Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

100 Mau a Mulungu Pa Nzeru Zochokera kwa Mzimu


1 Akorinto 12:8

Pakuti kwa mmodzi kwapatsidwa mwa Mzimu mau a nzeru; koma kwa mnzake mau a chidziwitso, monga mwa Mzimu yemweyo:

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:6

Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:17

kuti Mulungu wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa ulemerero, akupatseni inu mzimu wa nzeru, ndi wa vumbulutso kuti mukamzindikire Iye;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 2:2-3

kuti itonthozeke mitima yao, nalumikizike pamodzi iwo m'chikondi, kufikira chuma chonse cha chidzalo cha chidziwitso, kuti akazindikire iwo chinsinsi cha Mulungu, ndiye Khristu,

Ngati munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nazo zoyamba za dziko lapansi, mugonjeranji kuzoikikazo, monga ngati moyo wanu mukhala nao m'dziko lapansi,

usaikapo dzanja, usalawa, usakhudza,

(ndizo zonse zakuonongedwa pochita nazo), monga mwa malangizo ndi maphunziro a anthu?

Zimene zili naotu manenedwe a nzeru m'kutumikira kwa chifuniro cha mwini wake, ndi kudzichepetsa, ndi kusalabadira thupi; koma zilibe mphamvu konse yakuletsa chikhutitso cha thupi.

amene zolemera zonse za nzeru ndi chidziwitso zibisika mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:7

Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa; opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:13

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 111:10

Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:7

Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:17

Koma nzeru yochokera kumwamba iyamba kukhala yoyera, nikhalanso yamtendere, yaulere, yomvera bwino, yodzala chifundo ndi zipatso zabwino, yopanda tsankho, yosadzikometsera pamaso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:10

Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova; kudziwa Woyerayo ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:10-11

Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako, moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

kulingalira kudzakudikira, kuzindikira kudzakutchinjiriza;

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:13

Kwa Iye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi luntha ali nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 11:33

Ha! Kuya kwake kwa kulemera ndi kwa nzeru ndi kwa kudziwa kwake kwa Mulungu! Osasanthulikadi maweruzo ake, ndi njira zake nzosalondoleka!

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:11

Pakuti nzeru iposa ngale, ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 4:29-30

Ndipo Mulungu anampatsa Solomoni nzeru ndi luntha lambiri, ndi mtima wodziwa za mitundumitundu, zonga mchenga uli m'mphepete mwa nyanja.

Elihorefe ndi Ahiya ana a Sisa alembi, Yehosafati mwana wa Ahiludi wolembera mbiri,

Ndipo nzeru ya Solomoni inaposa nzeru za anthu onse akum'mawa, ndi nzeru zonse za ku Ejipito.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:15-16

Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;

akuchita machawi, popeza masiku ali oipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:7

Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:14

Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa; ndine luntha; ndili ndi mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:15

ndi kuti kuyambira ukhanda wako wadziwa malembo opatulika, okhoza kukupatsa nzeru kufikira chipulumutso, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:16

Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golide, kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:6-7

Koma tilankhula nzeru mwa angwiro; koma si nzeru ya nthawi ino ya pansi pano, kapena ya akulu a nthawi ino ya pansi pano, amene alinkuthedwa;

koma tilankhula nzeru ya Mulungu m'chinsinsi, yobisikayo, imene Mulungu anaikiratu, pasanakhale nyengo za pansi pano, ku ulemerero wathu,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:30

Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru, ndi lilime lake linena chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:66

Mundiphunzitse chisiyanitso ndi nzeru; pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:13

Ndani ali wanzeru, ndi waluso mwa inu? Aonetsere ndi mayendedwe ake abwino ntchito zake mu nzeru yofatsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 1:17

Koma anyamata amene anai, Mulungu anawapatsa chidziwitso ndi luntha la m'mabuku ali onse, ndi nzeru; koma Daniele anali nalo luntha la m'masomphenya ndi maloto onse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:12

Mutidziwitse kuwerenga masiku athu motero, kuti tikhale nao mtima wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:33

Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru; ndipo chifatso chitsogolera ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:20

Tamvera uphungu, nulandire mwambo, kuti ukhale wanzeru pa chimaliziro chako.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:98-99

Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga; pakuti akhala nane chikhalire.

Ndili nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse; pakuti ndilingalira mboni zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 33:6

Ndipo kudzakhala chilimbiko m'nthawi zako, chipulumutso chambiri, nzeru ndi kudziwa; kuopa kwa Yehova ndiko chuma chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:3-4

Nzeru imangitsa nyumba; luntha liikhazikitsa.

Ndinapita pamunda wa waulesi, polima mphesa munthu wosowa nzeru.

Taonani, ponsepo panamera minga, ndi kuwirirapo khwisa; tchinga lake lamiyala ndi kupasuka.

Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira, ndinaona ndi kulandira mwambo.

Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono, kungomanga manja pang'ono m'kugona,

ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala; ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa.

Kudziwa kudzaza zipinda zake ndi chuma chonse chofunika cha mtengo wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:23

Masewero a chitsiru ndiwo kuchita zoipa; koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 7:24

Chifukwa chimenechi yense amene akamva mau anga amenewa, ndi kuwachita, ndidzamfanizira iye ndi munthu wochenjera, amene anamanga nyumba yake pathanthwe;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:8

Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake; koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 16:27

kwa Mulungu wanzeru yekhayo, mwa Yesu Khristu, kwa yemweyo ukhale ulemerero kunthawi zonse. Amen.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:130

Potsegulira mau anu paunikira; kuzindikiritsa opusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:20

Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:24

koma kwa iwo oitanidwa, ndiwo Ayuda ndi Agriki, Khristu mphamvu ya Mulungu, ndi nzeru ya Mulungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:28

Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 4:5-6

Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kuchita machawi nthawi ingatayike.

Mau anu akhale m'chisomo, okoleretsa, kuti mukadziwe inu mayankhidwe anu a kwa yense akatani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:30

Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 21:15

Pakuti Ine ndidzakupatsani inu kamwa ndi nzeru, zimene adani anu onse sadzatha kuzikana kapena kuzitsutsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:10

Koma kwa ife Mulungu anationetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula zonse, zakuya za Mulungu zomwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:15

Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake; koma wanzeru amamvera uphungu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:2

Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa; koma m'kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 28:29

Ichinso chifumira kwa Yehova wa makamu, uphungu wake uzizwitsa ndi nzeru yake impambana.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 3:10

kuti mu Mpingo azindikiritse tsopano kwa akulu ndi maulamuliro m'zakumwamba nzeru ya mitundumitundu ya Mulungu,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 32:8

Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo; ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:35

pakuti wondipeza ine apeza moyo; Yehova adzamkomera mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:2

Pakudza kudzikuza padzanso manyazi; koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 50:4

Ambuye Yehova wandipatsa Ine lilime la ophunzira, kuti ndidziwe kunena mau akuchirikiza iye amene ali wolema. Iye andigalamutsa m'mawa ndi m'mawa, nagalamutsa khutu langa kuti limve monga ophunzira.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 2:21

pakuti amasanduliza nthawi ndi nyengo, achotsa mafumu, nalonga mafumu, apatsa anzeru nzeru, ndi chidziwitso kwa iwo okhoza kuzindikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:12-13

Koma nzeru, idzapezeka kuti? Ndi luntha, malo ake ali kuti?

Munthu sadziwa mtengo wake; ndipo silipezeka m'dziko la amoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:15

Mtima wa wozindikira umaphunzira; khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4-5

Mundidziwitse njira zanu, Yehova; Mundiphunzitse mayendedwe anu.

Munditsogolere m'choonadi chanu, ndipo mundiphunzitse; pakuti Inu ndinu Mulungu wa chipulumutso changa; Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:9

Anatizindikiritsa ife chinsinsi cha chifuniro chake, monga kunamkomera ndi monga anatsimikiza mtima kale mwa Iye,

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:28

amene timlalikira ife, ndi kuchenjeza munthu aliyense ndi kuphunzitsa munthu aliyense mu nzeru zonse, kuti tionetsere munthu aliyense wamphumphu mwa Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:8

Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima; malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:6

Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza; koma wozindikira saona vuto m'kuphunzira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:97-98

Ha! Ndikondadi chilamulo chanu; ndilingiriramo ine tsiku lonse.

Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga; pakuti akhala nane chikhalire.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:16-17

Lemba lililonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m'chilungamo:

kuti munthu wa Mulungu akhale woyenera, wokonzeka kuchita ntchito iliyonse yabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:30

Koma kwa Iye muli inu mwa Khristu Yesu, amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi chilungamo ndi chiyeretso ndi chiombolo;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:5-6

Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

usasiye nzeru, ndipo idzakusunga; uikonde, idzakutchinjiriza.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 32:7-8

Ndinati, Amisinkhu anene, ndi a zaka zochuluka alangize nzeru.

Koma m'munthu muli mzimu, ndi mpweya wa Wamphamvuyonse wawazindikiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Eksodo 31:3

ndipo ndamdzaza ndi mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi chidziwitso, ndi m'ntchito zilizonse,

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 3:9

Patsani tsono kapolo wanu mtima womvera wakuweruza anthu anu; kuti ndizindikire pakati pa zabwino ndi zoipa; pakuti akutha ndani kuweruza anthu anu ambiri amene?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:9

Mtima wa munthu ulingalira njira yake; koma Yehova ayendetsa mapazi ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:1-6

Mwananga, ukalandira mau anga, ndi kusunga malamulo anga;

Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako, moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

kulingalira kudzakudikira, kuzindikira kudzakutchinjiriza;

kukupulumutsa kunjira yoipa, kwa anthu onena zokhota;

akusiya mayendedwe olungama, akayende m'njira za mdima;

omwe asangalala pochita zoipa, nakondwera ndi zokhota zoipa;

amene apotoza njira zao, nakhotetsa mayendedwe ao.

Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere, kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake;

wosiya bwenzi la ubwana wake, naiwala chipangano cha Mulungu wake.

Nyumba yake itsikira kuimfa, ndi mayendedwe ake kwa akufa;

onse akunka kwa iye sabweranso, safika kunjira za moyo;

kutcherera makutu ako kunzeru, kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

nzeru idzakuyendetsa m'njira ya anthu abwino, kuti usunge mayendedwe a olungama.

Pakuti oongoka mtima adzakhala m'dziko, angwiro nadzatsalamo.

Koma oipa adzalikhidwa m'dziko, achiwembu adzazulidwamo.

ukaitananso luntha, ndi kufuulira kuti ukazindikire;

ukaifunafuna ngati siliva, ndi kuipwaira ngati chuma chobisika;

pompo udzazindikira kuopa Yehova ndi kumdziwadi Mulungu.

Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 5:11-12

pali munthu mu ufumu mwanu mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera; ndipo masiku a atate wanu munapezeka mwa iye kuunika, ndi luntha, ndi nzeru, ngati nzeru ya milungu; ndipo mfumu Nebukadinezara atate wanu, inde mfumu atate wanu anamuika akhale mkulu wa alembi, openda, Ababiloni, ndi alauli;

popeza mu Daniele yemweyo, amene mfumu adamutcha Belitesazara, mudapezeka mzimu wopambana, ndi chidziwitso, ndi luntha, kumasulira maloto ndi kutanthauzira mau ophiphiritsa ndi kumasula mfundo. Amuitane Daniele tsono, iye adzafotokozera kumasuliraku.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 2:40

Ndipo mwanayo anakula nalimbika, nalikudzala ndi nzeru; ndi chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:8-9

chimene anatichulukitsira ife m'nzeru zonse, ndi chisamaliro.

Anatizindikiritsa ife chinsinsi cha chifuniro chake, monga kunamkomera ndi monga anatsimikiza mtima kale mwa Iye,

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 34:11

Idzani ananu ndimvereni ine, ndidzakulangizani zakumuopa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:23

Gula ntheradi, osaigulitsa; nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yeremiya 9:23-24

Atero Yehova, wanzeru asadzitamandire m'nzeru zake, wamphamvu asadzitamandire m'mphamvu yake, wachuma asadzitamandire m'chuma chake;

koma wakudzitamandira adzitamandire adzikweze umo, kuti ali wakuzindikira, ndi kundidziwa Ine, kuti ndine Yehova wakuchita zokoma mtima, chiweruziro, ndi chilungamo m'dziko lapansi, pakuti m'menemo ndikondwerera, ati Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Atesalonika 5:21

Yesani zonse; sungani chokomacho,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:17

Akundikonda ndiwakonda; akundifunafuna adzandipeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Machitidwe a Atumwi 6:3

Chifukwa chake, abale, yang'anani mwa inu amuna asanu ndi awiri a mbiri yabwino, odzala ndi Mzimu ndi nzeru, amene tikawaike asunge ntchito iyi.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:24

Nzeru ili pamaso pa wozindikira; koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:12-13

Koma sitinalandira ife mzimu wa dziko lapansi, koma Mzimu wa kwa Mulungu, kuti tikadziwe zimene zipatsidwa kwa ife ndi Mulungu kwaufulu.

Zimenenso tilankhula, si ndi mau ophunzitsidwa ndi nzeru za munthu, koma ophunzitsidwa ndi Mzimu; ndi kulinganiza zamzimu ndi zamzimu.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:28

Kodi iwe sunadziwe? Kodi sunamve? Mulungu wachikhalire, Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, salefuka konse, salema; nzeru zake sizisanthulika.

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 3:16

Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalimo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Luka 11:49

Mwa ichinso nzeru ya Mulungu inati, Ndidzatumiza kwa iwo aneneri ndi atumwi; ndipo ena a iwo adzawapha, nadzawazunza;

Mutu    |  Mabaibulo
Aroma 12:2

Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:5-6

Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;

umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

Mutu    |  Mabaibulo
Mateyu 10:16

Taonani, Ine ndikutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu; chifukwa chake khalani ochenjera monga njoka, ndi oona mtima monga nkhunda.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:10

Landirani mwambo wanga, si siliva ai; ndi nzeru kopambana ndi golide wosankhika.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:34

Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu; ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:5

kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira; ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:6-8

Pita kunyerere, waulesi iwe, penya njira zao nuchenjere;

zilibe mfumu, ngakhale kapitao, ngakhale mkulu;

koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe; ndipo zituta dzinthu zao m'masika.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:12

Kwa okalamba kuli nzeru, ndi kwa a masiku ochuluka luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:14

Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa; koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:30

Chipatso cha wolungama ndi mtengo wa moyo; ndipo wokola mtima ali wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:9

Kuopa Yehova kuli mbee, kwakukhalabe nthawi zonse; maweruzo a Yehova ali oona, alungama konsekonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Yohane 16:13

Koma atadza Iyeyo, Mzimu wa choonadi, adzatsogolera inu m'choonadi chonse; pakuti sadzalankhula za Iye mwini; koma zinthu zilizonse adzazimva, adzazilankhula; ndipo zinthu zilinkudza adzakulalikirani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:1

Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate; koma wonyoza samvera chidzudzulo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 12:31

Koma funitsitsani mphatso zoposa. Ndipo ndikuonetsani njira yokoma yoposatu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:160

Chiwerengero cha mau anu ndicho choonadi; ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo