi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 54:4

Komatu, Mulungu ndiye amandithandiza, Ambuye ndiwo amachirikiza moyo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 6:4

Bwerani, Inu Chauta, mudzandilanditse. Mundipulumutse chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:1

Tamanda Chauta, iwe mtima wanga, moyo wanga wonse umuyamike potchula dzina lake loyera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 23:3

Amatsitsimutsa moyo wanga. Amanditsogolera m'njira za chilungamo malinga ndi ulemerero wa dzina lake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 131:2

Koma ndautonthoza ndi kuukhalitsa chete mtima wanga, monga mwana amene mai wake amamtonthoza ndi bere. Momwemo mtima wanga uli phe m'kati mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 6:16

Mau a Chauta ndi aŵa, “Imani pa mphambano, ndipo mupenye. Mufunse kumene kuli njira zakale ndi kumene kuli njira yabwino. Tsono mutsate njira yabwinoyo, ndipo mudzakhala pa mtendere. Koma inuyo mudati, ‘Sitidzaitsata.’

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 18:4

Moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa mwana ndi wanga, wa bambo ndi wanganso. Munthu amene wachimwa, ndiye amene adzafe.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 8:36-37

Nanga ndiye kuti munthu wapindulanji atapata zonse za pansi pano, iyeyo nkutaya moyo wake?

Munthu angalipire chiyani choti aombolere moyo wake?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 42:1-2

Monga momwe mbaŵala imakhumbira mtsinje wamadzi, ndimo m'mene mtima wanga umakhumbira Inu Mulungu wanga.

Kunyoza kwa adani anga kumandipweteka ngati bala lofa nalo la m'thupi mwanga, akamandifunsa nthaŵi zonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”

Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika choncho m'kati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamtamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

Mtima wanga ukumva ludzu lofuna Mulungu, Mulungu wamoyo. Kodi ndidzafika liti pamaso pa Mulungu?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 62:1-2

Mtima wanga umakhala chete kuyembekezera Mulungu yekha, pakuti chipulumutso changa chimafumira kwa Iye.

Musakhulupirire kuti zachiwawa zingakuthandizeni. Musaganize kuti kuba kungakupindulitseni. Chuma chikachuluka musaikepo mtima.

Mulungu adalankhula kamodzi, ine ndaphunzirapo zinthu ziŵiri, china ndi chakuti mphamvu ndi zanu, Inu Mulungu,

chikondi chanu nchosasinthika, Inu Ambuye; china ndi chakuti Inu mumabwezera munthu molingana ndi ntchito zake.

Iye yekhayo ndiye thanthwe langa, chipulumutso changa, ndi linga langa. Sindidzagwedezeka konse.

Mutu    |  Mabaibulo
Genesis 2:7

Tsono Chauta adatenga dothi pa nthaka, ndipo adaumba munthu ndi dothilo. Adamuuzira mpweya wopatsa moyo m'mphuno zake, ndipo munthuyo adakhala wamoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 18:20

Munthu wochimwa ndiye amene adzafe, osati wina. Mwana sadzafera machimo a bambo wake, ndipo bambo sadzafera machimo a mwana wake. Munthu wabwino adzakolola zipatso za ubwino wake. Munthu woipa adzakolola zipatso za kuipa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:23

Mtima wako uziwulonda bwino, pakuti m'menemo ndimo muli magwero a moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 53:10

Komabe ndi Chauta yemwe amene adaafuna kuti amuzunze, ndipo adamsautsadi. Iye adapereka moyo wake kuti ukhale nsembe yokhululukira machimo. Choncho adzaona zidzukulu zake, adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Chauta chidzachitika mwa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 6:9

Zitatha izi, Mwanawankhosa uja adamatula chimatiro chachisanu. Ndipo ndidaona kunsi kwa guwa lansembe mizimu ya anthu amene adaphedwa chifukwa cha kulalika mau a Mulungu, ndiponso chifukwa chochitira mauwo umboni wamphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 1:9

Pakutero mukupata mphotho ya chikhulupiriro, ndiye kuti chipulumutso chanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:18

Chauta amakhala pafupi ndi anthu a mtima wosweka, amapulumutsa otaya mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Deuteronomo 4:29

Kumeneko inu mudzafunafuna Chauta, Mulungu wathu, ndipo ngati mudzamfunafuna ndi mtima wonse ndi moyo wanu wonse, mudzampeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 12:7

Pamenepo thupi lidzabwerera ku dothi monga m'mene lidaaliri, ndipo mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene adaupereka.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 12:20

Koma Mulungu adamuuza kuti, ‘Wopusawe! Usiku womwe uno akulanda moyo wako. Nanga zonse zimene wadzisungirazi zidzakhala za yani?’ ”

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:16

Mzimu Woyera mwiniwakeyo ndi amene amavomerezana ndi mitima yathu kutsimikiza kuti ndife ana a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 2:11

Okondedwa anga, popeza kuti ndinu alendo pansi pano, ndikukupemphani kuti musagonjere zilakolako zathupi zimene zimachita nkhondo ndi mzimu wanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:175

Lolani kuti ndikhale moyo, kuti ndizikutamandani, ndipo malangizo anu azindithandiza.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 11:28-30

“Bwerani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa, ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo.

Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wa mtima wodzichepetsa; mukatero mudzapeza mpumulo m'mitima mwanu.

“Kodi Inu ndinu uja ankati adzabwerayu, kapena tiziyembekezera wina?”

Pajatu goli limene ndimakoleka Ine nlosavuta, ndipo katundu amene ndimasenzetsa Ine ngwopepuka.”

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 139:14

Ndikukutamandani, Inu oopsa ndi odabwitsa. Ntchito zanu zonse nzodabwitsa. Mumandidziŵa bwino kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:21

Nchifukwa chake siyani chizoloŵezi chilichonse chonyansa, ndiponso kuipamtima kulikonse. Muŵalandire mofatsa mau amene Mulungu adabzala m'mitima mwanu, pakuti ndiwo angathe kukupulumutsani.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:12

Paja mau a Mulungu ndi amoyo ndi ogwira ntchito mwamphamvu. Ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konsekonse. Amabaya mpaka molumikizirana mwa moyo ndi mzimu, ndiponso molumikizirana mfundo ndi mafuta a m'mafupa. Amaweruza ngakhale zimene anthu amalingalira ndi kulakalaka m'mitima mwao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 121:7-8

Chauta adzakuteteza ku zoipa zonse, adzasamala moyo wako.

Chauta adzakusunga kulikonse kumene udzapita, kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 26:9

Mtima wanga wonse umalakalaka Inu usiku, mzimu wanga m'kati mwa ine umakufunafunani. Pamene muweruza dziko lapansi, anthu onse okhalamo amaphunzira chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:23

Mulungu mwini, amene amatipatsa mtendere, akusandutseni angwiro pa zonse. Akusungeni athunthu m'nzeru, mumtima ndi m'thupi, kuti mudzakhale opanda chilema pobwera Ambuye athu Yesu Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:2

Muzifunafuna za Kumwamba, osati zapansipano.

Mutu    |  Mabaibulo
Chivumbulutso 20:4

Pambuyo pake ndidaona mipando yachifumu, ndipo okhala pamipandopo adapatsidwa mphamvu zoweruzira milandu. Ndidaonanso mizimu ya anthu amene adaŵadula pakhosi chifukwa cha kuchitira Yesu umboni, ndiponso chifukwa cha kulalika mau a Mulungu. Iwowo sadapembedze nao chilombo chija kapena fano lake lija, ndipo adakana kulembedwa chizindikiro chija pa mphumi kapena pa dzanja. Adakhalanso ndi moyo nkumalamulira pamodzi ndi Khristu zaka chikwi chimodzi.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:1

Thupi limene timakhalamo pansi pano lili ngati msasa chabe. Koma tikudziŵa kuti msasawu ukadzapasuka, tidzakhala ndi nyumba ina imene Mulungu adatikonzera Kumwamba. Nyumbayo ndi yosamangidwa ndi manja a anthu, ndipo ndi yamuyaya.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:3

“Ngodala anthu amene ali osauka mumtima mwao, pakuti Ufumu wakumwamba ndi wao.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:16

Chimene ndikufuna kunena ndi ichi: Mulole Mzimu Woyera kuti azikutsogolerani. Mukatero, pamenepo simudzachita zimene khalidwe lanu lokonda zoipa limalakalaka.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:21-23

Kwa inetu moyo ndi Khristu amene, ndipo nayonso imfa ili ndi phindu.

Koma ngati kukhalabe moyo kungandipatse mwai woti ndigwire ntchito yoonetsa zipatso, sindidziŵa kaya ndingasankhe chiti.

Ndagwira njakata. Kwinaku ndikulakalaka kuti ndisiye moyo uno ndikakhale pamodzi ndi Khristu, pakuti chimenechi ndiye chondikomera koposa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 2:1

Kale inu munali akufa chifukwa cha zolakwa zanu ndi machimo anu.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye wanga Wamuyaya, Wamkulu, ndi Wamphamvu ndinu! Mzimu wanga ukutamandani ndi kukudalitsani, zikomo chifukwa chondikomera mtima ndi kupulumutsa moyo wanga ku manda. Ndikukupemphani mulandire thupi langa, mzimu wanga, ndi moyo wanga wonse, ndi kuti munditsanulire njala ndi ludzu la Mzimu Wanu Woyera, kuti tsiku lililonse moyo wanga usangalale ndi kukondwera pamaso panu. Zikomo chifukwa ndinu mlonda wanga ndi woteteza moyo wanga. Pakuti ndinu amene mumandigwira ndi dzanja lanu lamanja ndi kundiuza kuti, Usachite mantha. Mawu anu amati: “Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse.” Atate, ndikukupemphani muchotse mwa ine malingaliro oipa, ndi kuti nthawi zonse ndizilemekeza dzina lanu Loyera ndi kukhala ndi mtima woyamikira chifukwa cha kukoma mtima kwanu. Ambuye Yesu, ndikupempheraninso miyoyo ya anthu omwe ali m’ndende, omwe asokonezedwa ndi mdani, m’mavuto, ndi ena m’zisangalalo za dziko lino. Mawu anu amati: “Pakuti phindu lake n’chiyani munthu akapeza dziko lonse lapansi, koma ataya moyo wake?” Yesu wanga wabwino, masulani miyoyo yawo ku chinyengo cha mdani, ndikukupemphani mutsegule maso ndi makutu awo auzimu kuti amvetse kuti ndinu Ambuye ndi Mpulumutsi wa miyoyo yawo. M’dzina la Yesu. Ameni.