Biblia Todo Logo
Mavesi a Baibulo
- Zotsatsa -


65 Mau a Mulungu Okhudza Mphatso Yaulosi

65 Mau a Mulungu Okhudza Mphatso Yaulosi


1 Akorinto 12:10

Amapatsa wina mphamvu zochitira zozizwitsa, wina mphatso ya kulalika mau a Mulungu, wina nzeru za kusiyanitsa pakati pa zinthu zochokera kwa Mzimu Woyera ndi zochokera kwina. Amapatsa wina mphatso ya kulankhula zilankhulo zosadziŵika, ndipo amapatsa wina mphatso ya kutanthauzira zilankhulozo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:1

Muziyesetsa kukhala nacho chikondi, komanso muike mtima pa mphatso zimene Mzimu Woyera amapereka, makamaka mphatso ya kulankhula mau ochokera kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:3

Koma wolankhula mau ochokera kwa Mulungu, amalankhula ndi anthu, ndipo amaŵathandiza, amaŵalimbitsa mtima ndi kuŵasangalatsa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:4

Munthu wolankhula chilankhulo chosadziŵika, amangothandizidwa yekha, koma wolankhula mau ochokera kwa Mulungu, amathandiza mpingo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:5

Ndikadakonda kuti nonsenu mukhale nayo mphatso ya kulankhula zilankhulo zosadziŵika, koma makamaka ndikadakonda kuti nonsenu mukhale ndi mphatso ya kulankhula mau ochokera kwa Mulungu. Pakuti munthu wolankhula mau ochokera kwa Mulungu, ndiye wofunika kwambiri kuposa wolankhula zilankhulo zosadziŵika, ngati palibe munthu wotanthauzira zilankhulo, kuti mpingo upindulepo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:22

Motero kulankhula m'zilankhulo zosadziŵika, ndi chizindikiro kwa anthu osakhulupirira, osati kwa anthu okhulupirira. Koma kulankhula mau ochokera kwa Mulungu, ndi chizindikiro kwa anthu okhulupirira, osati kwa osakhulupirira.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:24-25

Koma ngati onse alankhula mau ochokera kwa Mulungu, ndipo munthu wosakhulupirira kapena wosadziŵa aloŵa, adzatsutsidwa ndi zonse zimene akumva. Mau onsewo adzamuloŵa mu mtima, ndipo zobisika za mumtima mwake zidzaonekera poyera. Pamenepo iye adzadzigwetsa choŵerama pansi ndi kupembedza Mulungu, ndipo adzavomereza kuti Mulungu ali pakati panudi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:29

Kunena za olankhula mau ochokera kwa Mulungu, aŵiri kapena atatu alankhule, ndipo ena onse aweruze zimene iwowo akunena.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:31

Nonsenu mungathe kulankhula mau ochokera kwa Mulungu malinga nkupatsana mpata, kuti onse aphunzire ndi kulimbikitsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:32

Anthu amene ali ndi mphatso ya kulankhula mau ochokera kwa Mulungu, adziŵe kuilamulira mphatsoyo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 14:39

Nchifukwa chake tsono, abale anga, ikani mtima pa kulankhula mau ochokera kwa Mulungu, ndipo musaletse anthu kulankhula zilankhulo zosadziŵika.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aefeso 4:11

Iyeyu ndiye amene “adapereka mphatso kwa anthu.” Mphatso zake zinali zakuti ena akhale atumwi, ena aneneri, ena alaliki, ena abusa ndi aphunzitsi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Aroma 12:6

Tili ndi mphatso zosiyanasiyana malinga ndi m'mene Mulungu adatigaŵira mwa kukoma mtima kwake. Ngati mphatso yathu nkulalika mau a Mulungu, tiigwiritse ntchito molingana ndi chikhulupiriro chathu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:17

“ ‘Mulungu akuti, Pa masiku otsiriza ndidzaika Mzimu wanga mwa anthu onse, ndipo ana anu aamuna ndi ana anu aakazi azidzalalika za Mulungu. Anyamata anu azidzaona zinthu m'masomphenya, ndipo nkhalamba zanu zizidzalota maloto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 2:18

Ndithu, pa masiku amenewo ndidzaika Mzimu wanga ngakhale mwa akapolo anga aamuna ndi aakazi, ndipo azidzalalika za Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 11:27-28

Masiku amenewo kudafika aneneri ena ku Antiokeya ochokera ku Yerusalemu. Mmodzi mwa iwo, dzina lake Agabu, adaimirira, ndipo ndi mphamvu za Mzimu Woyera adalosa kuti padzakhala njala yaikulu pa dziko lonse lapansi. Njalayo idabweradi pa nthaŵi ya Klaudio.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 13:1

Mu mpingo wa ku Antiokeya munali alaliki ndi aphunzitsi aŵa: Barnabasi, Simeoni (wotchedwa Wakuda), Lusio wa ku Kirene, Manaene (amene adaaleredwa pamodzi ndi bwanamkubwa Herode), ndiponso Saulo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 19:6

Pamene Paulo adaŵasanjika manja, Mzimu Woyera adadza pa iwo, ndipo adayamba kulankhula zilankhulo zosadziŵika, ndi kumalalika mau ochokera kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 3:7

Zoonadi, Ambuye Chauta sachita kanthu osadziŵitsa atumiki ao, aneneri, zimene akonzekera.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 1:9

Tsono Chauta adatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga. Ndipo adandiwuza kuti, “Tamvera, ndikuika mau anga m'kamwa mwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 23:28

Ngati mneneri walota maloto, afotokoze maloto akewo. Koma amene ali ndi mau anga, alalike mau angawo moona. Kodi mungu ungafanane ndi tirigu?” Akuterotu Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 2:7

Popeza kuti iwowo ngaupandu, kaya akamvera kaya akakana, udzaŵauze ndithu mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yoweli 2:28

“Patapita nthaŵi, tsiku lidzafika pamene ndidzatsitsa mzimu wanga pa mtundu uliwonse wa anthu. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzalosa. Nkhalamba zanu zidzalota maloto, ndipo achinyamata anu adzaona zinthu m'masomphenya.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mika 3:8

Koma ine Chauta wandidzaza ndi mphamvu, wandidzaza ndi mzimu wake. Wandidzaza ndi kulungama ndi kulimba mtima, kuti ndidzudzule a banja la Yakobe chifukwa cha zolakwa zao, kuti ndiwonetse Aisraele zoipa zao.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Atesalonika 5:20

Musanyoze mau olalikidwa m'dzina la Mulungu,

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Petro 1:21

Paja mau a aneneri sadadze konse ndi kufuna kwa munthu yekha, koma Mzimu Woyera adaŵalankhulitsa mau ochokera kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 1:3

Ngwodala munthu amene aŵerenga momveka mauŵa. Ngodalanso anthu amene amvera mau a m'buku limeneli loneneratu zam'tsogolo, ndi kutsata zimene zalembedwamo. Pakuti nthaŵi yoti zichitike zonsezi ili pafupi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 19:10

Apo ndidadzigwetsa ku mapazi ake kuti ndimpembedze. Koma iye adandiwuza kuti, “Zimenezo iyai. Ndine mtumiki chabe, ngati iwe wemwe, ndiponso ngati abale ako amene amachitira Yesu umboni. Iwe pembedza Mulungu.” Pajatu kuchitira Yesu umboni ndiye thima la uneneri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 28:9

Koma ngati mneneri alosa za mtendere, zimene walosazo zikachitikadi, pamenepo zidzadziŵika kuti Chauta adamtumadi.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Numeri 12:6

Chauta adati, “Imvani mau anga. Pakakhala mneneri pakati panupa, Ine Chauta ndimadziwonetsa kwa munthuyo m'masomphenya, ndimalankhula naye m'maloto.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 20:1

Nthaŵi imeneyo Hezekiya adaadwala, ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi, adapita kukamuwona, namuuza kuti, “Chauta akuti ukonze zonse bwino lomwe, poti ufa, suchira ai.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 3:20

Ndipo Aisraele onse, kuyambira ku Dani mpaka ku Beereseba, adadziŵa kuti Chauta adamsankha Samuele kuti akhale mneneri.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 6:8

Kenaka ndidamva mau a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani, ndani adzatipitire?” Apo ndidati “Ndilipo ineyo, tumeni.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 23:16

Chauta Wamphamvuzonse akuuza anthu kuti, “Musamvere zimene akunena aneneri, iwowo amakuloserani zonyenga. Zimene amakuuzani kuti akuziwona m'masomphenya ndi maganizo ao chabe, si zolankhula Chauta ai.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yesaya 30:10

Amauza oona zobisika kuti, ‘Musaonenso.’ Amauza aneneri kuti, ‘Musatiloserenso zoona. Mutiwuze zotikomera, mutilosere zam'mutu chabe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 22:14

Koma Mikaya adati, “Pali Chauta wamoyo, zimene Chautayo andiwuze, ndizo ndidzalankhule.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 1:6

Kodi mau anga ndi malamulo anga amene ndidauza atumiki anga aneneri, suja adamveka kwa makolo anu? Choncho iwo adalapa ndi kunena kuti, ‘Chauta Wamphamvuzonse watichitadi zomwe adaatsimikiza kuti adzatichita, potsata makhalidwe athu ndi ntchito zathu zoipa.’ ”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 7:15

“Chenjera nawoni aneneri onyenga. Amadza kwa inu ali ndi maonekedwe ofatsa ngati nkhosa, koma m'kati mwao ndi mimbulu yolusa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 24:24

Chifukwa kudzaoneka anthu onama omanena kuti ‘Ndine Khristu uja,’ kapena kuti, ‘Ndine mneneri.’ Anthuwo azidzachita ntchito zamphamvu ndiponso zinthu zozizwitsa, kuti ngati nkotheka asokeze ngakhale osankhidwa a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Luka 1:70

Izi ndi zomwe Iye adaaneneratu kalekale kudzera mwa aneneri ake oyera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 3:18

Koma Mulungu adaaneneratu mwa aneneri onse kuti Wodzozedwa wake wolonjezedwa uja adzamva zoŵaŵa, ndipo zidachitikadi momwemo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 17:13

Monsemo Chauta adatuma amithenga ndi aneneri ake ku Israele ndi ku Yuda, okalalika kuti, “Musinthe makhalidwe anu auchimo ndipo mumvere Malamulo anga amene ndidaŵapereka kwa makolo anu, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 14:14

Koma Chauta adandiyankha kuti, “Zakuti aneneriwo amalosa m'dzina langa, ili ndi bodza. Ine sindidaŵasankhe, sindidaŵatume kapena kulankhula nawo. Iwo amakuloserani zinthu zonama zimene akuti adaziwona m'masomphenya. Amaombeza zabodza, zimene amalankhula ndi zonyenga zopeka iwo eni ake.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 13:3

Ine Ambuye Chauta ndikunena kuti, Tsoka kwa aneneri opusa amene amachita kupeka zolosa zao, chonsecho sadaone chilichonse chochokera kwa Ine.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 23:21

Chauta adati, “Aneneri ameneŵa sindidaŵatume ndine, komabe ankathamanga uku ndi uku ndi mithenga yao. Sindidalankhule nawo, komabe ankalosa.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yeremiya 23:29

“Kodi suja mau anga amatentha ngati moto? Kodi suja mau anga ali ngati nyundo imene imaphwanya thanthwe?

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Mateyu 10:41

Munthu wolandira nthumwi ya Mulungu chifukwa choti ndi nthumwi, adzalandira mphotho ya nthumwi ya Mulungu. Wolandira munthu wolungama chifukwa choti ngwolungama, adzalandira mphotho ya munthu wolungama.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 22:18

Ine Yohane, ndikuchenjeza aliyense womva mau a m'buku lino oneneratu zam'tsogolo. Wina akadzaonjezerapo kanthu pa mau ameneŵa, Mulungu adzamuwonjezera miliri ija yalembedwa m'buku munoyi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Chivumbulutso 10:11

Pamenepo adandiwuza kuti, “Uyenera kulengezanso za mitundu yambiri ya anthu, za zilankhulo zosiyanasiyana, ndi za mafumu ambiri.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 18:22

Tsono Eliya adauza anthu aja kuti, “Ine ndatsala ndekha mwa aneneri a Chauta, koma aneneri a Baala alipo 450 pamodzi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mafumu 2:15

Pamene a m'gulu la aneneri amene ankakhala ku Yeriko adaona Elisayo akuwoloka, adati, “Mphamvu ndi nzeru za Eliya zaloŵa mwa Elisa.” Tsono adabwera kudzakumana naye, namgwadira Elisayo, nkuŵeramitsa mitu yao pansi.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Machitidwe a Atumwi 13:2

Tsiku lina pamene iwo adasonkhana kuti apembedze Ambuye ndi kuti asale zakudya, Mzimu Woyera adaŵauza kuti, “Mundipatulire Barnabasi ndi Saulo kuti akagwire ntchito imene ndaŵaitanira.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Amosi 7:15

Chauta adachita kukanditenga, kundileketsa ntchito yoŵeta nkhosa, nandiwuza kuti, ‘Pita, ukalalikire anthu anga, Aisraele.’

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Yona 3:4

Yona adaloŵa mumzindamo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi. Adayamba kulalika kuti, “Pakapita masiku makumi anai, Ninive aonongeka!”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 37:4

Apo adandiwuza kuti, “Alalikire mafupa ameneŵa, uŵauze mafupa oumawo kuti amve mau a Ine Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Akorinto 12:7

Mzimu Woyera amapatsa munthu aliyense mphatso yakutiyakuti yoti aigwiritse ntchito yopindulitsa anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zefaniya 3:17

Chauta, Mulungu wako, ali nawe pamodzi, ngati wankhondo wokuthandiza kugonjetsa adani. Adzasangalala ndi chimwemwe chifukwa cha iwe. Adzakubwezera m'chikondi chake. Adzakondwera nawe poimba nyimbo zachimwemwe.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Zekariya 8:9

“Zimene ndikunena Ine Chauta Wamphamvuzonse ndi izi: Inu masiku ano mukumva mau a aneneri amene ankalankhula pa nthaŵi yoyala maziko a Nyumba ya Chauta Wamphamvuzonse. Choncho limbani mtima, kuti Nyumbayi imangidwenso.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Hoseya 12:10

Ndidalankhula ndi aneneri. Ndine amene ndidaŵaonetsa zinthu zambiri ngati kutulo. Ndidalankhula m'mafanizo kudzera mwa iwo.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Ezekieli 13:9

Ndidzakantha aneneri onama amene amati adaona zakutizakuti ngati kutulo, amenenso kulosa kwao nkwabodza. Sadzakhala nao m'bwalo la aphungu la anthu anga. Sadzalembedwa m'kaundula wa nzika za Israele, ndipo sadzaloŵa m'dziko la Israele. Motero mudzadziŵa kuti Ine ndine Ambuye Chauta.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
2 Mbiri 20:20

Tsono anthuwo adadzuka m'mamaŵa nakaloŵa m'chipululu cha ku Tekowa. Pamene ankatuluka, Yehosafati adaima nati, “Tamverani inu anthu a ku Yuda ndi inu okhala mu Yerusalemu. Khulupirirani Chauta, Mulungu wanu, ndipo mudzalimbika, khulupirirani aneneri ake, ndipo mudzapambana.”

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Samueli 10:5-6

Pambuyo pake mufika ku phiri la Mulungu ku Gibea kumene kuli gulu lankhondo la Afilisti. Ndipo kumeneko, pamene mukuyandikira mzindawo, mukumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku kachisi ku phiri, akuimba zeze, ting'oma, chitoliro ndi pangwe, ndipo akulosa. Pamenepo mzimu wa Chauta ukuloŵa mwamphamvu, ndipo nawenso uyamba kulosa nao, usinthika ndi kukhala munthu wina.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
1 Mafumu 19:16

Yehu mwana wa Nimisi ukamdzoze kuti akhale mfumu ya ku Israele. Ndipo Elisa, mwana wa Safati wa ku Abele-Mehola, ukamdzoze kuti akhale mneneri woloŵa m'malo mwako.

Mutu    |  Mabaibulo Koperani
Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa