Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 5:9 - Buku Lopatulika

9 Odala ali akuchita mtendere; chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

9 Odala ali akuchita mtendere; chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

9 Ngodala anthu odzetsa mtendere, pakuti Mulungu adzaŵatcha ana ake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

9 Ndi odala amene amabweretsa mtendere, chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 5:9
31 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide anatuluka kukomana nao, nayankha, nanena nao, Ngati mwandidzera mwamtendere kundithandiza, mtima wanga udzalumikizana nanu; koma ngati mwafika kundipereka kwa adani anga, popeza m'manja mwanga mulibe chiwawa, Mulungu wa makolo athu achione ndi kuchilanga.


Moyo wanga unakhalitsa nthawi pamodzi ndi iye wakudana nao mtendere.


Munthu wokhumba moyo ndani, wokonda masiku, kuti aone zabwino?


kotero kuti mukakhale ana a Atate wanu wa Kumwamba; chifukwa Iye amakwezera dzuwa lake pa oipa ndi pa abwino, namavumbitsira mvula pa olungama ndi pa osalungama.


Chifukwa chake inu mukhale angwiro, monga Atate wanu wa Kumwamba ali wangwiro.


Pakuti sangathe kufanso nthawi zonse; pakuti afanafana ndi angelo; ndipo ali ana a Mulungu, popeza akhala ana a kuuka kwa akufa.


Koma takondanani nao adani anu, ndi kuwachitira zabwino, ndipo kongoletsani osayembekeza kanthu konse, ndipo mphotho yanu idzakhala yaikulu, ndipo inu mudzakhala ana a Wamkulukuluyo; chifukwa Iye achitira zokoma anthu osayamika ndi oipa.


Ndipo m'mawa mwake anawaonekera alikulimbana ndeu, ndipo anati awateteze, ayanjanenso, nati, Amuna inu, muli abale; muchitirana choipa bwanji?


Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.


Pakuti onse amene atsogozedwa ndi Mzimu wa Mulungu, amenewo ali ana a Mulungu.


Mzimu yekha achita umboni pamodzi ndi mzimu wathu, kuti tili ana a Mulungu;


Pakuti chiyembekezetso cha cholengedwa chilindira vumbulutso la ana a Mulungu.


koma mbale anena mlandu ndi mbale, ndikotu kwa osakhulupirira?


Chotsalira, abale, kondwerani. Muchitidwe angwiro; mutonthozedwe; khalani a mtima umodzi, khalani mumtendere; ndipo Mulungu wa chikondi ndi mtendere akhale pamodzi ndi inu.


Chifukwa chake tili atumiki m'malo mwa Khristu, monga ngati Mulungu alikudandaulira mwa ife; tiumiriza inu m'malo mwa Khristu, yanjanitsidwani ndi Mulungu.


Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,


Ndikudandaulirani inu tsono, ine wandende mwa Ambuye, muyende koyenera maitanidwe amene munaitanidwa nao,


Ndidandaulira Yuwodiya, ndidandaulira Sintike, alingirire ndi mtima umodzi mwa Ambuye.


kulolerana wina ndi mnzake, ndi kukhululukirana eni okha, ngati wina ali nacho chifukwa pa mnzake; monganso Ambuye anakhululukira inu, teroni inunso;


Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi chiyeretso chimene, akapanda ichi, palibe mmodzi adzaona Ambuye:


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa