Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -

2 Samueli 22 - Buku Lopatulika


Nyimbo yoyamikira Yehova ya Davide
( Mas. 18 )

1 Ndipo Davide analankhula kwa Yehova mau a nyimbo iyi tsikuli Yehova anampulumutsa m'dzanja la adani ake onse, ndi m'dzanja la Saulo.

2 Ndipo anati, Yehova ndiye thanthwe langa, ndi ngaka yanga, ndi Mpulumutsi wanga, wangadi.

3 Mulungu wa thanthwe langa, Iye ndidzamkhulupirira; chikopa changa, ndi nyanga ya chipulumutso changa, nsanja yanga yaitali, ndi populumukirapo panga; Mpulumutsi wanga, mundipulumutsa kuchiwawa.

4 Ndidzaitana kwa Yehova amene ayenera timtamande; chomwecho ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.

5 Pakuti mafunde a imfa anandizinga, mitsinje ya zopanda pake inandiopsa ine.

6 Zingwe za kumanda zinandizingira; misampha ya imfa inandifikira ine.

7 M'kusauka kwanga ndinaitana kwa Yehova, inde ndinakuwira kwa Mulungu wanga; ndipo Iye anamva mau anga ali mu Kachisi wake, ndi kulira kwanga kunafika ku makutu ake.

8 Pomwepo dziko linagwedezeka ndi kunthunthumira. Maziko a dziko la kumwamba anasunthika. Nagwedezeka, chifukwa Iye anakwiya.

9 M'mphuno mwake munatuluka utsi, ndi moto wotuluka m'kamwa mwake unaononga; makala anayaka nao.

10 Anaweramitsa miyambanso, natsika; ndipo mdima wandiweyani unali pansi pa mapazi ake.

11 Ndipo Iye anaberekeka pa kerubi nauluka; inde anaoneka pa mapiko a mphepo.

12 Ndipo anayesa mdimawo ngati mahema omzungulira Iye, kusonkhana kwa madzi ndi mitambo yochindikira ya mlengalenga.

13 Cheza cha pamaso pake makala a moto anayaka.

14 Yehova anagunda kumwamba; ndipo Wam'mwambamwamba ananena mau ake.

15 Ndipo Iye anatumiza mivi, nawawaza; mphezi, nawaopsa.

16 Pamenepo m'munsi mwa nyanja munaoneka, maziko a dziko anaonekera poyera, ndi mtonzo wa Yehova, ndi mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwake.

17 Iye anatumiza kuchokera kumwamba nanditenga; Iye ananditulutsa m'madzi aakulu.

18 Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, kwa iwo akudana ndi ine; pakuti anandiposa mphamvu.

19 Anandifikira ine tsiku la tsoka langa; koma Yehova anali mchirikizo wanga.

20 Iye ananditulutsanso ku malo aakulu; Iye anandipulumutsa, chifukwa akondwera ndi ine.

21 Yehova anandibwezera monga mwa cholungama changa; monga mwa kuyera kwa manja anga anandipatsa mphotho.

22 Pakuti ndinasunga njira za Yehova, osapatukira ku zoipa kusiya Mulungu wanga.

23 Pakuti maweruzo ake onse anali pamaso panga; ndipo za malemba ake, sindinawapatukire.

24 Ndinakhalanso wangwiro kwa Iye, ndipo ndinadzisunga kusachita kuipa kwanga.

25 Chifukwa chake Yehova anandibwezera monga mwa cholungama changa; monga mwa kuyera kwanga pamaso pake.

26 Ndi chifundo Inu mudzadzionetsa wachifundo, ndi munthu wangwiro mudzadzionetsa wangwiro.

27 Ndi oyera mtima mudzadzionetsa woyera mtima; ndi otsutsatsutsa mudzadzionetsa wopotoza.

28 Ndipo mudzapulumutsa anthu osautsidwa; koma maso anu ali pa odzikuza kuti muwachepetse.

29 Pakuti Inu ndinu nyali yanga, Yehova; ndipo Yehova adzaunika mumdima mwanga.

30 Pakuti ndi Inu ndithamangira gulu; ndi Mulungu wanga ndilumphira linga.

31 Kunena za Mulungu, njira yake ili yangwiro; mau a Yehova anayesedwa; Iye ndiye chikopa kwa onse akukhulupirira Iye.

32 Pakuti Mulungu ndani, koma Yehova? Ndipo thanthwe ndani, koma Mulungu wathu?

33 Mulungu ndiye linga langa lamphamvu; ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake.

34 Iye asandutsa mapazi ake akunga mapazi a mbawala; nandiika pa misanje yanga.

35 Iye aphunzitsa manja anga nkhondo; kotero kuti manja anga alifula uta wamkuwa.

36 Ndiponso munandipatsa chikopa cha chipulumutso chanu; ndi kufatsa kwanu kunandikulitsa.

37 Munakulitsa kulunza kwanga pansi panga, ndi mapazi anga sanaterereke.

38 Ndinapirikitsa adani anga, ndi kuwaononga; ndiponso sindinabwerere mpaka nditawatha.

39 Ndinawatha ndi kuwapyoza, kuti sangathe kuuka, inde anagwa pansi pa mapazi anga.

40 Pakuti Inu munandimanga m'chuuno ndi mphamvu ya kunkhondo; munandigonjetsera akundiukira.

41 Munatembenuzitsanso adani anga andipatse mbuyo, kuti ndiwalikhe akudana ndi ine.

42 Anayang'ana iwo, koma panalibe wopulumutsa; ngakhale kwa Yehova, koma Iye sanawayankhe.

43 Pomwepo ndinawasansantha asalale ngati fumbi la padziko, ndinawapondereza ngati dothi la m'makwalala.

44 Inunso munandipulumutsa ine pa kulimbana kwa anthu anga; munandisunga ndikhale mutu wa amitundu; Anthu amene sindinawadziwe adzanditumikira ine.

45 Alendo adzandigonjera ine, pakumva za ine, adzandimvera pomwepo.

46 Alendo adzafota, nadzabwera ndi kunthunthumira otuluka mokwiririka mwao.

47 Yehova ali ndi moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa; ndipo akulitsidwe Mulungu wa thanthwe la chipulumutso changa;

48 inde Mulungu wakundibwezera chilango ine, ndi kundigonjetsera anthu a mitundu.

49 Amene anditulutsa kwa adani anga; inde mundikweza ine pamwamba pa iwo akundiukira; mundipulumutsa kwa munthu wachiwawa.

50 Chifukwa chake ndidzakuongani Yehova, pakati pa amitundu, ndipo ndidzaimba zolemekeza dzina lanu.

51 Iye apatsa mfumu yake chipulumutso chachikulu; naonetsera chifundo wodzozedwa wake, kwa Davide ndi mbeu yake ku nthawi zonse.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa