Mavesi a Baibulo

Zotsatsa


Gulu Laling'ono

150 Maupangiri a Mulungu Ochokera m'Baibulo


Miyambo 2:6

Pakuti Yehova apatsa nzeru; kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m'kamwa mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 1:5

Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:10

Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova; kudziwa Woyerayo ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:13-14

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha;

pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:7

Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa; opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 111:10

Kumuopa Yehova ndiko chiyambi cha nzeru; onse akuchita chotero ali nacho chidziwitso chokoma; chilemekezo chake chikhalitsa kosatha.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:7

Nzeru ipambana, tatenga nzeru; m'kutenga kwako konseko utenge luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 12:13

Kwa Iye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi luntha ali nazo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:20

Tamvera uphungu, nulandire mwambo, kuti ukhale wanzeru pa chimaliziro chako.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 1:17

kuti Mulungu wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa ulemerero, akupatseni inu mzimu wa nzeru, ndi wa vumbulutso kuti mukamzindikire Iye;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:11

Pakuti nzeru iposa ngale, ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yakobo 3:17

Koma nzeru yochokera kumwamba iyamba kukhala yoyera, nikhalanso yamtendere, yaulere, yomvera bwino, yodzala chifundo ndi zipatso zabwino, yopanda tsankho, yosadzikometsera pamaso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:10-11

Landirani mwambo wanga, si siliva ai; ndi nzeru kopambana ndi golide wosankhika.

Pakuti nzeru iposa ngale, ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:16

Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golide, kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 2:2-3

kuti itonthozeke mitima yao, nalumikizike pamodzi iwo m'chikondi, kufikira chuma chonse cha chidzalo cha chidziwitso, kuti akazindikire iwo chinsinsi cha Mulungu, ndiye Khristu,

Ngati munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nazo zoyamba za dziko lapansi, mugonjeranji kuzoikikazo, monga ngati moyo wanu mukhala nao m'dziko lapansi,

usaikapo dzanja, usalawa, usakhudza,

(ndizo zonse zakuonongedwa pochita nazo), monga mwa malangizo ndi maphunziro a anthu?

Zimene zili naotu manenedwe a nzeru m'kutumikira kwa chifuniro cha mwini wake, ndi kudzichepetsa, ndi kusalabadira thupi; koma zilibe mphamvu konse yakuletsa chikhutitso cha thupi.

amene zolemera zonse za nzeru ndi chidziwitso zibisika mwa Iye.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:25

Chifukwa kuti chopusa cha Mulungu chiposa anthu ndi nzeru zao; ndipo chofooka cha Mulungu chiposa anthu ndi mphamvu yao.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:15

Mtima wa wozindikira umaphunzira; khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:23

Masewero a chitsiru ndiwo kuchita zoipa; koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:28

Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 7:12

Pakuti nzeru itchinjiriza monga ndalama zitchinjiriza; koma kudziwa kupambana, chifukwa nzeru isunga moyo wa eni ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:10

Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:8

Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake; koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:2

Pakudza kudzikuza padzanso manyazi; koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:6-7

Koma tilankhula nzeru mwa angwiro; koma si nzeru ya nthawi ino ya pansi pano, kapena ya akulu a nthawi ino ya pansi pano, amene alinkuthedwa;

koma tilankhula nzeru ya Mulungu m'chinsinsi, yobisikayo, imene Mulungu anaikiratu, pasanakhale nyengo za pansi pano, ku ulemerero wathu,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:5-6

Tenga nzeru, tenga luntha; usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

usasiye nzeru, ndipo idzakusunga; uikonde, idzakutchinjiriza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:2

kutcherera makutu ako kunzeru, kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:11

Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru, ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 33:6

Ndipo kudzakhala chilimbiko m'nthawi zako, chipulumutso chambiri, nzeru ndi kudziwa; kuopa kwa Yehova ndiko chuma chake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:1-2

Kodi nzeru siitana, luntha ndi kukweza mau ake?

Landirani mwambo wanga, si siliva ai; ndi nzeru kopambana ndi golide wosankhika.

Pakuti nzeru iposa ngale, ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo.

Ine Nzeru ndikhala m'kuchenjera, ngati m'nyumba yanga; ndimapeza kudziwa ndi zolingalira.

Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa; kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.

Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa; ndine luntha; ndili ndi mphamvu.

Mwa ine mafumu alamulira; akazembe naweruza molungama.

Mwa ine akalonga ayang'anira, ndi akulu, ngakhale oweruza onse a m'dziko.

Akundikonda ndiwakonda; akundifunafuna adzandipeza.

Katundu ndi ulemu zili ndi ine, chuma chosatha ndi chilungamo.

Chipatso changa chiposa golide, ngakhale golide woyengeka; phindu langa liposa siliva wosankhika.

Iima pamwamba pa mtunda, pa mphambano za makwalala;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:13

Gwira mwambo, osauleka; uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:12

Lozetsa mtima wako kumwambo, ndi makutu ako ku mau anzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:5

kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira; ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:66

Mundiphunzitse chisiyanitso ndi nzeru; pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:35-36

pakuti wondipeza ine apeza moyo; Yehova adzamkomera mtima.

Koma wondichimwira apweteka moyo wake; onse akundida ine akonda imfa.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Timoteyo 3:15

ndi kuti kuyambira ukhanda wako wadziwa malembo opatulika, okhoza kukupatsa nzeru kufikira chipulumutso, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:9

Ukachenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yake; ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:7

Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:7

Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:20-21

Mwananga, tamvera mau anga; tcherera makutu ku zonena zanga.

Asachoke kumaso ako; uwasunge m'kati mwa mtima wako.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 22:17

Tchera makutu ako, numvere mau a anzeru, nulozetse mtima wako kukadziwa zanga.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:97-98

Ha! Ndikondadi chilamulo chanu; ndilingiriramo ine tsiku lonse.

Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga; pakuti akhala nane chikhalire.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:21

Mwananga, zisachokere kumaso ako; sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:14

Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa; koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:12-13

Koma nzeru, idzapezeka kuti? Ndi luntha, malo ake ali kuti?

Munthu sadziwa mtengo wake; ndipo silipezeka m'dziko la amoyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:3-4

Nzeru imangitsa nyumba; luntha liikhazikitsa.

Ndinapita pamunda wa waulesi, polima mphesa munthu wosowa nzeru.

Taonani, ponsepo panamera minga, ndi kuwirirapo khwisa; tchinga lake lamiyala ndi kupasuka.

Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira, ndinaona ndi kulandira mwambo.

Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono, kungomanga manja pang'ono m'kugona,

ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala; ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa.

Kudziwa kudzaza zipinda zake ndi chuma chonse chofunika cha mtengo wake.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 40:13-14

Ndani anapangira mzimu wa Yehova, kapena kukhala phungu lake, ndi kumphunzitsa Iye?

Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya chiweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:10-11

Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako, moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

kulingalira kudzakudikira, kuzindikira kudzakutchinjiriza;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 4:5

Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kuchita machawi nthawi ingatayike.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 1:1-2

Wodala munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa, kapena wosaimirira m'njira ya ochimwa, kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.

Komatu m'chilamulo cha Yehova muli chikondwerero chake; ndipo m'chilamulo chake amalingirira usana ndi usiku.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:12

Mutidziwitse kuwerenga masiku athu motero, kuti tikhale nao mtima wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:33

Imvani mwambo, mukhale anzeru osaukana.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:27

Wopanda chikamwakamwa apambana kudziwa; ndipo wofatsa mtima ali wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:8

Wolandira nzeru akonda moyo wake; wosunga luntha adzapeza zabwino.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 3:19

Pakuti nzeru ya dziko lino lapansi ili yopusa kwa Mulungu. Pakuti kwalembedwa, Iye agwira anzeru m'chenjerero lao;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:5

Oipa samvetsetsa chiweruzo; koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 32:8

Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo; ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:6

Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza; koma wozindikira saona vuto m'kuphunzira.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:33

Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru; ndipo chifatso chitsogolera ulemu.

Mutu    |  Mabaibulo
Aefeso 5:15-17

Potero, penyani bwino umo muyendera, si monga opanda nzeru, koma monga anzeru;

akuchita machawi, popeza masiku ali oipa.

Chifukwa chake musakhale opusa, koma dziwitsani chifuniro cha Ambuye nchiyani.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:14

Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa; ndine luntha; ndili ndi mphamvu.

Mutu    |  Mabaibulo
Danieli 2:20-21

Daniele anayankha, nati, Lilemekezedwe dzina la Mulungu kunthawi za nthawi, pakuti nzeru ndi mphamvu zili zake;

pakuti amasanduliza nthawi ndi nyengo, achotsa mafumu, nalonga mafumu, apatsa anzeru nzeru, ndi chidziwitso kwa iwo okhoza kuzindikira.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 6:6-8

Pita kunyerere, waulesi iwe, penya njira zao nuchenjere;

zilibe mfumu, ngakhale kapitao, ngakhale mkulu;

koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe; ndipo zituta dzinthu zao m'masika.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:2

Wopusa sakondwera ndi kuzindikira; koma kungovumbulutsa za m'mtima mwake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 25:4-5

Mundidziwitse njira zanu, Yehova; Mundiphunzitse mayendedwe anu.

Munditsogolere m'choonadi chanu, ndipo mundiphunzitse; pakuti Inu ndinu Mulungu wa chipulumutso changa; Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 55:8-9

Pakuti maganizo anga sali maganizo anu, ngakhale njira zanu sizili njira zanga, ati Yehova.

Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, momwemo njira zanga zili zazitali kupambana njira zanu, ndi maganizo anga kupambana maganizo anu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:8

Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo; koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 4:29

Ndipo Mulungu anampatsa Solomoni nzeru ndi luntha lambiri, ndi mtima wodziwa za mitundumitundu, zonga mchenga uli m'mphepete mwa nyanja.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:1

Wokonda mwambo akonda kudziwa; koma wakuda chidzudzulo apulukira.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:144

Mboni zanu ndizo zolungama kosatha; mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 5:12-13

Apititsa pachabe ziwembu za ochenjera, kuti manja ao sangathe kuchita chopangana chao.

Akola eni nzeru m'kuchenjera kwao, ndi uphungu wa opotoka mtima usonthokera pachabe.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:21

Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru; koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 10:12

Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga chisomo; koma milomo ya chitsiru idzachimeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:1

Mwananga, ukalandira mau anga, ndi kusunga malamulo anga;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:20-21

Nzeru ifuula panja; imveketsa mau ake pabwalo;

iitana posonkhana anthu polowera pachipata; m'mzinda inena mau ake,

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:33-34

Imvani mwambo, mukhale anzeru osaukana.

Ngwodala amene andimvera, nadikira pa zitseko zanga tsiku ndi tsiku, ndi kulinda pa mphuthu za makoma anga;

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 2:26

Pakuti yemwe Mulungu amuyesa wabwino ampatsa nzeru ndi chidziwitso ndi chimwemwe; koma wochimwa amlawitsa vuto la kusonkhanitsa ndi kukundika, kuti aperekere yemwe Mulungu amuyesa wabwino. Ichinso ndi chabe ndi kungosautsa mtima.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:1-2

Ananu, mverani mwambo wa atate, nimutchere makutu mukadziwe luntha;

Tamvera mwananga, nulandire mau anga; ndipo zaka za moyo wako zidzachuluka.

Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru, ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.

Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda; ukathamanga, sudzaphunthwa.

Gwira mwambo, osauleka; uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

Usalowe m'mayendedwe ochimwa, usayende m'njira ya oipa.

Pewapo, osapitamo; patukapo, nupitirire.

Pakuti akapanda kuchita zoipa, samagona; ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwachokera.

Pakuti amadya chakudya cha uchimo, namwa vinyo wa chifwamba.

Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha, kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee.

Njira ya oipa ikunga mdima; sadziwa chimene chiwaphunthwitsa.

pakuti ndikuphunzitsani zabwino; musasiye chilangizo changa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 73:24

Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu, ndipo mutatero, mudzandilandira mu ulemerero.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:15

Alipo golide ndi ngale zambiri; koma milomo yodziwa ndiyo chokometsera cha mtengo wapatali.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:130

Potsegulira mau anu paunikira; kuzindikiritsa opusa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yesaya 5:21

Tsoka kwa iwo amene adziyesera anzeru ndi ochenjera!

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:14

Potero udzadziwa kuti nzeru ili yotero m'moyo wako; ngati waipeza padzakhala mphotho, ndipo chiyembekezo chako sichidzalephereka.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Mafumu 3:9

Patsani tsono kapolo wanu mtima womvera wakuweruza anthu anu; kuti ndizindikire pakati pa zabwino ndi zoipa; pakuti akutha ndani kuweruza anthu anu ambiri amene?

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:10

Landirani mwambo wanga, si siliva ai; ndi nzeru kopambana ndi golide wosankhika.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:14

Anzeru akundika zomwe adziwa; koma m'kamwa mwa chitsiru muononga tsopano lino.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:1

Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate; koma wonyoza samvera chidzudzulo.

Mutu    |  Mabaibulo
2 Petro 1:5-6

Ndipo mwa ichi chomwe, pakutengeraponso changu chonse, muonjezerapo ukoma pa chikhulupiriro chanu, ndi paukoma chizindikiritso;

ndi pachizindikiritso chodziletsa; ndi pachodziletsa chipiriro; ndi pachipiriro chipembedzo;

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:99

Ndili nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse; pakuti ndilingalira mboni zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:3-4

Chifundo ndi choonadi zisakusiye; uzimange pakhosi pako; uzilembe pamtima pako;

Usakangane ndi munthu chabe, ngati sanakuchitire choipa.

Usachitire nsanje munthu wachiwawa; usasankhe njira yake iliyonse.

Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova; koma chinsinsi chake chili ndi oongoka.

Yehova atemberera za m'nyumba ya woipa; koma adalitsa mokhalamo olungama.

Anyozadi akunyoza, koma apatsa akufatsa chisomo.

Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao; koma opusa adzakweza manyazi.

motero udzapeza chisomo ndi nzeru yabwino, pamaso pa Mulungu ndi anthu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:23

Mtima wa wanzeru uchenjeza m'kamwa mwake, nuphunzitsanso milomo yake.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:30

Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru, ndi lilime lake linena chiweruzo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 5:1-2

Mwananga, mvera nzeru yanga; tcherera makutu ku luntha langa;

kuti mphamvu yako isakhutitse alendo, ndi kuti usagwire ntchito m'nyumba ya wachilendo;

ungalire pa chimaliziro chako, pothera nyama yako ndi thupi lako;

ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo, mtima wanga ndi kunyoza chidzudzulo;

ndipo sindinamvere mau a aphunzitsi anga; ngakhale kutcherera makutu kwa akundilanga mwambo!

Ndikadakhala m'zoipa zonse, m'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.

Imwa madzi a m'chitsime mwako, ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.

Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja, ndi mitsinje ya madzi m'makwalala?

Ikhale ya iwe wekha, si ya alendo okhala nawe ai.

Adalitsike kasupe wako; ukondwere ndi mkazi wokula nayo.

Ngati mbawala yokonda ndi chinkhoma chachisomo, maere ake akukwanire nthawi zonse; ukodwe ndi chikondi chake osaleka.

ukasunge zolingalira, milomo yako ilabadire zomwe udziwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:19-20

Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha.

pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere.

Zakuya zinang'ambika ndi kudziwa kwake; thambo ligwetsa mame.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:12

kukupulumutsa kunjira yoipa, kwa anthu onena zokhota;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 15:7

Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru, koma mtima wa opusa suli wolungama.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:13-14

Mwananga, idya uchi pakuti ngwabwino, ndi chisa chake chitsekemera m'kamwa mwako.

Potero udzadziwa kuti nzeru ili yotero m'moyo wako; ngati waipeza padzakhala mphotho, ndipo chiyembekezo chako sichidzalephereka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:20

Wolabadira mau adzapeza bwino; ndipo wokhulupirira Yehova adala.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 12:8

Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yake; koma wokhota mtima adzanyozedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 32:8

Koma m'munthu muli mzimu, ndi mpweya wa Wamphamvuyonse wawazindikiritsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 1:2-4

Kudziwa nzeru ndi mwambo; kuzindikira mau ozindikiritsa;

Nzeru ifuula panja; imveketsa mau ake pabwalo;

iitana posonkhana anthu polowera pachipata; m'mzinda inena mau ake,

Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu? Onyoza ndi kukonda kunyoza, opusa ndi kuda nzeru?

Tembenukani pamene ndikudzudzulani; taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga, ndikudziwitsani mau anga.

Chifukwa ndaitana, ndipo munakana; ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;

koma munapeputsa uphungu wanga wonse, ndi kukana kudzudzula kwanga.

Inetu ndidzachitira chiphwete tsoka lanu, ndidzatonyola pakudza mantha anu;

pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula, ndi pofika tsoka lanu ngati kamvulumvulu; pakudza kwa inu vuto ndi nsautso.

Pamenepo adzandiitana, koma sindidzavomera; adzandifunatu, osandipeza ai;

chifukwa anada nzeru, sanafune kuopa Yehova;

kulandira mwambo wakusamalira machitidwe, chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika;

anakana uphungu wanga, nanyoza kudzudzula kwanga konse;

momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao, nadzakhuta zolingalira zao.

Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa achibwana kudzawapha; ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka, nadzakhala phee osaopa zoipa.

kuchenjeza achibwana, kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 23:15-16

Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru, mtima wanga wa inedi udzakondwa.

Imso zanga zidzasangalala, polankhula milomo yako zoongoka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 49:3

Pakamwa panga padzanena zanzeru; ndipo chilingiriro cha mtima wanga chidzakhala cha chidziwitso.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 1:30

Koma kwa Iye muli inu mwa Khristu Yesu, amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi chilungamo ndi chiyeretso ndi chiombolo;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:13

Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira; koma wopusa pamsana pake nthyole.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 11:30

Chipatso cha wolungama ndi mtengo wa moyo; ndipo wokola mtima ali wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:2

Kukhumba kosadziwa sikuli kwabwino; ndipo wofulumira ndi mapazi ake amachimwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 13:20

Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:11

Kulingalira kwa munthu kuchedwetsa mkwiyo; ulemerero wake uli wakuti akhululukire cholakwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:3

Nzeru imangitsa nyumba; luntha liikhazikitsa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:19

Pochuluka mau zolakwa sizisoweka; koma wokhala chete achita mwanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:24

Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna; munthu tsono angazindikire bwanji njira yake?

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 19:8

Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima; malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 16:32

Wosakwiya msanga aposa wamphamvu; wolamulira mtima wake naposa wolanda mzinda.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:25

Menya wonyoza, ndipo achibwana adzachenjera; nudzudzule wozindikira adzazindikira nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 49:15

Koma Mulungu adzaombola moyo wanga kumphamvu ya manda. Pakuti adzandilandira ine.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:10

Chidzudzulo chilowa m'kati mwa wozindikira, kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 28:26

Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa; koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:3

Utsiru wa munthu ukhotetsa njira yake; mtima wake udandaula pa Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 8:1

Ndani akunga wanzeru? Ndani adziwa tanthauzo la mau? Nzeru ya munthu iwalitsa nkhope yake, kuduwa kwa nkhope yake ndi kusanduka.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 119:125

Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni; kuti ndidziwe mboni zanu.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 2:3-4

ukaitananso luntha, ndi kufuulira kuti ukazindikire;

ukaifunafuna ngati siliva, ndi kuipwaira ngati chuma chobisika;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:18

Menya mwanako, chiyembekezero chilipo, osafunitsa kumuononga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 19:27

Ukangofuna, mwananga, kusochera kusiya mau akudziwitsa, leka kumva mwambo.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 20:18

Uphungu utsimikiza zolingalira, ponya nkhondo utapanga upo.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Akorinto 2:10-12

Koma kwa ife Mulungu anationetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula zonse, zakuya za Mulungu zomwe.

Pakuti ndani wa anthu adziwa za munthu, koma mzimu wa munthuyu uli mwa iye? Momwemonso za Mulungu palibe wina azidziwa, koma Mzimu wa Mulungu.

Koma sitinalandira ife mzimu wa dziko lapansi, koma Mzimu wa kwa Mulungu, kuti tikadziwe zimene zipatsidwa kwa ife ndi Mulungu kwaufulu.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 37:5

Pereka njira yako kwa Yehova; khulupiriranso Iye, adzachichita.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:5

Achibwana inu, chenjerani, opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 25:12

Monga mphete yagolide ndi chipini chagolide woyengeka, momwemo wanzeru wodzudzula pa khutu lomvera.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 4:25-27

Maso ako ayang'ane m'tsogolo, zikope zako zipenye moongoka.

Sinkhasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako; njira zako zonse zikonzeke.

Usapatuke kudzanja lamanja kapena kulamanzere; suntha phazi lako kusiya zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 10:31

M'kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru; koma lilime lokhota lidzadulidwa.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 90:17

Ndipo chisomo chake cha Ambuye Mulungu wathu chikhalire pa ife; ndipo mutikhazikitsire ife ntchito ya manja athu; inde, ntchito ya manja athu muikhazikitse.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 18:4

Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya; kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 17:24

Nzeru ili pamaso pa wozindikira; koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:9

Onsewo amveka ndi iye amene azindikira; alungama kwa akupeza nzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:11

Polangidwa wonyoza, wachibwana alandira nzeru, naphunzira pakuyang'ana pa wanzeru.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:15

Wachibwana akhulupirira mau onse; koma wochenjera asamalira mayendedwe ake.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 21:30

Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

Mutu    |  Mabaibulo
Masalimo 36:9

Pakuti chitsime cha moyo chili ndi Inu, M'kuunika kwanu tidzaona kuunika.

Mutu    |  Mabaibulo
Yobu 28:20-21

Koma nzeru ifuma kuti? Ndi luntha, pokhala pake pali kuti?

Popeza pabisikira maso a zamoyo zonse, pabisikiranso mbalame za m'mlengalenga.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:17

Akundikonda ndiwakonda; akundifunafuna adzandipeza.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 3:1-2

Mwananga, usaiwale malamulo anga, mtima wako usunge malangizo anga;

motero nkhokwe zako zidzangoti thee, mbiya zako zidzasefuka vinyo.

Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova, ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwake;

pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda; monga atate mwana amene akondwera naye.

Wodala ndi wopeza nzeru, ndi woona luntha;

pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, phindu lake liposa golide woyengeka.

Mtengo wake uposa ngale; ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lake; chuma ndi ulemu m'dzanja lake lamanzere.

Njira zake zili zokondweretsa, mayendedwe ake onse ndiwo mtendere.

Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira; wakuiumirira ngwodala.

Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; naika zamwamba ndi luntha.

pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, ndi zaka za moyo ndi mtendere.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 8:32-34

Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine, ngodala akusunga njira zanga.

Imvani mwambo, mukhale anzeru osaukana.

Ngwodala amene andimvera, nadikira pa zitseko zanga tsiku ndi tsiku, ndi kulinda pa mphuthu za makoma anga;

Mutu    |  Mabaibulo
Akolose 1:28

amene timlalikira ife, ndi kuchenjeza munthu aliyense ndi kuphunzitsa munthu aliyense mu nzeru zonse, kuti tionetsere munthu aliyense wamphumphu mwa Khristu;

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 24:5

Mwamuna wanzeru ngwamphamvu; munthu wodziwa ankabe nalimba.

Mutu    |  Mabaibulo
1 Timoteyo 4:15-16

Izi uzisamalitse; mu izi ukhale; kuti kukula mtima kwako kuonekere kwa onse.

Udzipenyerere wekha, ndi chiphunzitsocho. Uzikhala mu izi; pakuti pochita ichi udzadzipulumutsa iwe wekha ndi iwo akumva iwe.

Mutu    |  Mabaibulo
Mlaliki 12:13-14

Mau atha; zonse zamveka zatha; opa Mulungu, musunge malamulo ake; pakuti choyenera anthu onse ndi ichi.

Pakuti Mulungu adzanena mlandu wa zochita zonse, ndi zobisika zonse, ngakhale zabwino ngakhale zoipa.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 9:8-9

Usadzudzule wonyoza kuti angakude; dzudzula wanzeru adzakukonda.

Ukachenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yake; ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira.

Mutu    |  Mabaibulo
Miyambo 14:33

Nzeru ikhalabe m'mtima wa wozindikira, nidziwika pakati pa opusa.

Mutu    |  Mabaibulo