Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mlaliki 10:12 - Buku Lopatulika

12 Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga chisomo; koma milomo ya chitsiru idzachimeza.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

12 Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga chisomo; koma milomo ya chitsiru idzachimeza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

12 Mau a pakamwa pa munthu wanzeru amakondweretsa, koma pakamwa pa chitsiru mpoononga.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

12 Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa, koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.

Onani mutuwo Koperani




Mlaliki 10:12
36 Mawu Ofanana  

Koma asanafe, Davide adanena naye, Wadziphetsa ndi mtima wako; chifukwa pakamwa pako padachita umboni wakukutsutsa ndi kuti, Ine ndinapha wodzozedwa wa Yehova.


Koma ndikadakulimbikitsani ndi m'kamwa mwanga, ndi chitonthozo cha milomo yanga chikadatsitsa chisoni chanu.


Kunena za mutu wao wa iwo akundizinga, choipa cha milomo yao chiwaphimbe.


Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru, ndi lilime lake linena chiweruzo.


Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa; onse akuwaona adzawathawa.


Wotsinzinira achititsa chisoni; koma wodzudzula momveka achita mtendere.


Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo; koma chitsiru cholongolola chidzagwa.


Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga; koma lilime la anzeru lilamitsa.


Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa; koma m'kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.


Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwake; ndi mau a pa nthawi yake kodi sali abwino?


Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa; wolankhula mabodza sadzapulumuka.


Wokonda kuyera mtima, mfumu idzakhala bwenzi lake chifukwa cha chisomo cha milomo yake.


Monga munga wolasa dzanja la woledzera, momwemo mwambi m'kamwa mwa zitsiru.


Atsegula pakamwa pake ndi nzeru, ndipo chilangizo cha chifundo chili pa lilime lake.


Mau a anzeru akunga zisonga, omwe akundika mau amene mbusa mmodzi awapatsa mau ao akunga misomali yokhomedwa zolimba.


Chitsiru chimanga manja ake, ndipo chidya nyama yakeyake.


Usalankhule mwanthuku mtima wako, usafulumire kunena kanthu pamaso pa Mulungu; pakuti Mulungu ali kumwamba, iwe uli pansi; chifukwa chake mau ako akhale owerengeka.


Usalole m'kamwa mwako muchimwitse thupi lako; usanene pamaso pa mthenga kuti, Ndinaphophonya; Mulungu akwiyire mau ako chifukwa ninji, naononge ntchito ya manja ako?


Mau a anzeru achete amveka koposa kufuula kwa wolamulira mwa zitsiru.


Munthu wabwino atulutsa zabwino m'chuma chake chabwino, ndi munthu woipa atulutsa zoipa m'chuma chake choipa.


Ananena kwa iye, Pakamwa pako ndikuweruza, kapolo woipa iwe. Unadziwa kuti ine ndine munthu wouma mtima, wonyamula chimene sindinachiike, ndi wotuta chimene sindinachifese;


Ndipo onse anamchitira Iye umboni nazizwa ndi mau a chisomo akutuluka m'kamwa mwake; nanena, Kodi uyu si mwana wa Yosefe?


Nkhani yonse yovunda isatuluke m'kamwa mwanu, koma ngati pali ina yabwino kukumangirira monga mofunika ndiyo, kuti ipatse chisomo kwa iwo akumva.


Mau anu akhale m'chisomo, okoleretsa, kuti mukadziwe inu mayankhidwe anu a kwa yense akatani.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa