Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

48 Mau a m'Baibulo Okhudza Anthu Ogwidwa ndi Ziwanda

Mizimu yoipa ndi yamphamvu kwambiri ndipo imafuna kuti tichite zinthu zoyipa. Mizimu iyi siyingachite chilichonse popanda thupi la munthu, choncho imafuna kukhala mwa ife. Koma sangakukakamize; uyenera kuwalola kuti alowe mwa iwe. Amagwiritsa ntchito zomwe umawona, zomwe umamva, ndi zomwe umagwira kuti alowe m'moyo mwako.

Satana safuna zabwino zako. Mizimu yoipa imapangitsa anthu ochita zoyipa kukhala ndi moyo wodetsa. Baibulo limanena za anthu omwe anali ndi mizimu yoipa, ndipo izi zinawabweretsera mavuto ambiri m'thupi lawo. Yuda ndi chitsanzo chabwino cha munthu amene anapatutsidwa ndi kulola kuti choipa chimulamule.

Mulungu analola kuti Mfumu Sauli, atamuchimwira, azunzidwe ndi mzimu woyipa. Izi zinamupangitsa kukhala wachisoni nthawi zonse ndiponso kufuna kupha Davide (1 Samueli 18:10-11).

Nkhani yabwino ndi yakuti Yesu Khristu satisiya, ngakhale titakhala bwanji kapena ngakhale anthu ena atatisiya. Njira yokha yopezera ufulu weniweni ndiyo kuyandikira Yesu. Pamene Yesu ali m'moyo mwathu, ndiye kuti tili omasuka kotheratu. Choncho, samalira mtima wako ndipo pemphera kwa Yesu kuti alamulire moyo wako, kuti Mdyerekezi asapeze malo mwa iwe.


Mateyu 12:28-30

Koma ngati Ine ndimatulutsa mizimu yoipa ndi mphamvu za Mzimu wa Mulungu, ndiye kuti Mulungu wayamba kukhazikitsa ufumu wake pakati panu.

“Palibe munthu amene angathe kuloŵa m'nyumba ya munthu wamphamvu nkufunkha chuma chake, atapanda kuyamba wamumanga munthu wamphamvuyo. Atatero ndiye angafunkhe zam'nyumbamo.

Iye adati, “Kani simudaŵerenge zimene adaachita Davide, pamene iye ndi anzake adaazingwa nayo njala?

“Munthu wosavomerezana ndi Ine, ndiye kuti ndi wotsutsana nane. Ndipo wosandithandiza kusonkhanitsa, ndiye kuti ameneyo ndi womwaza.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 7:26

Maiyo anali mkunja, wa mtundu wa anthu a ku Siro-Fenisiya. Adapempha Yesu kuti akatulutse mzimu woipawo mwa mwana wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 1:32

Madzulo amenewo, dzuŵa litaloŵa, anthu adabwera kwa Yesu ndi anzao onse ovutika, ndi ogwidwa ndi mizimu yoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 6:12

Paja sitikulimbana ndi anthu chabetu ai. Tikulimbana ndi maufumu, aulamuliro ndi mphamvu za dziko lino lapansi lamdima, ndiponso ndi mizimu yoipa yamumlengalenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 2:19

Inu mumakhulupirira kuti Mulungu ndi mmodzi yekha. Ai chabwino, mumakhoza, komatu ndi mizimu yoipa yomwe imakhulupirira zimenezi, imachitanso kunjenjemera.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:1

Mzimu Woyera akunena momveka kuti pa masiku otsiriza anthu ena adzataya chikhulupiriro chao. Adzamvera mizimu yonyenga ndi zophunzitsa zochokera kwa mizimu yoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 3:11

Mizimu yoipa inkati ikamuwona, inkadzigwetsa pansi pafupi ndi Iye nkumafuula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 17:18

Atatero, Yesu adazazira mzimu woipawo, ndipo udatuluka mwa mnyamatayo. Pompo iye adachira.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 8:7

Pakuti mizimu yonyansa inkatuluka mwa anthu ambiri amene anali atagwidwa nayo, nimafuula kwambiri. Ndipo ambiri amene anali akufa ziwalo kapena opunduka, ankachira.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 5:1-20

Tsono Yesu ndi ophunzira ake adafika ku tsidya la Nyanja ya Galileya, ku dera la Agerasa.

Ndipo iye adadandaulira Yesu kwambiri kuti mizimuyo asaitulutsire kunja kwa dera limenelo.

Pafupi pomwepo, pachitunda poteropo, pankadya gulu lalikulu la nkhumba.

Tsono mizimu yoipa ija idapempha Yesu kuti, “Tipirikitsireni ku nkhumbazo, tiloleni tikaloŵe m'menemo.”

Yesu adailoladi. Iyo idatuluka nkukaloŵadi m'nkhumbazo. Pomwepo gulu lonselo lidaguduka kutsika chitunda chija mwaliŵiro, nkukadziponya m'nyanja, mpaka kufera m'madzimo. Zonse zidaalipo ngati zikwi ziŵiri.

Oŵeta nkhumbazo adathaŵa, nakasimbira anthu mu mzinda ndi ku midzi. Pamenepo anthu adatuluka kuti akaone zimene zidaachitikazo.

Atafika kumene kunali Yesuko, adaona munthu adaagwidwa ndi mizimu yoipa uja atakhala pansi, atavala, misala ija itatha, munthu woti adaloŵedwa ndi chigulu cha mizimu yoipa. Anthuwo adagwidwa ndi mantha.

Anzao amene adaaonerera zonse zikuchitika, adaŵasimbira zimene zidaamuchitikira munthu wamizimuyo ndiponso nkhumba zija.

Apo anthuwo adampempha Yesu kuti achoke ku dera laolo.

Pamene Yesu ankakaloŵa m'chombo, munthu amene adaagwidwa ndi mizimu yoipa uja adampempha kuti apite nao.

Koma Yesu adakana namuuza kuti, “Iyai, iwe pita kumudzi kwa anthu akwanu, ukaŵafotokozere zazikulu zimene Ambuye akuchitira mwa chifundo chao.”

Yesu atangotuluka m'chombo, munthu wina wogwidwa ndi mzimu woipa adadzakumana naye kuchokera ku manda.

Munthuyo adapitadi nakayamba kufalitsa ku dera lotchedwa Mizinda Khumi, zazikulu zimene Yesu adaamchitira. Atamva zimenezo anthu onse adazizwa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 10:17

Anthu 72 aja adabwerako ndi chimwemwe nati, “Ambuye, ngakhale mizimu yoipa yomwe imatigonjera tikamailamula m'dzina lanu.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 15:22

Mai wina wachikanani, wa ku madera amenewo, adadza kwa Yesu. Adafuula kuti, “Mundichitire chifundo, Inu Ambuye, Mwana wa Davide. Mwana wanga wamkazi ngwogwidwa koopsa ndi mzimu woipa.”

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 9:17-18

Mmodzi mwa anthuwo adayankha kuti, “Aphunzitsi, ine ndinabwera ndi mwana wanga wamwamuna kuti ndidzampereke kwa Inu, chifukwa adaloŵedwa ndi mzimu woipa womuletsa kulankhula.

Umati ukangomugwira, umamgwetsa pansi, mwanayo nkumangoti thovu tututu kukamwa, namakukuta mano, mpaka thupi gwagwagwa kuuma. Ndiye ndinapempha ophunzira anuŵa kuti autulutse, koma alephera.”

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 5:16

Kunkasonkhananso anthu ochuluka ochokera ku midzi yozungulira Yerusalemu. Anali atanyamula anthu odwala, ndiponso ena osautsidwa ndi mizimu yoŵaipitsa. Onsewo ankachiritsidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 8:28-34

Yesu atafika ku tsidya la nyanja, ku dera la Agadara, anthu aŵiri ogwidwa ndi mizimu yoipa adadzakumana naye kuchokera ku manda. Anali aukali kwambiri, kotero kuti panalibe munthu ndi mmodzi yemwe wotha kudzera njira imeneyo.

Mwadzidzidzi anthuwo adayamba kufuula kuti, “Kodi takuputani chiyani, Inu Mwana wa Mulungu? Kodi mwabwera kuno kudzatizunza nthaŵi isanakwane?”

Yesu adatambalitsa dzanja nkumukhudza, nati, “Chabwino, ndikufuna, chira!” Pomwepo khate lake lija lidatha, ndipo adachiradi.

Pafupi pomwepo pankadya gulu lalikulu la nkhumba.

Tsono mizimu yoipa ija idapempha Yesu kuti, “Mukatitulutsa, bwanji mutitume kuti tikaloŵe m'gulu la nkhumba zili apozo.”

Yesu adaiwuza kuti, “Chabwino, pitani!” Iyo idatuluka nkukaloŵadi m'nkhumbazo. Pomwepo gulu lonselo lidaguduka kutsika chitunda chija mwaliŵiro, nkukadziponya m'nyanja mpaka kufera m'madzimo.

Oŵeta nkhumbazo adathaŵa. Atakaloŵa mu mzinda, adakasimbira anthu zonse zimene zidachitika, ndiponso zimene zidaŵaonekera ogwidwa ndi mizimu yoipa aja.

Pamenepo anthu onse amumzindamo adatuluka kuti akakumane ndi Yesu. Tsono atampeza, adamupempha kuti achoke ku dera laolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 5:18

Pamene Yesu ankakaloŵa m'chombo, munthu amene adaagwidwa ndi mizimu yoipa uja adampempha kuti apite nao.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 8:26-39

Iwo adafika ku dziko la Ageregesa, limene lidapenyana ndi Galileya.

Pamene Yesu adafika pa mtunda, munthu wina wochokera ku mudzi wakomweko, adadzakumana naye. Munthuyo adaali ndi mizimu yoipa, ndipo kuyambira kale sankavalanso zovala. Sankakhala m'nyumba, koma ku manda.

Pamene iye adaona Yesu, adafuula nadzigwetsa ku mapazi ake, ndipo adanena mokweza mau kuti, “Kodi ndakuputani chiyani Inu Yesu, Mwana wa Mulungu Wopambanazonse? Ndakupembani, musandizunze.”

Adaatero chifukwa Yesu anali atalamula mzimu woipawo kuti utuluke mwa munthuyo. (Ndiye kuti kaŵirikaŵiri ukamugwira, anthu ankamumanga manja ndi maunyolo, nkumumanganso miyendo ndi zitsulo kuti amugwiritse bwino. Koma iyeyo ankazingomwetsula zomangirazo, ndipo mzimuwo unkamupirikitsira ku thengo.)

Yohana, mkazi wa Kuza, kapitao wa Herode; Suzana, ndiponso azimai ena ambiri amene ndi ndalama zao ankathandiza Yesu ndi ophunzira ake.

Tsono Yesu adamufunsa munthuyo kuti, “Dzina lako ndani?” Iye adayankha kuti, “Dzina langa ndine Chigulu,” chifukwa mizimu yoipa yochuluka inali itamuloŵa.

Kenaka mizimuyo idapempha Yesu kuti asailamule kuti ikaloŵe ku chiphompho chao.

Pafupi pomwepo, pachitunda poteropo, pankadya gulu lalikulu la nkhumba. Tsono mizimu yoipa ija idapempha Yesu kuti ailole ikaloŵe m'nkhumbazo. Yesu adailoladi.

Iyo idatuluka, nkukaloŵadi m'nkhumbazo. Pomwepo gulu lonselo lidaguduka kutsika chitunda chija mwaliŵiro, nkukadziponya m'nyanja, mpaka kufera m'madzimo.

Oŵeta nkhumbazo ataona zimenezi, adathaŵa, nakauza anthu ku mzinda ndi ku midzi.

Anthuwo adatuluka kuti akaone zimene zidaachitikazo. Atafika kumene kunali Yesuko, adapeza munthu amene adaamtulutsa mizimu yoipa uja, atakhala pansi ku mapazi a Yesu, atavala, misala ija itatha. Anthuwo adagwidwa ndi mantha.

Anzao amene adaaonerera zonse zikuchitika, adaŵasimbira m'mene munthu wamizimuyo adaamchiritsira.

Apo anthu onse a ku malo ozungulira Geregesa adapempha Yesu kuti achoke kumeneko, chifukwa iwo anali ndi mantha aakulu. Choncho Yesu adaloŵa m'chombo, nkumabwerera ku tsidya.

Munthu amene adaamtulutsa mizimu yoipa uja adapempha Yesu kuti apite nao. Koma Yesu adamubweza namuuza kuti,

“Iyai, iwe bwerera kwanu, ukafotokoze zazikulu zimene Mulungu wakuchitira.” Munthuyo adapitadi kwao nkumakalengeza mumzinda monse zazikulu zimene Yesu adaamchitira.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 5:2

Yesu atangotuluka m'chombo, munthu wina wogwidwa ndi mzimu woipa adadzakumana naye kuchokera ku manda.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 1:32-34

Madzulo amenewo, dzuŵa litaloŵa, anthu adabwera kwa Yesu ndi anzao onse ovutika, ndi ogwidwa ndi mizimu yoipa.

Anthu a m'mudzi monsemo adaasonkhana pakhomopo.

Yesu adachiritsa ambiri amene ankavutika ndi matenda osiyanasiyana, ndipo adatulutsa mizimu yoipa yambiri. Koma mizimuyo ankailetsa kuti isalankhule, chifukwa idaamzindikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 11:24

“Mzimu woipa ukatuluka mwa munthu, umakayendayenda ku malo opanda madzi, kufunafuna malo opumulirako. Ndipo ukapanda kuŵapeza, umati, ‘Ndibwerera kunyumba kwanga komwe ndidatuluka kuja.’

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 4:33-36

M'nyumba yamapempheroyo munali munthu wogwidwa ndi mzimu womuipitsa. Adalankhula mokuwa kuti,

“Aah, kodi takuputani chiyani, Inu Yesu wa ku Nazarete? Kodi mwadzatiwononga? Ndakudziŵani, ndinu Woyera uja wa Mulungu.”

Koma Yesu adazazira mzimu woipawo, adati, “Khala chete, tuluka mwa munthuyu.” Apo mzimu womuipitsa uja udamugwetsa pansi munthuyo pakati pa anthu, nkutuluka, osamupweteka konse.

Anthu onse aja adazizwa, mpaka kumafunsana kuti, “Mau ameneŵa ngotani? Ngakhale mizimu yoipitsa anthu yomwe akuilamula ndi mphamvu ndi ulamuliro, ndipo ikutulukadi.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 8:28

Yesu atafika ku tsidya la nyanja, ku dera la Agadara, anthu aŵiri ogwidwa ndi mizimu yoipa adadzakumana naye kuchokera ku manda. Anali aukali kwambiri, kotero kuti panalibe munthu ndi mmodzi yemwe wotha kudzera njira imeneyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 1:23-26

M'nyumba yamapempheroyo mudaaloŵa munthu wogwidwa ndi mzimu womuipitsa. Adalankhula mokuŵa kuti,

“Kodi takuputani chiyani, Inu Yesu wa ku Nazarete? Kodi mwadzatiwononga? Ndakudziŵani, ndinu Woyera uja wa Mulungu.”

Koma Yesu adazazira mzimu woipawo, adati, “Khala chete, tuluka mwa munthuyu.”

Apo mzimu womuipitsa uja udamugwedeza kwamphamvu munthuyo, ndipo udakuwa koopsa, nkutuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 13:11

M'menemo munali mai wina amene anali ndi mzimu woipa umene udamudwalitsa zaka 18. Anali ndi msana wokhota, mwakuti sankatha konse kuŵeramuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 9:25

Pamene Yesu adaona kuti chikhamu cha anthu chija chayamba kupanikizana pamenepo, adazazira mzimu woipawo, adati, “Iwe mzimu woletsa kulankhula ndi kumva, ndikukulamula kuti utuluke mwa mwanayu, ndipo usadzaloŵenso mwa iye.”

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 11:14-15

Tsiku lina Yesu ankatulutsa mzimu woipa woletsa munthu kulankhula. Mzimuwo utatuluka, munthu amene anali wosalankhulayo adayamba kulankhula, mwakuti anthu ambirimbiri amene anali pomwepo adazizwa kwabasi.

Koma ena mwa iwo adati, “Mphamvu zimene iyeyu amatulutsira mizimu yoipazi nzochokera kwa Belezebulu, mkulu wa mizimu yoipayo.”

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 9:37-43

M'maŵa mwake Yesu ndi ophunzira atatuwo adatsika kuphiri kuja, ndipo anthu ambirimbiri adadzamchingamira.

Munthu wina pakati pa anthuwo adanena mokweza mau kuti, “Aphunzitsi, chonde tandiwonerani mwana wangayu, ine mwana ndi mmodzi yemweyu.

Ali ndi mzimu woipa umene umati ukamugwira, amayamba kukuwa mwadzidzidzi. Tsono ukamzunguza kolimba, mwanayu amangoti thovu tututu kukamwa. Ndipo sumusiya mpaka utampweteka ndithu.

Ndipo mukafikira kunyumba kwina, mukhale nao kumeneko mpaka itakwana nthaŵi yoti muchoke kumudziko.

Ndinapempha ophunzira anuŵa kuti autulutse, koma alephera.”

Yesu adati, “Ha! Anthu a mbadwo wopanda chikhulupiriro ndi wopotoka maganizo. Ndiyenera kukhala nanube ndi kukupirirani mpaka liti? Tabwera nayeni kuno mwana wanuyo.”

Pamene mwanayo ankabwera, mzimu woipawo udamgwetsa pansi nkumuzunguza kolimba. Koma Yesu adazazira mzimu woipawo. Kenaka atamchiritsa mwanayo, adamperekanso kwa bambo wake.

Apo anthu onse aja adazizwa nazo mphamvu za Mulunguzi. Pamene anthu onse aja ankazizwabe ndi zonse zimene Yesu adaachita, Iye adauza ophunzira ake kuti,

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 12:22

Pambuyo pake anthu adadza kwa Yesu ndi munthu wakhungu, wosatha kulankhula, ndi woloŵedwa mizimu yoipa. Tsono Yesu adamchiritsa, kotero kuti adayamba kulankhula ndi kupenya.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 16:16-18

Nthaŵi ina pamene tinkapita ku malo opemphererako, tidakumana ndi kapolo wachitsikana amene adaagwidwa ndi mzimu woipa womunenetsa zakutsogolo. Ankapindulitsa mbuye wake kwambiri ndi kulosa kwakeko.

Iyeyo adayamba kutitsatira Paulo ndi ife, akufuula kuti, “Anthu aŵa ndi atumiki a Mulungu Wopambanazonse, akukulalikirani njira ya chipulumutso.”

Mtsikanayo adachita zimenezi masiku ambiri. Koma Paulo zimenezo zidamunyansa, choncho adatembenuka nauza mzimu woipa uja kuti, “Iwe, m'dzina la Yesu Khristu ndikukulamula kuti utuluke mwa munthuyu.” Ndipo nthaŵi yomweyo udatulukadi.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:1

Yesu adasonkhanitsa ophunzira ake khumi ndi aŵiri aja, naŵapatsa mphamvu pa mizimu yoipitsa anthu, kuti aziitulutsa mwa anthuwo, ndiponso mphamvu zochiritsira nthenda zonse za anthu ndi zofooka zao zam'thupi.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 9:17-27

Mmodzi mwa anthuwo adayankha kuti, “Aphunzitsi, ine ndinabwera ndi mwana wanga wamwamuna kuti ndidzampereke kwa Inu, chifukwa adaloŵedwa ndi mzimu woipa womuletsa kulankhula.

Umati ukangomugwira, umamgwetsa pansi, mwanayo nkumangoti thovu tututu kukamwa, namakukuta mano, mpaka thupi gwagwagwa kuuma. Ndiye ndinapempha ophunzira anuŵa kuti autulutse, koma alephera.”

Apo Yesu adati, “Ha! Anthu a mbadwo wopanda chikhulupiriro! Ndiyenera kukhala nanube mpaka liti? Ndiyenera kukupirirani mpaka liti? Tabwera nayeni kuno mwanayo.”

Patapita masiku asanu ndi limodzi, Yesu adatenga Petro ndi Yakobe ndi Yohane, nakwera nawo ku phiri lalitali, kwaokha. Tsono maonekedwe a Yesu adasinthika iwo akuwona.

Adabwera nayedi. Mzimu woipa uja utangoona Yesu, nthaŵi yomweyo wayamba kumzunguza mwamphamvu mnyamata uja, mpaka iye pansi khu, nkumangovimvinizika, thovu lili tututu kukamwa.

Yesu adafunsa bambo wake uja kuti, “Kodi zimenezi zidamuyamba liti?” Bambo wakeyo adati, “Zidamuyamba ali mwana ndithu.

Mzimu umenewu wakhala ukumugwetsa kaŵirikaŵiri, mwina amagwa pa moto, mwina m'madzi, kufuna kumupha. Koma ngati Inu mungathe kuchitapo kanthu, chonde tatichitirani chifundo, mutithandize.”

Yesu adati, “Bwanji mukuti, ‘Ngati mungathe?’ Zinthu zonse nzotheka kwa amene ali ndi chikhulupiriro.”

Pomwepo bambo wa mwana uja adanena mokweza mau kuti, “Ndikukhulupirira, koma mpang'ono chabe. Thandizeni kuti ndikhulupirire kwenikweni.”

Pamene Yesu adaona kuti chikhamu cha anthu chija chayamba kupanikizana pamenepo, adazazira mzimu woipawo, adati, “Iwe mzimu woletsa kulankhula ndi kumva, ndikukulamula kuti utuluke mwa mwanayu, ndipo usadzaloŵenso mwa iye.”

Mzimuwo udafuula numzunguza mwamphamvu mwana uja, kenaka nkutuluka. Mwanayo adangoti zii ngati wafa, mpaka ambiri nkumati, “Watsirizika basi!”

Koma Yesu adamugwira dzanja namdzutsa, mwanayo nkuimirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 7:25-30

Nthaŵi yomweyo mai wina, amene mwana wake wamkazi ankavutika ndi mzimu woipa, adamva za Iye. Adabwera kwa Yesu nagwada kumapazi kwake.

Maiyo anali mkunja, wa mtundu wa anthu a ku Siro-Fenisiya. Adapempha Yesu kuti akatulutse mzimu woipawo mwa mwana wake.

Koma Yesu adamuyankha kuti, “Ai, alekeni ana ayambe adya nkukhuta. Sibwino kutenga chakudya cha ana nkuponyera agalu.”

Apo maiyo adati, “Nzoonadi, Ambuye, koma suja ngakhale agalu omwe amakhala m'munsi mwa tebulo nkumadyako nyenyeswa zimene ataya ana?”

Apo Yesu adamuuza kuti, “Chifukwa cha mau mwanenaŵa, pitani, mzimu woipawo watuluka mwa mwana wanu.”

Pajatu Afarisi ndi Ayuda ena onse saadya asanasambe m'manja mwa njira yoyenera. Amatero kuti asunge mwambo wa makolo.

Mai uja adabwerera kunyumba kwake, nakapezadi mwanayo ali gone pa bedi, mzimu woipa uja utatuluka.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 9:32-33

Pamene iwowo ankatuluka m'nyumbamo, anthu ena adabwera kwa Yesu ndi munthu wosatha kulankhula, chifukwa chogwidwa ndi mzimu woipa.

Yesu atatulutsa mzimu woipawo, munthu uja adayamba kulankhula. Apo anthu onse adazizwa nati, “Nkale lonse Aisraele sadaziwone zotere.”

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 8:16

Madzulo amenewo, anthu adabwera kwa Yesu ndi anzao ambiri ogwidwa ndi mizimu yoipa. Yesu adaitulutsa mizimuyo ndi mau chabe, ndipo onse amene ankadwala adaŵachiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 17:14-18

Pamene iwo adafikanso kumene kunali khamu la anthu kuja, munthu wina adadzagwadira Yesu.

Adati, “Ambuye mchitireni chifundo mwana wanga. Ali ndi khunyu ndipo amavutika koopsa. Kaŵirikaŵiri amagwa pa moto mwinanso m'madzi.

Ndinabwera naye kwa ophunzira anuŵa, koma alephera kumchiritsa.”

Yesu adati, “Ha! Anthu a m'badwo wopanda chikhulupiriro ndi wopotoka maganizo! Ndiyenera kukhala nanube mpaka liti? Ndiyenera kukupirirani mpaka liti? Tabwera nayeni kuno mwanayo.”

Atatero, Yesu adazazira mzimu woipawo, ndipo udatuluka mwa mnyamatayo. Pompo iye adachira.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 16:16

Nthaŵi ina pamene tinkapita ku malo opemphererako, tidakumana ndi kapolo wachitsikana amene adaagwidwa ndi mzimu woipa womunenetsa zakutsogolo. Ankapindulitsa mbuye wake kwambiri ndi kulosa kwakeko.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 8:2

Panalinso azimai ena amene Yesu adaaŵatulutsa mizimu yoipa ndi kuŵachiza nthenda zina. Azimaiwo ndi aŵa: Maria, wotchedwa Magadalena, (amene mwa iye mudaatuluka mizimu yoipa isanu ndi iŵiri);

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 19:16

Kenaka munthu wogwidwa ndi mizimu yoipa uja adaŵalumphira naŵagwira onse. Adaŵagonjetsa kotero kuti iwowo adathaŵanso m'nyumba muja ali maliseche ndiponso atapwetekedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:8

Muzikachiritsa odwala, muzikaukitsa akufa, muzikachotsa khate, muzikatulutsa mizimu yoipa. Mwalandira mwaulere, kaperekeni mwaulere.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 3:11-12

Mizimu yoipa inkati ikamuwona, inkadzigwetsa pansi pafupi ndi Iye nkumafuula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu.”

Koma Iye ankailetsa mwamphamvu kuti isamuulule.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 10:17-20

Anthu 72 aja adabwerako ndi chimwemwe nati, “Ambuye, ngakhale mizimu yoipa yomwe imatigonjera tikamailamula m'dzina lanu.”

Yesu adaŵauza kuti, “Ndidaona Satana alikugwa ngati mphezi kuchokera Kumwamba.

Ndakupatsanitu mphamvu kuti muziponda njoka ndi zinkhanira, ndi kumagonjetsa mphamvu zonse za mdani uja. Palibe kanthu kamene kangakupwetekeni.

Adaŵauza kuti, “Dzinthu ndzambiri, koma antchito ngochepa. Nchifukwa chake pemphani Mwini dzinthu kuti atume antchito kukatuta dzinthudzo.

Komabe musakondwere chifukwa choti mizimu yoipa ikukugonjerani, koma muzikondwera kuti maina anu adalembedwa Kumwamba.”

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 9:25-27

Pamene Yesu adaona kuti chikhamu cha anthu chija chayamba kupanikizana pamenepo, adazazira mzimu woipawo, adati, “Iwe mzimu woletsa kulankhula ndi kumva, ndikukulamula kuti utuluke mwa mwanayu, ndipo usadzaloŵenso mwa iye.”

Mzimuwo udafuula numzunguza mwamphamvu mwana uja, kenaka nkutuluka. Mwanayo adangoti zii ngati wafa, mpaka ambiri nkumati, “Watsirizika basi!”

Koma Yesu adamugwira dzanja namdzutsa, mwanayo nkuimirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Marko 5:15

Atafika kumene kunali Yesuko, adaona munthu adaagwidwa ndi mizimu yoipa uja atakhala pansi, atavala, misala ija itatha, munthu woti adaloŵedwa ndi chigulu cha mizimu yoipa. Anthuwo adagwidwa ndi mantha.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:4

Koma inu, ana anga, ndinu ake a Mulungu, ndipo mwaŵapambana aneneri onamawo. Pakuti Iye amene ali mwa inu, ndi wopambana iye uja amene ali mwa anthu odalira zapansipano.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 5:1

Khristu adatimasula kuti tikhale mfulu ndithu. Muzichilimikira tsono, osalola kumangidwanso m'goli la ukapolo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 16:20

Ndipo Mulungu amene amapatsa mtendere, posachedwa adzatswanya Satana pansi pa mapazi anu. Ambuye athu Yesu Khristu akudalitseni.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:7

Tsono muzigonjera Mulungu. Satana muzilimbana naye, ndipo adzakuthaŵani.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:13

Adatilanditsa ku mphamvu za mdima wa zoipa, nkutiloŵetsa mu Ufumu wa Mwana wake wokondedwa.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse, ulemerero ndi ulemu zikhale zako! Mulungu wanga wakumwamba ndimabwera kwa Inu kudzera mwa Ambuye wanga Yesu Khristu. Atate Woyera, ndikupemphani podziwa kuti Inu nokha muli ndi Mphamvu yomasula ndipo ndikutenga ulamuliro umene mwandipatsa kudzera mwa Mzimu Woyera wanu kuti ndigwetse maganizo onse abodza ndi chinyengo omwe abwera pa moyo wanga. Pakadali pano ndikudzudzula mzimu uliwonse woyipa ndi ntchito iliyonse yoipa ndikuzilengeza kuti sizigwira ntchito. Mawu anu amati: "Koma ngati ine nditulutsa ziwanda ndi Mzimu wa Mulungu, ndiye kuti Ufumu wa Mulungu wafika kwa inu. Iye amene sali nane ali kunditsutsa; ndipo iye amene sasuntha nane amabalalitsa." Ndikukupemphani kuti mulimbitse chikhulupiriro changa ndipo mundithandize kugonjetsa mantha, chisokonezo chilichonse, kuti kuyuma tsopano Mzimu Woyera utenge ulamuliro wa maganizo anga, malingaliro anga ndi umunthu wanga wonse. Lero ndikusiya uchimo ndi zonyansa zonse ndipo ndikudzilongeza kuti ndine womasuka ku ukapolo uliwonse wa mdani. Ambuye, ndikupemphani kuti mumasule ndi kubwezeretsa miyoyo ya anthu omwe pakadali pano akukumana ndi zovuta, kaya ndi matenda, zachuma kapena m'banja. Ndimawalengeza kuti ali omasuka ku zowawa zonse, chifukwa kumene kuli Mzimu wanu wa Ambuye, kuli ufulu. M'dzina la Yesu. Ameni.