Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Masalimo 119:34 - Buku Lopatulika

34 Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu; ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

34 Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu; ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

34 Patseni nzeru kuti ndizisunga malamulo anu, ndiziŵatsata ndi mtima wanga wonse.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.

Onani mutuwo Koperani




Masalimo 119:34
26 Mawu Ofanana  

Chokhachi, Yehova akupatse nzeru ndi luntha, nakulangize za Israele, kuti usunge chilamulo cha Yehova Mulungu wako.


Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.


Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.


Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse; ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.


Ndizindikira koposa okalamba popeza ndinasunga malangizo anu.


Malangizo anu andizindikiritsa; chifukwa chake ndidana nao mayendedwe onse achinyengo.


Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni; kuti ndidziwe mboni zanu.


Potsegulira mau anu paunikira; kuzindikiritsa opusa.


Mboni zanu ndizo zolungama kosatha; mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.


Kufuula kwanga kuyandikire pamaso panu, Yehova; mundizindikiritse monga mwa mau anu.


Odala iwo akusunga mboni zake, akumfuna ndi mtima wonse;


Ndinapemba pankhope panu ndi mtima wanga wonse: Mundichitire chifundo monga mwa mau anu.


Mundiphunzitse chisiyanitso ndi nzeru; pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.


Odzikuza anandipangira bodza: Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.


Manja anu anandilenga nandiumba; mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.


Ndinatonthola osanena mau, ndinakhala chete osalawa chokoma; ndipo chisoni changa chinabuka.


Chifukwa chake yense wakumasula limodzi la malamulo amenewa ang'onong'ono, nadzaphunzitsa anthu chomwecho, adzatchulidwa wamng'onong'ono mu Ufumu wa Kumwamba; koma yense wakuchita ndi kuphunzitsa awa, iyeyu adzatchulidwa wamkulu mu Ufumu wa Kumwamba.


Chifukwa chimenechi yense amene akamva mau anga amenewa, ndi kuwachita, ndidzamfanizira iye ndi munthu wochenjera, amene anamanga nyumba yake pathanthwe;


Ngati munthu aliyense afuna kuchita chifuniro chake, adzazindikira za chiphunzitsocho, ngati chichokera kwa Mulungu, kapena ndilankhula zochokera kwa Ine ndekha.


Chifukwa chake asungeni, achiteni; pakuti ichi ndi nzeru zanu ndi chidziwitso chanu pamaso pa mitundu ya anthu akumva malemba ndi kuti, Ndithu mtundu waukulu uwu, ndiwo athu anzeru ndi akuzindikira.


Koma iye wakupenyerera m'lamulo langwiro, ndilo laufulu, natero chipenyerere, ameneyo, posakhala wakumva wakuiwala, komatu wakuchita ntchito, adzakhala wodala m'kuchita kwake.


Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.


Musamanenerana, abale. Wonenera mbale, kapena woweruza mbale wake, anenera lamulo, naweruza lamulo: koma ngati uweruza lamulo, suli wochita lamulo, komatu woweruza.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa