Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

109 Mau a Mulungu Okhudza Kupempherera Ena

Ndili ndi chimwemwe chodabwitsa chifukwa cha Yesu amene anatiyandikira kwa Mulungu pomwalira pa mtanda. Tsopano nditha kupempherera Akhristu anzanga, komanso anthu amene asokera, kuti Mulungu akwaniritse zofuna zawo monga mmene Iye akufunira.

Mulungu amafuna kuti tonsefe, okhulupirira, tizipemphera mwachangu, kupemphererana. Ndi mwayi waukulu kwambiri umene tili nawo woti tilankhule momasuka pamaso pa Mulungu Wamphamvuyonse ndi mapemphero athu!

Mawu a Mulungu amati: “Ndani adzaimba mlandu osankhidwa a Mulungu? Mulungu ndiye wolungamitsa. Ndani adzatsutsa? Khristu Yesu ndiye amene anafa, ndithu, amenenso anaukitsidwa kwa akufa, amene ali kudzanja lamanja la Mulungu, amenenso amatipempherera.” (Aroma 8:34)

Mulungu akuitana ife tonse Akhristu kuti tizipemphererana.


Aefeso 6:18

mwa pemphero lonse ndi pembedzero mupemphere nthawi yonse mwa Mzimu, ndipo pochezera pamenepo chichezerere ndi kupembedzera oyera mtima onse,

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 7:25

kuchokera komweko akhoza kupulumutsa konsekonse iwo akuyandikira kwa Mulungu mwa Iye, popeza ali nao moyo wake chikhalire wa kuwapembedzera iwo.

Mutu    |  Mabaibulo
Ezekieli 22:30

Ndipo ndinafunafuna munthu pakati pao wakumanganso linga, ndi kuimira dziko popasukira pamaso panga, kuti ndisaliononge; koma ndinapeza palibe.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 9:3

Ndipo ndinaika nkhope yanga kwa Ambuye Mulungu, kumfunsa Iye m'pemphero, ndi mapembedzero, ndi kusala, ndi ziguduli, ndi mapulusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 29:7

Nimufune mtendere wa mzinda umene ndinakutengerani am'nsinga, nimuwapempherere kwa Yehova; pakuti mwa mtendere wake inunso mudzakhala ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Samueli 12:23

Ndipo inenso, kukhale kutali ndi ine, kuchimwira Yehova ndi kuleka kukupemphererani; koma ndidzakulangizani njira yabwino ndi yolungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 3:14

Chifukwa cha ichi ndipinda maondo anga kwa Atate,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:25

Abale, tipempherereni ife.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:26-27

Ndipo momwemonso Mzimu athandiza kufooka kwathu; pakuti chimene tizipempha monga chiyenera, sitidziwa; koma Mzimu mwini atipempherera ndi zobuula zosatheka kuneneka;

ndipo Iye amene asanthula m'mitima adziwa chimene achisamalira Mzimu, chifukwa apempherera oyera mtima monga mwa chifuniro cha Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 1:2

Tiyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu nonse, ndi kukumbukira inu m'mapemphero athu;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:26

Ndipo momwemonso Mzimu athandiza kufooka kwathu; pakuti chimene tizipempha monga chiyenera, sitidziwa; koma Mzimu mwini atipempherera ndi zobuula zosatheka kuneneka;

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 3:1

Chotsalira, abale, mutipempherere, kuti mau a Ambuye athamange, nalemekezedwe, monganso kwanu;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:44

koma Ine ndinena kwa inu, Kondanani nao adani anu, ndi kupempherera iwo akuzunza inu;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 2:1-3

Ndidandaulira tsono, poyambayamba, kuti achitike mapembedzo, mapemphero, mapembedzero, mayamiko, chifukwa cha anthu onse;

komatu (umo mokomera akazi akuvomereza kulemekeza Mulungu), mwa ntchito zabwino.

Mkazi aphunzire akhale wachete m'kumvera konse.

Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale chete.

Pakuti Adamu anayamba kulengedwa, pamenepo Heva;

ndipo Adamu sananyengedwe, koma mkaziyo ponyengedwa analowa m'kulakwa;

koma adzapulumutsidwa mwa kubala mwana, ngati akhala m'chikhulupiriro ndi chikondi ndi chiyeretso pamodzi ndi chidziletso.

chifukwa cha mafumu ndi onse akuchita ulamuliro; kuti m'moyo mwathu tikakhale odika mtima ndi achete m'kulemekeza Mulungu, ndi m'kulemekezeka monse.

Pakuti ichi nchokoma ndi cholandirika pamaso pa Mulungu Mpulumutsi wathu;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 2:1-2

Ndidandaulira tsono, poyambayamba, kuti achitike mapembedzo, mapemphero, mapembedzero, mayamiko, chifukwa cha anthu onse;

komatu (umo mokomera akazi akuvomereza kulemekeza Mulungu), mwa ntchito zabwino.

Mkazi aphunzire akhale wachete m'kumvera konse.

Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale chete.

Pakuti Adamu anayamba kulengedwa, pamenepo Heva;

ndipo Adamu sananyengedwe, koma mkaziyo ponyengedwa analowa m'kulakwa;

koma adzapulumutsidwa mwa kubala mwana, ngati akhala m'chikhulupiriro ndi chikondi ndi chiyeretso pamodzi ndi chidziletso.

chifukwa cha mafumu ndi onse akuchita ulamuliro; kuti m'moyo mwathu tikakhale odika mtima ndi achete m'kulemekeza Mulungu, ndi m'kulemekezeka monse.

Mutu    |  Mabaibulo
Numeri 21:7

Ndipo anthu anadza kwa Mose, nati, Tachimwa, popeza tinanena motsutsana ndi Yehova, ndi inu; pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi. Ndipo Mose anawapempherera anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 1:11

pothandizana inunso ndi pemphero lanu la kwa ife; kuti pa mphatso ya kwa ife yodzera kwa anthu ambiri, payamikike ndi anthu ambiri chifukwa cha ife.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 5:16

Chifukwa chake muvomerezane wina ndi mnzake machimo anu, ndipo mupempherere wina kwa mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama likhoza kwakukulu m'machitidwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:14-15

Ndipo uku ndi kulimbika mtima kumene tili nako kwa Iye, kuti ngati tipempha kanthu monga mwa chifuniro chake, atimvera;

ndipo ngati tidziwa kuti atimvera chilichonse tichipempha, tidziwa kuti tili nazo izi tazipempha kwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 4:16

Potero tilimbike mtima poyandikira mpando wachifumu wachisomo, kuti tilandire chifundo ndi kupeza chisomo cha kutithandiza nthawi yakusowa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 122:6

Mupempherere mtendere wa Yerusalemu; akukonda inu adzaona phindu.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:2

Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse chilamulo cha Khristu.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 1:3-5

Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;

ndi kukhala nacho inu chilimbano chomwechi mudachiona mwa ine, nimukumva tsopano chili mwa ine.

nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndichita pembedzerolo ndi kukondwera,

chifukwa cha chiyanjano chanu chakuthandizira Uthenga Wabwino, kuyambira tsiku loyambalo, kufikira tsopano lino;

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 42:10

Ndipo Yehova anachotsa ukapolo wa Yobu, pamene anapempherera mabwenzi ake; Yehova nachulukitsa zake zonse za Yobu mpaka kuziwirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 22:32

koma ndinakupempherera kuti chikhulupiriro chako chingazime; ndipo iwe, pamene watembenuka ukhazikitse abale ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 103:1-2

Lemekeza Yehova, moyo wanga; ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.

Sanatichitira monga mwa zolakwa zathu, kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.

Pakuti monga m'mwamba mutalikira ndi dziko lapansi, motero chifundo chake chikulira iwo akumuopa Iye.

Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo, momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.

Monga atate achitira ana ake chifundo, Yehova achitira chifundo iwo akumuopa Iye.

Popeza adziwa mapangidwe athu; akumbukira kuti ife ndife fumbi.

Koma munthu, masiku ake akunga udzu; aphuka monga duwa lakuthengo.

Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe: Ndi malo ake salidziwanso.

Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye, ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana;

kwa iwo akusunga chipangano chake, ndi kwa iwo akukumbukira malangizo ake kuwachita.

Yehova anakhazika mpando wachifumu wake Kumwamba; ndi ufumu wake uchita mphamvu ponsepo.

Lemekeza Yehova, moyo wanga, ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 15:30-32

Ndipo ndikudandaulirani, abale, ndi Ambuye wathu Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mzimu, kuti mudzalimbike pamodzi ndi ine m'mapemphero anu kwa Mulungu chifukwa cha ine;

kuti ndikapulumutsidwe kwa osamvera aja a ku Yudeya; ndi kuti utumiki wanga wa ku Yerusalemu ukhale wolandiridwa bwino ndi oyera mtima;

kuti ndi chimwemwe ndikadze kwa inu mwa chifuniro cha Mulungu, ndi kupumula pamodzi ndi inu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:17

Iwowo anaitana, ndipo Yehova anawamva, nawalanditsa kumasautso ao onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:29

Yehova atalikira oipa; koma pemphero la olungama alimvera.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:19-20

Ndiponso ndinena kwa inu kuti ngati awiri a inu avomerezana pansi pano chinthu chilichonse akachipempha, Atate wanga wa Kumwamba adzawachitira.

Ndipo pamene Yesu anaitana kamwana, anakaimitsa pakati pao,

Pakuti kumene kuli awiri kapena atatu asonkhanira m'dzina langa, ndili komweko pakati pao.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 28:9

Pulumutsani anthu anu, ndi kudalitsa cholowa chanu; muwawetenso, ndi kuwanyamula nthawi zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 53:12

Chifukwa chake ndidzamgawira gawo ndi akulu; ndipo adzagawana ndi amphamvu zofunkha; pakuti Iye anathira moyo wake kuimfa; ndipo anawerengedwa pamodzi ndi olakwa; koma ananyamula machimo a ambiri, napembedzera olakwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 6:28

dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani iwo akuchitira inu chipongwe.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 3:12

Pakuti maso a Ambuye ali pa olungama, ndi makutu ake akumva pembedzo lao; koma nkhope ya Ambuye ili pa ochita zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 55:17

Madzulo, m'mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula, ndipo adzamva mau anga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:25

Mtima wa mataya udzalemera; wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:16-17

sindileka kuyamika chifukwa cha inu, ndi kukumbukira inu m'mapemphero anga;

kuti Mulungu wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa ulemerero, akupatseni inu mzimu wa nzeru, ndi wa vumbulutso kuti mukamzindikire Iye;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 8:34

ndani adzawatsutsa? Khristu Yesu ndiye amene adafera, inde makamaka, ndiye amene adauka kwa akufa, amene akhalanso padzanja lamanja la Mulungu, amenenso atipempherera ife.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 5:20

Chifukwa chake tili atumiki m'malo mwa Khristu, monga ngati Mulungu alikudandaulira mwa ife; tiumiriza inu m'malo mwa Khristu, yanjanitsidwani ndi Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:147

Ndinafuula kusanake: ndinayembekezera mau anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 4:3

ndi kutipempherera ifenso pomwepo, kuti Mulungu atitsegulire ife pakhomo pa mau, kuti tilankhule chinsinsi cha Khristu; chimenenso ndikhalira m'ndende,

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 26:41

Chezerani ndi kupemphera, kuti mungalowe m'kuyesedwa: mzimutu uli wakufuna, koma thupi lili lolefuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:4

Udzikondweretsenso mwa Yehova; ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:12

kondwerani m'chiyembekezo, pirirani m'masautso; limbikani chilimbikire m'kupemphera.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 130:5-6

Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira, ndiyembekeza mau ake.

Moyo wanga uyang'anira Ambuye, koposa alonda matanda kucha; inde koposa alonda matanda kucha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 59:16

Ndipo Iye anaona kuti palibe munthu, nazizwa kuti palibe wopembedzera; chifukwa chake mkono wakewake unadzitengera yekha chipulumutso; ndi chilungamo chake chinamchirikiza.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 1:3

Monga ndinakudandaulira iwe utsalire mu Efeso, popita ine ku Masedoniya, nditeronso, kuti ukalamulire ena ajawa asaphunzitse kanthu kena,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:25

Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu; koma mau abwino aukondweretsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 86:6-7

Tcherani khutu pemphero langa, Yehova; nimumvere mau a kupemba kwanga.

Tsiku la msauko wanga ndidzaitana Inu; popeza mudzandivomereza.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:17

Ndipo chisomo chake cha Ambuye Mulungu wathu chikhalire pa ife; ndipo mutikhazikitsire ife ntchito ya manja athu; inde, ntchito ya manja athu muikhazikitse.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:7

Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo chidzatsegulidwa kwa inu;

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 3:20

Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife,

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 91:15

Adzandifuulira Ine ndipo ndidzamyankha; kunsautso ndidzakhala naye pamodzi; ndidzamlanditsa, ndi kumchitira ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 3:22

ndipo chimene chilichonse tipempha, tilandira kwa Iye, chifukwa tisunga malamulo ake, ndipo tichita zomkondweretsa pamaso pake.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:19-21

Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Koma ngati mdani wako akumva njala, umdyetse, ngati akumva ludzu, ummwetse; pakuti pakutero udzaunjika makala a moto pamutu pake.

Musagonje kwa choipa, koma ndi chabwino gonjetsani choipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 4:19

Tiana tanga, amene ndilikumvanso zowawa za kubala inu, kufikira Khristu aumbika mwa inu,

Mutu    |  Mabaibulo
2 Atesalonika 1:11

Kukatero tikupemphereraninso nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akakuyeseni inu oyenera kuitanidwa kwanu, nakakwaniritse chomkomera chonse, ndi ntchito ya chikhulupiriro mumphamvu;

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 13:3

Kumbukirani am'nsinga, monga am'nsinga anzao; ochitidwa zoipa, monga ngati inunso adatero nanu m'thupi.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 27:4

Chinthu chimodzi ndinachipempha kwa Yehova, ndidzachilondola ichi, Kuti ndikhalitse m'nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, kupenya kukongola kwake kwa Yehova ndi kufunsitsa mu Kachisi wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 141:2

Pemphero langa liikike ngati chofukiza pamaso panu; kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalimo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 2:1-2

Ngati tsono muli chitonthozo mwa Khristu, ngati chikhazikitso cha chikondi, ngati chiyanjano cha Mzimu, ngati phamphu, ndi zisoni,

kuti m'dzina la Yesu bondo lililonse lipinde, la za m'mwamba ndi za padziko, ndi za pansi padziko,

ndi malilime onse avomere kuti Yesu Khristu ali Ambuye, kuchitira ulemu Mulungu Atate.

Potero, okondedwa anga, monga momwe mumvera nthawi zonse, posati pokhapokha pokhala ine ndilipo, komatu makamaka tsopano pokhala ine palibe, gwirani ntchito yake ya chipulumutso chanu ndi mantha, ndi kunthunthumira;

pakuti wakuchita mwa inu kufuna ndi kuchita komwe, chifukwa cha kukoma mtima kwake, ndiye Mulungu.

Chitani zonse kopanda madandaulo ndi makani,

kuti mukakhale osalakwa ndi oona, ana a Mulungu opanda chilema pakati pa mbadwo wokhotakhota ndi wopotoka, mwa iwo amene muonekera monga mauniko m'dziko lapansi,

akuonetsera mau a moyo; kuti ine ndikakhale wakudzitamandira nao m'tsiku la Khristu, kuti sindinathamange chabe, kapena kugwiritsa ntchito chabe.

Komatu ngatinso ndithiridwa pa nsembe ndi kutumikira kwa chikhulupiriro chanu, ndikondwera, ndipo ndikondwera pamodzi ndi inu nonse;

momwemonso kondwerani inu, nimukondwere pamodzi ndi ine.

Koma ndiyembekeza mwa Ambuye Yesu kuti ndidzatumiza Timoteo kwa inu msanga, kuti inenso nditonthozeke bwino pozindikira za kwa inu.

kwaniritsani chimwemwe changa, kuti mukalingalire mtima zomwezo, akukhala nacho chikondi chomwe, a moyo umodzi, olingalira mtima umodzi;

Mutu    |  Mabaibulo
1 Petro 4:7

Koma chitsiriziro cha zinthu zonse chili pafupi; chifukwa chake khalani anzeru, ndipo dikirani m'mapemphero;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 40:1-3

Kuyembekeza ndayembekeza Yehova; ndipo anandilola, namva kufuula kwanga.

Chilungamo chanu sindinachibise m'kati mwamtima mwanga; chikhulupiriko chanu ndi chipulumutso chanu ndinachinena; chifundo chanu ndi choonadi chanu sindinachibisire msonkhano waukulu.

Inu Yehova, simudzandikaniza nsoni zanu, chifundo chanu ndi choonadi chanu zindisunge chisungire.

Pakuti zoipa zosawerengeka zandizinga, zochimwa zanga zandipeza kotero kuti sindikhoza kupenya; ziposa tsitsi la mutu wanga, ndipo wandichokera mtima.

Ndikupemphani, Yehova, ndilanditseni; fulumirani kudzandithandiza, Yehova.

Achite manyazi nadodome iwo akulondola moyo wanga kuti auononge. Abwerere m'mbuyo, nachite manyazi iwo okondwera kundichitira choipa.

Apululuke, mobwezera manyazi ao amene anena nane, Hede, hede.

Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu; iwo akukonda chipulumutso chanu asaleke kunena, Abuke Yehova.

Ndipo ine ndine wozunzika ndi waumphawi; koma Ambuye andikumbukira ine. Inu ndinu mthandizi wanga, ndi Mpulumutsi wanga, musamachedwa, Mulungu wanga.

Ndipo anandikweza kunditulutsa m'dzenje la chitayiko, ndi m'thope la pachithaphwi; nandipondetsa pathanthwe, nakhazika mayendedwe anga.

Ndipo anapatsa nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, chilemekezo cha kwa Mulungu wanga; ambiri adzachiona, nadzaopa, ndipo adzakhulupirira Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:105

Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga, ndi kuunika kwa panjira panga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 10:1

Abale, kufunitsa kwa mtima wanga ndi pemphero langa limene ndiwapempherera kwa Mulungu, ndilo, kuti apulumuke.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 56:7

naonso ndidzanka nao kuphiri langa lopatulika, ndi kuwasangalatsa m'nyumba yanga yopemphereramo; zopereka zao zopsereza ndi nsembe zao zidzalandiridwa paguwa langa la nsembe; pakuti nyumba yanga idzatchedwa nyumba yopemphereramo anthu onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 4:15

koma ndi kuchita zoona mwa chikondi tikakule m'zinthu zonse, kufikira Iye amene ali mutu ndiye Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Ahebri 10:24-25

ndipo tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino,

osaleka kusonkhana kwathu pamodzi, monga amachita ena, komatu tidandaulirane, ndiko koposa monga momwe muona tsiku lilikuyandika.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 5:16

Wina akaona mbale wake alikuchimwa tchimo losati la kuimfa, apemphere Mulungu, ndipo Iye adzampatsira moyo wa iwo akuchita machimo osati a kuimfa. Pali tchimo la kuimfa: za ililo sindinena kuti mupemphere.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 78:64

Ansembe ao anagwa ndi lupanga; ndipo amasiye ao sanachite maliro.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:1

Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze wotereyo mu mzimu wa chifatso; ndi kudzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:17

Bwenzi limakonda nthawi zonse; ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 106:23

Potero Iye adati awaononge, pakadapanda Mose wosankhika wake, kuima pamaso pake pogamukapo, kubweza ukali wake ungawaononge.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 9:36-38

Koma Iye, poona makamuwo, anagwidwa m'mtima ndi chisoni chifukwa cha iwo, popeza anali okambululudwa ndi omwazikana, akunga nkhosa zopanda mbusa.

Pomwepo ananena kwa ophunzira ake, Zotuta zichulukadi koma antchito ali owerengeka.

Chifukwa chake pempherani Mwini zotuta kuti akokose antchito kukututa kwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:14

Mau a m'kamwa mwanga ndi maganizo a m'mtima wanga avomerezeke pamaso panu, Yehova, thanthwe langa, ndi Mombolo wanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 1:9

Pakuti Mulungu ali mboni yanga, amene ndimtumikira mu mzimu wanga, mu Uthenga Wabwino wa Mwana wake, kuti kosalekeza ndikumbukira inu,

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:3-4

Tiyamika Mulungu Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu ndi kupempherera inu nthawi zonse,

popeza tidamva za chikhulupiriro chanu cha mwa Khristu Yesu, ndi chikondi muli nacho kwa oyera mtima onse;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 84:11

Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 58:9

Pamenepo udzaitana, ndipo Yehova adzayankha; udzafuula ndipo Iye adzati, Ndine pano. Ngati uchotsa pakati pa iwe goli, kukodolana moipa, ndi kulankhula moipa,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 2:5

Pakuti pali Mulungu mmodzi, ndi Mtetezi mmodzi pakati pa Mulungu ndi anthu, ndiye munthu, Khristu Yesu,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 28:7

Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi chikopa changa; mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza, chifukwa chake mtima wanga ukondwera kwakukulu; ndipo ndidzamyamika nayo nyimbo yanga.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Akorinto 4:1

Chifukwa chake popeza tili nao utumiki umene, monga talandira chifundo, sitifooka;

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 18:10

Yang'anirani kuti musanyoze mmodzi wa ang'ono awa; pakuti ndinena kwa inu, kuti angelo ao apenya chipenyere nkhope ya Atate wanga wa Kumwamba.

Mutu    |  Mabaibulo
Agalatiya 6:7

Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Yohane 4:20

Munthu akati, kuti, Ndikonda Mulungu, nadana naye mbale wake, ali wabodza: pakuti iye wosakonda mbale wake amene wamuona, sangathe kukonda Mulungu amene sanamuone.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 5:5

ndipo chiyembekezo sichichititsa manyazi; chifukwa chikondi cha Mulungu chinatsanulidwa m'mitima mwathu mwa Mzimu Woyera, amene wapatsidwa kwa ife.

Mutu    |  Mabaibulo
Afilipi 4:6

Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 116:1-2

Ndimkonda, popeza Yehova amamva mau anga ndi kupemba kwanga.

Ndinakhulupirira, chifukwa chake ndinalankhula; ndinazunzika kwambiri.

Pofulumizidwa mtima ndinati ine, anthu onse nga mabodza.

Ndidzabwezera Yehova chiyani chifukwa cha zokoma zake zonse anandichitira?

Ndidzanyamula chikho cha chipulumutso, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Ndidzachita zowinda zanga za kwa Yehova, tsopano, pamaso pa anthu ake onse.

Imfa ya okondedwa ake nja mtengo wake pamaso pa Yehova.

Ndiloleni, Yehova, indetu ndine mtumiki wanu; ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; mwandimasulira zondimanga.

Ndidzapereka kwa Inu nsembe yachiyamiko, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

Ndidzachita zowinda zanga za kwa Yehova, tsopano, pamaso pa anthu ake onse.

M'mabwalo a nyumba ya Yehova, pakati pa inu, Yerusalemu. Aleluya.

Popeza amanditcherera khutu lake, chifukwa chake ndidzaitanira Iye masiku anga onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 50:4

Ambuye Yehova wandipatsa Ine lilime la ophunzira, kuti ndidziwe kunena mau akuchirikiza iye amene ali wolema. Iye andigalamutsa m'mawa ndi m'mawa, nagalamutsa khutu langa kuti limve monga ophunzira.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 141:1-2

Yehova, ndaitana kwa Inu; ndifulumireni ine; munditcherere khutu, pamene ndiitana kwa Inu.

Oipa agwe pamodzi m'maukonde ao, kufikira nditapitirira ine.

Pemphero langa liikike ngati chofukiza pamaso panu; kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 1:13

Koma mngelo anati kwa iye, Usaope Zekariya, chifukwa kuti lamveka pemphero lako, ndipo mkazi wako Elizabeti adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha dzina lake Yohane.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 4:3

Mupempha, ndipo simulandira, popeza mupempha koipa, kuti mukachimwaze pochita zikhumbitso zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 138:3

Tsiku loitana ine, munandiyankha, munandilimbitsa ndi mphamvu m'moyo mwanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 6:13

ndipo musapereke ziwalo zanu kuuchimo, zikhale zida za chosalungama; koma mudzipereke inu nokha kwa Mulungu, monga amoyo atatuluka mwa akufa, ndi ziwalo zanu kwa Mulungu zikhale zida za chilungamo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:16-18

Kondwerani nthawi zonse;

Pempherani kosaleka;

M'zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:17

Ndipo chilichonse mukachichita m'mau kapena muntchito, chitani zonse m'dzina la Ambuye Yesu, ndi kuyamika Mulungu Atate mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4-5

Mundidziwitse njira zanu, Yehova; Mundiphunzitse mayendedwe anu.

Munditsogolere m'choonadi chanu, ndipo mundiphunzitse; pakuti Inu ndinu Mulungu wa chipulumutso changa; Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 5:9

Odala ali akuchita mtendere; chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:24

Woyanjana ndi ambiri angodziononga; koma lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:5

Pereka njira yako kwa Yehova; khulupiriranso Iye, adzachichita.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 61:1

Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine; pakuti Yehova wandidzoza ine ndilalikire mau abwino kwa ofatsa; Iye wanditumiza ndikamange osweka mtima, ndikalalikire kwa am'nsinga mamasulidwe, ndi kwa omangidwa kutsegulidwa kwa m'ndende;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:1-2

Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.

M'chikondano cha anzanu wina ndi mnzake mukondane ndi chikondi chenicheni; mutsogolerane ndi kuchitira wina mnzake ulemu;

musakhale aulesi m'machitidwe anu; khalani achangu mumzimu, tumikirani Ambuye;

kondwerani m'chiyembekezo, pirirani m'masautso; limbikani chilimbikire m'kupemphera.

Patsani zosowa oyera mtima; cherezani aulendo.

Dalitsani iwo akuzunza inu; dalitsani, musawatemberere.

Kondwani nao iwo akukondwera; lirani nao akulira.

Mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake. Musasamalire zinthu zazikulu, koma phatikanani nao odzichepetsa. Musadziyesere anzeru mwa inu nokha.

Musabwezere munthu aliyense choipa chosinthana ndi choipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.

Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.

Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 87:5

Ndipo adzanena za Ziyoni, uyu ndi uyo anabadwa m'mwemo; ndipo Wam'mwambamwamba ndiye adzaukhazikitsa.

Mutu    |  Mabaibulo

Pemphero kwa Mulungu

Chauta Wamuyaya, Ambuye Wapamwamba! Ndikukutamandani chifukwa ndinu Wolungama, Woyera, woyenera kutamandidwa ndi kupembedzedwa kwakukulu. Ndikupempha kuti muwatsitse mwa amuna ndi akazi chilakolako chofuna kukupezani, kuti Mzimu Wanu Woyera utsanulidwe pa iwo. Kuti akonze mitima yawo kukuimbirani ndi kupempherera mpingo, mabanja ndi mitundu. Imitsani opemphera ngati Nehemiya, ofuna nkhope yanu mu kusala kudya, pemphero ndi kupembedza. Ndi chikondi chenicheni ndi mtima wolimba wodzipereka m'malo mwa ena chifukwa cha chikondi ndi chisoni pa iwo, okonzeka kutenga udindo woimbira zabwino za anzawo, kutseka mipata yonse ya mdani. Ambuye, opemphera odzipereka ndi achangu, ogwirizana mu Mzimu umodzi, akuimbira ndi kupemphera, kugwada chifukwa cha chifundo pa ena, achisoni ndi omvera ku ululu ndi mavuto a ena. M'dzina la Yesu. Ameni.