Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

Masalimo 87 - Buku Lopatulika


Yehova akonda Ziyoni
Salimo la ana a Kora. Nyimbo.

1 Maziko ake ali m'mapiri oyera.

2 Yehova akonda zipata za Ziyoni koposa zokhalamo zonse za Yakobo.

3 Mzinda wa Mulungu, inu, akunenerani zakukulemekezani.

4 Ndidzatchula Rahabu ndi Babiloni kwa iwo ondidziwa Ine; taonani, Filistiya ndi Tiro pamodzi ndi Kusi; uyu anabadwa komweko.

5 Ndipo adzanena za Ziyoni, uyu ndi uyo anabadwa m'mwemo; ndipo Wam'mwambamwamba ndiye adzaukhazikitsa.

6 Yehova adzawerenga, polembera mitundu ya anthu, uyu anabadwa komweko.

7 Ndipo oimba ndi oomba omwe adzati, akasupe anga onse ali mwa inu.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa