Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -

Miyambo 2 - Buku Lopatulika


Ukoma ndi phindu lake la Nzeru

1 Mwananga, ukalandira mau anga, ndi kusunga malamulo anga;

2 kutcherera makutu ako kunzeru, kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

3 ukaitananso luntha, ndi kufuulira kuti ukazindikire;

4 ukaifunafuna ngati siliva, ndi kuipwaira ngati chuma chobisika;

5 pompo udzazindikira kuopa Yehova ndi kumdziwadi Mulungu.

6 Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

7 Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; ndiye chikopa cha oyenda molunjika;

8 kuti atchinjirize njira za chiweruzo, nadikire khwalala la opatulidwa ake.

9 Pamenepo udzazindikira chilungamo ndi chiweruzo, zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10 Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako, moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

11 kulingalira kudzakudikira, kuzindikira kudzakutchinjiriza;

12 kukupulumutsa kunjira yoipa, kwa anthu onena zokhota;

13 akusiya mayendedwe olungama, akayende m'njira za mdima;

14 omwe asangalala pochita zoipa, nakondwera ndi zokhota zoipa;

15 amene apotoza njira zao, nakhotetsa mayendedwe ao.

16 Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere, kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake;

17 wosiya bwenzi la ubwana wake, naiwala chipangano cha Mulungu wake.

18 Nyumba yake itsikira kuimfa, ndi mayendedwe ake kwa akufa;

19 onse akunka kwa iye sabweranso, safika kunjira za moyo;

20 nzeru idzakuyendetsa m'njira ya anthu abwino, kuti usunge mayendedwe a olungama.

21 Pakuti oongoka mtima adzakhala m'dziko, angwiro nadzatsalamo.

22 Koma oipa adzalikhidwa m'dziko, achiwembu adzazulidwamo.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi
Titsatireni:



Zotsatsa