Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 130 - Buku Lopatulika


Pemphero lakuti akhululukidwe
Nyimbo yokwerera.

1 M'mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.

2 Ambuye, imvani liu langa; makutu anu akhale chimverere mau a kupemba kwanga.

3 Mukasunga mphulupulu, Yehova, adzakhala chilili ndani, Ambuye?

4 Koma kwa Inu kuli chikhululukiro, kuti akuopeni.

5 Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira, ndiyembekeza mau ake.

6 Moyo wanga uyang'anira Ambuye, koposa alonda matanda kucha; inde koposa alonda matanda kucha.

7 Israele, uyembekezere Yehova; chifukwa kwa Yehova kuli chifundo, kwaonso kuchulukira chiombolo.

8 Ndipo adzaombola Israele ku mphulupulu zake zonse.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa